< Ezekieli 29 >

1 Pa tsiku lakhumi ndi chiwiri la mwezi wakhumi, chaka chakhumi, Yehova anandiyankhula kuti:
I KA umi o ka makahiki, i ka umi o ka malama, i ka la umikumamalua o ka malama, hiki mai la ka olelo a Iehova ia'u, i mai la,
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Farao, mfumu ya Igupto, ndipo unenere modzudzula mfumuyo pamodzi ndi dziko lake.
E ke keiki a ke kanaka, e kau e aku oe i kou maka ia Parao, i ke alii o Aigupita, a e wanana ku e ia ia, a me Aigupita a pau.
3 Uyiwuze mfumuyo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndine mdani wako, iwe Farao mfumu ya Igupto, iwe ngʼona yayikulu yogona pakati pa mitsinje yako. Umanena kuti, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinadzipangira ndekha.’
E olelo aku oe, e i aku, Ke i mai nei Iehova ka Haku, Eia hoi, ke ku e nei au ia oe, e Parao, ke alii o Aigupita, ka moo nui e moe ana iwaena o kona mau muliwai, ka mea i olelo, No'u no kuu muliwai, na'u no ia i hana no'u.
4 Koma ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako ndipo nsomba za mʼmitsinje yako zidzakangamira ku mamba ako. Tsono ndidzakutulutsa mu mtsinje mwakomo pamodzi ndi nsomba zimene zakangamira ku mamba ako.
E hookomo aku au i na kilou iloko o kou mau a, a e hoopili aku au i na ia o kou mau muliwai i kou mau unahi; a e lawe mai au ia oe mai waenakonu mai o kou mau muliwai, a me na ia a pau o kou mau muliwai e pili ana i kou mau unahi.
5 Ndidzakutaya ku chipululu, iwe pamodzi ndi nsomba zonse za mʼmitsinje yako. Udzagwera pamtetete kuthengo popanda munthu woti akutole kuti akayike maliro ako. Ndidzakusandutsa chakudya cha zirombo za pa dziko lapansi ndi mbalame za mlengalenga.
A e waiho aku au ia oe iloko o ka waonahele, ia oe, a me na ia a pau o ko'u mau muliwai, a e haule oe ma ka aina mawaho; aole oe e hoakoakoaia, aole hoi e houluuluia; ua haawi aku au ia oe i ai na na holoholona o ke kula, a me na manu o ka lewa.
6 Motero aliyense amene amakhala mu Igupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova. “‘Iwe unakhala ngati ndodo yabango ku Aisraeli.
A e ike no ka poe a pau e noho ana ma Aigupita owau no Iehova, no ka mea, ua lilo lakou i kookoo ohe i ka ohana a Iseraela.
7 Pamene anakugwira unathethekera mʼmanja mwawo ndi kucheka mapewa awo. Pamene anakutsamira, unathyoka ndipo misana yawo inagwedezeka.
A i ko lakou lalau ana ia oe ma kou lima, ua uhai oe, ua wawahi hoi i ko lakou poohiwi a pau; a i ko lakou hilinai ana maluna ou, ua haki oe, a haalulu ko lakou puhaka okoa.
8 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, ndikubweretsera lupanga kuti lidzaphe anthu pamodzi ndi nyama zomwe.
Nolaila, ke i mai nei Iehova ka Haku, penei; E lawe mai au i ka pahikaua maluna ou, a e oki aku i kanaka a me ka holoholona mai ou aku nei;
9 Dziko la Igupto lidzasanduka lopanda anthu. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova. “‘Popeza iwe unati, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinawupanga ndine,’
A e neoneo aku ka aina o Aigupita e noho ole ia, a e ike lakou owau no Iehova; no ka mea, ua olelo oia, No'u no ka muliwai, a na'u no ia i hana.
10 nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawe pamodzi ndi mitsinje yakoyo, ndipo ndidzasandutsa dziko la Igupto bwinja kuyambira chipululu cha Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani, kukafika ku malire a Kusi.
Nolaila, ea, ke ku e nei au ia oe, a i kou muliwai; a e hooneoneo loa au i ka aina Aigupita e noho ole ia, mai ka palena o Seena a hiki i ka palena o Aitiopa.
11 Palibe phazi la munthu kapena la nyama limene lidzapondepo. Kudzakhala kopanda anthu kwa zaka makumi anayi.
Aole wawae kanaka e hele mawaena ona, aole wawae holoholona e hele mawaena ona, aole hoi e nohoia a kanaha na makahiki.
12 Ndidzasandutsa dziko la Igupto kukhala chipululu ngati zipululu za mayiko ena. Kwa zaka makumi anayi mizinda yakenso idzakhala yopasuka pakati pa mizinda yopasuka. Ndipo ndidzathamangitsira Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndi kuwabalalitsira mʼmayiko.
