< Ezekieli 28 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
La parole de l’Eternel me fut adressée en ces termes:
2 “Iwe mwana wa munthu, iwuze mfumu ya ku Turo mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, “‘Iwe ndi mtima wako wodzikuza umanena kuti, ‘Ine ndine mulungu; ndimakhala pa mpando wa mulungu pakati pa nyanja.’ Koma ndiwe munthu chabe osati mulungu, ngakhale ukuganiza kuti ndiwe wanzeru ngati mulungu.
"Fils de l’homme, dis au souverain de Tyr: Ainsi parle le Seigneur Dieu: Puisque ton coeur s’est exalté, que tu as dit: "Je suis un Dieu, j’occupe une demeure divine au sein des mers," alors que tu n’es qu’un homme et non un Dieu, et puisque tu t’es attribué un coeur pareil au coeur d’un Dieu,
3 Taona, ndiwedi wanzeru kupambana Danieli. Ndipo palibe chinsinsi chobisika kwa iwe.
en vérité, tu es plus sage que Daniel! Aucun secret ne t’échappe;
4 Mwa nzeru zako ndi kumvetsa kwako unadzipezera chuma ndipo unasonkhanitsa golide ndi siliva mʼnyumba zosungira chuma chako.
par ton habileté et ton intelligence tu t’es acquis de la richesse, tu as amassé de l’or et de l’argent dans tes trésors;
5 Ndi nzeru zako zochitira malonda unachulukitsa chuma chako ndipo wayamba kunyada chifukwa cha chuma chakocho.
par ta grande habileté au commerce, tu as multiplié ta fortune, et ton coeur s’est exalté en raison de ta fortune,
6 “‘Choncho Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Popeza umadziganizira kuti ndiwe mulungu,
c’est pourquoi, ainsi parle le Seigneur Dieu: Puisque tu t’es attribué un coeur pareil au coeur d’un Dieu,
7 Ine ndidzabwera ndi anthu achilendo, anthu ankhanza, kuti adzalimbane nawe. Adzakuthira nkhondo kuti awononge zonse zimene unazipeza ndi nzeru zako, ndipo adzawononga kunyada kwakoko.
c’est pourquoi, voici que je vais amener contre toi des étrangers, les plus violents des peuples; ils brandiront l’épée contre ta belle habileté et ils terniront ta splendeur.
8 Iwo adzakuponyera ku dzenje ndipo udzafa imfa yoopsa mʼnyanja yozama.
Ils te feront descendre à la fosse, et tu mourras de mort violente au sein des mers.
9 Kodi udzanenabe kuti, ‘Ine ndine mulungu,’ pamaso pa iwo amene akukupha? Iwe udzaoneka kuti ndiwe munthu chabe, osati mulungu, mʼmanja mwa iwo amene akukuphawo.
Oseras-tu dire encore: "Je suis un Dieu", en face de tes meurtriers? Mais tu n’es qu’un homme et non un Dieu entre les mains de ceux qui te blessent à mort.
10 Udzafa imfa ya anthu osachita mdulidwe mʼmanja mwa anthu achilendo. Ine ndayankhula zimenezi, akutero Ambuye Yehova.’”
Tu mourras de la mort des incirconcis par la main des étrangers, car c’est 'moi qui parle, dit le Seigneur Dieu."
11 Yehova anandiyankhula kuti:
La parole de l’Éternel me fut adressée en ces termes:
12 “Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira mfumu ya Turo ndipo uyiwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, “‘Iwe unali chitsanzo cha ungwiro weniweni, wodzaza ndi nzeru ndi wokongola kwambiri.
"Fils de l’homme, entonne une élégie sur le roi de Tyr; tu lui diras: Ainsi parle le Seigneur Dieu: Tu étais le sceau de la perfection, plein d’habileté et d’une beauté achevée.
13 Iwe unkakhala ngati mu Edeni, munda wa Mulungu. Miyala yokongola ya mitundu yonse: rubi, topazi ndi dayimondi, kirisoliti, onikisi, yasipa, safiro, kalineliyoni ndi berili ndiwo inali zofunda zako. Ndipo zoyikamo miyalayo zinali zagolide. Anakupangira zonsezi pa tsiku limene unalengedwa.
Tu étais dans l’Eden, le jardin de Dieu; toutes les pierres précieuses te couvraient: rubis, topaze et émeraude, tartessienne, onyx et jaspe, saphir, escarboucle et diamant, de l’or également; tu possédais des tambourins et des flûtes bien travaillés; pour toi, ils étaient prêts dès le jour de ta naissance.
14 Ndinayika kerubi kuti azikulondera. Unkakhala pa phiri langa lopatulika, ndipo unkayendayenda pakati pa miyala ya moto.
Tu étais le Keroub d’élection qui protège de ses ailes; je t’avais posté et tu étais sur la montagne sainte de Dieu; au milieu des pierres de feu, tu circulais.
