< Ezekieli 26 >

1 Pa chaka cha khumi ndi chimodzi, tsiku loyamba la mwezi, Yehova anandiyankhula kuti:
and to be in/on/with eleven ten year in/on/with one to/for month to be word LORD to(wards) me to/for to say
2 “Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Turo ananyogodola Yerusalemu kuti ‘Hii! Uja amene anali chipata choloweramo anthu a mitundu ina wawonongeka. Zitseko zake zatsekukira ife. Tidzalemera popeza wasanduka bwinja.’
son: child man because which to say Tyre upon Jerusalem Aha! to break door [the] people to turn: turn to(wards) me to fill to destroy
3 Nʼchifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulangani, inu anthu a ku Turo. Ndidzakuyitanirani anthu a mitundu ina kuti adzakulangeni monga momwe mafunde amawombera pa Nyanja.
to/for so thus to say Lord YHWH/God look! I upon you Tyre and to ascend: attack upon you nation many like/as to ascend: attack [the] sea to/for heap: wave his
4 Anthuwo adzawononga makoma a Turo ndi kugwetsa nsanja zake. Ndidzapala dothi lake ndipo ndidzamusandutsa thanthwe losalala.
and to ruin wall Tyre and to overthrow tower her and to scrape dust her from her and to give: make [obj] her to/for bare crag
5 Udzakhala poyanikapo makoka pakati pa nyanja. Ine Ambuye Yehova ndayankhula zimenezo. Udzasanduka chofunkha cha anthu a mitundu ina.
spreading-place net to be in/on/with midst [the] sea for I to speak: speak utterance Lord YHWH/God and to be to/for plunder to/for nation
6 Anthu okhala ku mtunda adzasakazidwa ndi lupanga. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
and daughter her which in/on/with land: country in/on/with sword to kill and to know for I LORD
7 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: Iwe Turo, ndidzakubweretsera Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni mfumu ya mafumu, kuchokera kumpoto pamodzi ndi akavalo ndiponso magaleta, anthu okwera pa akavalo ndi gulu lalikulu la ankhondo.
for thus to say Lord YHWH/God look! I to come (in): bring to(wards) Tyre Nebuchadnezzar king Babylon from north king king in/on/with horse and in/on/with chariot and in/on/with horseman and assembly and people: soldiers many
8 Anthu okhala ku mtunda adzawapha ndi lupanga. Adzapanga mitumbira yankhondo ndi kukukwezera zishango kuti alimbane nawe.
daughter your in/on/with land: country in/on/with sword to kill and to give: put upon you siegework and to pour: scatter upon you mound and to arise: raise upon you shield
9 Adzagwetsa makoma ako ndi zida zogumulira khoma ndi kugwetsa nsanja zako ndi nkhwangwa zake.
and blow battering-ram his to give: give in/on/with wall your and tower your to tear in/on/with sword his
10 Akavalo ake adzakhala ochuluka kwambiri kotero kuti adzakukwirira ndi fumbi lawo. Makoma ako adzagwedezeka ndi mdidi wa akavalo, ngolo ndi magaleta pamene iye adzalowa pa zipata monga mmene amalowera mu mzinda umene makoma ake agwetsedwa.
from abundance horse his to cover you dust their from voice: sound horseman and wheel and chariot to shake wall your in/on/with to come (in): come he in/on/with gate your like/as entrance city to break up/open
11 Akavalo ake adzapondaponda mʼmisewu yako yonse ndi ziboda zawo. Adzapha anthu ako ndi lupanga. Mizati yako yolimba idzagwetsedwa.
in/on/with hoof horse his to trample [obj] all outside your people your in/on/with sword to kill and pillar strength your to/for land: soil to go down
12 Iwo adzafunkha chuma chako ndipo adzalanda zinthu zako za malonda. Adzagwetsa makoma ako ndi kuwononga nyumba zako zabwino. Adzaponya miyala yako, matabwa ako ndi dothi lako mʼnyanja.
