< Ezekieli 3 >

1 Tsono Mulungu anandiwuza kuti, “Mwana wa munthu, idya chimene ndikukupatsachi. Idya kenaka upite ukayankhule ndi Aisraeli.”
I powiedział do mnie: Synu człowieczy, zjedz to, co jest przed tobą; zjedz ten zwój i idź, przemawiaj do domu Izraela.
2 Choncho ndinayasama ndipo anandipatsa mpukutuwo kuti ndidye.
Otworzyłem więc swe usta i dał mi zjeść ten zwój.
3 Kenaka Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, idya mpukutu umene ndikukupatsa kuti ukhute.” Choncho ndinadya, ndipo unkatsekemera ngati uchi mʼkamwa mwanga.
I powiedział mi: Synu człowieczy, nakarm swój brzuch i napełnij swoje wnętrzności tym zwojem, który ci daję. Zjadłem [go], a był w moich ustach słodki jak miód.
4 Pamenepo Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, pita tsopano kwa Aisraeli ndipo ukawawuze mawu anga.
Potem powiedział do mnie: Synu człowieczy, idź, udaj się do domu Izraela i mów do niego moimi słowami.
5 Sindikukutuma kwa anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, koma kwa Aisraeli.
Bo nie posyłam cię do ludu o niezrozumiałej mowie lub trudnym języku, [ale] do domu Izraela;
6 Sindikukutuma kwa mitundu yambiri ya anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, amene mawu ake sungawamvetse. Ndithu ndikanakutuma kwa iwowa, bwenzi iwo atakumvera.
Nie do wielu narodów o niezrozumiałej mowie i trudnym języku, których słów byś nie zrozumiał, chociaż gdybym cię do nich posłał, usłuchałyby cię.
7 Koma Aisraeli sadzakumvera chifukwa iwo sakufuna kumvera Ine. Paja Aisraeli onse ndi okanika ndiponso a mtima wowuma.
Lecz dom Izraela nie będzie chciał cię słuchać, ponieważ mnie [samego] nie chce usłuchać. Cały dom Izraela ma bowiem twarde czoło i zatwardziałe serce.
8 Tsono ine ndakhwimitsa nkhope yako mofanana ndi nkhope zawo. Ndalimbitsanso mutu wako mofanana ndi mitu yawo.
Oto uczyniłem twoją twarz twardą przeciwko ich twarzom, a twoje czoło twarde przeciwko ich czołom.
9 Ine ndidzakusandutsa wolimba ngati mwala wa dayimondi umene uposa thanthwe lina lililonse kulimba kwake. Usachite nawo mantha kapena kuopsedwa nawo. Paja anthuwa ndi awupandu.”
Uczyniłem twe czoło jak diament, twardszym od krzemienia. Nie bój się ich ani nie lękaj się ich twarzy, gdyż są domem buntowniczym.
10 Anatinso, “Iwe mwana wa munthu, umvetsetse bwino zimene ndikukuwuzazi ndipo mawu angawa uwasunge bwino mu mtima mwako.
I powiedział do mnie: Synu człowieczy, weź sobie do serca wszystkie moje słowa, które będę do ciebie mówić, i słuchaj ich uszami.
11 Tsopano upite kwa Aisraeli anzako amene ali ku ukapolo ndipo ukayankhule nawo. ‘Kaya akamvera kaya sakamvera,’ koma uzikawawuza kuti, Ambuye Wamphamvuzonse akuti zakutizakuti.”
Idź, udaj się do pojmanych, do synów twego ludu, i powiedz im: Tak mówi Pan BÓG – czy będą słuchać, czy nie.
12 Pamenepo Mzimu unandinyamula ndipo kumbuyo kwanga ndinamva liwu lamphamvu ngati chivomerezi chachikulu, lonena kuti, “Utamandike ulemerero wa Yehova kumene Iye amakhala!”
Wtedy duch uniósł mnie i usłyszałem za sobą huk wielkiego grzmotu: [Niech będzie] błogosławiona chwała PANA ze swego miejsca.
13 Phokoso ndinkalimvalo linali la kugundana kwa mapiko a zamoyo ndiponso phokoso la mikombero ya pambali pake ija, limene linkamveka ngati chivomerezi chachikulu.
[Usłyszałem też] szum skrzydeł tych istot żywych, które się dotykały nawzajem, głos kół naprzeciwko nich i głos wielkiego grzmotu.
14 Mzimu wa Yehova unandikweza ndi kundinyamula ndipo ndinachokapo ndili wowawidwa ndi wonyuka mu mtima. Ndipo dzanja la Yehova linali pa ine mwa mphamvu.
A duch uniósł mnie i zabrał. I poszedłem w goryczy i w gniewie swego ducha, lecz ręka PANA mocno ciążyła nade mną.
15 Choncho ndinafika kwa amene anali mu ukapolo ku Telabibu pafupi ndi mtsinje wa Kebara. Ndinakhala pansi pakati pawo masiku asanu ndi awiri, ndili wothedwa nzeru kwambiri.
