< Ezekieli 26 >

1 Pa chaka cha khumi ndi chimodzi, tsiku loyamba la mwezi, Yehova anandiyankhula kuti:
II arriva dans la onzième année, le premier du mois, que la parole de l’Eternel me fut adressée en ces termes:
2 “Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Turo ananyogodola Yerusalemu kuti ‘Hii! Uja amene anali chipata choloweramo anthu a mitundu ina wawonongeka. Zitseko zake zatsekukira ife. Tidzalemera popeza wasanduka bwinja.’
"Fils de l’homme, parce que Tyr s’est écriée au sujet de Jérusalem: Ah! Elle est brisée, celle qui était la porte des nations! Mon tour est venu: je vais être comblée, puisqu’elle est ruinée,
3 Nʼchifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulangani, inu anthu a ku Turo. Ndidzakuyitanirani anthu a mitundu ina kuti adzakulangeni monga momwe mafunde amawombera pa Nyanja.
c’est pourquoi, ainsi parle le Seigneur Dieu: Voici que je m’en prends à toi, Tyr; je soulèverai contre toi des nations nombreuses comme la mer soulève ses vagues.
4 Anthuwo adzawononga makoma a Turo ndi kugwetsa nsanja zake. Ndidzapala dothi lake ndipo ndidzamusandutsa thanthwe losalala.
Elles détruiront les remparts de Tyr et démoliront ses tours; je la dénuderai de sa poussière et je ferai d’elle une roche aride.
5 Udzakhala poyanikapo makoka pakati pa nyanja. Ine Ambuye Yehova ndayankhula zimenezo. Udzasanduka chofunkha cha anthu a mitundu ina.
Elle deviendra un étendoir à filets au milieu de la mer, car c’est moi qui parle, dit le Seigneur Dieu, et elle sera une proie pour les nations.
6 Anthu okhala ku mtunda adzasakazidwa ndi lupanga. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Et ses filles qui sont dans la campagne seront massacrées par le glaive; ainsi ils sauront que je suis l’Eternel.
7 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: Iwe Turo, ndidzakubweretsera Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni mfumu ya mafumu, kuchokera kumpoto pamodzi ndi akavalo ndiponso magaleta, anthu okwera pa akavalo ndi gulu lalikulu la ankhondo.
Oui, ainsi parle le Seigneur Dieu, je vais, du Nord, amener contre Tyr Nabuchodonosor, roi de Babylone, le roi des rois, avec des chevaux, des chars, des cavaliers, une grande multitude et un peuple nombreux.
8 Anthu okhala ku mtunda adzawapha ndi lupanga. Adzapanga mitumbira yankhondo ndi kukukwezera zishango kuti alimbane nawe.
Tes filles qui sont dans la campagne, il les fera périr par l’épée, et contre toi il élèvera des retranchements, jettera des redoutes et dressera des boucliers.
9 Adzagwetsa makoma ako ndi zida zogumulira khoma ndi kugwetsa nsanja zako ndi nkhwangwa zake.
Les coups de son bélier, il les assénera sur tes remparts, et tes tours, il les brisera par ses armes.
10 Akavalo ake adzakhala ochuluka kwambiri kotero kuti adzakukwirira ndi fumbi lawo. Makoma ako adzagwedezeka ndi mdidi wa akavalo, ngolo ndi magaleta pamene iye adzalowa pa zipata monga mmene amalowera mu mzinda umene makoma ake agwetsedwa.
Grâce à la multitude de ses chevaux, il te couvrira de leur poussière; du bruit des cavaliers, des roues et des chars tes murailles trembleront, quand il entrera par tes portes comme on entre dans une ville éventrée.
11 Akavalo ake adzapondaponda mʼmisewu yako yonse ndi ziboda zawo. Adzapha anthu ako ndi lupanga. Mizati yako yolimba idzagwetsedwa.
Sous les sabots de ses chevaux il foulera toutes tes rues, ta population, il la tuera par l’épée, et les monuments de ta puissance tomberont à terre.
12 Iwo adzafunkha chuma chako ndipo adzalanda zinthu zako za malonda. Adzagwetsa makoma ako ndi kuwononga nyumba zako zabwino. Adzaponya miyala yako, matabwa ako ndi dothi lako mʼnyanja.
