< Ezekieli 28 >
1 Yehova anandiyankhula nati:
I doszło do mnie słowo PANA mówiące:
2 “Iwe mwana wa munthu, iwuze mfumu ya ku Turo mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, “‘Iwe ndi mtima wako wodzikuza umanena kuti, ‘Ine ndine mulungu; ndimakhala pa mpando wa mulungu pakati pa nyanja.’ Koma ndiwe munthu chabe osati mulungu, ngakhale ukuganiza kuti ndiwe wanzeru ngati mulungu.
Synu człowieczy, powiedz księciu Tyru: Tak mówi Pan BÓG: Ponieważ uniosło się twoje serce i powiedziałeś: Ja jestem Bogiem, zasiadam na Bożym tronie w sercu mórz – ale ty jesteś człowiekiem, a nie Bogiem, choć twoje serce stawiasz na równi z sercem Boga;
3 Taona, ndiwedi wanzeru kupambana Danieli. Ndipo palibe chinsinsi chobisika kwa iwe.
Oto jesteś mądrzejszy od Daniela, żadna tajemnica nie jest zakryta przed tobą;
4 Mwa nzeru zako ndi kumvetsa kwako unadzipezera chuma ndipo unasonkhanitsa golide ndi siliva mʼnyumba zosungira chuma chako.
Swoją mądrością i roztropnością zdobyłeś sobie bogactwo i nagromadziłeś złota i srebra w swoich skarbcach;
5 Ndi nzeru zako zochitira malonda unachulukitsa chuma chako ndipo wayamba kunyada chifukwa cha chuma chakocho.
Dzięki wielkości twojej mądrości i twojemu kupiectwu rozmnożyłeś swoje bogactwa; a tak uniosło się twoje serce z powodu twoich bogactw;
6 “‘Choncho Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Popeza umadziganizira kuti ndiwe mulungu,
Dlatego tak mówi Pan BÓG: Ponieważ postawiłeś swoje serce jak serce Boga;
7 Ine ndidzabwera ndi anthu achilendo, anthu ankhanza, kuti adzalimbane nawe. Adzakuthira nkhondo kuti awononge zonse zimene unazipeza ndi nzeru zako, ndipo adzawononga kunyada kwakoko.
Oto sprowadzę na ciebie cudzoziemców, najsroższe z narodów. Dobędą swoje miecze przeciwko piękności twej mądrości i splugawią twój blask.
8 Iwo adzakuponyera ku dzenje ndipo udzafa imfa yoopsa mʼnyanja yozama.
Strącą cię do dołu i umrzesz srogą śmiercią w sercu mórz.
9 Kodi udzanenabe kuti, ‘Ine ndine mulungu,’ pamaso pa iwo amene akukupha? Iwe udzaoneka kuti ndiwe munthu chabe, osati mulungu, mʼmanja mwa iwo amene akukuphawo.
Czy powiesz przed tym, który cię zabije: Jestem Bogiem? Przecież jesteś człowiekiem, a nie Bogiem w ręku tego, który cię zabije.
10 Udzafa imfa ya anthu osachita mdulidwe mʼmanja mwa anthu achilendo. Ine ndayankhula zimenezi, akutero Ambuye Yehova.’”
Umrzesz śmiercią nieobrzezanych, z ręki cudzoziemców. Ja bowiem [to] powiedziałem, mówi Pan BÓG.
11 Yehova anandiyankhula kuti:
I doszło do mnie słowo PANA mówiące:
12 “Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira mfumu ya Turo ndipo uyiwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, “‘Iwe unali chitsanzo cha ungwiro weniweni, wodzaza ndi nzeru ndi wokongola kwambiri.
Synu człowieczy, podnieś lament nad królem Tyru i mów do niego: Tak mówi Pan BÓG: Ty pieczętujesz sumę, pełen mądrości i doskonały w swej piękności;
13 Iwe unkakhala ngati mu Edeni, munda wa Mulungu. Miyala yokongola ya mitundu yonse: rubi, topazi ndi dayimondi, kirisoliti, onikisi, yasipa, safiro, kalineliyoni ndi berili ndiwo inali zofunda zako. Ndipo zoyikamo miyalayo zinali zagolide. Anakupangira zonsezi pa tsiku limene unalengedwa.
Byłeś w Edenie, ogrodzie Bożym; twoim nakryciem był wszelki drogi kamień: karneol, topaz i jaspis, chryzolit, onyks i beryl, szafir, karbunkuł i szmaragd oraz złoto. Wykonanie twoich bębenków i fletów zostało przygotowane w dniu, kiedy zostałeś stworzony.
14 Ndinayika kerubi kuti azikulondera. Unkakhala pa phiri langa lopatulika, ndipo unkayendayenda pakati pa miyala ya moto.
Ty jesteś namaszczonym cherubinem nakrywającym; ja cię ustanowiłem. Byłeś na świętej górze Boga, przechadzałeś się wśród kamieni ognistych.
