< Ezekieli 28 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
LEUM GOD El kaskas nu sik ac fahk,
2 “Iwe mwana wa munthu, iwuze mfumu ya ku Turo mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, “‘Iwe ndi mtima wako wodzikuza umanena kuti, ‘Ine ndine mulungu; ndimakhala pa mpando wa mulungu pakati pa nyanja.’ Koma ndiwe munthu chabe osati mulungu, ngakhale ukuganiza kuti ndiwe wanzeru ngati mulungu.
“Kom, mwet sukawil moul la, fahkang nu sin leum lun Tyre kas su nga, LEUM GOD Fulatlana, fahk nu sel inge: Ke sripen kom inse fulat, kom sifacna pangon mu god se pa kom. Kom fahk mu kom muta fin sie tron oana sie god, ac acn meoa raunikomla. Kom finne sifacna pangon mu god se pa kom, tusruktu kom mwet se na, ac kom ac fah misa.
3 Taona, ndiwedi wanzeru kupambana Danieli. Ndipo palibe chinsinsi chobisika kwa iwe.
Kom nunku mu kom lalmwetmet lukel Danel, ac wangin ma lukma ku in wikinyukla nu sum.
4 Mwa nzeru zako ndi kumvetsa kwako unadzipezera chuma ndipo unasonkhanitsa golide ndi siliva mʼnyumba zosungira chuma chako.
Ke sripen kom lalmwetmet ac pah in orekma, oru kom kasrup ke gold ac silver.
5 Ndi nzeru zako zochitira malonda unachulukitsa chuma chako ndipo wayamba kunyada chifukwa cha chuma chakocho.
Kom usrnguk in orala inkanek in kuka, ac yokna kapak lom kac. Kom arulana inse fulat ke sripen mwe kasrup lom!
6 “‘Choncho Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Popeza umadziganizira kuti ndiwe mulungu,
“Pa inge ma nga, LEUM GOD Fulatlana, fahk nu sum: Mweyen kom nunku mu kom lalmwetmet oana sie god,
7 Ine ndidzabwera ndi anthu achilendo, anthu ankhanza, kuti adzalimbane nawe. Adzakuthira nkhondo kuti awononge zonse zimene unazipeza ndi nzeru zako, ndipo adzawononga kunyada kwakoko.
nga ac fah use mwet lokoalok sulallal in mweuni kom. Elos ac fah kunausla nufon ma kato ma kom eisla ke inkanek in usrnguk ac lalmwetmet.
8 Iwo adzakuponyera ku dzenje ndipo udzafa imfa yoopsa mʼnyanja yozama.
Elos ac fah unikomi ac siskomla nu inkof uh, su pa ingan kulyuk lom uh.
9 Kodi udzanenabe kuti, ‘Ine ndine mulungu,’ pamaso pa iwo amene akukupha? Iwe udzaoneka kuti ndiwe munthu chabe, osati mulungu, mʼmanja mwa iwo amene akukuphawo.
Ke elos ac tuku in unikomi, ya kom ac srakna fahk mu god se pa kom? Ke kom ac tu ye mutun mwet ma ac unikom uh, kom ac mwet se na ac tiana god se.
10 Udzafa imfa ya anthu osachita mdulidwe mʼmanja mwa anthu achilendo. Ine ndayankhula zimenezi, akutero Ambuye Yehova.’”
Kom ac fah misa oana soko kosro ngalngul inpoun mwetsac su tia etu ke God. Nga, LEUM GOD Fulatlana pa sap in ouinge.”
11 Yehova anandiyankhula kuti:
LEUM GOD El sifilpa kaskas nu sik ac fahk,
12 “Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira mfumu ya Turo ndipo uyiwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, “‘Iwe unali chitsanzo cha ungwiro weniweni, wodzaza ndi nzeru ndi wokongola kwambiri.
“Mwet sukawil, kom in asor ke ongoiya se ma ac sikyak nu sin tokosra lun siti Tyre. Fahkang nu sel kas ma nga, LEUM GOD Fulatlana, fahk inge: Meet kom tuh sie mwe srikasrak ke moul suwohs. Kom tuh arulana lalmwetmet ac oasku!
13 Iwe unkakhala ngati mu Edeni, munda wa Mulungu. Miyala yokongola ya mitundu yonse: rubi, topazi ndi dayimondi, kirisoliti, onikisi, yasipa, safiro, kalineliyoni ndi berili ndiwo inali zofunda zako. Ndipo zoyikamo miyalayo zinali zagolide. Anakupangira zonsezi pa tsiku limene unalengedwa.
Kom tuh muta in acn Eden, ima lun God, ac wulu kain eot saok nukewa: ruby, diamond, topaz, beryl, carnelian, jasper, sapphire, emerald, ac garnet. Oasr mwe walwal gold pac lom. Ma inge tuh akoeyuk nu sum ke len se na ma nga orekomla.
14 Ndinayika kerubi kuti azikulondera. Unkakhala pa phiri langa lopatulika, ndipo unkayendayenda pakati pa miyala ya moto.
Nga filiya sie lipufan na aksangeng ingo in taran kom. Kom tuh muta fineol mutal sik, ac fufahsryesr inmasrlon wek saromrom.
