< Ezekieli 29 >

1 Pa tsiku lakhumi ndi chiwiri la mwezi wakhumi, chaka chakhumi, Yehova anandiyankhula kuti:
La dixième année, au douzième [jour] du dixième mois, la parole de l'Eternel me fut [adressée], en disant:
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Farao, mfumu ya Igupto, ndipo unenere modzudzula mfumuyo pamodzi ndi dziko lake.
Fils d'homme, tourne ta face contre Pharaon Roi d'Egypte, et prophétise contre lui, et contre toute l'Egypte.
3 Uyiwuze mfumuyo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndine mdani wako, iwe Farao mfumu ya Igupto, iwe ngʼona yayikulu yogona pakati pa mitsinje yako. Umanena kuti, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinadzipangira ndekha.’
Parle, et dis: ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: voici, j'en veux à toi, Pharaon Roi d'Egypte, grande Baleine couchée au milieu de tes bras d'eau, qui as dit: mes bras d'eau sont à moi, et je me les suis faits.
4 Koma ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako ndipo nsomba za mʼmitsinje yako zidzakangamira ku mamba ako. Tsono ndidzakutulutsa mu mtsinje mwakomo pamodzi ndi nsomba zimene zakangamira ku mamba ako.
C'est pourquoi je mettrai des crocs dans tes mâchoires, et je ferai attacher à tes écailles les poissons de tes bras d'eau; et je te tirerai hors de tes bras d'eau, avec tous les poissons de tes bras d'eau, qui auront été attachés à tes écailles.
5 Ndidzakutaya ku chipululu, iwe pamodzi ndi nsomba zonse za mʼmitsinje yako. Udzagwera pamtetete kuthengo popanda munthu woti akutole kuti akayike maliro ako. Ndidzakusandutsa chakudya cha zirombo za pa dziko lapansi ndi mbalame za mlengalenga.
Et [t'ayant tiré] dans le désert, je te laisserai là, toi, et tous les poissons de tes bras d'eau; tu seras étendu sur le dessus de la campagne; tu ne seras point recueilli ni ramassé; je t'ai livré aux bêtes de la terre, et aux oiseaux des cieux, pour en être dévoré.
6 Motero aliyense amene amakhala mu Igupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova. “‘Iwe unakhala ngati ndodo yabango ku Aisraeli.
Et tous les habitants d'Egypte sauront que je suis l'Eternel; parce qu'ils auront été à la maison d'Israël un bâton, qui n'était qu'un roseau.
7 Pamene anakugwira unathethekera mʼmanja mwawo ndi kucheka mapewa awo. Pamene anakutsamira, unathyoka ndipo misana yawo inagwedezeka.
Quand ils t'ont pris par la main, tu t'es rompu, et tu leur as percé toute l'épaule; et quand ils se sont appuyés sur toi, tu t'es cassé, et tu les as fait tomber à la renverse.
8 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, ndikubweretsera lupanga kuti lidzaphe anthu pamodzi ndi nyama zomwe.
C'est pourquoi ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: voici, je m'en vais faire venir l'épée sur toi, et j'exterminerai du milieu de toi les hommes et les bêtes.
9 Dziko la Igupto lidzasanduka lopanda anthu. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova. “‘Popeza iwe unati, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinawupanga ndine,’
Et le pays d'Egypte sera en désolation et en désert, et ils sauront que je suis l'Eternel, parce que [le Roi d'Egypte] a dit: les bras d'eau sont à moi, et je les ai faits.
10 nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawe pamodzi ndi mitsinje yakoyo, ndipo ndidzasandutsa dziko la Igupto bwinja kuyambira chipululu cha Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani, kukafika ku malire a Kusi.
C'est pourquoi voici, j'en veux à toi, et à tes bras d'eau, et je réduirai le pays d'Egypte en désert de sécheresse et de désolation, depuis la tour de Syène, jusques aux marches de Cus.
11 Palibe phazi la munthu kapena la nyama limene lidzapondepo. Kudzakhala kopanda anthu kwa zaka makumi anayi.
Nul pied d'homme ne passera par là, et il n'y passera non plus aucun pied de bête, et elle sera quarante ans sans être habitée.
