< Ezekieli 30 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
Кувынтул Домнулуй мь-а ворбит астфел:
2 “Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena. “‘Ufuwule mawu awa akuti, ‘Kalanga, tsiku lafika!’
„Фиул омулуй, пророчеште ши спуне: ‘Аша ворбеште Домнул Думнезеу: «Вэитаци-вэ!… Ненорочитэ зи!
3 Pakuti tsiku layandikira, tsiku la Yehova lili pafupi, tsiku la mitambo yakuda, tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.
Кэч се апропие зиуа, се апропие зиуа Домнулуй, зи ынтунекоасэ – ачаста ва фи время нямурилор.
4 Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto ndipo mavuto adzafika pa Kusi. Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto, chuma chake chidzatengedwa ndipo maziko ake adzagumuka.
Сабия ва пэтрунде ын Еӂипт ши ын Етиопия ва фи гроазэ кынд вор кэдя морций ын Еӂипт, кынд и се вор ридика богэцииле ши и се вор рэстурна темелииле.
5 Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.
Етиопия, Пут, Луд, тоатэ Арабия, Куб ши фиий цэрий уните ку еле вор кэдя ымпреунэ ку ей ловиць де сабие.»
6 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: “‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu. Adzaphedwa ndi lupanga kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’” ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Аша ворбеште Домнул: «Сприжиниторий Еӂиптулуй вор кэдя ши мындрия тэрией луй се ва прэбуши! Дин Мигдол пынэ ла Сиене вор кэдя ловиць де сабие», зиче Домнул Думнезеу.
7 “‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja kupambana mabwinja ena onse opasuka, ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka kupambana mizinda ina yonse.
«Вор фи пустииць ынтре алте цэрь пустиите ши четэциле луй вор фи нимичите ын мижлокул алтор четэць нимичите.
8 Nditatha kutentha Igupto ndi kupha onse omuthandiza, pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Ши вор шти кэ Еу сунт Домнул кынд вой пуне фок ын Еӂипт ши кынд тоць сприжиниторий луй вор фи здробиць.
9 “‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.
Ын зиуа ачея, ниште соль се вор дуче дин партя мя ку корэбииле сэ тулбуре Етиопия ын лиништя ей ши-й ва апука спаймэ маре ын зиуа Еӂиптулуй, кэч ятэ кэ лукруриле ачестя се ынтымплэ!»
10 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.
Аша ворбеште Домнул Думнезеу: «Вой перде мулцимя Еӂиптулуй прин мына луй Небукаднецар, ымпэратул Бабилонулуй.
11 Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja adzabwera kudzawononga dzikolo. Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.
Ел ши попорул луй ку ел, чел май грозав динтре попоаре, вор фи тримишь сэ нимичяскэ цара. Вор скоате сабия ымпотрива Еӂиптулуй ши вор умпле цара де морць.
12 Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa. Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo. Ine Yehova ndayankhula.
Каналеле ле вой сека, вой да цара ын мыниле челор рэй; вой пустии цара ку тот че купринде еа прин мына стрэинилор. Еу, Домнул, ам ворбит!»
13 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzawononga mafano ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi. Simudzakhalanso mfumu mu Igupto, ndipo ndidzaopseza dziko lonse.
Аша ворбеште Домнул Думнезеу: «Вой нимичи идолий ши вой стырпи дин Ноф кипуриле дешарте. Ну ва май фи ничун воевод дин цара Еӂиптулуй ши вой рэспынди гроаза ын цара Еӂиптулуй.
14 Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi, ndi kutentha mzinda wa Zowani. Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.
Вой пустии Патросул, вой пуне фок Цоанулуй ши-Мь вой адуче ла ындеплинире жудекэциле асупра Ноулуй.
15 Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu, linga lolimba la Igupto, ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.
Ымь вой вэрса урӂия асупра Синулуй, четэцуя Еӂиптулуй, ши вой нимичи ку десэвыршире мулцимя дин Но.
16 Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto; Peluziumu adzazunzika ndi ululu. Malinga a Thebesi adzagumuka, ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.
Вой пуне фок Еӂиптулуй; Синул ва фи купринс де спаймэ; Ноул ва фи дескис прин спэртурэ ши Нофул, кучерит зиуа-н амяза маре де врэжмашь.
17 Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti adzaphedwa ndi lupanga ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.
Тинерий дин Он ши дин Пи-Бесет вор кэдя учишь де сабие ши четэциле ачестя се вор дуче ын робие.
18 Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima pamene ndidzathyola goli la Igupto; motero kunyada kwake kudzatha. Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda, ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.
Ла Тахпанес се ва ынтунека зиуа кынд вой сфэрыма жугул Еӂиптулуй ши кынд се ва сфырши мындрия тэрией луй; ун нор ва акопери Тахпанесул ши четэциле луй вор мерӂе ын робие.
19 Kotero ndidzalanga dziko la Igupto, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
Ымь вой адуче астфел ла ындеплинире жудекэциле асупра Еӂиптулуй ши вор шти кэ Еу сунт Домнул.»’”
20 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti:
Ын анул ал унспрезечеля, ын зиуа а шаптя а луний ынтый, кувынтул Домнулуй мь-а ворбит астфел:
21 “Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga.
„Фиул омулуй, ам фрынт брацул луй Фараон, ымпэратул Еӂиптулуй, ши ятэ кэ ну-й вор лега рана ка сэ се виндече, ну-л вор обложи ку легэтурь, ну-л вор лега ка сэ се ынтремезе ши сэ поатэ мынуи сабия.
22 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake.
Де ачея аша ворбеште Домнул Думнезеу: ‘Ятэ, ам неказ пе Фараон, ымпэратул Еӂиптулуй, ши-й вой рупе брацеле, пе чел таре ши пе чел фрынт, ка сэ-й кадэ сабия дин мынэ.
23 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri.
Яр пе еӂиптень ый вой ымпрэштия принтре нямурь ши-й вой рисипи ын фелурите цэрь.
24 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo.
Ын скимб, вой ынтэри брацеле ымпэратулуй Бабилонулуй ши-й вой пуне о сабие ын мынэ, яр брацеле луй Фараон ле вой фрынӂе, ка сэ ӂямэ ынаинтя луй кум ӂем чей рэниць де моарте.
25 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto.
Дар вой ынтэри брацеле ымпэратулуй Бабилонулуй, яр брацеле луй Фараон вор кэдя. Ши вор шти кэ Еу сунт Домнул кынд вой пуне сабия Мя ын мына ымпэратулуй Бабилонулуй ши кынд о ва ынтоарче ымпотрива цэрий Еӂиптулуй.
26 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
Вой ымпрэштия пе еӂиптень принтре нямурь, ый вой рисипи ын фелурите цэрь ши вор шти кэ Еу сунт Домнул.’”

< Ezekieli 30 >