15 Makhalidwe ako anali abwino kuyambira pamene unalengedwa mpaka nthawi imene unayamba kuchita zoyipa.
Ouiya lom tuh suwosna oe ke len se ma orekla kom, nwe ke pacl se kom mutawauk in oru ma koluk.
16 Unatanganidwa ndi zamalonda. Zotsatira zake zinali zoti unachulukitsa zandewu ndi kumachimwa. Choncho ndinakuchotsa ku phiri langa lopatulika. Mkerubi amene ankakulondera uja anakupirikitsa kukuchotsa ku miyala yamoto.
Kom tuh kafofo na ke oru orekma in kuka, ac ma inge kolkomla nu ke sulallal ac orekma koluk. Na pa nga liskomla liki eol mutal sik, ac lipufan se su taran kom el ukwekomyak liki inmasrlon wek saromrom uh.
17 Unkadzikuza mu mtima mwako chifukwa cha kukongola kwako, ndipo unayipitsa nzeru zako chifukwa chofuna kutchuka. Kotero Ine ndinakugwetsa pansi kuti ukhala chenjezo pamaso pa mafumu.
Kom tuh konkin ke oaskuiyom, ac pwengpeng lom uh oru kom orekma in mwet lalfon. Ke sripa inge nga siskomi nu infohk uh, ac oru tuh tokosra ngia in ku in liye kom.
18 Ndi malonda ako achinyengo unachulukitsa machimo ako. Motero unayipitsa malo ako achipembedzo. Choncho ndinabutsa moto pakati pako, ndipo unakupsereza, ndipo unasanduka phulusa pa dziko lapansi pamaso pa anthu onse amene amakuona.
Yokla ma koluk kom oru ke inkanek in kuka lom, pwanang acn in alu lom uh kolukla. Ouinge nga esukak siti uh, nwe ke ma nukewa apatla. Mwet nukewa su liye kom in pacl inge elos liye lah akpusiselyeyuk kom.
19 Anthu onse amitundu amene ankakudziwa akuchita mantha chifukwa cha iwe. Watheratu mochititsa mantha ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.’”
Kom wanginla, wanginla ma pahtpat! Mutunfacl nukewa ma etekom uh elos sangengla, ac sensen elos in sun ongoiya oana kom!”
20 Yehova anandiyankhula nati:
Na LEUM GOD El fahk nu sik,
21 “Iwe mwana wa munthu, utembenukire ku mzinda wa Sidoni ndipo unenere mowudzudzula kuti,
“Mwet sukawil, fahkak kas in palu lain siti Sidon.
22 ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndine mdani wako, iwe Sidoni, ndipo ndidzalemekezedwa chifukwa cha iwe. Anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova ndikadzakulanga ndi kudzionetsa kuti ndine woyera pakati pako.
Fahk nu sin mwet we ma nga, LEUM GOD Fulatlana, fahk kaclos inge: Sidon, nga lain kom. Mwet uh ac fah kaksakinyu ke ma su nga ac oru nu sum uh. Elos ac fah etu lah nga pa LEUM GOD ke nga ac kalyei mwet su muta inmasrlom. Ma inge ac akkalemye lah nga mutal.
23 Ndidzatumiza mliri pa iwe ndi kuchititsa magazi kuti ayende mʼmisewu yako. Anthu ophedwa ndi lupanga adzagwa mbali zonse. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Nga fah supwaot mas upa nu fom, ac oru tuh srah in soror inkanek lom. Un mwet mweun ac fah tuku liki acn nukewa, ac onela mwet lom. Na kom fah etu lah nga pa LEUM GOD.”
24 “‘Nthawi imeneyo Aisraeli sadzakhalanso ndi anthu pafupi achipongwe amene ali ngati nthula zowawa ndi ngati minga zopweteka. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
Na LEUM GOD El fahk, “Wangin sin mutunfacl ma raunela Israel su aksruksrukal meet, ac fah sifilpa oana otonsak ac mwe fahkfuk in akkeokye Israel. Elos ac fah etu lah nga pa LEUM GOD Fulatlana.”
25 “‘Ine Ambuye Yehova mawu anga ndi awa: Nditasonkhanitsa Aisraeli kuchoka ku mayiko kumene anamwazikira, ndidzadzionetsa kuti ndine woyera pakati pawo pamaso pa anthu a mitundu ina. Adzakhala mʼdziko lawo, limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo.
LEUM GOD Fulatlana El fahk, “Nga ac fah folokonma mwet Israel liki facl nukewa su nga akfahsryeloselik nu we, na mutunfacl nukewa ac fah etu lah nga mutal. Mwet Israel elos ac fah muta in facl selos sifacna, su nga tuh sang nu sel Jacob, mwet kulansap luk.
26 Adzakhala kumeneko mwamtendere ndipo adzamanga nyumba ndi kulima minda ya mpesa. Adzakhala kumeneko mwamtendere pamene ndidzalange anthu oyandikana nawo, amene ankawanyoza. Motero iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.’”
Elos ac fah muta we in misla. Elos ac fah musai lohm selos, ac yok ima in grape. Nga fah kalyei mwet tulan lalos su aklokoalokyalos, ac Israel ac fah muta in misla. Na elos fah etu lah nga LEUM GOD lalos.”

< Ezekieli 28 >