< Ezekieli 29 >

1 Pa tsiku lakhumi ndi chiwiri la mwezi wakhumi, chaka chakhumi, Yehova anandiyankhula kuti:
Sürgünlüğümüzün onuncu yılı, onuncu ayın on ikinci günü RAB bana şöyle seslendi:
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Farao, mfumu ya Igupto, ndipo unenere modzudzula mfumuyo pamodzi ndi dziko lake.
“İnsanoğlu, yüzünü firavuna çevir, ona ve Mısır'a karşı peygamberlik et.
3 Uyiwuze mfumuyo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndine mdani wako, iwe Farao mfumu ya Igupto, iwe ngʼona yayikulu yogona pakati pa mitsinje yako. Umanena kuti, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinadzipangira ndekha.’
Onlara de ki, ‘Egemen RAB şöyle diyor: “‘Kendi kanallarının içinde yatan Büyük canavar firavun, İşte, sana karşıyım. Sen ki, Nil benimdir, Onu kendim için yaptım dersin.
4 Koma ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako ndipo nsomba za mʼmitsinje yako zidzakangamira ku mamba ako. Tsono ndidzakutulutsa mu mtsinje mwakomo pamodzi ndi nsomba zimene zakangamira ku mamba ako.
Çenelerine çengeller takacak, Kanallarındaki balıkları Senin pullarına yapıştıracağım. Pullarına yapışmış balıklarla birlikte Seni kanallarından çıkaracağım.
5 Ndidzakutaya ku chipululu, iwe pamodzi ndi nsomba zonse za mʼmitsinje yako. Udzagwera pamtetete kuthengo popanda munthu woti akutole kuti akayike maliro ako. Ndidzakusandutsa chakudya cha zirombo za pa dziko lapansi ndi mbalame za mlengalenga.
Seni de kanallarındaki bütün balıkları da Çöle atacağım. Kırlara düşeceksin, Toplanmayacak, gömülmeyeceksin. Seni yem olarak yabanıl hayvanlara Ve yırtıcı kuşlara vereceğim.
6 Motero aliyense amene amakhala mu Igupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova. “‘Iwe unakhala ngati ndodo yabango ku Aisraeli.
O zaman Mısır'da yaşayan herkes Benim RAB olduğumu anlayacak. “‘Çünkü sen İsrail halkına kamış bir değnek oldun.
7 Pamene anakugwira unathethekera mʼmanja mwawo ndi kucheka mapewa awo. Pamene anakutsamira, unathyoka ndipo misana yawo inagwedezeka.
Seni elleriyle tuttuklarında parçalanıp onların omuzlarını yardın. Sana dayandıklarında parçalanıp bellerini burktun.
8 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, ndikubweretsera lupanga kuti lidzaphe anthu pamodzi ndi nyama zomwe.
“‘Bu yüzden Egemen RAB şöyle diyor: Üzerine halkını ve hayvanlarını öldürecek bir kılıç gönderiyorum.
9 Dziko la Igupto lidzasanduka lopanda anthu. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova. “‘Popeza iwe unati, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinawupanga ndine,’
Mısır kimsesiz bırakılacak, viraneye çevrilecek. O zaman benim RAB olduğumu anlayacaklar. “‘Madem Nil benimdir, onu ben yaptım dedin,
10 nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawe pamodzi ndi mitsinje yakoyo, ndipo ndidzasandutsa dziko la Igupto bwinja kuyambira chipululu cha Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani, kukafika ku malire a Kusi.
ben de sana ve kanallarına karşıyım. Mısır'ı Migdol'dan Asvan'a, Kûş sınırına dek kimsesiz bırakacak, viraneye çevireceğim.
11 Palibe phazi la munthu kapena la nyama limene lidzapondepo. Kudzakhala kopanda anthu kwa zaka makumi anayi.
İçinden insan ayağı da, hayvan ayağı da geçmeyecek. Kırk yıl orada kimse yaşamayacak.
12 Ndidzasandutsa dziko la Igupto kukhala chipululu ngati zipululu za mayiko ena. Kwa zaka makumi anayi mizinda yakenso idzakhala yopasuka pakati pa mizinda yopasuka. Ndipo ndidzathamangitsira Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndi kuwabalalitsira mʼmayiko.
