< Ezekieli 25 >
1 Yehova anandiyankhula kuti:
Og Herrens Ord kom til mig saaledes:
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenukira anthu a ku Amoni ndipo unenere mowadzudzula.
Du Menneskesøn! vend dit Ansigt imod Ammons Børn, og spaa imod dem,
3 Awawuze kuti, ‘Inu anthu a ku Amoni, imvani zimene Ambuye Yehova akunena. Iye akuti: Inu munanena mawu onyoza pamene Nyumba yanga yopatulika inkayipitsidwa. Munanyozanso dziko la Israeli pamene linaguga ndiponso anthu a ku Yuda pamene anatengedwa ukapolo.
og sig til Ammons Børn: Hører den Herre, Herres Ord: Saa siger den Herre, Herre: Efterdi du sagde: Ha ha! over min Helligdom, fordi den er vanhelliget, og over Israels Land, fordi det er ødelagt, og over Judas Hus, fordi de ere vandrede i Landflygtighed:
4 Nʼchifukwa chake Ine ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu akummawa ngati cholowa chawo. Iwo adzamanga misasa yawo ndi kukhoma matenti awo pakati panu. Adzadya zipatso zanu ndi kumwa mkaka wanu.
Derfor se, jeg vil give dig til Ejendom for Østens Folk, og de skulle opslaa deres Teltbyer i dig og sætte deres Boliger i dig; de skulle æde din Frugt, og de skulle drikke din Mælk.
5 Ndidzasandutsa Raba kuti akhale busa la ngamira ndi mizinda ya Aamoni kuti ikhale makola a nkhosa. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Og jeg vil gøre Rabba til Græsgang for Kameler og Ammons Børns Land til Faareleje; og I skulle fornemme, at jeg er Herren.
6 Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu munawomba mʼmanja ndi kumalumphalumpha. Munkakondwa mu mtima mwanu pamene munkanyoza dziko la Israeli.
Thi saa siger den Herre, Herre: Fordi du klappede i Haanden og stampede med Foden og glædede dig i al din Haan efter din Sjæls Lyst imod Israels Land:
7 Nʼchifukwa chake ndidzatambasula dzanja langa kuti ndikulangeni, ndipo ndidzakuperekani kuti mukhale chofunkha cha anthu a mitundu ina. Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukufafanizani mʼmayiko onse. Ndidzakuwonongani, ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova!’”
Derfor se, jeg ud rækker min Haand imod dig og giver dig hen til Bytte for Folkene og udrydder dig af Folkeslægternes Tal og lader dig forsvinde af Lan dene; jeg vil ødelægge dig, og du skal fornemme, at jeg er Herren.
8 “Ambuye Yehova akuti, ‘Anthu a ku Mowabu ndi a ku Seiri ananena kuti anthu a ku Yuda ali ngati mayiko ena onse.’
Saa siger den Herre, Herre: Fordi Moab og Sejr sige: Se, Judas Hus er ligesom alle Hedningerne:
9 Nʼchifukwa chake ndidzagumula mbali ina ya Mowabu, kuyambira ku mizinda yake ya kumalire; mizinda yokongola ya Beti-Yesimoti, Baala-Meoni ndi Kiriataimu.
Derfor se, jeg vil aabne Moabs Side fra Stæderne af, fra dets Grænsestæder af, Landets Pryd, Beth-Jesimoth, Baal-Meon og Kirjathama,
10 Ndidzapereka Amowabu pamodzi ndi Aamoni mʼmanja mwa anthu akummawa kotero kuti Aamoni adzayiwalikiratu pakati pa anthu a mitundu ina.
for Østens Børn tillige med Ammons Børns Land, og jeg vil give dem det til Ejendom, paa det man ikke skal ihukomme Ammons Børn iblandt Folkene;
11 Ndidzawalangadi Amowabuwo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
og jeg vil holde Ret over Moab, at de skulle fornemme, at jeg er Herren.
12 “Ambuye Yehova akuti, ‘Pakuti Edomu analipsira Ayuda, ndiye kuti analakwa kwambiri pochita zimenezi.
Saa siger den Herre, Herre: Fordi Edom tog en svar Hævn over Judas Hus og gjorde sig saare skyldig, da de hævnede sig paa dem:
13 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kulanga Edomu ndi kupha anthu ake ndiponso nyama zawo. Ndidzawonongeratu Edomu ndipo adzaphedwa ndi lupanga kuchokera ku Temani mpaka ku Dedani.
Derfor, saa siger den Herre, Herre: Jeg vil udrække min Haand over Edom og udrydde Mennesker og Kvæg deraf: Og jeg vil gøre det øde fra Theman af, og indtil Dedan skulle de falde ved Sværdet;
14 Ndidzalanga Edomu ndi dzanja la anthu anga Aisraeli. Adzalanga anthu a ku Edomu molingana ndi mkwiyo ndi ukali wanga. Choncho adzaona kulipsira kwanga akutero Ambuye Yehova.’”
og jeg vil føre min Hævn over Edom ved mit Folk Israels Haand, og de skulle gøre ved Edom efter min Vrede og efter min Fortørnelse, og de skulle kende min Hævn, siger den Herre, Herre.
15 “Ambuye Yehova akuti, ‘Afilisti analanga anthu anga mwankhanza ndi kuwalipsira.
Saa siger den Herre, Herre: Fordi Filisterne have taget Hævn og have hævnet sig svarlig i Haan efter deres Sjæls Lyst for at ødelægge med et evigt Fjendskab:
16 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kukantha Afilistiwo. Ndidzafafaniza Akereti ndi kuwononga iwo amene amakhala mʼmbali mwa nyanja.
Derfor, saa siger den Herre, Herre: Se, jeg vil udrække min Haand over Filisterne og udrydde Kreterne; og jeg vil tilintetgøre de overblevne ved Havets Strand;
17 Ndidzawabwezera chilango choopsa ndipo ndidzawalanga mu mkwiyo wanga. Ndikadzawalipsira ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
og jeg vil tage en stor Hævn over dem med grumme Straffe, og de skulle fornemme, at jeg er Herren, naar jeg fører min Hævn over dem.