< Ezekieli 30 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
RAB bana şöyle seslendi:
2 “Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena. “‘Ufuwule mawu awa akuti, ‘Kalanga, tsiku lafika!’
“İnsanoğlu, peygamberlik et ve de ki, ‘Egemen RAB şöyle diyor: “‘Ah o gün diye haykır.
3 Pakuti tsiku layandikira, tsiku la Yehova lili pafupi, tsiku la mitambo yakuda, tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.
Çünkü o gün yakın. RAB'bin günü yakın, Bulutların günü, Ulusların yıkım zamanı.
4 Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto ndipo mavuto adzafika pa Kusi. Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto, chuma chake chidzatengedwa ndipo maziko ake adzagumuka.
Bir kılıç Mısır'a karşı çıkacak. Kûş'u acılar saracak. Mısır'da vurulanlar yere serilince Ülkenin serveti alınıp götürülecek, Temelleri yok edilecek.
5 Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.
Mısır'la birlikte Kûş, Pût, Lud, Arabistan, Kuv ve antlaşma yaptığım halkım Kılıçtan geçirilecek.
6 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: “‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu. Adzaphedwa ndi lupanga kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’” ndikutero Ine Ambuye Yehova.
“‘RAB şöyle diyor: Mısır'ı destekleyenler öldürülecek, Mısır'ın övündüğü ordu çökecek, Migdol'dan Asvan'a dek kılıçtan geçirilecekler. Böyle diyor Egemen RAB.
7 “‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja kupambana mabwinja ena onse opasuka, ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka kupambana mizinda ina yonse.
Kimsesiz kalmış ülkeler arasında Kimsesiz kalacaklar. Kentleri viran olmuş kentler gibi olacak.
8 Nditatha kutentha Igupto ndi kupha onse omuthandiza, pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Mısır'ı ateşe verdiğimde, Onu destekleyenler ezildiğinde, Benim RAB olduğumu anlayacaklar.
9 “‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.
“‘O gün kaygısız Kûşlular'ı korkutmak için gemilerle ulaklar göndereceğim. Mısır'ın yıkım günü geldiğinde korkuya kapılacaklar. İşte o gün geliyor.
10 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.
“‘Egemen RAB şöyle diyor: Babil Kralı Nebukadnessar aracılığıyla Mısır'ın zenginliğine son vereceğim.
11 Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja adzabwera kudzawononga dzikolo. Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.
O ve ordusu, ulusların en acımasızı, Ülkeyi yerle bir etmek için gelecekler. Mısır'a karşı kılıçlarını çekecek, Ülkeyi öldürülenlerle dolduracaklar.
12 Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa. Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo. Ine Yehova ndayankhula.
Nil'in kanallarını kurutup Ülkeyi kötü kişilere teslim edeceğim, Ülkeyi de içindeki her şeyi de Yabancılar eliyle viran edeceğim. Bunu ben RAB söylüyorum.
13 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzawononga mafano ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi. Simudzakhalanso mfumu mu Igupto, ndipo ndidzaopseza dziko lonse.
Egemen RAB şöyle diyor: Putları yok edecek, Nof'taki değersiz putlara son vereceğim. Mısır'da artık önder olmayacak, Ülkeye korku salacağım.
14 Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi, ndi kutentha mzinda wa Zowani. Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.
Patros'u viraneye çevirecek, Soan'ı ateşe verecek, No Kenti'ni cezalandıracağım.
15 Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu, linga lolimba la Igupto, ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.
Öfkemi Mısır'ın kalesi Sin üzerine boşaltacak, Kalabalık No halkına son vereceğim.
16 Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto; Peluziumu adzazunzika ndi ululu. Malinga a Thebesi adzagumuka, ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.
Mısır'ı ateşe vereceğim, Sin acıdan kıvranacak, No Kenti'nin surları yarılacak, Nof sürekli tedirgin olacak.
17 Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti adzaphedwa ndi lupanga ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.
On Kenti ve Pi-Beset gençleri Kılıçtan geçirilecek, Oradaki halk sürgüne gönderilecek.
18 Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima pamene ndidzathyola goli la Igupto; motero kunyada kwake kudzatha. Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda, ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.
Tahpanhes'te Mısır'ın boyunduruğunu kırdığım zaman, Orada gündüz geceye dönecek, Övündüğü orduya son verilecek, Kent bulutlarla kaplanacak, Köylerindeki halk sürgüne gönderilecek.
19 Kotero ndidzalanga dziko la Igupto, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
Mısır'ı böyle cezalandırdığımda Benim RAB olduğumu anlayacaklar.’”
20 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti:
Sürgünlüğümüzün on birinci yılı, birinci ayın yedinci günü RAB bana şöyle seslendi:
21 “Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga.
“İnsanoğlu, firavunun kolunu kırdım. İyileşmesin, kılıç tutacak kadar güçlenmesin diye kimse onu bağlamadı, sargı beziyle sarmadı.
22 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake.
Bu yüzden Egemen RAB şöyle diyor: Firavuna karşıyım. Her iki kolunu, sağlam olanı da kırık olanı da kıracağım. Kılıcı elinden düşüreceğim.
23 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri.
Mısırlılar'ı uluslar arasına gönderecek, ülkelere dağıtacağım.
24 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo.
Babil Kralı'nın kollarını güçlendirip kılıcımı onun eline vereceğim. Firavunun ise kollarını kıracağım. Babil Kralı'nın önünde ağır yaralı biri gibi inleyecek.
25 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto.
Babil Kralı'nın gücüne güç katacak, firavunun gücünü zayıflatacağım. Kılıcımı Babil Kralı'nın eline verdiğimde ve o kılıcı Mısır'a doğru uzattığında, benim RAB olduğumu anlayacaklar.
26 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
Mısırlılar'ı uluslar arasına gönderecek, ülkelere dağıtacağım. O zaman benim RAB olduğumu anlayacaklar.”

< Ezekieli 30 >