< Ezekieli 3 >
1 Tsono Mulungu anandiwuza kuti, “Mwana wa munthu, idya chimene ndikukupatsachi. Idya kenaka upite ukayankhule ndi Aisraeli.”
Så sagde han til mig: "Menneskesøn, slug hvad du her har for dig, slug denne Bogrulle og gå så hen og tal til Israels Hus!"
2 Choncho ndinayasama ndipo anandipatsa mpukutuwo kuti ndidye.
Så åbnede jeg Munden, og han lod mig sluge Bogrullen
3 Kenaka Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, idya mpukutu umene ndikukupatsa kuti ukhute.” Choncho ndinadya, ndipo unkatsekemera ngati uchi mʼkamwa mwanga.
og sagde til mig: "Menneskesøn! Lad din Bug fortære den Bogrulle, jeg her giver dig, og fyld dine Indvolde dermed!" Og jeg slugte den, og den var sød som Honning i min Mund.
4 Pamenepo Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, pita tsopano kwa Aisraeli ndipo ukawawuze mawu anga.
Så sagde han til mig: "Menneskesøn, gå til Israels Hus og tal mine Ord til dem!
5 Sindikukutuma kwa anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, koma kwa Aisraeli.
Thi du sendes til Israels Folk, ikke til et Folk med dybt Mål og tungt Mæle,
6 Sindikukutuma kwa mitundu yambiri ya anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, amene mawu ake sungawamvetse. Ndithu ndikanakutuma kwa iwowa, bwenzi iwo atakumvera.
ikke til mange Hånde Folkeslag med dybt Mål og tungt Mæle, hvis Tale du ikke fatter, hvis jeg sendte dig til dem, vilde de høre dig.
7 Koma Aisraeli sadzakumvera chifukwa iwo sakufuna kumvera Ine. Paja Aisraeli onse ndi okanika ndiponso a mtima wowuma.
Men Israels Hus vil ikke høre dig, thi de vil ikke høre mig; thi hele Israels Hus har hårde Pander og stive Hjerter.
8 Tsono ine ndakhwimitsa nkhope yako mofanana ndi nkhope zawo. Ndalimbitsanso mutu wako mofanana ndi mitu yawo.
Se, jeg gør dit Ansigt hårdt som deres Ansigter og din Pande hård som deres Pander;
9 Ine ndidzakusandutsa wolimba ngati mwala wa dayimondi umene uposa thanthwe lina lililonse kulimba kwake. Usachite nawo mantha kapena kuopsedwa nawo. Paja anthuwa ndi awupandu.”
som Diamant, hårdere end Flint gør jeg din Pande. Frygt ikke for dem og vær ikke ræd for deres Ansigter, thi de er en genstridig Slægt!"
10 Anatinso, “Iwe mwana wa munthu, umvetsetse bwino zimene ndikukuwuzazi ndipo mawu angawa uwasunge bwino mu mtima mwako.
Videre sagde han til mig: "Menneskesøn, alle mine Ord, som jeg taler til dig, skal du optage i dit Hjerte og høre med dine Ører;
11 Tsopano upite kwa Aisraeli anzako amene ali ku ukapolo ndipo ukayankhule nawo. ‘Kaya akamvera kaya sakamvera,’ koma uzikawawuza kuti, Ambuye Wamphamvuzonse akuti zakutizakuti.”
og gå så hen til dine landflygtige Landsmænd og tal til dem og sig: Så siger den Herre HERREN! - hvad enten de så hører eller ej!"
12 Pamenepo Mzimu unandinyamula ndipo kumbuyo kwanga ndinamva liwu lamphamvu ngati chivomerezi chachikulu, lonena kuti, “Utamandike ulemerero wa Yehova kumene Iye amakhala!”
Så løftede Ånden mig, og jeg hørte bag mig Larmen af et vældigt Jordskælv, da HERRENs Herlighed hævede sig fra sit Sted,
13 Phokoso ndinkalimvalo linali la kugundana kwa mapiko a zamoyo ndiponso phokoso la mikombero ya pambali pake ija, limene linkamveka ngati chivomerezi chachikulu.
og Suset af de levende Væseners Vinger, der rørte hverandre, og samtidig Lyden af Hjulene og Larmen af Jordskælvet.
14 Mzimu wa Yehova unandikweza ndi kundinyamula ndipo ndinachokapo ndili wowawidwa ndi wonyuka mu mtima. Ndipo dzanja la Yehova linali pa ine mwa mphamvu.
Og Ånden løftede mig og førte mig bort, og jeg vandrede bitter og gram i Hu, idet HERRENs Hånd var over mig med Vælde.
15 Choncho ndinafika kwa amene anali mu ukapolo ku Telabibu pafupi ndi mtsinje wa Kebara. Ndinakhala pansi pakati pawo masiku asanu ndi awiri, ndili wothedwa nzeru kwambiri.
