< Ezekieli 30 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
Et la parole du Seigneur me fut adressée, disant:
2 “Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena. “‘Ufuwule mawu awa akuti, ‘Kalanga, tsiku lafika!’
Fils d’un homme, prophétise, et dis: Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Hurlez, malheur, malheur au jour;
3 Pakuti tsiku layandikira, tsiku la Yehova lili pafupi, tsiku la mitambo yakuda, tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.
Car le jour est près, et il approche, le jour du Seigneur, jour de nuage; ce sera le temps des nations.
4 Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto ndipo mavuto adzafika pa Kusi. Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto, chuma chake chidzatengedwa ndipo maziko ake adzagumuka.
Et viendra un glaive sur l’Egypte; et la frayeur sera dans l’Ethiopie, lorsque tomberont les blessés en Egypte; quand sa multitude sera enlevée, et que ses fondements seront détruits.
5 Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.
L’Ethiopie, et la Libye, et la Lydie, et tout le reste des peuples, et Chub, et les fils de la terre de l’alliance avec eux, sous le glaive tomberont.
6 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: “‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu. Adzaphedwa ndi lupanga kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’” ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Et ils tomberont, ceux qui soutenaient l’Egypte, et l’orgueil de son empire sera détruit; depuis la tour de Syène, ils tomberont par l’épée, dit le Seigneur Dieu des armées;
7 “‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja kupambana mabwinja ena onse opasuka, ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka kupambana mizinda ina yonse.
Et ils seront dispersés au milieu des terres désolées, et ses villes seront entre les cités désertes.
8 Nditatha kutentha Igupto ndi kupha onse omuthandiza, pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Et ils sauront que je suis le Seigneur, lorsque j’aurai mis le feu dans l’Egypte et qu’auront été brisés tous ses auxiliaires.
9 “‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.
En ce jour-là, sortiront de devant ma face des messagers sur des trirèmes, pour détruire la confiance de l’Ethiopie; et la frayeur sera sur eux au jour de l’Egypte, parce que sans aucun doute ce jour viendra.
10 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.
Voici ce que dit le Seigneur Dieu: J’anéantirai la multitude de l’Egypte par la main de Nabuchodonosor, roi de Babylone.
11 Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja adzabwera kudzawononga dzikolo. Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.
Lui et son peuple avec lui, les plus puissants des nations seront amenés pour détruire le pays; ils tireront leurs glaives contre l’Egypte, et ils rempliront la terre de tués.
12 Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa. Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo. Ine Yehova ndayankhula.
Et je mettrai à sec les lits des fleuves, et je livrerai le pays entre les mains des plus méchants; je détruirai le pays et sa plénitude, par la main des étrangers; c’est moi le Seigneur, qui ai parlé.
13 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzawononga mafano ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi. Simudzakhalanso mfumu mu Igupto, ndipo ndidzaopseza dziko lonse.
Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Et j’exterminerai les simulacres, et j’anéantirai les idoles de Memphis; il n’y aura plus de prince du pays d’Egypte; et je porterai la terreur dans la terre d’Egypte.
14 Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi, ndi kutentha mzinda wa Zowani. Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.
Je perdrai entièrement la terre de Phathurès, et je mettrai le feu dans Taphnis, et j’exercerai des jugements dans Alexandrie.
15 Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu, linga lolimba la Igupto, ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.
Et je répandrai mon indignation sur Péluse, la force de l’Egypte; je perdrai la multitude d’Alexandrie,
16 Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto; Peluziumu adzazunzika ndi ululu. Malinga a Thebesi adzagumuka, ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.
Et je mettrai le feu dans l’Egypte; comme une femme en travail, Péluse sera dans les douleurs; Alexandrie sera ravagée et dans Memphis seront des angoisses continuelles.
17 Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti adzaphedwa ndi lupanga ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.
Les jeunes hommes d’Héliopolis et de Bubaste tomberont sous le glaive, et les femmes elles-mêmes seront emmenées captives.
18 Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima pamene ndidzathyola goli la Igupto; motero kunyada kwake kudzatha. Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda, ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.
Et à Taphnis s’obscurcira le jour, lorsque j’y briserai les sceptres de l’Egypte, et que l’orgueil de sa puissance s’y évanouira: un nuage la couvrira elle-même, mais ses filles seront emmenées en captivité.
19 Kotero ndidzalanga dziko la Igupto, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
Et j’exercerai des jugements en Egypte; et ils sauront que je suis le Seigneur.
20 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti:
Et il arriva en la onzième année, au premier mois, au septième jour du mois, que la parole du Seigneur me fut adressée, disant:
21 “Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga.
Fils d’un homme, j’ai brisé le bras de Pharaon, roi d’Egypte; et voilà qu’il n’a pas été enveloppé, de manière que la guérison lui fût rendue; qu’il fût lié avec des compresses, et qu’il fût entouré de linges, afin qu’ayant repris sa force, il pût tenir un glaive.
22 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake.
C’est pourquoi voici ce que dit le Seigneur Dieu: Voilà que moi je viens vers Pharaon, roi d’Egypte; et je mettrai en pièces son bras fort, mais brisé; et je ferai tomber le glaive de sa main;
23 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri.
Et je disperserai les Egyptiens parmi les nations, et je les jetterai au vent dans les divers pays.
24 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo.
Et je fortifierai le bras du roi de Babylone, et je mettrai mon glaive dans sa main, et je briserai les bras de Pharaon, et les siens pousseront de grands gémissements, étant tués devant sa face.
25 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto.
Et je fortifierai les bras du roi de Babylone, et les bras de Pharaon tomberont; et ils sauront que je suis le Seigneur, lorsque j’aurai mis mon glaive dans la main du roi de Babylone, et qu’il l’aura étendu sur la terre d’Egypte.
26 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
Et je disperserai les Egyptiens parmi les nations, je les jetterai au vent dans les divers pays; et ils sauront que je suis le Seigneur.

< Ezekieli 30 >