< Ezekieli 27 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
The word of the LORD came again to me, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira Turo.
"You, son of man, take up a lamentation over Tyre;
3 Uza Turo, mzinda wokhala pa dooko la nyanja, wochita malonda ndi anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja kuti: Ambuye Yehova akuti, “Iwe Turo, umanena kuti, ‘Ndine wokongola kwambiri.’
and tell Tyre, 'You who dwell at the entry of the sea, who are the merchant of the peoples to many islands, thus says the LORD: "You, Tyre, have said, 'I am perfect in beauty.'
4 Malire ako anali mʼkati mwenimweni mwa nyanja; amisiri ako anakukongoletsa kwambiri.
Your borders are in the heart of the seas; your builders have perfected your beauty.
5 Anakupanga ndi matabwa a payini ochokera ku Seniri; anatenga mikungudza ya ku Lebanoni kupangira mlongoti wako.
They have made all your planks of fir trees from Senir; they have taken a cedar from Lebanon to make a mast for you.
6 Ndi mitengo ya thundu ya ku Basani anapanga zopalasira zako; ndi matabwa a mitengo ya payini yochokera ku zilumba za Kitimu. Pakuti anapanga thandala lako pakati pa matabwawo panali minyanga ya njovu.
Of the oaks of Bashan have they made your oars; they have made your deck with cypress wood inlaid with ivory, from the islands of Kittim.
7 Nsalu yabafuta yopeta yochokera ku Igupto inali thanga yako, ndipo inakhala ngati mbendera. Nsalu zophimba matenti ako zinali za mtundu wamtambo ndi pepo zochokera ku zilumba za Elisa.
Of fine linen with embroidered work from Egypt was your sail, that it might be to you for a banner; blue and purple from the islands of Elishah was your awning.
8 Anthu a ku Sidoni ndi Arivadi ndi amene anali opalasa ako. Anthu aluso ako, iwe Turo, anali mwa iwe ndiwo amene ankakuyendetsa.
The inhabitants of Sidon and Arvad were your rowers: your wise men, Tyre, were in you, they were your pilots.
9 Akuluakulu ndi eni luso a ku Gebala anali mʼkati mwako, ngati okonza zibowo zako. Sitima za pa nyanja zonse, ndi oyendetsa ake ankabwera pamodzi ndi katundu kudzachita nawe malonda.
The old men of Gebal and the wise men of it were in you your repairers of ship seams: all the ships of the sea with their mariners were in you to deal in your merchandise.
10 “Anthu a ku Perisiya, a ku Ludi ndi Puti anali asilikali mʼgulu lako la nkhondo. Iwo ankapachika zishango ndi zipewa zawo zankhondo pa makoma ako, kubweretsa kwa iwe ulemerero.
Persia and Lud and Put were in your army, your men of war: they hanged the shield and helmet in you; they set forth your comeliness.
11 Anthu a ku Arivadi ndi Heleki ankalondera mbali zonse za mpanda wako; anthu a ku Gamadi anali mu nsanja zako, Iwo ankapachika zishango zawo pa makoma ako onse. Amenewo ndiwo anakukongoletsa kwambiri.
The men of Arvad with your army were on your walls all around, and valorous men were in your towers; they hanged their shields on your walls all around; they have perfected your beauty.
12 “Dziko la Tarisisi linachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako wamtundumtundu. Iwo ankapereka siliva, chitsulo, chitini ndi mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
Tarshish was your merchant by reason of the multitude of all kinds of riches; with silver, iron, tin, and lead, they traded for your wares.
13 “Yavani, Tubala ndi Mesaki ankachita nawe malonda; iwo ankapereka akapolo ndi ziwiya za mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
Javan, Tubal, and Meshech, they were your traffickers; they traded the persons of men and vessels of bronze for your merchandise.
14 “Anthu a ku Beti Togarima ankapereka akavalo antchito, akavalo ankhondo ndi abulu mosinthanitsa ndi katundu wako.
They of the house of Togarmah traded for your wares with horses and war horses and mules.
15 “Anthu a ku Dedani ankachita nawe malonda, ndipo anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja anali ogula malonda ako. Ankakupatsa minyanga ya njovu ndi phingo.
The men of Dedan were your traffickers; many islands were the market of your hand: they brought you in exchange horns of ivory and ebony.
16 “Anthu a ku Aramu ankachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa zinthu zako. Iwo ankapereka miyala ya emeradi, nsalu zapepo, nsalu zopetapeta, nsalu zabafuta, korali ndi miyala ya rubi mosinthanitsa ndi katundu wako.
Aram was your merchant by reason of the multitude of your handiworks: they traded for your wares with emeralds, purple, and embroidered work, and fine linen, and coral, and rubies.
17 “Yuda ndi Israeli ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka tirigu ochokera ku Miniti ndi zokometsera zakudya, uchi, mafuta ndi mankhwala mosinthanitsa ndi katundu wako.
Judah, and the land of Israel, they were your traffickers: they traded for your merchandise wheat of Minnith, and confections, and honey, and oil, and balm.
18 “Anthu a ku Damasiko, chifukwa cha zinthu zako za malonda zambiri ndi katundu wako wosiyanasiyana, ankachita nawe malonda a vinyo wochokera ku Heliboni ndi ubweya wankhosa ochokera ku Zahari.
