< Ezekieli 24 >

1 Pa tsiku lakhumi la mwezi wakhumi chaka chachisanu ndi chinayi, Yehova anandiyankhula kuti:
And the word of the Lord came unto me in the ninth year, in the tenth month, on the tenth day of the month, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu lemba dzina la tsiku lalero, lero lomwe lino, chifukwa mfumu ya Babuloni yazungulira Yerusalemu lero lino.
Son of man, write thee down the name of this day, of this same day: the king of Babylon hath advanced against Jerusalem on this same day.
3 Uwaphere mwambi anthu owukirawa ndi kuwawuza kuti: ‘Ambuye Yehova akuti, “‘Ikani mʼphika pa moto, ndipo mu mʼphikamo muthiremo madzi.
And speak concerning the rebellious family a parable, and say unto them, Thus hath said the Lord Eternal, Set on the pot, set it on, and also pour water into it;
4 Mu mʼphikamo muyikemo nthuli za nyama, nthuli zonse zabwino kwambiri za mwendo wathako ndi mwendo wamwamba. Mudzadzemo mafupa abwino kwambiri.
Gather the proper pieces into it, every good piece, the thigh, and the shoulder; fill it up with the choice bones.
5 Pa gulu la nkhosa musankhepo nkhosa yabwino kwambiri. Muyike nkhuni pansi pa mʼphikawo. Madzi awire. Kenaka muphike nyamayo pamodzi ndi mafupa omwe.’
Take the choice of the flock, and make also a fire for the bones under it: cause it to seethe well, that even the bones therein may be fully boiled through.
6 “‘Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova akuti, “‘Tsoka kwa mzinda wokhetsa magazi, tsoka kwa mʼphika wadzimbiri; dzimbiri lake losachoka! Mutulutsemo nthuli imodzimodzi osasankhulapo.
Therefore thus hath said the Lord Eternal, Woe to the city of blood-guiltiness, to the pot the scum of which is yet in it, and the scum of which is not gone out of it! one of its pieces after the other take out from it: no lot is cast for it.
7 “‘Paja magazi amene anakhetsa akanali pakati pake mu mzindamo. Iye awakhuthulira pa thanthwe losalala. Sanawakhutulire pa dothi kuopa kuti fumbi lingawafotsere.
For her blood was in the midst of her; on the naked rock did she place it: she poured it not upon the ground, to cover it over with dust.
8 Ndinasiya magaziwo pa mwala wosalala kuti asafotseredwe ndi fumbi chifukwa ndinafuna kuonetsa mkwiyo wanga ndi kulipsira.
To cause my fury to arise to take vengeance, do I place her blood upon the naked rock, so that it shall not be covered up.
9 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: “‘Tsoka kwa mzinda wokhetsa magazi! Inenso, ndidzawunjika mulu waukulu wa nkhuni.
Therefore thus hath said the Lord Eternal, Woe to the city of blood-guiltiness! I also will myself build up a large burning pile,
10 Choncho wonjeza nkhuni ndipo muyatse moto. Phikani nyamayo bwinobwino, muthiremo zokometsera, mutsanule msuzi, ndipo mupsereze mafupawo.
Heaping on the wood, kindling the fire, thoroughly boiling the flesh, and stirring the mixture, that the bones may be scorched.
11 Tsono muyike pa makala mʼphika wopanda kanthuwo mpaka utenthe kuchita kuti psuu kuti zonyansa zake zisungunuke ndi kuti dzimbiri lake lichoke.
Then will I set it empty upon its coals, in order that it may become hot, and its copper be made to glow, and its uncleanness may be molten in it, that its scum may be consumed.
12 Koma mʼphikawo walephereka kuyeretsedwa. Dzimbiri lake linalowerera silingatheke kuchoka ngakhale ndi moto womwe.
With fraud hath she wearied [the poor]; therefore shall not go forth from her the greatness of her scum: through fire shall her scum [be removed].
13 “‘Tsono dzimbiri limeneli ndi zilakolako za dama lako. Pakuti ine ndinayesa kukutsuka koma iwe sunayere, ndipo sudzayeranso mpaka ukali wanga utakwaniratu pa iwe.
In thy uncleanness is [thy] incest; because I endeavored to cleanse thee, and thou wouldst not be clean, thou shalt not be cleansed from thy uncleanness any more, until I have assuaged my fury on thee.
14 “‘Ine Yehova ndayankhula. Zimenezi zikubwera ndipo ndidzazichitadi. Sindidzabwerera mʼmbuyo. Sindidzakulekerera kapena kukuchitira chifundo. Ndidzakulanga molingana ndi makhalidwe ndi machitidwe ako, akutero Ambuye Yehova.’”