12 Ndidzasandutsa dziko la Igupto kukhala chipululu ngati zipululu za mayiko ena. Kwa zaka makumi anayi mizinda yakenso idzakhala yopasuka pakati pa mizinda yopasuka. Ndipo ndidzathamangitsira Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndi kuwabalalitsira mʼmayiko.
Car je réduirai le pays d'Egypte en désolation entre les pays désolés, et ses villes entre les villes réduites en désert; elles seront en désolation durant quarante ans, je disperserai les Egyptiens parmi les nations, et je les répandrai parmi les pays.
13 “‘Komabe Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pakutha pa zaka makumi anayi ndidzasonkhanitsa Aigupto onse kuchokera ku mayiko amene ndinawabalalitsirako.
Toutefois, ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: au bout de quarante ans je ramasserai les Egyptiens d'entre les peuples parmi lesquels ils auront été dispersés;
14 Ndidzachotsa Aiguptowo ku ukapolo ndipo ndidzawabwezera ku Patirosi kumene anachokera. Kumeneko iwo adzakhala ufumu wotsika.
Et je ramènerai les captifs d'Egypte, et les ferai retourner au pays de Pathros, au pays de leur extraction, mais ils seront là un Royaume abaissé.
15 Udzakhala ufumu wotsika kwambiri kupambana maufumu ena onse ndipo sudzadzitukumula pakati pa mitundu ina. Ndidzawufowoketsa kwambiri kotero kuti sudzathanso kulamulira mitundu ya anthu.
Il sera le plus bas des Royaumes, et il ne s'élèvera plus au dessus des nations, et je le diminuerai, afin qu'il ne domine point sur les nations.
16 Aisraeli sadzadaliranso Aigupto. Koma kuti chilango chawo chidzawakumbutsa tchimo lawo lija lofunafuna thandizo kuchokera ku Igupto. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.’”
Et il ne sera plus l'assurance de la maison d'Israël, les faisant souvenir de [leur] iniquité quand [les enfants d'Israël] regardaient après eux; et ils sauront que je suis le Seigneur l'Eternel.
17 Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba, chaka cha 27, Yehova anandiyankhula kuti:
Et il arriva la vingt-septième année, au premier [jour] du premier mois, que la parole de l'Eternel me fut [adressée], en disant:
18 “Iwe mwana wa munthu, kale Nebukadinezara mfumu ya Babuloni inagwiritsa ntchito ankhondo ake kukathira nkhondo mzinda wa Turo, mpaka munthu aliyense anachita dazi chifukwa chosenza katundu, ndipo ananyuka pa phewa. Komabe ngakhale iyeyo, kapena gulu lake lankhondo sanaphulepo kanthu pa ntchito yonse imene anayigwira polimbana ndi mzindawo.
Fils d'homme, Nébucadnetsar Roi de Babylone a fait servir son armée dans un service pénible contre Tyr; toute tête en est devenue chauve, et toute épaule en a été foulée, mais il n'a point eu de salaire, ni lui, ni son armée, à cause de Tyr, pour le service qu'il a fait contre elle.
19 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndidzapereka Igupto kwa Nebukadinezara mfumu ya Babuloni, ndipo iyo idzatenga chuma chake ndi kuchifunkha ngati malipiro a gulu lake lankhondo.
C'est pourquoi ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: voici, je m'en vais donner à Nébucadnetsar Roi de Babylone le pays d'Egypte; et il en enlèvera la multitude, il en emportera le butin, et en fera le pillage; et ce sera là le salaire de son armée.
20 Ndamupatsa Nebukadinezara Igupto ngati mphotho ya kulimbika kwake chifukwa iyo ndi gulu lake lankhondo anandigwirira ntchito, akutero Ambuye Yehova.
Pour [le salaire de] l'ouvrage auquel il a servi contre Tyr, je lui ai donné le pays d'Egypte, parce qu'ils ont travaillé pour moi, dit le Seigneur l'Eternel.
21 “Pa nthawi imeneyo ndidzapereka mphamvu yatsopano pa Aisraeli, ndipo ndidzatsekula pakamwa pako, iwe, Ezekieli kuti uthe kuyankhula pakati pawo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
En ce jour-là je ferai germer la corne de la maison d'Israël, et j'ouvrirai ta bouche au milieu d'eux, et ils sauront que je suis l'Eternel.

< Ezekieli 29 >