< Ezekieli 27 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
HERRENs Ord kom til mig således:
2 “Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira Turo.
Du, Menneskesøn, istem en Klagesang over Tyrus og sig til Tyrus,
3 Uza Turo, mzinda wokhala pa dooko la nyanja, wochita malonda ndi anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja kuti: Ambuye Yehova akuti, “Iwe Turo, umanena kuti, ‘Ndine wokongola kwambiri.’
som ligger ved Adgangen til Havet og driver Handel med Folkeslagene på de mange fjerne Strande: Så siger den Herre HERREN: Tyrus, du siger: "Fuldendt i Skønhed er jeg!"
4 Malire ako anali mʼkati mwenimweni mwa nyanja; amisiri ako anakukongoletsa kwambiri.
De bygged dig midt i Havet, fuldendte din Skønhed.
5 Anakupanga ndi matabwa a payini ochokera ku Seniri; anatenga mikungudza ya ku Lebanoni kupangira mlongoti wako.
De tømred af Senircypresser hver Planke i dig, fra Libanon hented de Cedre at lave din Mast,
6 Ndi mitengo ya thundu ya ku Basani anapanga zopalasira zako; ndi matabwa a mitengo ya payini yochokera ku zilumba za Kitimu. Pakuti anapanga thandala lako pakati pa matabwawo panali minyanga ya njovu.
af Basans højeste Ege skar de dig Årer, de lagde dit Dæk af Fyr fra Kittæernes Strande;
7 Nsalu yabafuta yopeta yochokera ku Igupto inali thanga yako, ndipo inakhala ngati mbendera. Nsalu zophimba matenti ako zinali za mtundu wamtambo ndi pepo zochokera ku zilumba za Elisa.
dit Sejl var ægyptisk Byssus i broget Væv, dit Tag var Purpur i blåt og rødt fra Elisjas Strande.
8 Anthu a ku Sidoni ndi Arivadi ndi amene anali opalasa ako. Anthu aluso ako, iwe Turo, anali mwa iwe ndiwo amene ankakuyendetsa.
Zidons og Arvads Folk var Rorkarle for dig, om Bord var de kyndigste i Zarepta, de var dine Styrmænd,
9 Akuluakulu ndi eni luso a ku Gebala anali mʼkati mwako, ngati okonza zibowo zako. Sitima za pa nyanja zonse, ndi oyendetsa ake ankabwera pamodzi ndi katundu kudzachita nawe malonda.
de ældste og kyndigste i Gebal, de bøded din Læk. Alle Havets Skibe med Søfolk var hos dig for at omsætte dine Varer.
10 “Anthu a ku Perisiya, a ku Ludi ndi Puti anali asilikali mʼgulu lako la nkhondo. Iwo ankapachika zishango ndi zipewa zawo zankhondo pa makoma ako, kubweretsa kwa iwe ulemerero.
Folk fra Persien, Lydien og Put var i din Hær som Krigsfolk, de ophængte Skjolde og Hjelme i dig; de gav dig Glans.
11 Anthu a ku Arivadi ndi Heleki ankalondera mbali zonse za mpanda wako; anthu a ku Gamadi anali mu nsanja zako, Iwo ankapachika zishango zawo pa makoma ako onse. Amenewo ndiwo anakukongoletsa kwambiri.
Arvaditerne og deres Hær stod rundt på dine Mure, Gammaditerne på dine Tårne; de ophængte deres Skjolde rundt på dine Mure, de fuldendte din Skønhed.
12 “Dziko la Tarisisi linachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako wamtundumtundu. Iwo ankapereka siliva, chitsulo, chitini ndi mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
Tarsis var din Handelsven, fordi du havde alskens Gods i Mængde; Sølv, Jern, Tin og Bly gav de dig for dine Varer.
13 “Yavani, Tubala ndi Mesaki ankachita nawe malonda; iwo ankapereka akapolo ndi ziwiya za mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
Javan, Tubal og Mesjek drev Handel med dig; Trælle og Kobberkar gav de dig i Bytte.
14 “Anthu a ku Beti Togarima ankapereka akavalo antchito, akavalo ankhondo ndi abulu mosinthanitsa ndi katundu wako.
Togarmas Hus gav dig Køreheste, Rideheste og Muldyr for dine Varer.
15 “Anthu a ku Dedani ankachita nawe malonda, ndipo anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja anali ogula malonda ako. Ankakupatsa minyanga ya njovu ndi phingo.
Rodosboerne drev Handel med dig, mange fjerne Strande var dine Handelsvenner; Elfenben og Ibenholt bragte de dig som Vederlag.
16 “Anthu a ku Aramu ankachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa zinthu zako. Iwo ankapereka miyala ya emeradi, nsalu zapepo, nsalu zopetapeta, nsalu zabafuta, korali ndi miyala ya rubi mosinthanitsa ndi katundu wako.
Edom var din Handelsven, fordi du havde Varer i Mængde; Karfunkler, Purpur, brogede Tøjer, fint Linned, Koraller og Rubiner gav de dig for dine Varer.
17 “Yuda ndi Israeli ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka tirigu ochokera ku Miniti ndi zokometsera zakudya, uchi, mafuta ndi mankhwala mosinthanitsa ndi katundu wako.
Juda og Israels Land drev Handel med dig; Hvede fra Minnit, Bagværk, Honning, Olie og Mastiksbalsam gav de dig i Bytte.
18 “Anthu a ku Damasiko, chifukwa cha zinthu zako za malonda zambiri ndi katundu wako wosiyanasiyana, ankachita nawe malonda a vinyo wochokera ku Heliboni ndi ubweya wankhosa ochokera ku Zahari.