I the Lord have spoken it; it cometh to pass, and I will do it; I will not recall my decree, and I will not have pity, nor will I repent: according to thy ways, and according to thy doings, shall men judge thee, saith the Lord Eternal.
15 Yehova anandiyankhula kuti:
And the word of the Lord came to me, saying,
16 “Iwe mwana wa munthu, Ine ndikulanda mwadzidzidzi mkazi amene amakukomera mʼmaso kwambiri. Koma usadandaule, usalire kapena kukhetsa misozi.
Son of man, behold, I will take away from thee the desire of thy eyes by a sudden death; but thou shalt neither mourn nor weep, nor shalt thou shed a tear.
17 Ubuwule koma mwakachetechete. Usamulire wakufayo. Uvale nduwira yako ndithu, nsapato zakonso usavule. Usaphimbe nkhope kapena kudya chakudya cha anamfedwa.”
Sigh in silence, make no mourning for the deceased, thy bonnet bind around thy head, and thy shoes put on thy feet, and cover not thyself to thy upper lip, and eat not the bread of [other] men.
18 Choncho ndinayankhula ndi anthu mmawa, ndipo madzulo mkazi wanga anamwalira. Mmawa mwake ndinachita monga momwe anandilamulira.
And when I had spoken unto the people in the morning, my wife died at evening: and I did in the morning as I had been commanded.
19 Ndipo anthu anandifunsa kuti, “Kodi sutifotokozera tanthauzo la zimene ukuchitazi?”
And the people said unto me, Wilt thou not tell us what these things mean for us, that thou doest so?
20 Ndinawayankha kuti, “Yehova anandipatsa uthenga wakuti,
And I said unto them, The word of the Lord came unto me, saying,
21 ‘Awuze Aisraeli kuti: Ine Ambuye Yehova ndikuti: ndidzayipitsa Nyumba yanga yopatulika, nyumba imene mwakhala mukuyinyadira. Mumakondwa kwambiri poyiona, ndipo mumayikonda ndi mtima onse. Ana aamuna ndi aakazi amene munawasiya mʼmbuyo adzaphedwa ndi lupanga.
Speak unto the house of Israel, Thus hath said the Lord Eternal, Behold, I will profane my sanctuary, the pride of your strength, the desire of your eyes, and the darling of your soul: and your sons and your daughters whom ye have left behind shall fall by the sword.
22 Ndipo mudzachita monga ndachitira inemu. Inu simudzaphimba nkhope zanu kapena kudya chakudya cha anamfedwa.
And ye shall do as I have done: ye shall not cover yourselves to your upper lip, and the bread of other men shall ye not eat.
23 Mudzavala nduwira zanu kumutu ndi nsapato zanu ku mapazi anu. Simudzabuma maliro kapena kukhetsa misozi koma mudzavutika kwambiri chifukwa cha machimo anu ndipo mudzabuwula pakati panu.
And your bonnets shall be around your heads, and your shoes shall be on your feet: ye shall not mourn nor shall ye weep; but ye shall pine away in your iniquities, and groan, looking one at the other.
24 Ine Ezekieli ndidzakhala chitsanzo chanu. Mudzachita monga momwe ndachitira. Izi zikadzachitika, akutero Yehova, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Wamphamvuzonse.’
Thus shall Ezekiel be unto you for a token; in accordance with all that he hath done shall ye do: when this cometh, then shall ye know that I am the Lord Eternal.
25 “Ndipo Yehova anandiyankhula nati: Iwe mwana wa munthu, tsiku lina ndidzawachotsera anthuwa linga lawo limene ankakondwerera kukongola kwake, limene linkawakomera mʼmaso mwawo, limenenso anayikapo mtima wawo kwambiri. Ndidzawachotsera ana awo aamuna ndi aakazi.
Also, thou son of man, behold, on the day when I take from them their stronghold, the joy of their glory, the desire of their eyes, and the coveted object of their soul, their sons and their daughters, —
26 Pa tsiku limenelo wothawa nkhondo adzabwera kudzakuwuzani zimenezo.
On that day there shall come one that hath escaped unto thee, and announce it to thy ears.
27 Pa tsiku limenelo pakamwa pako padzatsekuka. Udzatha kuyankhula naye ndipo sudzakhalanso chete. Motero udzakhala chizindikiro kwa iwo, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
On that day shall thy mouth be opened through him that hath escaped, and thou shalt speak, and thou shalt not be silenced any more: and thou shalt be a token unto them, and they shall know that I am the Lord.

< Ezekieli 24 >