< Ezekieli 27 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
La parole de Yahvé me fut adressée de nouveau, en ces termes:
2 “Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira Turo.
« Toi, fils de l'homme, élève une complainte sur Tyr;
3 Uza Turo, mzinda wokhala pa dooko la nyanja, wochita malonda ndi anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja kuti: Ambuye Yehova akuti, “Iwe Turo, umanena kuti, ‘Ndine wokongola kwambiri.’
et dis à Tyr: « Toi qui habites à l'entrée de la mer, toi qui es le marchand des peuples dans de nombreuses îles, le Seigneur Yahvé dit: « Toi, Tyr, tu as dit, « Je suis d'une beauté parfaite.
4 Malire ako anali mʼkati mwenimweni mwa nyanja; amisiri ako anakukongoletsa kwambiri.
Tes frontières sont au cœur des mers. Tes bâtisseurs ont perfectionné ta beauté.
5 Anakupanga ndi matabwa a payini ochokera ku Seniri; anatenga mikungudza ya ku Lebanoni kupangira mlongoti wako.
On a fait toutes tes planches avec des cyprès de Senir. Ils ont pris un cèdre du Liban pour te faire un mât.
6 Ndi mitengo ya thundu ya ku Basani anapanga zopalasira zako; ndi matabwa a mitengo ya payini yochokera ku zilumba za Kitimu. Pakuti anapanga thandala lako pakati pa matabwawo panali minyanga ya njovu.
Ils ont fait tes rames avec des chênes de Basan. Ils ont fait tes bancs en ivoire incrusté dans du bois de cyprès des îles de Kittim.
7 Nsalu yabafuta yopeta yochokera ku Igupto inali thanga yako, ndipo inakhala ngati mbendera. Nsalu zophimba matenti ako zinali za mtundu wamtambo ndi pepo zochokera ku zilumba za Elisa.
Ta voile était de fin lin brodé d'Égypte, qu'elle puisse être pour vous une bannière. Le bleu et le violet des îles d'Elishah étaient votre auvent.
8 Anthu a ku Sidoni ndi Arivadi ndi amene anali opalasa ako. Anthu aluso ako, iwe Turo, anali mwa iwe ndiwo amene ankakuyendetsa.
Les habitants de Sidon et d'Arvad étaient tes rameurs. Tes sages, Tyr, étaient en toi. C'étaient vos pilotes.
9 Akuluakulu ndi eni luso a ku Gebala anali mʼkati mwako, ngati okonza zibowo zako. Sitima za pa nyanja zonse, ndi oyendetsa ake ankabwera pamodzi ndi katundu kudzachita nawe malonda.
Les vieillards de Gebal et ses sages étaient vos réparateurs de coutures de navires en vous. Tous les navires de la mer et leurs marins étaient en toi. pour traiter votre marchandise.
10 “Anthu a ku Perisiya, a ku Ludi ndi Puti anali asilikali mʼgulu lako la nkhondo. Iwo ankapachika zishango ndi zipewa zawo zankhondo pa makoma ako, kubweretsa kwa iwe ulemerero.
"''La Perse, Lud et Put étaient dans ton armée, vos hommes de guerre. Ils ont accroché le bouclier et le casque en vous. Ils ont montré votre beauté.
11 Anthu a ku Arivadi ndi Heleki ankalondera mbali zonse za mpanda wako; anthu a ku Gamadi anali mu nsanja zako, Iwo ankapachika zishango zawo pa makoma ako onse. Amenewo ndiwo anakukongoletsa kwambiri.
Les hommes d'Arvad avec ton armée étaient sur tes murs tout autour, et des hommes vaillants étaient dans tes tours. Ils ont accroché leurs boucliers sur vos murs tout autour. Ils ont perfectionné votre beauté.
12 “Dziko la Tarisisi linachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako wamtundumtundu. Iwo ankapereka siliva, chitsulo, chitini ndi mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
"''Tarsis était ton marchand en raison de la multitude de richesses de toutes sortes. Ils échangeaient pour tes marchandises de l'argent, du fer, de l'étain et du plomb.