I przyszedłem do pojmanych w Tel-Abib, którzy mieszkali nad rzeką Kebar, i usiadłem [tam], gdzie oni mieszkali, pozostałem tam osłupiały wśród nich przez siedem dni.
16 Atatha masiku asanu ndi awiriwo, Yehova anandiwuza kuti,
A gdy minęło siedem dni, doszło do mnie słowo PANA mówiące:
17 “Iwe mwana wa munthu, Ine ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Uziti ukamva mawu anga, ndiye uzikawachenjeza.
Synu człowieczy, ustanowiłem cię stróżem domu Izraela. Usłysz więc słowo z moich ust i upominaj go ode mnie.
18 Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe udzafa ndithu,’ koma iwe osamuchenjeza kapena kumuyankhula kuti aleke njira zake zoyipa ndi kuti akhale ndi moyo, munthu woyipayo adzafa mu uchimo wake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
Gdy powiem bezbożnemu: Z pewnością umrzesz, a nie upomnisz go ani nie ostrzeżesz, aby go odwieść od jego bezbożnej drogi, aby uratować jego życie, to ten bezbożny umrze w swojej nieprawości, ale jego krwi zażądam z twojej ręki.
19 Koma ukamuchenjeza munthu woyipa koma iye osatembenuka mtima kuleka zoyipa zake kapena kusiya njira zake zoyipa, munthuyo adzafa chifukwa cha uchimo wake koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
Lecz jeśli ostrzeżesz bezbożnego, a on nie odwróci się od swej bezbożności i od swej bezbożnej drogi, to on umrze w swojej nieprawości, ale ty wybawisz swoją duszę.
20 “Ngati munthu wolungama asiya chilungamo chake ndi kuchita uchimo ndipo Ine nʼkumuyika mʼzoopsa, munthuyo adzafa ndithu. Popeza iwe sunamuchenjeze, adzafadi chifukwa cha tchimo ndipo chilungamo chake sichidzakumbukiridwa, koma ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
Gdy zaś sprawiedliwy odwróci się od swojej sprawiedliwości i popełni nieprawość, a ja ześlę na niego przeszkodę, to on umrze. Ponieważ nie ostrzegłeś go, umrze w swym grzechu i nie będzie się pamiętać o jego sprawiedliwości, którą czynił, lecz jego krwi zażądam z twojej ręki.
21 Koma ngati umuchenjeza munthu wolungama kuti asachimwe ndipo iye nʼkuleka kuchimwa adzakhala ndi moyo ndithu chifukwa anamvera chenjezo, ndipo iwe udzapulumutsa moyo wako.”
Ale jeśli ostrzeżesz sprawiedliwego, aby sprawiedliwy nie zgrzeszył, i on nie zgrzeszy, na pewno będzie żył, bo przyjął ostrzeżenie, a ty ocalisz swoją duszę.
22 Nthawi ina dzanja la Yehova linali pa ine ndipo anandiwuza kuti, “Nyamuka upite ku chigwa, kumeneko ndikayankhula nawe.”
I spoczęła tam nade mną ręka PANA, i powiedział do mnie: Wstań i pójdź na równinę, tam będę z tobą mówił.
23 Choncho ndinanyamuka kupita ku chigwa. Ndipo ndinaona ulemerero wa Yehova kumeneko, ngati ulemerero umene ndinaona mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara ndipo ndinagwa pansi chafufumimba.
Wstałem więc i wyszedłem na równinę, a oto chwała PANA stała tam, taka jak chwała, którą widziałem nad rzeką Kebar, i upadłem na twarz.
24 Koma Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa. Tsono Yehova anandiyankhula nati: “Pita, kadzitsekere mʼnyumba mwako.
Wtedy duch wstąpił we mnie, postawił mnie na nogi i przemówił do mnie: Idź i zamknij się w swym domu.
25 Ndipo iwe mwana wa munthu, adzakumanga ndi zingwe motero kuti sudzatha kuyendanso pakati pa anthu.
Bo oto, synu człowieczy, włożą na ciebie powrozy i zwiążą cię nimi, a nie będziesz mógł wyjść między nich.
26 Ndidzamatirira lilime lako kukhosi, kotero kuti udzakhala chete wosatha kuwadzudzula, chifukwa iwo ndi anthu aupandu.
A ja sprawię, że twój język przylgnie do twego podniebienia i będziesz niemy, i nie będziesz dla nich człowiekiem, który strofuje, gdyż są domem buntowniczym.
27 Koma pamene ndidzayankhula kwa iwe, ndidzatsekula pakamwa pako ndipo udzawawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti zakutizakuti.’ Aliyense wofuna kumva amve ndipo wokana kumva, muleke akane; pakuti iwo ndi anthu opanduka.”
Ale gdy będę z tobą mówić, otworzę ci usta i powiesz do nich: Tak mówi Pan BÓG: Kto [chce] słuchać, niech słucha, a kto nie chce, niech nie słucha – gdyż są domem buntowniczym.

< Ezekieli 3 >