< Ezekieli 23 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
بار دیگر خداوند با من سخن گفت و فرمود:
2 “Iwe mwana wa munthu, panali atsikana awiri ana a mayi mmodzi.
«ای پسر انسان، دو خواهر بودند که در جوانی در مصر به زناکاری و روسپی‌گری کشانده شدند.
3 Iwo ankachita za chiwerewere ku Igupto. Za chiwerewerezo anayamba ali achichepere. Kumeneko anthu ankangowasisita pa chifuwa ndi kuwagwiragwira mawere awo aja.
4 Wamkulu dzina lake anali Ohola, ndipo mngʼono wakeyo anali Oholiba. Ine ndinawakwatira ndipo anabereka ana aamuna ndi ana aakazi. Ohola ndiye Samariya, ndipo Yerusalemu ndiye Oholiba.
نام خواهر بزرگتر، اهوله، و نام خواهر کوچکتر اهولیبه بود. این دو خواهر، یکی سامره است و دیگری اورشلیم! من با آن دو ازدواج کردم و آنها برایم پسران و دختران زاییدند.
5 “Ohola anachita zachiwerewere ngakhale anali mkazi wanga; ndipo iye anakangamira abwenzi ake a ku Asiriya.
ولی بعد، اهوله از من روگرداند و به بتها دل بست و عاشق و دلباخته همسایه‌اش، قوم آشور شد،
6 Amenewo anali asilikali ovala zibakuwa zamlangali, abwanamkubwa ndiponso atsogoleri a nkhondo. Onsewo anali anyamata osiririka ndipo ankakwera pa akavalo.
چون آنها جوانانی جذاب و خوش‌اندام، فرماندهان و سردارانی با لباسهای آبی خوشرنگ و سوارکارانی ماهر بودند.
7 Ohola anachita zachiwerewere ndi onsewa, anthu otchuka a ku Asiriya. Iye anadziyipitsa ndi mafano a munthu aliyense amene anagona naye.
پس، او با آنها که برگزیده‌ترین مردان آشور بودند زنا کرد، بتهایشان را پرستید و خود را نجس ساخت.
8 Iye sanaleke za chiwerewere zimene anaziphunzira ku Igupto. Paja akanali mtsikana anyamata ankagona naye. Iwo ankamusisita mawere akanali anthete nachita naye zachiwerewere.
علّتش این بود که وقتی مصر را ترک گفت، از فاحشگی دست نکشید، بلکه همچون دوران جوانی‌اش که با مصری‌ها همخواب می‌شد و زنا می‌کرد، به هرزگی خود ادامه داد.
9 “Nʼchifukwa chake Ine ndinamupereka kwa achikondi ake, Asiriya, amene iye ankawalakalaka.
«پس، من او را به دست آشوری‌ها تسلیم نمودم، به دست کسانی که خدایانشان را اینقدر دوست می‌داشت!
10 Iwowa anamuvula, namulanda ana ake aamuna ndi aakazi ndipo anamupha ndi lupanga. Ndipo atalangidwa choncho, iye anasanduka chinthu chonyozeka pakati pa akazi.
ایشان رختهای او را کندند و او را کشتند و بچه‌هایش را برای بردگی با خود بردند. زنان دیگر از سرنوشت او درس عبرت گرفتند و دانستند که او به سزای اعمالش رسیده است.
11 “Mphwake Oholiba anaona zimenezi natengerako. Koma iye anachita zachiwerewere kuposa mkulu wake.
«اهولیبه، یعنی اورشلیم، با اینکه دید بر سر خواهرش چه آمد، اما در هوسرانی و زناکاری از او هم فاسدتر شد.
12 Iyenso anakangamira Asiriya, abwanamkubwa, olamulira asilikali, ankhondo ovala zovala zonse za nkhondo ndi okwera pa akavalo. Onsewa anali anyamata osiririka.
او به همسایه خود قوم آشور، دل بست که مردانی جذاب، خوش‌اندام و سرداران و سوارکارانی با لباسهای آبی خوشرنگ بودند.
13 Ndinaona kuti iyenso anadziyipitsa; ndipo onse awiriwo anatsata njira imodzi.
دیدم که او نیز آلوده شد و به راه خواهر بزرگترش رفت.
14 “Koma Oholiba uja anachita chigololo kopitirira mkulu wake. Iye anaona zithunzi za amuna pa khoma, zithunzi za Ababuloni zolembedwa ndi inki yofiira,
«او روز‌به‌روز بیشتر در عمق فساد غرق می‌شد. او مجذوب تصاویری گردید که بر دیوار نقش شده بود، تصاویر سرداران بابِلی با لباسهای قرمز، کمربندهای زیبا و کلاه‌های رنگارنگ!