Ils pilleront tes richesses, feront main basse sur tes marchandises; ils démoliront tes murailles et abattront tes maisons de plaisance; tes pierres, tes bois et ta poussière, ils les jetteront dans l’eau.
13 Choncho ndidzathetsa phokoso la nyimbo zanu, ndipo kulira kwa apangwe ako sikudzamvekanso.
Je mettrai fin à la rumeur de tes chants, et le son de tes harpes ne se fera plus entendre.
14 Ndidzakusandutsa thanthwe losalala, ndipo udzakhala malo woyanikapo makoka a nsomba. Sudzamangidwanso, pakuti Ine Yehova ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
Je ferai de toi une roche aride, tu deviendras un étendoir à filets. Tu ne seras plus rebâtie, car c’est moi, l’Eternel, qui parle, dit le Seigneur Dieu."
15 “Ine Ambuye Yehova ndikukuwuza, iwe mzinda wa Turo, kuti zilumba zidzagwedezeka pakumva za kugwa kwako ndiponso poona anthu opweteka akubuwula ndipo anthu akuphedwa pakati pako.
Ainsi parle le Seigneur Dieu à Tyr: "Certes, au bruit de ta chute, aux gémissements des mourants, quand s’accomplira la tuerie au milieu de toi, les îles trembleront.
16 Pamenepo mafumu a mʼmbali mwa nyanja adzatsika pa mipando yawo yaufumu. Adzayika pambali mikanjo yawo ndi kuvala zovala zawo zamakaka. Adzachita mantha ndipo adzakhala pansi akunjenjemera kosalekeza. Adzathedwa nzeru poona zimene zakugwera.
Ils descendront de leurs trônes, tous les princes de la mer, ils ôteront leurs manteaux et dépouilleront leurs vêtements brodés; ils se vêtiront d’épouvante, s’asseoiront à terre, frissonneront à tout instant et seront atterrés à cause de toi.
17 Pamenepo adzayimba nyimbo yokudandaula ndipo adzati kwa iwe: “‘Nʼkuchita kuwonongeka chotere, iwe mzinda wotchuka, wodzaza ndi anthu a ku nyanja! Unali wamphamvu pa nyanja, iwe ndi nzika zako; unkaopseza anthu onse amene ankakhala kumeneko.
Ils entonneront sur toi une complainte et te diront: "Comme tu as péri, toi si populeuse grâce aux mers, ville illustre, si puissante sur les flots, toi et tes habitants, qui inspiraient la terreur à tous les voisins!
18 Tsopano mayiko a mʼmbali mwa nyanja akunjenjemera chifukwa cha kugwa kwako; okhala pa zilumba nawonso agwidwa ndi mantha aakulu chifukwa cha kugwa kwako.’
Maintenant les côtes tremblent au jour de ta chute, et les îles qui sont dans la mer sont épouvantées de ta fin.
19 “Mawu a Ine Ambuye Yehova ndi awa: Ndidzakusandutsa bwinja, ngati mizinda imene anthu sangathe kukhalamo. Ndidzakuphimba ndi madzi ozama a mʼnyanja, madzi amphamvu woti akumize.
Car, ainsi parle le Seigneur Dieu, lorsque je ferai de toi une ville ruinée, pareille aux villes qui ne sont plus habitées, lorsque je soulèverai contre toi les ondes de l’abîme et que te couvriront les eaux profondes,
20 Ndidzakugwetsa pansi kuti ukhale pamodzi ndi anthu amvulazakale amene akutsikira ku manda. Ine ndidzakusunga ku dzenjeko ngati ku bwinja losiyidwa kalekale, pamodzi ndi anthu amene anafa kale motero sudzabwererako kukhala pakati pa anthu amoyo.
alors je te précipiterai avec ceux qui sont descendus dans la fosse, auprès des gens des temps antiques, et je te confinerai dans les régions souterraines, dans les ruines éternelles, auprès de ceux qui sont descendus dans la fosse, afin que tu cesses d’être habitée, tandis que je répandrai de la beauté au pays des vivants.
21 Ine ndidzakuthetsa mochititsa mantha, ndipo sudzakhalaponso. Anthu adzakufunafuna, koma sudzapezekanso, akutero Ambuye Yehova.”
Je te réduirai à néant et c’en sera fini de toi: l’on te cherchera et plus jamais l’on ne te trouvera", dit le Seigneur Dieu."

< Ezekieli 26 >