< Ezekieli 26 >

1 Pa chaka cha khumi ndi chimodzi, tsiku loyamba la mwezi, Yehova anandiyankhula kuti:
And it came to pass in the eleventh year, on the first of the month, that the word of Yahweh came unto me, saying:
2 “Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Turo ananyogodola Yerusalemu kuti ‘Hii! Uja amene anali chipata choloweramo anthu a mitundu ina wawonongeka. Zitseko zake zatsekukira ife. Tidzalemera popeza wasanduka bwinja.’
Son of man, Because Tyre hath said concerning Jerusalem. Aha! She is broken that was the doors of the peoples. She is turned unto me, — I shall be filled, She is laid waste,
3 Nʼchifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulangani, inu anthu a ku Turo. Ndidzakuyitanirani anthu a mitundu ina kuti adzakulangeni monga momwe mafunde amawombera pa Nyanja.
Therefore, Thus, saith My Lord Yahweh, Behold me! against thee O Tyre, — So then I will bring up against thee many nations, As the sea bringeth up its rolling waves;
4 Anthuwo adzawononga makoma a Turo ndi kugwetsa nsanja zake. Ndidzapala dothi lake ndipo ndidzamusandutsa thanthwe losalala.
And they shall destroy the walls of Tyre. And break down her towers, And I will scrape clean her dust from off her, —And make of her the glaring face of a cliff:
5 Udzakhala poyanikapo makoka pakati pa nyanja. Ine Ambuye Yehova ndayankhula zimenezo. Udzasanduka chofunkha cha anthu a mitundu ina.
A place for the spreading of nets, shall she become, in the midst of the sea, For, I, have spoken Declareth My Lord. Yahweh, -And she shall become a prey to the nations.
6 Anthu okhala ku mtunda adzasakazidwa ndi lupanga. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
And her daughters that are in the field: with the sword shall be slain: So shall they know that I am Yahweh.
7 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: Iwe Turo, ndidzakubweretsera Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni mfumu ya mafumu, kuchokera kumpoto pamodzi ndi akavalo ndiponso magaleta, anthu okwera pa akavalo ndi gulu lalikulu la ankhondo.
For thus saith My Lord. Yahweh, Behold me! bringing against Tyre. Nebuchadrezzar king of Babylon out of the North. a king of kings, —with horses and with chariots and with horsemen, and a gathered host, and much people.
8 Anthu okhala ku mtunda adzawapha ndi lupanga. Adzapanga mitumbira yankhondo ndi kukukwezera zishango kuti alimbane nawe.
Thy daughters in the field—with the sword, shall he slay, - And shall set against thee a siege-wall And cast up against thee an earthwork, And set up against thee a large shield;
9 Adzagwetsa makoma ako ndi zida zogumulira khoma ndi kugwetsa nsanja zako ndi nkhwangwa zake.
And the stroke of his attacking-engine, will he direct against thy walls, — And thy towers, will he break down with his axes.
10 Akavalo ake adzakhala ochuluka kwambiri kotero kuti adzakukwirira ndi fumbi lawo. Makoma ako adzagwedezeka ndi mdidi wa akavalo, ngolo ndi magaleta pamene iye adzalowa pa zipata monga mmene amalowera mu mzinda umene makoma ake agwetsedwa.
By reason of the multitude of his horses, their dust shall cover thee, — At the noise of horseman and wheel and chariot, shall thy walls tremble, when he entereth into thy gates Just as they do who enter a city broken open.
11 Akavalo ake adzapondaponda mʼmisewu yako yonse ndi ziboda zawo. Adzapha anthu ako ndi lupanga. Mizati yako yolimba idzagwetsedwa.
With the hoofs of his horses, shall he tread down all thy streets, — Thy people-with the sword, shall he slay, And thy pillars of strength to the earth, shall go down.
12 Iwo adzafunkha chuma chako ndipo adzalanda zinthu zako za malonda. Adzagwetsa makoma ako ndi kuwononga nyumba zako zabwino. Adzaponya miyala yako, matabwa ako ndi dothi lako mʼnyanja.
