< Ezekieli 3 >

1 Tsono Mulungu anandiwuza kuti, “Mwana wa munthu, idya chimene ndikukupatsachi. Idya kenaka upite ukayankhule ndi Aisraeli.”
Yasisithi kimi: Ndodana yomuntu, dlana lokho ozakuthola; dlana lumqulu, uhambe uyekhuluma kuyo indlu kaIsrayeli.
2 Choncho ndinayasama ndipo anandipatsa mpukutuwo kuti ndidye.
Ngasengivula umlomo wami, yasingidlisa lowomqulu.
3 Kenaka Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, idya mpukutu umene ndikukupatsa kuti ukhute.” Choncho ndinadya, ndipo unkatsekemera ngati uchi mʼkamwa mwanga.
Yasisithi kimi: Ndodana yomuntu, yenza isisu sakho sidle, ugcwalise amathumbu akho ngalumqulu engikunika wona. Ngasengisidla; njalo waba emlonyeni wami njengoluju ngenxa yobumnandi.
4 Pamenepo Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, pita tsopano kwa Aisraeli ndipo ukawawuze mawu anga.
Yasisithi kimi: Ndodana yomuntu, hamba uye endlini yakoIsrayeli, ukhulume ngamazwi ami kubo.
5 Sindikukutuma kwa anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, koma kwa Aisraeli.
Ngoba kawuthunywanga ebantwini abalenkulumo ejulileyo lolimi olunzima, kodwa endlini yakoIsrayeli.
6 Sindikukutuma kwa mitundu yambiri ya anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, amene mawu ake sungawamvetse. Ndithu ndikanakutuma kwa iwowa, bwenzi iwo atakumvera.
Hatshi ebantwini abanengi abalenkulumo ejulileyo lolimi olunzima, abamazwi abo ongeke uwezwe. Isibili, uba bengikuthume kubo, bona bebezakukuzwa.
7 Koma Aisraeli sadzakumvera chifukwa iwo sakufuna kumvera Ine. Paja Aisraeli onse ndi okanika ndiponso a mtima wowuma.
Kodwa indlu kaIsrayeli kayiyikuvuma ukukulalela, ngoba kabavumi ukungilalela; ngoba yonke indlu yakoIsrayeli ilobuso obuqinileyo, njalo balukhuni ngenhliziyo.
8 Tsono ine ndakhwimitsa nkhope yako mofanana ndi nkhope zawo. Ndalimbitsanso mutu wako mofanana ndi mitu yawo.
Khangela, ngenze ubuso bakho baqina bumelene lobuso babo, lebunzi lakho liqine limelene lebunzi labo.
9 Ine ndidzakusandutsa wolimba ngati mwala wa dayimondi umene uposa thanthwe lina lililonse kulimba kwake. Usachite nawo mantha kapena kuopsedwa nawo. Paja anthuwa ndi awupandu.”
Ngenze ibunzi lakho libe njengendayimana elukhuni kulensengetshe. Ungabesabi, ungatshaywa luvalo yibuso babo, lanxa beyindlu evukelayo.
10 Anatinso, “Iwe mwana wa munthu, umvetsetse bwino zimene ndikukuwuzazi ndipo mawu angawa uwasunge bwino mu mtima mwako.
Futhi yathi kimi: Ndodana yomuntu, wonke amazwi ami engizawakhuluma kuwe, emukele enhliziyweni yakho, uzwe ngendlebe zakho.
11 Tsopano upite kwa Aisraeli anzako amene ali ku ukapolo ndipo ukayankhule nawo. ‘Kaya akamvera kaya sakamvera,’ koma uzikawawuza kuti, Ambuye Wamphamvuzonse akuti zakutizakuti.”
Hamba-ke, uye kwabathunjiweyo, ebantwaneni babantu bakho, ukhulume kubo, uthi kubo: Itsho njalo iNkosi uJehova; loba bezakuzwa loba bezayekela.
12 Pamenepo Mzimu unandinyamula ndipo kumbuyo kwanga ndinamva liwu lamphamvu ngati chivomerezi chachikulu, lonena kuti, “Utamandike ulemerero wa Yehova kumene Iye amakhala!”
UMoya wasengiphakamisa; ngasengisizwa emva kwami ilizwi lomdumo omkhulu, lisithi: Kayidunyiswe inkazimulo yeNkosi ivela endaweni yayo.
13 Phokoso ndinkalimvalo linali la kugundana kwa mapiko a zamoyo ndiponso phokoso la mikombero ya pambali pake ija, limene linkamveka ngati chivomerezi chachikulu.
Ngezwa futhi umsindo wempiko zezidalwa eziphilayo, ezazithintana, lomsindo wamavili maqondana lazo, lomsindo womdumo omkhulu.
14 Mzimu wa Yehova unandikweza ndi kundinyamula ndipo ndinachokapo ndili wowawidwa ndi wonyuka mu mtima. Ndipo dzanja la Yehova linali pa ine mwa mphamvu.
UMoya wasengiphakamisa, wangisusa; ngasengihamba ngokubaba ekuvutheni komoya wami; kodwa isandla seNkosi sasilamandla phezu kwami.
15 Choncho ndinafika kwa amene anali mu ukapolo ku Telabibu pafupi ndi mtsinje wa Kebara. Ndinakhala pansi pakati pawo masiku asanu ndi awiri, ndili wothedwa nzeru kwambiri.
