< Ezekieli 29 >

1 Pa tsiku lakhumi ndi chiwiri la mwezi wakhumi, chaka chakhumi, Yehova anandiyankhula kuti:
La dixième année, au dixième mois, le douze du mois, la parole de Yahweh me fut adressée en ces termes:
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Farao, mfumu ya Igupto, ndipo unenere modzudzula mfumuyo pamodzi ndi dziko lake.
« Fils de l’homme, tourne ta face contre Pharaon, roi d’Égypte, et prophétise sur lui et sur l’Égypte tout entière;
3 Uyiwuze mfumuyo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndine mdani wako, iwe Farao mfumu ya Igupto, iwe ngʼona yayikulu yogona pakati pa mitsinje yako. Umanena kuti, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinadzipangira ndekha.’
parle et dis: Ainsi parle le Seigneur Yahweh: Voici que je viens à toi, Pharaon, roi d’Égypte, toi le grand crocodile, couché au milieu de tes fleuves, qui as dit: « Mon fleuve est à moi, et c’est moi qui me le suis fait. »
4 Koma ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako ndipo nsomba za mʼmitsinje yako zidzakangamira ku mamba ako. Tsono ndidzakutulutsa mu mtsinje mwakomo pamodzi ndi nsomba zimene zakangamira ku mamba ako.
Je mettrai des crochets dans tes mâchoires, et je ferai s’attacher à tes écailles les poissons de tes fleuves; et je te ferai monter du milieu de tes fleuves, toi et tous les poissons de tes fleuves, attachés à tes écailles;
5 Ndidzakutaya ku chipululu, iwe pamodzi ndi nsomba zonse za mʼmitsinje yako. Udzagwera pamtetete kuthengo popanda munthu woti akutole kuti akayike maliro ako. Ndidzakusandutsa chakudya cha zirombo za pa dziko lapansi ndi mbalame za mlengalenga.
et je te jetterai au désert, toi et tous les poissons de tes fleuves; tu tomberas sur la face des champs, tu ne seras ni relevé, ni ramassé; je te donne en pâture aux bêtes de la terre et aux oiseaux du ciel;
6 Motero aliyense amene amakhala mu Igupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova. “‘Iwe unakhala ngati ndodo yabango ku Aisraeli.
et tous les habitants de l’Égypte sauront que je suis Yahweh — parce qu’ils ont été un appui de roseau pour la maison d’Israël!
7 Pamene anakugwira unathethekera mʼmanja mwawo ndi kucheka mapewa awo. Pamene anakutsamira, unathyoka ndipo misana yawo inagwedezeka.
Quand ils te prennent avec la main, tu casses, et tu leur déchires toute l’épaule; et quand ils s’appuient sur toi, tu te brises, tu les fais se tenir sur leurs reins à tous.
8 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, ndikubweretsera lupanga kuti lidzaphe anthu pamodzi ndi nyama zomwe.
C’est pourquoi ainsi parle le Seigneur Yahweh: Voici que je ferai venir sur toi l’épée et j’exterminerai du milieu de toi hommes et bêtes;
9 Dziko la Igupto lidzasanduka lopanda anthu. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova. “‘Popeza iwe unati, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinawupanga ndine,’
et la terre d’Égypte deviendra une désolation et un désert, et l’on saura que je suis Yahweh. Parce que Pharaon a dit: « Le fleuve est à moi, et c’est moi qui l’ai fait, »
10 nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawe pamodzi ndi mitsinje yakoyo, ndipo ndidzasandutsa dziko la Igupto bwinja kuyambira chipululu cha Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani, kukafika ku malire a Kusi.
à cause de cela, voici que je viens à toi et à tes fleuves; et je ferai du pays d’Égypte des ruines désertes et désolées, de Migdol a Syène, et jusqu’à la frontière de l’Ethiopie.
11 Palibe phazi la munthu kapena la nyama limene lidzapondepo. Kudzakhala kopanda anthu kwa zaka makumi anayi.
Il n’y passera nul pied d’homme, et nul pied de bête n’y passera, et il sera inhabité pendant quarante ans.
12 Ndidzasandutsa dziko la Igupto kukhala chipululu ngati zipululu za mayiko ena. Kwa zaka makumi anayi mizinda yakenso idzakhala yopasuka pakati pa mizinda yopasuka. Ndipo ndidzathamangitsira Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndi kuwabalalitsira mʼmayiko.