Så kom jeg til de landflygtige i Tel-Abib, de, som boede ved Floden Kebar, og der sad jeg syv Dage iblandt dem og stirrede hen for mig.
16 Atatha masiku asanu ndi awiriwo, Yehova anandiwuza kuti,
Syv Dage senere kom HERRENs Ord til mig således:
17 “Iwe mwana wa munthu, Ine ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Uziti ukamva mawu anga, ndiye uzikawachenjeza.
Menneskesøn! Jeg sætter dig til Vægter for Israels Hus; hører du et Ord af min Mund, skal du advare dem fra mig.
18 Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe udzafa ndithu,’ koma iwe osamuchenjeza kapena kumuyankhula kuti aleke njira zake zoyipa ndi kuti akhale ndi moyo, munthu woyipayo adzafa mu uchimo wake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
Når jeg siger til den gudløse: "Du skal visselig dø!" og du ikke advarer ham eller for at bevare hans Liv taler til ham om at omvende sig fra sin gudløse Vej, så skal samme gudløse dø for sin Misgerning, men hans Blod vil jeg kræve af din Hånd.
19 Koma ukamuchenjeza munthu woyipa koma iye osatembenuka mtima kuleka zoyipa zake kapena kusiya njira zake zoyipa, munthuyo adzafa chifukwa cha uchimo wake koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
Advarer du derimod den gudløse, og han ikke omvender sig fra sin Gudløshed og sin Vej, så skal samme gudløse dø for sin Misgerning, men du har reddet din Sjæl.
20 “Ngati munthu wolungama asiya chilungamo chake ndi kuchita uchimo ndipo Ine nʼkumuyika mʼzoopsa, munthuyo adzafa ndithu. Popeza iwe sunamuchenjeze, adzafadi chifukwa cha tchimo ndipo chilungamo chake sichidzakumbukiridwa, koma ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
Og når en retfærdig vender sig fra sin Retfærdighed og gør Uret, og jeg lægger Anstød for ham, så han dør, og du ikke har advaret ham, så dør han for sin Synd, og den Retfærdighed, han har øvet, skal ikke tilregnes ham, men hans Blod vil jeg kræve af din Hånd.
21 Koma ngati umuchenjeza munthu wolungama kuti asachimwe ndipo iye nʼkuleka kuchimwa adzakhala ndi moyo ndithu chifukwa anamvera chenjezo, ndipo iwe udzapulumutsa moyo wako.”
Har du derimod advaret den retfærdige mod at synde, og han ikke synder, så skal samme retfærdige leve, fordi han lod sig advare, og du har reddet din Sjæl.
22 Nthawi ina dzanja la Yehova linali pa ine ndipo anandiwuza kuti, “Nyamuka upite ku chigwa, kumeneko ndikayankhula nawe.”
Siden kom HERRENs Hånd over mig der, og han sagde til mig: "Stå op og gå ud i dalen, der vil jeg tale med dig!"
23 Choncho ndinanyamuka kupita ku chigwa. Ndipo ndinaona ulemerero wa Yehova kumeneko, ngati ulemerero umene ndinaona mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara ndipo ndinagwa pansi chafufumimba.
Så stod jeg op og gik ud i Dalen, og se, der stod HERRENs Herlighed, som jeg havde set denved Floden Kebar. Da faldt jeg på mit Ansigt.
24 Koma Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa. Tsono Yehova anandiyankhula nati: “Pita, kadzitsekere mʼnyumba mwako.
Men Ånden kom i mig og rejste mig på mine Fødder. Så taIede han til mig og sagde: Gå hjem og luk dig inde i dit Hus!
25 Ndipo iwe mwana wa munthu, adzakumanga ndi zingwe motero kuti sudzatha kuyendanso pakati pa anthu.
Og du, Menneskesøn, se, man skal lægge Bånd på dig og binde dig, så du ikke kan gå ud iblandt dem;
26 Ndidzamatirira lilime lako kukhosi, kotero kuti udzakhala chete wosatha kuwadzudzula, chifukwa iwo ndi anthu aupandu.
og din Tunge lader jeg hænge ved Ganen, så du bliver stum og ikke kan være dem en Revser; thi de er en genstridig Slægt.
27 Koma pamene ndidzayankhula kwa iwe, ndidzatsekula pakamwa pako ndipo udzawawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti zakutizakuti.’ Aliyense wofuna kumva amve ndipo wokana kumva, muleke akane; pakuti iwo ndi anthu opanduka.”
Men når jeg taler til dig, vil jeg åbne din Mund, og du skal sige til dem: Så siger den Herre HERREN! Så får den, der vil høre, høre, og den, der ikke vil, får lade være; thi de er en genstridig Slægt.