Mısır'ı ıssız kalmış ülkeler gibi ıssız bırakacağım. Kentleri, viran olmuş kentler arasında kırk yıl kimsesiz kalacak. Mısırlılar'ı uluslar arasına gönderecek, ülkelere dağıtacağım.
13 “‘Komabe Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pakutha pa zaka makumi anayi ndidzasonkhanitsa Aigupto onse kuchokera ku mayiko amene ndinawabalalitsirako.
“‘Egemen RAB şöyle diyor: Kırk yıl sonra onları dağılmış oldukları uluslardan toplayacağım.
14 Ndidzachotsa Aiguptowo ku ukapolo ndipo ndidzawabwezera ku Patirosi kumene anachokera. Kumeneko iwo adzakhala ufumu wotsika.
Sürgündekileri geri getirip Patros'a, yurtlarına döndüreceğim. Orada güçsüz bir krallık oluşturacaklar.
15 Udzakhala ufumu wotsika kwambiri kupambana maufumu ena onse ndipo sudzadzitukumula pakati pa mitundu ina. Ndidzawufowoketsa kwambiri kotero kuti sudzathanso kulamulira mitundu ya anthu.
Krallıkların en güçsüzü olacak, bir daha ulusların üzerinde egemenlik sürmeyecek. Ulusları yönetmesinler diye onları küçük düşüreceğim.
16 Aisraeli sadzadaliranso Aigupto. Koma kuti chilango chawo chidzawakumbutsa tchimo lawo lija lofunafuna thandizo kuchokera ku Igupto. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.’”
Mısır bir daha İsrail halkının güveneceği bir yer olmayacak. Ancak Mısırlılar onlara Mısır'a dönmekle işledikleri günahı anımsatacaklar. O zaman İsrailliler benim Egemen RAB olduğumu anlayacaklar.’”
17 Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba, chaka cha 27, Yehova anandiyankhula kuti:
Sürgünlüğümüzün yirmi yedinci yılı, birinci ayın birinci günü RAB bana şöyle seslendi:
18 “Iwe mwana wa munthu, kale Nebukadinezara mfumu ya Babuloni inagwiritsa ntchito ankhondo ake kukathira nkhondo mzinda wa Turo, mpaka munthu aliyense anachita dazi chifukwa chosenza katundu, ndipo ananyuka pa phewa. Komabe ngakhale iyeyo, kapena gulu lake lankhondo sanaphulepo kanthu pa ntchito yonse imene anayigwira polimbana ndi mzindawo.
“İnsanoğlu, Babil Kralı Nebukadnessar ordusunu Sur Kenti'ne karşı büyük bir saldırıya geçirdi; herkesin saçı döküldü, ağır yük yüzünden omuz derileri yüzüldü. Ama Sur'a karşı ordusunu saldırıya geçirmesine karşın, bundan ne kendisi ne de ordusu yararlandı.
19 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndidzapereka Igupto kwa Nebukadinezara mfumu ya Babuloni, ndipo iyo idzatenga chuma chake ndi kuchifunkha ngati malipiro a gulu lake lankhondo.
Bu yüzden Egemen RAB şöyle diyor: Mısır'ı Babil Kralı Nebukadnessar'a vereceğim, onun servetini alıp götürecek. Ordusuna ücret olarak ülkeden yağmaladığı çapul malını dağıtacak.
20 Ndamupatsa Nebukadinezara Igupto ngati mphotho ya kulimbika kwake chifukwa iyo ndi gulu lake lankhondo anandigwirira ntchito, akutero Ambuye Yehova.
Hizmetine karşılık Mısır'ı ona verdim; çünkü o da ordusu da bana hizmet ettiler. Egemen RAB böyle diyor.
21 “Pa nthawi imeneyo ndidzapereka mphamvu yatsopano pa Aisraeli, ndipo ndidzatsekula pakamwa pako, iwe, Ezekieli kuti uthe kuyankhula pakati pawo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
“O gün İsrail halkını güçle donatacağım. Onların arasında senin dilini çözeceğim. O zaman benim RAB olduğumu anlayacaklar.”

< Ezekieli 29 >