< Ezekieli 30 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
And there is a word of YHWH to me, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena. “‘Ufuwule mawu awa akuti, ‘Kalanga, tsiku lafika!’
“Son of man, prophesy, and you have said, Thus said Lord YHWH: Howl, Aah! For the day!
3 Pakuti tsiku layandikira, tsiku la Yehova lili pafupi, tsiku la mitambo yakuda, tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.
For a day [is] near, a day [is] near to YHWH! It is a time of cloud [over] the nations.
4 Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto ndipo mavuto adzafika pa Kusi. Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto, chuma chake chidzatengedwa ndipo maziko ake adzagumuka.
And a sword has come into Egypt, And there has been great pain in Cush, In the falling of the wounded in Egypt, And they have taken its store, And its foundations have been broken down.
5 Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.
Cush, and Phut, and Lud, and all the mixture, and Chub, And the sons of the land of the covenant fall by sword with them,
6 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: “‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu. Adzaphedwa ndi lupanga kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’” ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Thus said YHWH: And those supporting Egypt have fallen, And the arrogance of her strength has come down, From Migdol to Syene, they fall by sword in her, A declaration of Lord YHWH.
7 “‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja kupambana mabwinja ena onse opasuka, ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka kupambana mizinda ina yonse.
And they have been desolated in the midst of desolate lands, And its cities are in the midst of cities [that are] laid waste.
8 Nditatha kutentha Igupto ndi kupha onse omuthandiza, pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
And they have known that I [am] YHWH, In My giving fire against Egypt, And all her helpers have been broken.
9 “‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.
In that day messengers go forth from before Me in ships, To trouble confident Cush, And there has been great pain among them, As the day of Egypt, for behold, it has come.
10 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.
Thus said Lord YHWH: I have caused the multitude of Egypt to cease, By the hand of Nebuchadnezzar king of Babylon,
11 Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja adzabwera kudzawononga dzikolo. Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.
He and his people with him—the terrible of nations, Are brought in to destroy the land, And they have drawn their swords against Egypt, And have filled the land [with] the wounded.
12 Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa. Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo. Ine Yehova ndayankhula.
And I have made floods a dry place, And I have sold the land into the hand of evildoers, And I have made the land desolate, And its fullness, by the hand of strangers, I, YHWH, have spoken.
13 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzawononga mafano ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi. Simudzakhalanso mfumu mu Igupto, ndipo ndidzaopseza dziko lonse.
Thus said Lord YHWH: And I have destroyed idols, And caused vain things to cease from Noph, And there is no longer a prince of the land of Egypt, And I give fear in the land of Egypt.
14 Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi, ndi kutentha mzinda wa Zowani. Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.
And I have made Pathros desolate, And I have given fire against Zoan, And I have done judgments in No,
15 Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu, linga lolimba la Igupto, ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.
And I have poured out My fury on Sin, the stronghold of Egypt, And I have cut off the multitude of No.
16 Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto; Peluziumu adzazunzika ndi ululu. Malinga a Thebesi adzagumuka, ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.
And I have given fire against Egypt, Sin is greatly pained, and No is to be broken, And Noph has daily distresses.
17 Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti adzaphedwa ndi lupanga ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.
The youths of Aven and Pi-Beseth fall by sword, And these go into captivity.
18 Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima pamene ndidzathyola goli la Igupto; motero kunyada kwake kudzatha. Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda, ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.
And the day has been dark in Tehaphnehes, In My breaking the yokes of Egypt there, And the excellence of her strength has ceased in her, Her! A cloud covers her, And her daughters go into captivity.
19 Kotero ndidzalanga dziko la Igupto, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
And I have done judgments in Egypt, And they have known that I [am] YHWH.”
20 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti:
And it comes to pass, in the eleventh year, in the first [month], on the seventh of the month, a word of YHWH has been to me, saying, “Son of man,
21 “Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga.
I have broken the arm of Pharaoh, king of Egypt, And behold, it has not been bound up to give healing, To put a bandage to bind it, To strengthen it—to lay hold on the sword.
22 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake.
Therefore, thus said Lord YHWH: Behold, I [am] against Pharaoh, king of Egypt, And I have broken his arms, The strong one and the broken one, And have caused the sword to fall out of his hand,
23 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri.
And I have scattered the Egyptians among nations, And have spread them through lands,
24 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo.
And I have strengthened the arms of the king of Babylon, And have given My sword into his hand, And I have broken the arms of Pharaoh, And he has groaned the groans of a pierced one—before him.
25 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto.
And I have strengthened the arms of the king of Babylon, And the arms of Pharaoh fall down, And they have known that I [am] YHWH, In My giving My sword into the hand of the king of Babylon, And he has stretched it out toward the land of Egypt.
26 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
And I have scattered the Egyptians among nations, And I have spread them through lands, And they have known that I [am] YHWH!”

< Ezekieli 30 >