15 Makhalidwe ako anali abwino kuyambira pamene unalengedwa mpaka nthawi imene unayamba kuchita zoyipa.
Tu fus irréprochable dans ta conduite depuis le jour où tu fus créé jusqu’à ce que la perversité se rencontrât en toi.
16 Unatanganidwa ndi zamalonda. Zotsatira zake zinali zoti unachulukitsa zandewu ndi kumachimwa. Choncho ndinakuchotsa ku phiri langa lopatulika. Mkerubi amene ankakulondera uja anakupirikitsa kukuchotsa ku miyala yamoto.
Par l’activité de ton trafic, ton enceinte s’est remplie de violence, et tu es devenu coupable; je t’ai donc rejeté de la montagne de Dieu et je t’ai fait disparaître, Keroub protecteur, d’entre les pierres de feu.
17 Unkadzikuza mu mtima mwako chifukwa cha kukongola kwako, ndipo unayipitsa nzeru zako chifukwa chofuna kutchuka. Kotero Ine ndinakugwetsa pansi kuti ukhala chenjezo pamaso pa mafumu.
Ton coeur s’était exalté à cause de ta beauté, et tu avais ruiné ta sagesse par ton faste; je t’ai donc précipité à terre, devant des rois je t’ai exposé, pour leur être en spectacle.
18 Ndi malonda ako achinyengo unachulukitsa machimo ako. Motero unayipitsa malo ako achipembedzo. Choncho ndinabutsa moto pakati pako, ndipo unakupsereza, ndipo unasanduka phulusa pa dziko lapansi pamaso pa anthu onse amene amakuona.
Par l’excès de tes fautes, par l’iniquité de ton trafic, tu as profané tes sanctuaires; aussi ai-je fait surgir du milieu de toi, un feu, qui t’a consumé, et je t’ai réduit en cendres sur la terre, aux yeux de tous ceux qui te regardent.
19 Anthu onse amitundu amene ankakudziwa akuchita mantha chifukwa cha iwe. Watheratu mochititsa mantha ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.’”
Tous ceux qui te connaissent parmi les nations sont stupéfaits à cause de toi: tu es devenu un néant, ç’en est fini de toi pour toujours."
20 Yehova anandiyankhula nati:
La parole de l’Éternel me fut adressée en ces termes:
21 “Iwe mwana wa munthu, utembenukire ku mzinda wa Sidoni ndipo unenere mowudzudzula kuti,
"Fils de l’homme, tourne ta face vers Sidon et prophétise sur elle.
22 ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndine mdani wako, iwe Sidoni, ndipo ndidzalemekezedwa chifukwa cha iwe. Anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova ndikadzakulanga ndi kudzionetsa kuti ndine woyera pakati pako.
Tu diras: Ainsi parle le Seigneur Dieu: Voici que je m’en prends à toi, Sidon, je veux me rendre glorieux au milieu de toi. L’On saura que je suis l’Éternel, quand je lui infligerai des châtiments et que j’y manifesterai ma sainteté.
23 Ndidzatumiza mliri pa iwe ndi kuchititsa magazi kuti ayende mʼmisewu yako. Anthu ophedwa ndi lupanga adzagwa mbali zonse. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
J’Enverrai contre elle la peste et l’effusion de sang dans ses rues, les morts joncheront son sol, frappés par le glaive qui l’atteindra de toutes parts, et ils sauront que je suis l’Eternel.
24 “‘Nthawi imeneyo Aisraeli sadzakhalanso ndi anthu pafupi achipongwe amene ali ngati nthula zowawa ndi ngati minga zopweteka. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
Et il n’y aura plus pour la maison d’Israël de ronce cuisante ni d’épine douloureuse parmi tous ses voisins d’alentour qui le traitent avec mépris, et on saura que je suis le Seigneur Dieu."
25 “‘Ine Ambuye Yehova mawu anga ndi awa: Nditasonkhanitsa Aisraeli kuchoka ku mayiko kumene anamwazikira, ndidzadzionetsa kuti ndine woyera pakati pawo pamaso pa anthu a mitundu ina. Adzakhala mʼdziko lawo, limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo.
Ainsi parle le Seigneur Dieu: "Quand je rassemblerai la maison d’Israël d’entre les peuples chez qui ils ont été dispersés, je me sanctifierai par eux aux yeux des nations, et ils demeureront sur le territoire que j’ai donné à mon serviteur Jacob.
26 Adzakhala kumeneko mwamtendere ndipo adzamanga nyumba ndi kulima minda ya mpesa. Adzakhala kumeneko mwamtendere pamene ndidzalange anthu oyandikana nawo, amene ankawanyoza. Motero iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.’”
Ils y demeureront en sécurité, ils bâtiront des maisons, planteront des vignes et demeureront en sécurité, parce que je ferai justice de tous leurs contempteurs d’alentour, et ils reconnaîtront que moi, l’Eternel, je suis leur Dieu."

< Ezekieli 28 >