15 atamanga malamba mʼchiwuno mwawo ndi kuvala nduwira pa mitu yawo. Onse amaoneka ngati atsogoleri a magaleta a Ababuloni, mbadwa za ku Kaldeya.
16 Oholiba atangowaona, anawalakalaka ndipo anatuma amithenga ku Kaldeya kukawayitana.
وقتی این تصاویر را دید، شعله عشق بابِلی‌ها در دلش زبانه کشید. پس قاصدانی فرستاد و ایشان را نزد خود دعوت کرد.
17 Ndipo Ababuloni anabwera nʼkudzagona naye. Choncho mwa chilakolako chawo anamuyipitsa. Koma atamuyipitsa choncho, iye ananyansidwa nawo.
آنها نیز آمده، با او زنا کردند و آنقدر او را بی‌عصمت و نجس ساختند که سرانجام از ایشان متنفر شد و با ایشان قطع رابطه نمود.
18 Iye atachita chiwerewere chake poyera ndi kuonetsa umaliseche wake, Ine ndinamuchokera monyansidwa monga mmene ndinachitira ndi mʼbale wake.
«من هم وقتی دیدم که اینچنین خود را در اختیار دیگران می‌گذارد تا با او زنا کنند، از او بیزار شدم، همان‌گونه که از خواهرش بیزار شده بودم.
19 Koma anachitabe zachiwerewere osalekeza. Ankakumbukira masiku a ubwana wake pamene ankachita za chiwerewere mʼdziko la Igupto.
اما او دوران جوانی و زناکاریهای خود را در مصر به یاد آورد و به فساد و هوسرانی خود افزود و با مردان شهوتران به فسق و فجور پرداخت.
20 Kumeneko iye ankalakalaka zibwenzi zake, amene ziwalo zawo zinali ngati za abulu ndipo kutentha kwawo kunali ngati kwa akavalo.
21 Motero, iwe Oholiba unafuna kuchitanso zadama monga unkachitira ku Igupto pamene unali mtsikana. Nthawi imene ija ankakusisita pa chifuwa ndi kugwiragwira mawere ako osagwa aja.
بله، او با حسرت، به فساد و هرزگی خود در مصر می‌اندیشید، به دورانی که بکارت خود را در اختیار مصری‌ها گذاشت!
22 “Tsono iwe Oholiba, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakudzutsira zibwenzi zako zimene unkanyansidwa nazo zija kuti zilimbane nawe. Ndidzaziyitana kuti zibwere kuchokera mbali zonse.
«حال، ای اهولیبه، خداوند یهوه چنین می‌فرماید: «اینک من همان قومهایی را که عاشقشان بودی و اکنون از ایشان متنفر شده‌ای، تحریک خواهم کرد که از هر سو علیه تو گرد آیند.
23 Ndidzayitana anthu a ku Babuloni ndi Akaldeya onse, anthu a ku Pekodi, Sowa ndi Kowa pamodzi ndi Asiriya onse. Onsewa ndi amuna osiririka, abwanamkubwa, atsogoleri a ankhondo, oyenda pa magaleta, anthu a maudindo akuluakulu. Onsewa ndi okwera akavalo.
بله، بابِلیان و تمام کلدانیان از فقود، شوع و قوع، و به همراه ایشان همهٔ آشوری‌ها که جوانانی خوب چهره و والامقام و چابک سوارند، خواهند آمد.
24 Iwo adzabwera kudzalimbana nawe ndi zida za nkhondo, magaleta ndi ngolo, pamodzi ndi anthu ambiri. Adzakuzinga mbali zonse atavala zishango zankhondo ndi zipewa zankhondo. Ndidzakupereka kwa iwo kuti akulange ndipo adzakulanga monga momwe adzafunire.
ایشان از شمال با سپاهی آماده، همراه با کالسکه‌ها و ارابه‌ها به جنگ تو خواهند آمد. مردانی که تا دندان مسلح می‌باشند، از هر سو تو را محاصره خواهند کرد و من تو را به ایشان تسلیم خواهم نمود تا مطابق راه و رسم خودشان، تو را مجازات نمایند.
25 Ndidzaonetsa mkwiyo wanga pa iwe ndipo iwo adzakulanga iwe mwankhanza. Adzadula mphuno zanu ndi makutu anu, ndipo amene adzatsalira mwa iwe adzaphedwa ndi lupanga. Iwo adzakulanda ana ako aamuna ndi aakazi ndipo amene adzatsalira adzaphedwa ndi moto.
