< Ezekieli 30 >
1 Yehova anandiyankhula kuti:
Perwerdigarning sözi manga kélip mundaq déyildi: —
2 “Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena. “‘Ufuwule mawu awa akuti, ‘Kalanga, tsiku lafika!’
I insan oghli, bésharet bérip: — Reb Perwerdigar mundaq deydu: — «Siler dad-peryad sélip: «Way shu küni!» — denglar!» — dégin.
3 Pakuti tsiku layandikira, tsiku la Yehova lili pafupi, tsiku la mitambo yakuda, tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.
Chünki kün yéqinlashti; berheq, Perwerdigarning küni, bulutlar qaplan’ghan kün yéqinlashti; u ellerning béshigha chüshidighan kündur.
4 Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto ndipo mavuto adzafika pa Kusi. Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto, chuma chake chidzatengedwa ndipo maziko ake adzagumuka.
Shuning bilen bir qilich Misir üstige chüshidu; öltürülgenler Misirda yiqilghanda, uning zor bayliqliri bulinip ketkende, uning ulliri örülüp chüshkende, Éfiopiyelikler derd-elem tartidu.
5 Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.
Éfiopiye, Put, Lud, barliq Erebiye, Liwiye we ehde qilin’ghan zémindikilermu Misir bilen bille qilichlinidu.
6 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: “‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu. Adzaphedwa ndi lupanga kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’” ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Reb Perwerdigar mundaq deydu: — Misirni qollaydighanlar yiqilidu; uning küchidin bolghan pexri yerge chüshidu; Migdoldin Sewen’giche bolghan xelq qilichlinidu, — deydu Reb Perwerdigar.
7 “‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja kupambana mabwinja ena onse opasuka, ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka kupambana mizinda ina yonse.
— Ular weyran qilin’ghan zéminlar arisida weyran qilinidu; uning sheherliri xarabe qilin’ghan sheherler arisida yatidu.
8 Nditatha kutentha Igupto ndi kupha onse omuthandiza, pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Shuning bilen, Men Misirgha ot salghinimda, uning yardimide bolghanlar sundurulghanda, ular Méning Perwerdigar ikenlikimni tonup yétidu;
9 “‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.
Shu küni elchiler Éfiopiyeni qorqitish üchün kémilerde olturup mendin chiqidu; Misirning béshigha chüshken kündek ularghimu azab-oqubet chüshidu; mana, u kéliwatidu!
10 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.
Reb Perwerdigar mundaq deydu: «Men yene Misirning top-top ademlirini Babil padishahi Néboqadnesarning qoli bilen tügitimen.
11 Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja adzabwera kudzawononga dzikolo. Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.
U we uning bilen kelgen xelqi, yeni ellerning arisidiki eng dehshetliki zéminni halak qilishqa élip kélinidu; ular Misir bilen qarshilishqa qilichlarni sughurup, zéminni öltürülgenler bilen tolduridu.
12 Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa. Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo. Ine Yehova ndayankhula.
Men Nil deryalirini qurutimen, We zéminni rezil ademlerning qoligha sétiwétimen; Zémin we uningda turghan hemmini yat ademlerning qolida weyrane qilimen; Menki Perwerdigar shundaq söz qilghan».
13 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzawononga mafano ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi. Simudzakhalanso mfumu mu Igupto, ndipo ndidzaopseza dziko lonse.
Reb Perwerdigar mundaq deydu: «Men Nof shehiridin butlarni yoqitimen, oyghan mebudlarnimu yoqitimen; Misir zéminidin qaytidin shahzade bolmas; Men Misir zéminini qorqunchqa chüshürimen.
14 Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi, ndi kutentha mzinda wa Zowani. Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.
Men Patros shehirini weyrane qilip, Zoan shehiride ot salimen, No shehiri üstidin höküm chiqirip jazalaymen.
15 Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu, linga lolimba la Igupto, ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.
Misirning istihkami bolghan Sin shehirining üstige qehrimni tökimen; No shehirining top-top ademlirini qiriwétimen.
16 Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto; Peluziumu adzazunzika ndi ululu. Malinga a Thebesi adzagumuka, ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.
Men Misirda bir ot salimen; Sin azablardin tolghinip kétidu; No shehiri bösülidu, Nof shehiri her küni yawlargha yüzlinidu.
17 Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti adzaphedwa ndi lupanga ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.
Awen we Pibeset sheherliridiki yigitler qilichlinidu; bu sheherler sürgün qilinidu.
18 Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima pamene ndidzathyola goli la Igupto; motero kunyada kwake kudzatha. Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda, ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.
Méning shu yerde Misirning boyunturuqlirini sundurghinimda, Tahpanes shehiride kün qarangghulishidu; uningda öz küchidin bolghan pexri yoqilidu; bir bulut uni qaplaydu; uning qizliri sürgün qilinidu.
19 Kotero ndidzalanga dziko la Igupto, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
Men shundaq qilip Misir üstidin höküm chiqirip jazalaymen; we shular Méning Perwerdigar ikenlikimni tonup yétidu».
20 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti:
On birinchi yili, birinchi ayning yettinchi künide shundaq boldiki, Perwerdigarning sözi manga kélip mundaq déyildi: —
21 “Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga.
I insan oghli, Men Misir padishahi Pirewnning bilikini sundurdum; we mana, u dawalinishqa téngilmidi, yaki qilich tutushqa téngiq bilen kücheytilmidi.
22 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake.
— Shunga Reb Perwerdigar mundaq deydu: «Mana, Men Misir padishahi Pirewn’ge qarshimen; Men uning bileklirini, hem küchlük bolghinini hem sundurulghan bilikini üzüwétimen; shuning bilen qilichini qolidin chüshürmen;
23 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri.
Misirliqlarni ellerge tarqitiwétimen, memliketler arisigha taritimen.
24 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo.
Men Babil padishahining qolini kücheytip, qilichimni uning qoligha tutquzimen; Men Pirewnning bileklirini sundurimenki, u Babil padishahi aldida ejili toshqan yarilan’ghan ademdek ah-zarlar bilen ingraydu.
25 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto.
Men Babil padishahining bileklirini kücheytimen, we Pirewnning bilekliri sanggilap qalidu; Men Öz qilichimni Babil padishahining qoligha tutquzghinimda, u uni Misir zémini üstige sozghinida, ular Méning Perwerdigar ikenlimni tonup yétidu;
26 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
we Men Misirliqlarni eller arisigha tarqitimen, memliketler ichige taritimen; we ular Méning Perwerdigar ikenlimni tonup yétidu».