< Ezekieli 25 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
Опет ми дође реч Господња говорећи:
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenukira anthu a ku Amoni ndipo unenere mowadzudzula.
Сине човечји, окрени лице своје према синовима Амоновим и пророкуј на њих.
3 Awawuze kuti, ‘Inu anthu a ku Amoni, imvani zimene Ambuye Yehova akunena. Iye akuti: Inu munanena mawu onyoza pamene Nyumba yanga yopatulika inkayipitsidwa. Munanyozanso dziko la Israeli pamene linaguga ndiponso anthu a ku Yuda pamene anatengedwa ukapolo.
И реци синовима Амоновим: Чујте реч Господа Господа: Овако вели Господ Господ: Што си говорио: Аха! За светињу моју, што се оскврни, и за земљу Израиљеву, што опусте, и за дом Јудин, што отиде у ропство;
4 Nʼchifukwa chake Ine ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu akummawa ngati cholowa chawo. Iwo adzamanga misasa yawo ndi kukhoma matenti awo pakati panu. Adzadya zipatso zanu ndi kumwa mkaka wanu.
Зато, ево, ја ћу те дати у наследство источним народима, и поградиће у теби дворове себи, и начиниће себи колибе у теби; они ће јести плодове твоје и пити млеко твоје.
5 Ndidzasandutsa Raba kuti akhale busa la ngamira ndi mizinda ya Aamoni kuti ikhale makola a nkhosa. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
И од Раве ћу начинити обор камилама и од земље синова Амонових тор овчији, и познаћете да сам ја Господ.
6 Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu munawomba mʼmanja ndi kumalumphalumpha. Munkakondwa mu mtima mwanu pamene munkanyoza dziko la Israeli.
Јер овако вели Господ Господ: Што си пљескао рукама и лупао ногом и веселио се из срца што си опустошио сву земљу Израиљеву,
7 Nʼchifukwa chake ndidzatambasula dzanja langa kuti ndikulangeni, ndipo ndidzakuperekani kuti mukhale chofunkha cha anthu a mitundu ina. Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukufafanizani mʼmayiko onse. Ndidzakuwonongani, ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova!’”
Зато, ево, ја ћу дигнути руку своју на те, и даћу те народима да те плене, и истребићу те између народа и затрћу те између земаља, и искоренићу те, и познаћеш да сам ја Господ.
8 “Ambuye Yehova akuti, ‘Anthu a ku Mowabu ndi a ku Seiri ananena kuti anthu a ku Yuda ali ngati mayiko ena onse.’
Овако вели Господ Господ: Што говори Моав и Сир: Ето, дом је Јудин као сви народи;
9 Nʼchifukwa chake ndidzagumula mbali ina ya Mowabu, kuyambira ku mizinda yake ya kumalire; mizinda yokongola ya Beti-Yesimoti, Baala-Meoni ndi Kiriataimu.
Зато, ево, ја ћу отворити страну Моавову од градова, од градова на међи, красну земљу вет-јесимотску, валмеонску и Киријат-ајимску,
10 Ndidzapereka Amowabu pamodzi ndi Aamoni mʼmanja mwa anthu akummawa kotero kuti Aamoni adzayiwalikiratu pakati pa anthu a mitundu ina.
Народима источним иза земље синова Амонових, и даћу им је у наследство да нема спомена синовима Амоновим међу народима.
11 Ndidzawalangadi Amowabuwo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
И на Моавцима ћу извршити своје судове, и познаће да сам ја Господ.
12 “Ambuye Yehova akuti, ‘Pakuti Edomu analipsira Ayuda, ndiye kuti analakwa kwambiri pochita zimenezi.
Овако вели Господ Господ: Што се Едом освети дому Јудином и тешко скриви осветивши им се,
13 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kulanga Edomu ndi kupha anthu ake ndiponso nyama zawo. Ndidzawonongeratu Edomu ndipo adzaphedwa ndi lupanga kuchokera ku Temani mpaka ku Dedani.
Зато овако вели Господ Господ: Дигнућу руку своју на едомску и истребићу из ње и људе и стоку, и обратићу је у пустош, од Темана до Дедана пашће од мача.
14 Ndidzalanga Edomu ndi dzanja la anthu anga Aisraeli. Adzalanga anthu a ku Edomu molingana ndi mkwiyo ndi ukali wanga. Choncho adzaona kulipsira kwanga akutero Ambuye Yehova.’”
И осветићу се Едомцима руком народа свог Израиља, и учиниће с Едомцима по гневу мом и по јарости мојој, и познаће моју освету, говори Господ Господ.
15 “Ambuye Yehova akuti, ‘Afilisti analanga anthu anga mwankhanza ndi kuwalipsira.
Овако вели Господ Господ: Што Филистеји радише из освете, и осветише се радујући се из срца и потирући из старе мржње,
16 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kukantha Afilistiwo. Ndidzafafaniza Akereti ndi kuwononga iwo amene amakhala mʼmbali mwa nyanja.
Зато овако вели Господ Господ: Ево ја ћу дигнути руку своју на Филистеје, и истребићу Херетеје, и потрћу остатак од приморја.
17 Ndidzawabwezera chilango choopsa ndipo ndidzawalanga mu mkwiyo wanga. Ndikadzawalipsira ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
И учинићу на њима велику освету карањем гневним, и познаће да сам ја Господ кад извршим освету своју на њима.

< Ezekieli 25 >