آتش خشم من بر تو شعله‌ور خواهد شد و خواهم گذاشت که با غضب با تو رفتار کنند. آنان بینی و گوشهایت را خواهند برید، بازماندگانت را خواهند کشت و فرزندانت را به اسارت خواهند برد؛ و هر چه باقی بماند، خواهند سوزاند؛
26 Adzakuvulaninso zovala zanu ndikukulandani zodzikongoletsera zanu zamtengowapatali.
ایشان رختهایت را خواهند کند و جواهرات زیبایت را به یغما خواهند برد.
27 Motero ndidzathetsa zonyansa zako ndi zachigololo zomwe unaziyamba ku Igupto. Choncho sudzalakalaka za ku Igupto kapena kuzikumbukiranso.
«آنگاه به هرزگی و زناکاری‌ات که از مصر به ارمغان آورده‌ای، پایان خواهم داد تا دیگر مشتاق مصر و خدایانش نباشی.
28 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikukupereka mʼmanja mwa amene amadana nawe, kwa iwo amene unawafulatira moyipidwa nawo.
زیرا من تو را در چنگ دشمنانت رها خواهم نمود، یعنی در چنگ همان کسانی که از ایشان بیزار و متنفر هستی.
29 Adzachita nawe mwachidani. Adzakulanda zonse zimene unagwirira ntchito. Adzakusiya wamaliseche ndiponso wausiwa. Kuyipa kwa makhalidwe ako achiwerewere kudzakhala pammbalambanda. Zonyansa zako ndi chiwerewere chako,
آنان با نفرت و کینه، هر چه که داری به زور گرفته، لخت و عریان رهایت خواهند کرد تا رسوایی و زناکاری‌ات بر همه آشکار شود.
30 zabweretsa izi pa iwe chifukwa unachita zonyansa ndi anthu a mitundu ndi kudziyipitsa ndi mafano awo.
«تمام این بلاها به این علّت بر سرت می‌آید که خدایان قومهای دیگر را پرستش نمودی و با این کار، خود را نجس و ناپاک ساختی؛
31 Unatsata zochita za mkulu wako; choncho Ine ndidzayika chikho cha chilango chake mʼdzanja lako.
تو راه خواهرت را در پیش گرفتی، بنابراین، من از جام او به تو نیز خواهم نوشانید.
32 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Udzamwera chikho cha mkulu wako, chikho chachikulu ndi chakuya; anthu adzakuseka ndi kukunyoza, pakuti chikhocho ndi chodzaza kwambiri.
«خداوند یهوه چنین می‌گوید: «از جام بزرگ و عمیق مجازات خواهرت، تو نیز خواهی نوشید؛ جامی که از تمسخر و استهزا پر است.
33 Udzaledzera ndipo mtima wako udzadzaza ndi chisoni. Chimenechi ndi chikho chachiwonongeko ndi chipasupasu, chikho cha mkulu wako Samariya.
مستی و اضطراب دامنگیرت خواهد شد، زیرا جام تو مانند جام خواهرت لبریز از دهشت و ویرانی خواهد شد.
34 Udzamwa chikhocho mpaka kugugudiza. Tsono udzaphwanyaphwanya chikhocho ndipo udzangʼamba mawere ako ndi zigoba zake. Ine ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
تو آن جام را تا به آخر سر خواهی کشید. سپس آن را خُرد خواهی کرد و به سینۀ خود خواهی کوبید. من، خداوند یهوه این را می‌گویم!
35 “Chifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza wandiyiwala Ine ndi kundifulatira, chomwecho uyenera kulangidwa chifukwa cha zonyansa zako ndi chiwerewere chako.”
«از آنجا که مرا فراموش کردی و از من روگردان شدی، سزای زناکاریها و گناهانت را خواهی دید!
36 Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza Ohola ndi Oholiba? Tsono uwayimbe mlandu chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
«ای پسر انسان، اهوله و اهولیبه را محکوم کن! گناهان کثیفشان را اعلام نما!
37 Iwo achita chigololo ndipo anapha anthu. Anachita chigololo popembedza mafano awo. Ngakhale ana amene anandiberekera Ine anawapereka kwa mafanowo ngati chakudya chawo.
ایشان مرتکب زنا و قتل شدند، بت‌پرستی کردند، و پسرانی را که برای من زاییده بودند بر مذبحهای خود قربانی کرده، سوزاندند.
38 Anachitanso izi: Iwo anayipitsa malo anga opatulika ndi kudetsa masabata anga.
علاوه بر این کارها، در همان روز، خانهٔ مرا نجس کردند و روز شَبّات را بی‌حرمت ساختند.