and to loot strength: rich your and to plunder merchandise your and to overthrow wall your and house: home desire your to tear and stone your and tree: wood your and dust your in/on/with midst water to set: put
13 Choncho ndidzathetsa phokoso la nyimbo zanu, ndipo kulira kwa apangwe ako sikudzamvekanso.
and to cease crowd song your and voice: sound lyre your not to hear: hear still
14 Ndidzakusandutsa thanthwe losalala, ndipo udzakhala malo woyanikapo makoka a nsomba. Sudzamangidwanso, pakuti Ine Yehova ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
and to give: make you to/for bare crag spreading-place net to be not to build still for I LORD to speak: speak utterance Lord YHWH/God
15 “Ine Ambuye Yehova ndikukuwuza, iwe mzinda wa Turo, kuti zilumba zidzagwedezeka pakumva za kugwa kwako ndiponso poona anthu opweteka akubuwula ndipo anthu akuphedwa pakati pako.
thus to say Lord YHWH/God to/for Tyre not from voice: sound carcass your in/on/with to groan slain: wounded in/on/with to kill slaughter in/on/with midst your to shake [the] coastland
16 Pamenepo mafumu a mʼmbali mwa nyanja adzatsika pa mipando yawo yaufumu. Adzayika pambali mikanjo yawo ndi kuvala zovala zawo zamakaka. Adzachita mantha ndipo adzakhala pansi akunjenjemera kosalekeza. Adzathedwa nzeru poona zimene zakugwera.
and to go down from upon throne their all leader [the] sea and to turn aside: remove [obj] robe their and [obj] garment embroidery their to strip trembling to clothe upon [the] land: soil to dwell and to tremble to/for moment and be desolate: appalled upon you
17 Pamenepo adzayimba nyimbo yokudandaula ndipo adzati kwa iwe: “‘Nʼkuchita kuwonongeka chotere, iwe mzinda wotchuka, wodzaza ndi anthu a ku nyanja! Unali wamphamvu pa nyanja, iwe ndi nzika zako; unkaopseza anthu onse amene ankakhala kumeneko.
and to lift: raise upon you dirge and to say to/for you how? to perish to dwell from sea [the] city [the] to boast: praise which to be strong in/on/with sea he/she/it and to dwell her which to give: give terror their to/for all to dwell her
18 Tsopano mayiko a mʼmbali mwa nyanja akunjenjemera chifukwa cha kugwa kwako; okhala pa zilumba nawonso agwidwa ndi mantha aakulu chifukwa cha kugwa kwako.’
now to tremble [the] coastland day carcass your and to dismay [the] coastland which in/on/with sea from to come out: come you
19 “Mawu a Ine Ambuye Yehova ndi awa: Ndidzakusandutsa bwinja, ngati mizinda imene anthu sangathe kukhalamo. Ndidzakuphimba ndi madzi ozama a mʼnyanja, madzi amphamvu woti akumize.
for thus to say Lord YHWH/God in/on/with to give: make I [obj] you city to destroy like/as city which not to dwell in/on/with to ascend: attack upon you [obj] abyss and to cover you [the] water [the] many
20 Ndidzakugwetsa pansi kuti ukhale pamodzi ndi anthu amvulazakale amene akutsikira ku manda. Ine ndidzakusunga ku dzenjeko ngati ku bwinja losiyidwa kalekale, pamodzi ndi anthu amene anafa kale motero sudzabwererako kukhala pakati pa anthu amoyo.
and to go down you with to go down pit to(wards) people forever: antiquity and to dwell you in/on/with land: country/planet lower like/as desolation from forever: antiquity with to go down pit because not to dwell and to give: put beauty in/on/with land: country/planet alive
21 Ine ndidzakuthetsa mochititsa mantha, ndipo sudzakhalaponso. Anthu adzakufunafuna, koma sudzapezekanso, akutero Ambuye Yehova.”
terror to give: make you and nothing you and to seek and not to find still to/for forever: enduring utterance Lord YHWH/God

< Ezekieli 26 >