And they shall spoil thy wealth And make a prey of thy merchandise, And break down thy walls And thy pleasant houses, shall they lay in ruins; And thy stones and thy timber and thy dust—in the midst of the waters, shall they lay.
13 Choncho ndidzathetsa phokoso la nyimbo zanu, ndipo kulira kwa apangwe ako sikudzamvekanso.
And I will cause to cease the hum of thy songs; And the sound of thy lyres, shall not be heard any more.
14 Ndidzakusandutsa thanthwe losalala, ndipo udzakhala malo woyanikapo makoka a nsomba. Sudzamangidwanso, pakuti Ine Yehova ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
And I will make of thee the glaring face of a cliff. A place for the spreading of nets, shalt thou become, Thou shalt not be but any more, For I. Yahweh have spoken it, Declareth My Lord Yahweh.
15 “Ine Ambuye Yehova ndikukuwuza, iwe mzinda wa Turo, kuti zilumba zidzagwedezeka pakumva za kugwa kwako ndiponso poona anthu opweteka akubuwula ndipo anthu akuphedwa pakati pako.
Thus saith My Lord. Yahweh, to Tyre: Shall it not be that. At the sound of thy fall. With the groan of thy pierced one. With the slaughter made in thy midst, The Coastlands shall tremble?
16 Pamenepo mafumu a mʼmbali mwa nyanja adzatsika pa mipando yawo yaufumu. Adzayika pambali mikanjo yawo ndi kuvala zovala zawo zamakaka. Adzachita mantha ndipo adzakhala pansi akunjenjemera kosalekeza. Adzathedwa nzeru poona zimene zakugwera.
Then shall come down from off their thrones all the princes of the sea, And shall lay aside their robes. And their embroidered garments, shall strip off, — With tremblings, shall they clothe them. selves Upon the ground, shall they sit, And shall tremble every moment and be astonished over thee.
17 Pamenepo adzayimba nyimbo yokudandaula ndipo adzati kwa iwe: “‘Nʼkuchita kuwonongeka chotere, iwe mzinda wotchuka, wodzaza ndi anthu a ku nyanja! Unali wamphamvu pa nyanja, iwe ndi nzika zako; unkaopseza anthu onse amene ankakhala kumeneko.
Then shall they take up over thee a dirge, And say to thee, - How hast thou perished, And ceased from the seas, - The city renowned which was strong in the sea She and they who dwelt in her, Who imparted their terror To all who dwelt in her.
18 Tsopano mayiko a mʼmbali mwa nyanja akunjenjemera chifukwa cha kugwa kwako; okhala pa zilumba nawonso agwidwa ndi mantha aakulu chifukwa cha kugwa kwako.’
Now, shall tremble the Coastlands, In the day of thy fall, - And shall shudder the isles that are in the sea. At thine exit!
19 “Mawu a Ine Ambuye Yehova ndi awa: Ndidzakusandutsa bwinja, ngati mizinda imene anthu sangathe kukhalamo. Ndidzakuphimba ndi madzi ozama a mʼnyanja, madzi amphamvu woti akumize.
For thus saith My Lord Yahweh, When I make thee a desolate city, Like cities which cannot be dwelt in, - When I bring up over thee the roaring deep, And the mighty waters cover thee,
20 Ndidzakugwetsa pansi kuti ukhale pamodzi ndi anthu amvulazakale amene akutsikira ku manda. Ine ndidzakusunga ku dzenjeko ngati ku bwinja losiyidwa kalekale, pamodzi ndi anthu amene anafa kale motero sudzabwererako kukhala pakati pa anthu amoyo.
Then will I bring thee down with them that go down into the pit. Unto the people of age-past times And cause thee to dwell in the earth below Among the desolations from age-past times With them that go down into the pit That thou mayest not be dwelt in, Nor yet present thyself in the land of the living.
21 Ine ndidzakuthetsa mochititsa mantha, ndipo sudzakhalaponso. Anthu adzakufunafuna, koma sudzapezekanso, akutero Ambuye Yehova.”
A terror, will I make thee And thou shalt not be: Though thou be sought for, Thou shalt not be found any more To times age-abiding, Declareth My Lord, Yahweh.

< Ezekieli 26 >