13 “Yavani, Tubala ndi Mesaki ankachita nawe malonda; iwo ankapereka akapolo ndi ziwiya za mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
"''Javan, Tubal et Meshech étaient tes commerçants. Ils échangeaient des personnes et des objets d'airain contre tes marchandises.
14 “Anthu a ku Beti Togarima ankapereka akavalo antchito, akavalo ankhondo ndi abulu mosinthanitsa ndi katundu wako.
"''Les gens de la maison de Togarma ont échangé vos marchandises avec des chevaux, des chevaux de guerre et des mules.
15 “Anthu a ku Dedani ankachita nawe malonda, ndipo anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja anali ogula malonda ako. Ankakupatsa minyanga ya njovu ndi phingo.
"''Les hommes de Dedan ont fait du commerce avec toi. De nombreuses îles ont été le marché de ta main. Ils vous ont apporté en échange des cornes d'ivoire et d'ébène.
16 “Anthu a ku Aramu ankachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa zinthu zako. Iwo ankapereka miyala ya emeradi, nsalu zapepo, nsalu zopetapeta, nsalu zabafuta, korali ndi miyala ya rubi mosinthanitsa ndi katundu wako.
"''La Syrie était ton marchand en raison de la multitude de tes ouvrages. Ils ont échangé pour tes marchandises des émeraudes, de la pourpre, des broderies, du lin fin, du corail et des rubis.
17 “Yuda ndi Israeli ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka tirigu ochokera ku Miniti ndi zokometsera zakudya, uchi, mafuta ndi mankhwala mosinthanitsa ndi katundu wako.
"''Juda et le pays d'Israël étaient vos commerçants. Ils échangeaient contre vos marchandises du blé de Minnith, des confiseries, du miel, de l'huile et du baume.
18 “Anthu a ku Damasiko, chifukwa cha zinthu zako za malonda zambiri ndi katundu wako wosiyanasiyana, ankachita nawe malonda a vinyo wochokera ku Heliboni ndi ubweya wankhosa ochokera ku Zahari.
"''Damas a été ton marchand pour la multitude de tes ouvrages, à cause de la multitude de richesses de toutes sortes, avec le vin d'Helbon et la laine blanche.
19 Adani ndi Agriki ochokera ku Uzala ankagula katundu wako. Iwo ankapereka chitsulo chosalala, kasiya ndi bango lonunkhira mosinthanitsa ndi katundu wako.
"''Vedan et Javan ont échangé avec le fil pour vos marchandises; le fer forgé, la casse et le calame étaient parmi vos marchandises.
20 “Anthu a ku Dedani ankakugulitsa nsalu zoyika pa zishalo za akavalo.
"''Dedan était votre marchand de précieuses couvertures de selle pour l'équitation.
21 “Arabiya ndi mafumu onse a ku Kedara anali ogula malonda ako. Iwo ankachita nawe malonda a ana ankhosa onenepa, nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
"''L'Arabie et tous les princes de Kédar étaient vos marchands préférés d'agneaux, de béliers et de chèvres. En cela, ils étaient vos marchands.
22 “Anthu amalonda a ku Seba ndi Raama ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka zonunkhira zosiyanasiyana zabwino kwambiri, miyala yokongola ndi golide mosinthanitsa ndi katundu wako.
"''Les commerçants de Saba et de Rama étaient vos commerçants. Ils échangeaient pour vos marchandises avec les meilleures de toutes les épices, toutes les pierres précieuses et l'or.
23 “Amalonda a ku Harani, Kane, Edeni, Seba, Asuri ndi Kilimadi ankachita nawe malonda.
"''Haran, Canneh, Eden, les marchands de Saba, Asshur et Chilmad, étaient tes marchands.
24 Iwowa ankasinthanitsana nawe zovala zokongola, nsalu zopetapeta, zoyala pansi za mawangamawanga, atazimanga bwino ndi zingwe zolimba.
Ils étaient tes marchands d'articles de choix, d'étoffes bleues et brodées, de coffres de cèdre, de riches vêtements liés par des cordes, parmi tes marchandises.