Damaskus var din Handelsven fordi du havde alskens Gods i Mængde; de kom med Vin fra Helbon og Uld fra Zahar.
19 Adani ndi Agriki ochokera ku Uzala ankagula katundu wako. Iwo ankapereka chitsulo chosalala, kasiya ndi bango lonunkhira mosinthanitsa ndi katundu wako.
Vedan og Javan gav Sager fra Uzal for dine Varer; smeddet Jern, Hassia og Kalmus fik du i Bytte.
20 “Anthu a ku Dedani ankakugulitsa nsalu zoyika pa zishalo za akavalo.
Dedan drev Handel med dig med Sadeldækkener til Ridning.
21 “Arabiya ndi mafumu onse a ku Kedara anali ogula malonda ako. Iwo ankachita nawe malonda a ana ankhosa onenepa, nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
Araberne og alle Kedars Fyrster var dine Hardelsvenner; med Lam, Vædre og Bukke handlede de med dig.
22 “Anthu amalonda a ku Seba ndi Raama ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka zonunkhira zosiyanasiyana zabwino kwambiri, miyala yokongola ndi golide mosinthanitsa ndi katundu wako.
Sabas og Ramas Handelsfolk drev Handel med dig; den allerfineste Balsam, alle Slags Ædelsten og Guld gav de dig for dine Varer.
23 “Amalonda a ku Harani, Kane, Edeni, Seba, Asuri ndi Kilimadi ankachita nawe malonda.
Karan, Kanne og Eden, Assyrerne og hele Medien drev Handel med dig;
24 Iwowa ankasinthanitsana nawe zovala zokongola, nsalu zopetapeta, zoyala pansi za mawangamawanga, atazimanga bwino ndi zingwe zolimba.
de handlede med dig med smukke Klæder, Purpurkapper, brogede Tøjer, farvede Tæpper, tvundet og fastsnoet Reb på dine Markeder;
25 “Sitima za pa madzi za ku Tarisisi zinali zonyamula malonda ako. Motero iwe uli ngati sitima yapamadzi yodzaza ndi katundu wolemera.
Tarsisskibene tjente dig ved din Omsætning. Du fyldtes, blev såre tung midt ude i Havet.
26 Anthu opalasa ako amakupititsa pa nyanja yozama. Koma mphepo yakummawa idzakuthyolathyola pakati pa nyanja.
I rum Sø fik de dig ud, dine roende Mænd; da knuste en Østenstorm dig midt ude på Havet;
27 Chuma chako, katundu wako, malonda ako, okuyendetsa ako, okuwongolera ako ndi opanga sitima za pa madzi, anthu ako amalonda ndi asilikali ako onse ndiponso aliyense amene ali mʼmenemo adzamira mʼnyanja tsiku limene udzawonongeka.
dit Gods, dine Varer, din Vinding, dine Søfolk og Styrmænd, de, der bøded din Læk, dine Handelsfolk, alt dit krigsfolk, som var om Bord, alt Mandskab i din Midte styrter i Havets dyb, den Dag du falder.
28 Madera a mʼmbali mwa nyanja adzagwedezeka chifukwa cha kufuwula kwa oyendetsa sitimawo.
Markerne skælver ved dine Styrmænds Skrig.
29 Onse amene amapalasa sitima zapamadzi, adzatuluka mʼsitima zawo; oyendetsa ndi onse owongolera sitima zapamadzi adzayimirira mʼmbali mwa nyanja.
Alle, der sidder ved Årer, går da fra Borde, Søfolk og alle Styrmænd går da i Land;
30 Iwo akufuwula, kukulira iwe kwambiri; akudzithira fumbi kumutu, ndi kudzigubuduza pa phulusa.
de løfter Røsten over dig, klager bittert; på Hovedet kaster de Jord og vælter sig i Støvet,
31 Akumeta mpala mitu yawo chifukwa cha iwe ndipo akuvala ziguduli. Akukulira iweyo ndi mitima yowawa kwambiri.
klipper sig skaldet for dig, klæder sig i Sæk, begræder dig, bitre i Hu, med Sjælekvide,
32 Akuyimba nyimbo yokudandaulira nʼkumati: ‘Ndani anawonongedwapo ngati Turo pakati pa nyanja?’
istemtner jamrende Klage over dig, klager: Ak, hvor Tyrus er øde midt i Havet!
33 Pamene malonda ako ankawoloka nyanja unakhutitsa mitundu yambiri ya anthu. Mafumu a dziko lapansi analemera ndi chuma chako komanso ndi malonda ako.
Når din Vinding kom ind fra Havet, mætted du mange Folkeslag; med dit meget Gods og dine Varer gjorde du Jordens konger rige.
34 Koma tsopano wathyokera mʼnyanja, pansi penipeni pa nyanja. Katundu wako ndi onse amene anali nawe amira pamodzi nawe.
Nu led du Skibbrud på Havet, på Vandets Dyb, dine Varer og alt dit Mandskab gik under med dig.
35 Onse amene amakhala mʼmbali mwa nyanja aopsedwa ndi zimene zakuchitikira. Mafumu awo akuchita mantha ndipo nkhope zangoti khululu.
Over dig gyser alle, som bor på de fjerne Strande, deres Konger er slagne af Angst, deres Ansigt blegner.
36 Anthu amalonda a mitundu ina akukunyogodola. Watha mochititsa mantha ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.”
Deres Kræmmere hånfløjter ad dig, til Rædsel blev du, er borte for evigt.

< Ezekieli 27 >