A e haawi au i ka aina Aigupita i neoneo, iwaena o na aina neo-neo, a o kona mau kulanakauhale iwaena o na kulanakauhale i hooneoneoia, e neoneo no i na makahiki he kanaha: a e hoopuehu au i ko Aigupita iwaena o na lahuikanaka, a e lulu aku au ia lakou iwaena o na aina.
13 “‘Komabe Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pakutha pa zaka makumi anayi ndidzasonkhanitsa Aigupto onse kuchokera ku mayiko amene ndinawabalalitsirako.
A ke i mai nei Iehova ka Haku, penei; I ka pau ana o na makahiki he kanaha, e houluulu mai au i ko Aigupita, mai loko mai o na lahuikanaka kahi i puehuia lakou.
14 Ndidzachotsa Aiguptowo ku ukapolo ndipo ndidzawabwezera ku Patirosi kumene anachokera. Kumeneko iwo adzakhala ufumu wotsika.
E hoihoi mai hoi au i ke pio ana o Aigupita, a e hoihoi mai au ia lakou e komo i ka aina o Paterosa a i ko lakou aina e noho ai; e noho lakou ilaila he aupuni haa-haa.
15 Udzakhala ufumu wotsika kwambiri kupambana maufumu ena onse ndipo sudzadzitukumula pakati pa mitundu ina. Ndidzawufowoketsa kwambiri kotero kuti sudzathanso kulamulira mitundu ya anthu.
E lilo ia i haahaa loa iwaena o na aupuni, aole ia e hookiekie hou iluna o na lahuikanaka; no ka mea, e hoemi au ia lakou, aole hoi lakou e hooalii ae maluna o ko na aina.
16 Aisraeli sadzadaliranso Aigupto. Koma kuti chilango chawo chidzawakumbutsa tchimo lawo lija lofunafuna thandizo kuchokera ku Igupto. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.’”
Aole loa aku ia he mea hilinai no ka ohana a Iseraela, ka mea i paipai i ka manao i ko lakou hewa, i ka wa e nana ai lakou ia lakou; aka, e ike no lakou, owau no Iehova ka Haku.
17 Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba, chaka cha 27, Yehova anandiyankhula kuti:
Eia keia, i ka iwakaluakumamahiku o na makahiki, i ka malama mua, i ka la mua o ka malama, hiki mai la ka olelo a Iehova ia'u, i mai la,
18 “Iwe mwana wa munthu, kale Nebukadinezara mfumu ya Babuloni inagwiritsa ntchito ankhondo ake kukathira nkhondo mzinda wa Turo, mpaka munthu aliyense anachita dazi chifukwa chosenza katundu, ndipo ananyuka pa phewa. Komabe ngakhale iyeyo, kapena gulu lake lankhondo sanaphulepo kanthu pa ntchito yonse imene anayigwira polimbana ndi mzindawo.
E ke keiki a ke kanaka, ua hooluhi o Nebukaneza, ke alii o Babulona i kona poe koa e hana i ka hana nui ku e ia Turo; ua hooohuleia na poo a pau, a ua poholeia na poohiwi a pau; aole hoi ona uku, aole hoi o kona poe kaua, no Turo, no ka hana, ana i hana ku e aku ai ia ia.
19 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndidzapereka Igupto kwa Nebukadinezara mfumu ya Babuloni, ndipo iyo idzatenga chuma chake ndi kuchifunkha ngati malipiro a gulu lake lankhondo.
Nolaila, ke i mai nei Iehova ka Haku, Aia hoi, e haawi aku au i ka aina Aigupita iloko o ka lima o Nebukaneza ke alii o Babulona; a e lawe oia i kona lehulehu, a e lawe hoi oia i kona waiwai pio, a e lawe hoi i kona waiwai kaili; a e lilo ia i uku no kona poe kaua.
20 Ndamupatsa Nebukadinezara Igupto ngati mphotho ya kulimbika kwake chifukwa iyo ndi gulu lake lankhondo anandigwirira ntchito, akutero Ambuye Yehova.
No kana hana, aua i hana ku e aku ai ia ia, ua haawi aku au i ka aina Aigupita ia ia, no ka mea, ua hana lakou no'u, wahi a Iehova ka Haku.
21 “Pa nthawi imeneyo ndidzapereka mphamvu yatsopano pa Aisraeli, ndipo ndidzatsekula pakamwa pako, iwe, Ezekieli kuti uthe kuyankhula pakati pawo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
Ia la no e hooopuu ae au i ka pepeiaohao o ka ohana a Iseraela, a e haawi aku au ia oe i ka oaka ana o ka waha iwaenakonu o lakou; a e ike lakou owau no Iehova.

< Ezekieli 29 >