Damascus was your merchant for the multitude of your handiworks, by reason of the multitude of all kinds of riches, with the wine of Helbon, and white wool.
19 Adani ndi Agriki ochokera ku Uzala ankagula katundu wako. Iwo ankapereka chitsulo chosalala, kasiya ndi bango lonunkhira mosinthanitsa ndi katundu wako.
Vedan and Javan traded with yarn for your wares: bright iron, cassia, and calamus, were among your merchandise.
20 “Anthu a ku Dedani ankakugulitsa nsalu zoyika pa zishalo za akavalo.
Dedan was your trafficker in precious cloths for riding.
21 “Arabiya ndi mafumu onse a ku Kedara anali ogula malonda ako. Iwo ankachita nawe malonda a ana ankhosa onenepa, nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
Arabia, and all the princes of Kedar, they were the merchants of your hand; in lambs, and rams, and goats, in these were they your merchants.
22 “Anthu amalonda a ku Seba ndi Raama ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka zonunkhira zosiyanasiyana zabwino kwambiri, miyala yokongola ndi golide mosinthanitsa ndi katundu wako.
The traffickers of Sheba and Raamah, they were your traffickers; they traded for your wares with the chief of all spices, and with all precious stones, and gold.
23 “Amalonda a ku Harani, Kane, Edeni, Seba, Asuri ndi Kilimadi ankachita nawe malonda.
Haran and Canneh and Eden, the traffickers of Sheba, Asshur and Chilmad, were your traffickers.
24 Iwowa ankasinthanitsana nawe zovala zokongola, nsalu zopetapeta, zoyala pansi za mawangamawanga, atazimanga bwino ndi zingwe zolimba.
These were your traffickers in choice wares, in wrappings of blue and embroidered work, and in chests of rich clothing, bound with cords and made of cedar, among your merchandise.
25 “Sitima za pa madzi za ku Tarisisi zinali zonyamula malonda ako. Motero iwe uli ngati sitima yapamadzi yodzaza ndi katundu wolemera.
The ships of Tarshish were your caravans for your merchandise: and you were replenished, and made very glorious in the heart of the seas.
26 Anthu opalasa ako amakupititsa pa nyanja yozama. Koma mphepo yakummawa idzakuthyolathyola pakati pa nyanja.
"'"Your rowers have brought you into great waters: the east wind has broken you in the heart of the seas.
27 Chuma chako, katundu wako, malonda ako, okuyendetsa ako, okuwongolera ako ndi opanga sitima za pa madzi, anthu ako amalonda ndi asilikali ako onse ndiponso aliyense amene ali mʼmenemo adzamira mʼnyanja tsiku limene udzawonongeka.
Your riches, and your wares, your merchandise, your mariners, and your pilots, your repairers of ship seams, and the dealers in your merchandise, and all your men of war, who are in you, with all your company which is in the midst of you, shall fall into the heart of the seas in the day of your ruin.
28 Madera a mʼmbali mwa nyanja adzagwedezeka chifukwa cha kufuwula kwa oyendetsa sitimawo.
At the sound of the cry of your pilots the suburbs shall shake.
29 Onse amene amapalasa sitima zapamadzi, adzatuluka mʼsitima zawo; oyendetsa ndi onse owongolera sitima zapamadzi adzayimirira mʼmbali mwa nyanja.
All who handled the oar, the mariners, and all the pilots of the sea, shall come down from their ships; they shall stand on the land,
30 Iwo akufuwula, kukulira iwe kwambiri; akudzithira fumbi kumutu, ndi kudzigubuduza pa phulusa.
and shall cause their voice to be heard over you, and shall cry bitterly, and shall cast up dust on their heads, they shall wallow themselves in the ashes:
31 Akumeta mpala mitu yawo chifukwa cha iwe ndipo akuvala ziguduli. Akukulira iweyo ndi mitima yowawa kwambiri.
and they shall make themselves bald for you, and clothe them with sackcloth, and they shall weep for you in bitterness of soul with bitter mourning.
32 Akuyimba nyimbo yokudandaulira nʼkumati: ‘Ndani anawonongedwapo ngati Turo pakati pa nyanja?’
In their wailing they shall take up a lamentation for you, and lament over you, saying, 'Who is there like Tyre, like her who is brought to silence in the midst of the sea?'
33 Pamene malonda ako ankawoloka nyanja unakhutitsa mitundu yambiri ya anthu. Mafumu a dziko lapansi analemera ndi chuma chako komanso ndi malonda ako.
When your wares went forth out of the seas, you filled many peoples; you enriched the kings of the earth with the multitude of your riches and of your merchandise.
34 Koma tsopano wathyokera mʼnyanja, pansi penipeni pa nyanja. Katundu wako ndi onse amene anali nawe amira pamodzi nawe.
In the time that you were broken by the seas in the depths of the waters, your merchandise and all your company fell in your midst.
35 Onse amene amakhala mʼmbali mwa nyanja aopsedwa ndi zimene zakuchitikira. Mafumu awo akuchita mantha ndipo nkhope zangoti khululu.
All the inhabitants of the islands are astonished at you, and their kings are horribly afraid; they are troubled in their face.
36 Anthu amalonda a mitundu ina akukunyogodola. Watha mochititsa mantha ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.”
The merchants among the peoples hiss at you; you are become a terror, and you shall nevermore have any being."'"

< Ezekieli 27 >