Ngasengifika kwabathunjiweyo eTelabibi, ababehlala ngasemfuleni iKebari; ngahlala lapho ababehlala khona, ngahlala khona insuku eziyisikhombisa ngithithibele phakathi kwabo.
16 Atatha masiku asanu ndi awiriwo, Yehova anandiwuza kuti,
Kwasekusithi ekucineni kwensuku eziyisikhombisa, ilizwi leNkosi lafika kimi, lisithi:
17 “Iwe mwana wa munthu, Ine ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Uziti ukamva mawu anga, ndiye uzikawachenjeza.
Ndodana yomuntu, ngikwenzile waba ngumlindi kuyo indlu kaIsrayeli. Ngakho zwana ilizwi elivela emlonyeni wami, ubaxwayise kuvela kimi.
18 Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe udzafa ndithu,’ koma iwe osamuchenjeza kapena kumuyankhula kuti aleke njira zake zoyipa ndi kuti akhale ndi moyo, munthu woyipayo adzafa mu uchimo wake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
Lapho ngisithi kokhohlakeleyo: Uzakufa lokufa; wena-ke ungamxwayisi, loba ungakhulumi ukumxwayisa okhohlakeleyo ukuthi asuke endleleni yakhe ekhohlakeleyo, ukuze agcine impilo yakhe, lowo okhohlakeleyo uzafela ebubini bakhe; kodwa igazi lakhe ngizalibiza esandleni sakho.
19 Koma ukamuchenjeza munthu woyipa koma iye osatembenuka mtima kuleka zoyipa zake kapena kusiya njira zake zoyipa, munthuyo adzafa chifukwa cha uchimo wake koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
Kodwa uba wena umxwayisa okhohlakeleyo, angaphenduki ekukhohlakaleni kwakhe lendleleni yakhe ekhohlakeleyo, yena uzafela ebubini bakhe; kodwa wena ukhulule umphefumulo wakho.
20 “Ngati munthu wolungama asiya chilungamo chake ndi kuchita uchimo ndipo Ine nʼkumuyika mʼzoopsa, munthuyo adzafa ndithu. Popeza iwe sunamuchenjeze, adzafadi chifukwa cha tchimo ndipo chilungamo chake sichidzakumbukiridwa, koma ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
Futhi, uba olungileyo ephenduka ekulungeni kwakhe, enze isiphambeko, njalo ngibeke isikhubekiso phambi kwakhe, yena uzakufa; ngoba wena ungamxwayisanga, uzafela esonweni sakhe, lokulunga kwakhe akwenzileyo kungakhunjulwa; kodwa igazi lakhe ngizalibiza esandleni sakho.
21 Koma ngati umuchenjeza munthu wolungama kuti asachimwe ndipo iye nʼkuleka kuchimwa adzakhala ndi moyo ndithu chifukwa anamvera chenjezo, ndipo iwe udzapulumutsa moyo wako.”
Kodwa uba wena umxwayisa olungileyo, ukuze olungileyo angoni, yena-ke angaze ona, isibili yena uzaphila, ngoba exwayisiwe; futhi wena uwukhulule umphefumulo wakho.
22 Nthawi ina dzanja la Yehova linali pa ine ndipo anandiwuza kuti, “Nyamuka upite ku chigwa, kumeneko ndikayankhula nawe.”
Isandla seNkosi sasesiphezu kwami lapho, yasisithi kimi: Sukuma, uphume uye egcekeni, lalapho ngizakhuluma lawe.
23 Choncho ndinanyamuka kupita ku chigwa. Ndipo ndinaona ulemerero wa Yehova kumeneko, ngati ulemerero umene ndinaona mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara ndipo ndinagwa pansi chafufumimba.
Ngasengisukuma ngaphuma ngaya egcekeni; khangela-ke, inkazimulo yeNkosi yayimi khona, njengenkazimulo engangiyibone ngasemfuleni iKebari; ngasengisithi mbo ngobuso bami.
24 Koma Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa. Tsono Yehova anandiyankhula nati: “Pita, kadzitsekere mʼnyumba mwako.
UMoya wasengena kimi, wangimisa ngenyawo zami, wakhuluma kimi wathi kimi: Hamba uyezivalela phakathi kwendlu yakho.
25 Ndipo iwe mwana wa munthu, adzakumanga ndi zingwe motero kuti sudzatha kuyendanso pakati pa anthu.
Wena-ke, ndodana yomuntu, khangela, bazafaka izibopho phezu kwakho, bakubophe ngazo, ukuze ungaphumi phakathi kwabo.
26 Ndidzamatirira lilime lako kukhosi, kotero kuti udzakhala chete wosatha kuwadzudzula, chifukwa iwo ndi anthu aupandu.
Njalo ngizakwenza ulimi lwakho lunamathele olwangeni lwakho, ukuze ube yisimungulu, njalo ungabi ngumuntu okhuzayo kubo; ngoba bayindlu evukelayo.
27 Koma pamene ndidzayankhula kwa iwe, ndidzatsekula pakamwa pako ndipo udzawawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti zakutizakuti.’ Aliyense wofuna kumva amve ndipo wokana kumva, muleke akane; pakuti iwo ndi anthu opanduka.”
Kodwa lapho ngikhuluma lawe, ngizavula umlomo wakho, ubususithi kubo: Itsho njalo iNkosi uJehova: Ozwayo kezwe, loyekelayo kayekele; ngoba bayindlu evukelayo.

< Ezekieli 3 >