< Ezekieli 30 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
La parole de l’Eternel me fut adressée en ces termes:
2 “Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena. “‘Ufuwule mawu awa akuti, ‘Kalanga, tsiku lafika!’
"Fils de l’homme, prophétise et dis: Ainsi parle le Seigneur Dieu: Lamentez-vous! Hélas, quel jour!
3 Pakuti tsiku layandikira, tsiku la Yehova lili pafupi, tsiku la mitambo yakuda, tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.
Car un jour est proche, oui, un jour est proche, fixé par l’Eternel, un jour de nuée: ce sera l’heure des nations.
4 Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto ndipo mavuto adzafika pa Kusi. Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto, chuma chake chidzatengedwa ndipo maziko ake adzagumuka.
Le glaive s’abattra sur l’Egypte; il y aura de l’épouvante en Ethiopie, quand tomberont les victimes en Egypte. On prendra ses richesses, ses fondements seront renversés.
5 Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.
L’Ethiopie, Pout et Loud, tout l’Occident, et Koub avec les fils du pays de l’Alliance tomberont sous le glaive.
6 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: “‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu. Adzaphedwa ndi lupanga kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’” ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Ainsi parle l’Eternel: "Les appuis de l’Egypte s’écrouleront, et sa fière puissance sera abaissée. De Migdol à Syène, ils y tomberont sous le glaive, dit le Seigneur Dieu.
7 “‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja kupambana mabwinja ena onse opasuka, ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka kupambana mizinda ina yonse.
Ils seront dévastés entre les pays dévastés, et ses villes seront au nombre des villes ruinées.
8 Nditatha kutentha Igupto ndi kupha onse omuthandiza, pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Et ils sauront que je suis l’Eternel, lorsque je mettrai le feu à l’Egypte et que tous ses auxiliaires seront brisés.
9 “‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.
Ce jour-là, des messagers partiront au-devant de moi dans des navires, pour troubler l’Ethiopie dans sa quiétude, et il y aura une terreur parmi eux au jour de l’Egypte, car le voici venir!"
10 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.
Ainsi parle le Seigneur Dieu: "J’Abolirai la richesse de l’Egypte par la main de Nabuchodonosor, roi de Babylone.
11 Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja adzabwera kudzawononga dzikolo. Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.
Lui et son peuple avec lui, les plus violents des peuples, seront amenés pour détruire le pays; ils tireront leurs glaives contre l’Egypte et rempliront le pays de cadavres.
12 Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa. Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo. Ine Yehova ndayankhula.
Je mettrai les cours d’eau à sec et je livrerai le pays à la merci de barbares; je dévasterai le pays avec ce qu’il renferme par la main d’étrangers, c’est moi, l’Eternel, qui le dis."
13 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzawononga mafano ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi. Simudzakhalanso mfumu mu Igupto, ndipo ndidzaopseza dziko lonse.
Ainsi parle le Seigneur Dieu: "J’Anéantirai les idoles, je ferai disparaître les faux dieux de Nof et le prince du pays d’Egypte: il n’y en aura plus. Je répandrai la terreur dans le pays d’Egypte.
14 Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi, ndi kutentha mzinda wa Zowani. Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.
Je ruinerai Pathros, je mettrai le feu à Çoân et j’infligerai des châtiments à Nô.
15 Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu, linga lolimba la Igupto, ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.
Je déverserai ma colère sur Sîn, forteresse de l’Egypte, et j’extirperai le peuple de Nô.
16 Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto; Peluziumu adzazunzika ndi ululu. Malinga a Thebesi adzagumuka, ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.
Je mettrai le feu à l’Egypte, Sin sera saisie de tremblement, Nô est pour être prise d’assaut, Nof sera livrée aux ennemis en plein jour.
17 Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti adzaphedwa ndi lupanga ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.
Les jeunes gens d’Avên et de Pibécet tomberont sous le glaive, et elles-mêmes Won; en captivité.
18 Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima pamene ndidzathyola goli la Igupto; motero kunyada kwake kudzatha. Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda, ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.
Et dans Tehafnehès, le jour sera ténébreux, quand j’y briserai les appuis de l’Egypte et que sera aboli en elle l’orgueil de sa puissance, une nuée la couvrira et ses filles iront en captivité.
19 Kotero ndidzalanga dziko la Igupto, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
Et j’exercerai des sévices sur l’Egypte, et ils sauront que c’est moi l’Eternel."
20 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti:
II advint, la onzième année, le sept du premier mois, que la parole de l’Eternel me fut adressée en ces termes:
21 “Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga.
"Fils de l’homme, j’ai brisé le bras de Pharaon, roi d’Egypte; or, on ne l’a point pansé en y appliquant des médicaments, en y posant un bandage comme pansement, afin qu’il reprenne des forces pour tenir une épée.
22 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake.
C’Est pourquoi, ainsi parle l’Eternel Dieu, je m’en prends à Pharaon, roi d’Egypte; je briserai ses bras, et celui qui est valide et celui qui est fracturé, et je lui ferai tomber l’épée de la main.
23 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri.
Je disperserai les Egyptiens parmi les peuples, je les disséminerai dans les pays.
24 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo.
Mais j’affermirai les bras du roi de Babylone et je mettrai mon épée dans sa main, tandis que je briserai les bras de Pharaon, de telle sorte qu’il râlera devant lui du râle de l’homme frappé à mort.
25 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto.
Oui, je fortifierai les bras du roi de Babylone alors que les bras de Pharaon tomberont, et on saura que c’est moi l’Eternel, quand je mettrai mon glaive dans la main du roi de Babylone, et qu’il le brandira contre le pays d’Egypte.
26 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
Et je disperserai les Egyptiens parmi les nations, je les disséminerai dans les pays, et ils sauront que je suis l’Eternel."

< Ezekieli 30 >