25 “Sitima za pa madzi za ku Tarisisi zinali zonyamula malonda ako. Motero iwe uli ngati sitima yapamadzi yodzaza ndi katundu wolemera.
"« Les navires de Tarsis étaient vos caravanes pour vos marchandises. Vous avez été réapprovisionné et rendu très glorieux au cœur des mers.
26 Anthu opalasa ako amakupititsa pa nyanja yozama. Koma mphepo yakummawa idzakuthyolathyola pakati pa nyanja.
Tes rameurs t'ont fait entrer dans de grandes eaux. Le vent d'est vous a brisé au cœur des mers.
27 Chuma chako, katundu wako, malonda ako, okuyendetsa ako, okuwongolera ako ndi opanga sitima za pa madzi, anthu ako amalonda ndi asilikali ako onse ndiponso aliyense amene ali mʼmenemo adzamira mʼnyanja tsiku limene udzawonongeka.
Vos richesses, vos biens, vos marchandises, vos marins, vos pilotes, vos réparateurs de coutures de navires, les revendeurs de votre marchandise, et tous vos hommes de guerre qui sont en vous, avec toute votre compagnie qui est parmi vous, tombera dans le cœur des mers au jour de ta ruine.
28 Madera a mʼmbali mwa nyanja adzagwedezeka chifukwa cha kufuwula kwa oyendetsa sitimawo.
Au son du cri de tes pilotes, les pâturages vont trembler.
29 Onse amene amapalasa sitima zapamadzi, adzatuluka mʼsitima zawo; oyendetsa ndi onse owongolera sitima zapamadzi adzayimirira mʼmbali mwa nyanja.
Tous ceux qui manient les rames, les marins et tous les pilotes de la mer, descendront de leurs vaisseaux. Ils se tiendront sur la terre,
30 Iwo akufuwula, kukulira iwe kwambiri; akudzithira fumbi kumutu, ndi kudzigubuduza pa phulusa.
et fera entendre sa voix sur vous, et pleurera amèrement. Ils jetteront de la poussière sur leurs têtes. Ils se vautreront dans les cendres.
31 Akumeta mpala mitu yawo chifukwa cha iwe ndipo akuvala ziguduli. Akukulira iweyo ndi mitima yowawa kwambiri.
Ils se rendront chauves pour toi, et se vêtir de sacs. Ils pleureront pour vous dans l'amertume de l'âme, avec un deuil amer.
32 Akuyimba nyimbo yokudandaulira nʼkumati: ‘Ndani anawonongedwapo ngati Turo pakati pa nyanja?’
Dans leurs gémissements, ils se lamenteront sur toi, et se lamenter sur vous, en disant, « Qui est là comme Tyr? comme celle qui est amenée au silence au milieu de la mer?
33 Pamene malonda ako ankawoloka nyanja unakhutitsa mitundu yambiri ya anthu. Mafumu a dziko lapansi analemera ndi chuma chako komanso ndi malonda ako.
Quand tes marchandises venaient des mers, tu as rempli de nombreux peuples. Tu as enrichi les rois de la terre avec la multitude de vos richesses et de vos marchandises.
34 Koma tsopano wathyokera mʼnyanja, pansi penipeni pa nyanja. Katundu wako ndi onse amene anali nawe amira pamodzi nawe.
Au temps où tu étais brisé par les mers, dans les profondeurs des eaux, votre marchandise et toute votre société sont tombées en vous.
35 Onse amene amakhala mʼmbali mwa nyanja aopsedwa ndi zimene zakuchitikira. Mafumu awo akuchita mantha ndipo nkhope zangoti khululu.
Tous les habitants des îles s'étonnent de toi, et leurs rois ont horriblement peur. Ils sont troublés dans leur visage.
36 Anthu amalonda a mitundu ina akukunyogodola. Watha mochititsa mantha ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.”
Les marchands parmi les peuples te sifflent. Vous avez connu une fin terrible, et vous ne serez plus. »'"

< Ezekieli 27 >