39 Atapereka ana awo kwa mafano, tsiku lomwelo anakalowanso mʼNyumba yanga yopatulika ndi kuyipitsamo. Izi ndi zimene anachita mʼNyumba mwanga.
آری، در همان روزی که فرزندان خود را برای بتهایشان قربانی کردند، به خانه من آمدند تا آن را بی‌حرمت سازند. آری، با این عملشان خانۀ مرا آلوده کردند!
40 “Iwo anatuma amithenga kukayitana amuna a ku mayiko akutali. Anthuwo atabwera, abale awiri aja anasambasamba, kudzola utoto wodzikometsera kumaso, kenaka ndi kuvala zovala zamakaka.
«این دو خواهر قاصدانی نیز به سرزمینهای دور دست فرستادند تا مردان آنجا را فرا خوانند، یعنی کاهنان و بتهایشان را. هنگامی که آمدند، با استقبال گرم آن دو روبرو شدند. آن دو خواهر، همچون روسپی‌ها، استحمام کردند، به چشمانشان سرمه کشیدند، و خود را به بهترین زیورآلات آراستند.
41 Anakhala pa bedi lokongola ndipo patsogolo pawo panali tebulo pamene munayikapo lubani ndi mafuta. Zonse zowapatsa Ine.
آنگاه با هم روی رختخواب زیبای قلابدوزی نشستند و بخور و روغنی را که از آنِ خانه من بود، بر سفره‌ای در مقابل خود گذاردند.
42 “Mfuwu wa chigulu cha anthu unamveka. Anthu oledzera ochokera ku chipululu anabwera pamodzi ndi anthu wamba ndipo anaveka akaziwo zibangiri kumanja ndi zipewa zaufumu zokongola ku mutu.
از آنجا صدای مردان عیاش شنیده می‌شد، مردانی هرزه، میگسار و بیابانگرد؛ آنها النگو به دست ایشان کردند و تاج زیبا بر سرشان گذاردند.
43 Ndipo ine ndinati za mkazi wotheratu ndi chigololoyo, ‘Tsono asiyeni kuti achite naye monga wachiwerewere, pakuti ichi ndi chimene iye ali basi.’
با خود گفتم که آیا ایشان رغبت می‌کنند با این فاحشه‌های زشت و فرتوت زنا کنند؟
44 Tsono anapita kwa iwo monga mmene anthu amapitira kwa mkazi wadama. Momwemo anapita kwa Ohola ndi kwa Oholiba kukachita nawo zadama.
با این حال، ایشان با همان میل و رغبت مردان شهوترانی که پیش فاحشه‌ها می‌روند، نزد اُهوله و اُهولیبه، این روسپی‌های بی‌حیا رفتند!
45 Koma anthu olungama adzawazenga anthuwa mlandu wa chigololo ndi wa kupha anthu. Ndi iwodi anthu achigololo ndiponso mʼmanja mwawo muli magazi.
بنابراین، اشخاص درستکار، آن دو را محکوم خواهند کرد، زیرا زناکارند و دستشان به خون آلوده است.
46 “Ambuye Yehova akuti: Itanitsani chigulu cha anthu kuti chidzawalange ndi kulanda chuma chawo.
«از این رو، من جماعت بزرگی را علیه ایشان خواهم فرستاد تا ایشان را پریشان ساخته، تاراج نمایند.
47 Anthuwo adzawaponye miyala akazi awiriwo ndi kuwatema ndi malupanga awo. Ana awo aamuna ndi aakazi adzawaphe ndi kutentha nyumba zawo.
آن جماعت آنان را سنگسار کرده، با شمشیر خواهند درید؛ پسران و دختران ایشان را خواهند کشت و خانه‌هایشان را خواهند سوزاند.
48 “Motero Ine ndidzathetsa zachigololo mʼdzikomo, ndipo akazi onse adzatengapo phunziro kuti asadzachite zachigololo monga za iwowo.
آنگاه در این سرزمین، به هرزگی و زناکاری پایان خواهم داد، تا این درس عبرتی گردد برای آنانی که بت‌پرستی را دوست می‌دارند.
49 Ndidzawalanga chifukwa cha ntchito zawo za dama ndipo adzazunzika chifukwa cha tchimo lawo lopembedza mafano. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.”
آن دو خواهر به سزای تمام زناکاریها و بت‌پرستی‌هایشان خواهند رسید. آنگاه خواهند دانست که من خداوند یهوه می‌باشم!»

< Ezekieli 23 >