15 Makhalidwe ako anali abwino kuyambira pamene unalengedwa mpaka nthawi imene unayamba kuchita zoyipa.
Byłeś doskonały w swoich drogach od dnia, kiedy zostałeś stworzony, aż znalazła się w tobie nieprawość.
16 Unatanganidwa ndi zamalonda. Zotsatira zake zinali zoti unachulukitsa zandewu ndi kumachimwa. Choncho ndinakuchotsa ku phiri langa lopatulika. Mkerubi amene ankakulondera uja anakupirikitsa kukuchotsa ku miyala yamoto.
Przez twój ogromny handel pełno pośród ciebie bezprawia, i zgrzeszyłeś. Dlatego zrzucę cię z góry Boga, cherubinie nakrywający, wyniszczę cię spośród kamieni ognistych.
17 Unkadzikuza mu mtima mwako chifukwa cha kukongola kwako, ndipo unayipitsa nzeru zako chifukwa chofuna kutchuka. Kotero Ine ndinakugwetsa pansi kuti ukhala chenjezo pamaso pa mafumu.
Uniosło się twoje serce z powodu twojej piękności, znieważyłeś swoją mądrość z powodu twojego blasku. Rzucę cię na ziemię i postawię cię przed królami, aby się tobie przypatrzyli.
18 Ndi malonda ako achinyengo unachulukitsa machimo ako. Motero unayipitsa malo ako achipembedzo. Choncho ndinabutsa moto pakati pako, ndipo unakupsereza, ndipo unasanduka phulusa pa dziko lapansi pamaso pa anthu onse amene amakuona.
Mnóstwem twoich nieprawości [i] nieprawością twego handlu splugawiłeś swoją świątynię. Dlatego wywiodę ogień z twego wnętrza, który cię pożre, a zamienię cię w popiół na ziemi na oczach wszystkich, którzy na ciebie patrzą.
19 Anthu onse amitundu amene ankakudziwa akuchita mantha chifukwa cha iwe. Watheratu mochititsa mantha ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.’”
Wszyscy, którzy cię znają wśród narodów, zdumieją się nad tobą. Staniesz się postrachem i nie będzie ciebie już na wieki.
20 Yehova anandiyankhula nati:
I doszło do mnie słowo PANA mówiące:
21 “Iwe mwana wa munthu, utembenukire ku mzinda wa Sidoni ndipo unenere mowudzudzula kuti,
Synu człowieczy, zwróć swoją twarz przeciw Sydonowi i prorokuj przeciw niemu;
22 ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndine mdani wako, iwe Sidoni, ndipo ndidzalemekezedwa chifukwa cha iwe. Anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova ndikadzakulanga ndi kudzionetsa kuti ndine woyera pakati pako.
Mów: Tak mówi Pan BÓG: Oto [jestem] przeciwko tobie, Sydonie, będę uwielbiony pośród ciebie. I poznają, że ja jestem PANEM, gdy wykonam na niego sądy i będę w nim uświęcony.
23 Ndidzatumiza mliri pa iwe ndi kuchititsa magazi kuti ayende mʼmisewu yako. Anthu ophedwa ndi lupanga adzagwa mbali zonse. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
I ześlę na niego zarazę i krew na jego ulice; zranieni upadną pośród niego od miecza, który [spadnie] na nich ze wszystkich stron. I poznają, że ja jestem PANEM.
24 “‘Nthawi imeneyo Aisraeli sadzakhalanso ndi anthu pafupi achipongwe amene ali ngati nthula zowawa ndi ngati minga zopweteka. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
I tak dla domu Izraela nie będzie już kłującego ciernia ani bolesnego kolca spośród wszystkich okolicznych mieszkańców, którzy nim wzgardzili. I poznają, że ja jestem Panem BOGIEM.
25 “‘Ine Ambuye Yehova mawu anga ndi awa: Nditasonkhanitsa Aisraeli kuchoka ku mayiko kumene anamwazikira, ndidzadzionetsa kuti ndine woyera pakati pawo pamaso pa anthu a mitundu ina. Adzakhala mʼdziko lawo, limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo.
Tak mówi Pan BÓG: Gdy zgromadzę dom Izraela spośród narodów, wśród których został rozproszony, i będę w nich uświęcony na oczach pogan, wtedy będą mieszkać w swojej ziemi, którą dałem swemu słudze Jakubowi.
26 Adzakhala kumeneko mwamtendere ndipo adzamanga nyumba ndi kulima minda ya mpesa. Adzakhala kumeneko mwamtendere pamene ndidzalange anthu oyandikana nawo, amene ankawanyoza. Motero iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.’”
I będą w niej mieszkać bezpiecznie, pobudują domy i zasadzą winnice. Będą mieszkać bezpiecznie, gdy wykonam sądy na wszystkich dokoła nich, którzy nimi wzgardzili. I poznają, że ja jestem PANEM, ich Bogiem.