Je ferai du pays d’Égypte une désolation, au milieu des pays désolés, et ses villes, au milieu des villes ruinées, seront une désolation, durant quarante ans; je disperserai les Egyptiens parmi les nations; et je les disséminerai en divers pays.
13 “‘Komabe Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pakutha pa zaka makumi anayi ndidzasonkhanitsa Aigupto onse kuchokera ku mayiko amene ndinawabalalitsirako.
Car ainsi parle le Seigneur Yahweh: Au bout de quarante ans, je rassemblerai les Egyptiens, d’entre les peuples chez lesquels ils auront été dispersés;
14 Ndidzachotsa Aiguptowo ku ukapolo ndipo ndidzawabwezera ku Patirosi kumene anachokera. Kumeneko iwo adzakhala ufumu wotsika.
je ferai revenir les captifs d’Égypte, et je les ramènerai dans le pays de Pathros, dans le pays de leur origine, et ils y seront un humble royaume.
15 Udzakhala ufumu wotsika kwambiri kupambana maufumu ena onse ndipo sudzadzitukumula pakati pa mitundu ina. Ndidzawufowoketsa kwambiri kotero kuti sudzathanso kulamulira mitundu ya anthu.
L’Égypte sera humble entre les royaumes, et elle ne s’élèvera plus au-dessus des nations; je réduirai leur nombre, afin qu’ils ne dominent pas sur les nations.
16 Aisraeli sadzadaliranso Aigupto. Koma kuti chilango chawo chidzawakumbutsa tchimo lawo lija lofunafuna thandizo kuchokera ku Igupto. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.’”
Ils ne seront plus pour la maison d’Israël un objet de confiance; ils lui rappelleront l’iniquité qu’elle commettait en se tournant vers eux; et l’on saura que je suis le Seigneur Yahweh. »
17 Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba, chaka cha 27, Yehova anandiyankhula kuti:
La vingt-septième année, au premier mois, le premier du mois, la parole de Yahweh me fut adressée en ces termes:
18 “Iwe mwana wa munthu, kale Nebukadinezara mfumu ya Babuloni inagwiritsa ntchito ankhondo ake kukathira nkhondo mzinda wa Turo, mpaka munthu aliyense anachita dazi chifukwa chosenza katundu, ndipo ananyuka pa phewa. Komabe ngakhale iyeyo, kapena gulu lake lankhondo sanaphulepo kanthu pa ntchito yonse imene anayigwira polimbana ndi mzindawo.
« Fils de l’homme, Nabuchodonosor, roi de Babylone, a fait faire à son armée un rude service contre Tyr; toute tête est devenue chauve, toute épaule meurtrie; et il n’a retiré de Tyr aucun salaire, ni pour lui, ni pour son armée, pour le service qu’il a fait contre elle.
19 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndidzapereka Igupto kwa Nebukadinezara mfumu ya Babuloni, ndipo iyo idzatenga chuma chake ndi kuchifunkha ngati malipiro a gulu lake lankhondo.
C’est pourquoi ainsi parle le Seigneur Yahweh: Voici que je donne à Nabuchodonosor, roi de Babylone, le pays d’Égypte; il en emportera les richesses; il dépouillera ce qu’il y a à dépouiller, il pillera son butin et prendra ses dépouilles: et ce sera un salaire pour son armée.
20 Ndamupatsa Nebukadinezara Igupto ngati mphotho ya kulimbika kwake chifukwa iyo ndi gulu lake lankhondo anandigwirira ntchito, akutero Ambuye Yehova.
Pour prix du travail qu’il a fait contre Tyr, je lui donne le pays d’Égypte, parce qu’ils ont travaillé pour moi — oracle du Seigneur Yahweh.
21 “Pa nthawi imeneyo ndidzapereka mphamvu yatsopano pa Aisraeli, ndipo ndidzatsekula pakamwa pako, iwe, Ezekieli kuti uthe kuyankhula pakati pawo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
En ce jour-là, je ferai pousser une corne à la maison d’Israël, et je te donnerai d’ouvrir la bouche au milieu d’eux; et ils sauront que je suis Yahweh. »

< Ezekieli 29 >