< Ezekieli 30 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
І було мені слово Господнє таке:
2 “Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena. “‘Ufuwule mawu awa akuti, ‘Kalanga, tsiku lafika!’
„Сину лю́дський, пророкуй, і скажеш: Так говорить Господь Бог: Голосіть „Ой!“цього дня!
3 Pakuti tsiku layandikira, tsiku la Yehova lili pafupi, tsiku la mitambo yakuda, tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.
Бо близьки́й день, і близьки́й день Господній, день хма́рний, настає час наро́дів!
4 Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto ndipo mavuto adzafika pa Kusi. Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto, chuma chake chidzatengedwa ndipo maziko ake adzagumuka.
І при́йде меч на Єгипет, і буде тремті́ння в Етіопії, коли будуть падати забиті в Єгипті, і заберу́ть багатство його, і будуть розбиті осно́ви його.
5 Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.
Куш, і Пут, і Луд, і ввесь помішаний наро́д, і Кув, і сини землі заповіту попа́дають з ними від меча.
6 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: “‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu. Adzaphedwa ndi lupanga kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’” ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Так говорить Господь: І попа́дають підпо́ри Єгипту, і так упаде́ гординя сили його, від Міґдолу аж до Севене, від меча попа́дають у ньому, говорить Господь Бог.
7 “‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja kupambana mabwinja ena onse opasuka, ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka kupambana mizinda ina yonse.
І буде він спусто́шений серед попусто́шених країв, а міста́ його будуть серед міст поруйно́ваних.
8 Nditatha kutentha Igupto ndi kupha onse omuthandiza, pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
І пізнають вони, що Я — Господь, коли Я дам огонь на Єгипет, і будуть поторо́щені всі, хто йому помагає.
9 “‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.
Того дня повихо́дять посланці́ з-перед Мого лиця на кораблях, щоб налякати безпечну Етіопію, і буде через них жах, як у день Єгипту, бо це ось надхо́дить!
10 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.
Так говорить Господь Бог: І Я зроблю́ кінець єгипетському многолю́дству рукою Навуходоно́сора, вавилонського царя.
11 Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja adzabwera kudzawononga dzikolo. Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.
Він та наро́д його з ним, насильники лю́дів, будуть спрова́джені зни́щити землю, і вони повитягують мечі свої на Єгипет, — і напо́внять край побитими!
12 Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa. Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo. Ine Yehova ndayankhula.
I оберну́ Я річки́ на суході́л, і передам землю в руку злочинців, і спусто́шу край та все, що в ньому, рукою чужих. Я, Господь, це сказав!
13 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzawononga mafano ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi. Simudzakhalanso mfumu mu Igupto, ndipo ndidzaopseza dziko lonse.
Так говорить Господь Бог: І повигу́блюю божкі́в, і зроблю́ кінець бовва́нам з Нофу, і не буде вже князі́в в єгипетському кра́ї, і дам по́страх на єгипетську зе́млю.
14 Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi, ndi kutentha mzinda wa Zowani. Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.
І Па́трос спусто́шу, і дам огонь у Цоан, і буду вико́нувати при́суди в Но.
15 Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu, linga lolimba la Igupto, ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.
І виллю Я гнів Свій на Сіна, тверди́ню єгипетську, і ви́тну многолю́дство Но.
16 Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto; Peluziumu adzazunzika ndi ululu. Malinga a Thebesi adzagumuka, ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.
І пошлю́ Я огонь на Єгипет, сильно буде ко́рчитись Сін, а Но буде прола́маний, а на Ноф нападуть вороги вдень.
17 Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti adzaphedwa ndi lupanga ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.
Юнаки́ Авену та Пі-Весету попа́дають від меча, а інші пі́дуть у поло́н.
18 Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima pamene ndidzathyola goli la Igupto; motero kunyada kwake kudzatha. Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda, ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.
А в Тахпанхесі поте́мніє день, коли Я ламатиму там єгипетські я́рма, і скінчи́ться в ньому пиха́ сили його. Самого його хмара закриє, а його до́чки пі́дуть у поло́н...
19 Kotero ndidzalanga dziko la Igupto, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
І буду виконувати при́суди над Єгиптом, і вони пізна́ють, що Я — Госпо́дь!“
20 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti:
І сталося, за одина́дцятого року, першого місяця, сьомого дня місяця, було мені слово Господнє таке:
21 “Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga.
„Сину лю́дський, Я зламав раме́но фараона, єгипетського царя, і ось воно не буде перев'я́зане, щоб дати ліки, щоб покласти пов'я́зку, щоб обви́нути його, і щоб зміцни́ти його вхопи́тися за меча.
22 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake.
Тому так говорить Господь Бог: Ось Я на фараона, єгипетського царя, і поламаю раме́на його, те дуже та те зла́мане, і викину меча з його руки́.
23 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri.
І розпоро́шу Єгипет серед народів, і порозсипа́ю їх по края́х.
24 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo.
І зміцню раме́на вавилонського царя, і дам меча Свого в його руку, — і зламаю Я фараонові раме́на, і він буде стогнати сто́гоном проко́леного перед ним.
25 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto.
І зміцню́ Я раме́на вавилонського царя, а фараонові раме́на опаду́ть. І пізнають вони, що Я — Господь, коли Я дам Свого меча в руку вавилонського царя, і простягну́ його на єгипетську землю.
26 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
І розпоро́шу Єгипет серед наро́дів, і порозсипа́ю їх по края́х. І пізнають вони, що Я — Господь!“

< Ezekieli 30 >