< Ezekieli 30 >
1 Yehova anandiyankhula kuti:
And the word of the Lord came unto me, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena. “‘Ufuwule mawu awa akuti, ‘Kalanga, tsiku lafika!’
Son of man, prophesy and say, Thus hath said the Lord Eternal, Wail ye, Woe unto the day!
3 Pakuti tsiku layandikira, tsiku la Yehova lili pafupi, tsiku la mitambo yakuda, tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.
For nigh is the day, yea nigh is the day of the Lord; a cloudy day; the time of the nations' [misfortune] shall it be.
4 Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto ndipo mavuto adzafika pa Kusi. Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto, chuma chake chidzatengedwa ndipo maziko ake adzagumuka.
And the sword shall come into Egypt, and there shall be trembling in Ethiopia, when the slain fall in Egypt, and when they take away its multitude, and its foundations shall be broken down.
5 Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.
Ethiopia, and Put, and Lud, and all the confederates, and Cub, and all the men of the leagued land, shall fall with them by the sword.
6 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: “‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu. Adzaphedwa ndi lupanga kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’” ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Thus hath said the Lord, Yea, there shall fall those that uphold Egypt; and there shall come down the pride of her strength: from Migdol to Seveneh shall they fall in her by the sword, saith the Lord Eternal.
7 “‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja kupambana mabwinja ena onse opasuka, ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka kupambana mizinda ina yonse.
And they shall be made desolate in the midst of the desolate countries, and its cities shall be counted in the midst of the cities that have been laid in ruins.
8 Nditatha kutentha Igupto ndi kupha onse omuthandiza, pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
And they shall know that I am the Lord, when I set fire to Egypt, and when all her helpers shall be broken.
9 “‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.
On that day shall messengers go forth from my presence in ships to terrify the secure Ethiopians, and there shall be trembling among them, as on the day of Egypt; for, lo, it cometh.
10 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.
Thus hath said the Lord Eternal, I will also cause the multitude of Egypt to cease through the hand of Nebuchadrezzar the king of Babylon.
11 Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja adzabwera kudzawononga dzikolo. Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.
He and his people with him, the fiercest of nations, shall be brought to destroy the land; and they shall draw their swords against Egypt, and they shall fill the land with the slain.
12 Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa. Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo. Ine Yehova ndayankhula.
And I will render the streams dry, and sell the land into the hand of evil men; and I will make the land desolate, and all that filleth it, by the hand of strangers: I the Lord have spoken it.
13 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzawononga mafano ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi. Simudzakhalanso mfumu mu Igupto, ndipo ndidzaopseza dziko lonse.
Thus hath said the Lord Eternal, I will also destroy the idols, and I will cause false gods to cease out of Noph; and a prince out of the land of Egypt shall there not be any more: and I will lay fear on the land of Egypt.
14 Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi, ndi kutentha mzinda wa Zowani. Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.
And I will make Pathros desolate, and set fire to Zo'an; and I will execute judgments in No.
15 Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu, linga lolimba la Igupto, ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.
And I will pour my fury over Sin, the stronghold of Egypt; and I will cut off the multitude of No.
16 Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto; Peluziumu adzazunzika ndi ululu. Malinga a Thebesi adzagumuka, ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.
And I will set fire to Egypt: Sin shall have great pain, and No shall be broken in, and [over] Noph shall the besiegers [prevail] by broad day.
17 Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti adzaphedwa ndi lupanga ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.
The young men of Aven and of Pi-besseth shall fall by the sword; and they themselves shall go into captivity.
18 Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima pamene ndidzathyola goli la Igupto; motero kunyada kwake kudzatha. Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda, ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.
And at Thechaphneches the day shall be darkened, when I break there the yoke-bars of Egypt, and the pride of her strength ceaseth therein: as for her, a cloud shall cover her, and her daughters shall go into captivity.
19 Kotero ndidzalanga dziko la Igupto, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
Thus will I execute judgments on Egypt: and they shall know that I am the Lord.
20 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti:
And it came to pass in the eleventh year, in the first month, on the seventh day of the month, that the word of the Lord came unto me, saying,
21 “Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga.
Son of man, the arm of Pharaoh the king of Egypt have I broken; and lo, it shall not be bound up to apply remedies, to put on a bandage to bind it up, to make it strong that it may grasp the sword.
22 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake.
Therefore thus hath said the Lord Eternal, Behold, I will be against Pharaoh the king of Egypt, and will break his arms, both the strong, and that which was already broken; and I will cause the sword to fall out of his hand.
23 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri.
And I will scatter the Egyptians among the nations, and I will disperse them through the countries.
24 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo.
And I will strengthen the arms of the king of Babylon, and will put my sword in his hand; but I will break the arms of Pharaoh, and he shall groan, with the groanings of a deadly wounded man before him.
25 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto.
Yea I will make strong the arms of the king of Babylon, but the arms of Pharaoh shall fall down: and they shall know that I am the Lord, when I place my sword into the hand of the king of Babylon, that he may stretch it out over the land of Egypt.
26 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
And I will scatter the Egyptians among the nations, and disperse them among the countries: and they shall know that I am the Lord.