< Ezekieli 23 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
Opět stalo se slovo Hospodinovo ke mně, řkoucí:
2 “Iwe mwana wa munthu, panali atsikana awiri ana a mayi mmodzi.
Synu člověčí, dvě ženy, dcery jedné mateře byly.
3 Iwo ankachita za chiwerewere ku Igupto. Za chiwerewerezo anayamba ali achichepere. Kumeneko anthu ankangowasisita pa chifuwa ndi kuwagwiragwira mawere awo aja.
Ty smilnily v Egyptě, v mladosti své smilnily. Tam jsou mačkány prsy jejich, tam opiplány prsy panenství jejich.
4 Wamkulu dzina lake anali Ohola, ndipo mngʼono wakeyo anali Oholiba. Ine ndinawakwatira ndipo anabereka ana aamuna ndi ana aakazi. Ohola ndiye Samariya, ndipo Yerusalemu ndiye Oholiba.
Jména pak jejich: větší Ahola, sestry pak její Aholiba. Tyť jsou byly mé, a rozplodily syny a dcery. Jména, pravím, jejich jsou: Samaří Ahola, Jeruzaléma pak Aholiba.
5 “Ohola anachita zachiwerewere ngakhale anali mkazi wanga; ndipo iye anakangamira abwenzi ake a ku Asiriya.
Ale Ahola maje mne, smilnila a frejů hleděla s milovníky svými, s Assyrskými blízkými,
6 Amenewo anali asilikali ovala zibakuwa zamlangali, abwanamkubwa ndiponso atsogoleri a nkhondo. Onsewo anali anyamata osiririka ndipo ankakwera pa akavalo.
Oděnými postavcem modrým, s vývodami a knížaty, i všemi napořád mládenci krásnými, a s jezdci jezdícími na koních.
7 Ohola anachita zachiwerewere ndi onsewa, anthu otchuka a ku Asiriya. Iye anadziyipitsa ndi mafano a munthu aliyense amene anagona naye.
Vydala se, pravím, v smilství svá s nimi, se všemi nejpřednějšími syny Assyrskými, a se všemi, jimž frejovala, a poškvrnila se všemi ukydanými bohy jejich.
8 Iye sanaleke za chiwerewere zimene anaziphunzira ku Igupto. Paja akanali mtsikana anyamata ankagona naye. Iwo ankamusisita mawere akanali anthete nachita naye zachiwerewere.
A tak smilství svých Egyptských nenechala; nebo ji zléhali v mladosti její, a oni mačkali prsy panenství jejího, a vylili smilství svá na ni.
9 “Nʼchifukwa chake Ine ndinamupereka kwa achikondi ake, Asiriya, amene iye ankawalakalaka.
Protož dal jsem ji v ruku frejířů jejích, v ruku Assyrských, jimž frejovala.
10 Iwowa anamuvula, namulanda ana ake aamuna ndi aakazi ndipo anamupha ndi lupanga. Ndipo atalangidwa choncho, iye anasanduka chinthu chonyozeka pakati pa akazi.
Oniť jsou odkryli nahotu její, syny i dcery její pobrali, ji pak samu mečem zamordovali. Takž vzata jest na slovo od jiných žen, když soudy vykonali při ní.
11 “Mphwake Oholiba anaona zimenezi natengerako. Koma iye anachita zachiwerewere kuposa mkulu wake.
To viděla sestra její Aholiba, však mnohem více než onano frejovala, a smilství její větší byla než smilství sestry její.
12 Iyenso anakangamira Asiriya, abwanamkubwa, olamulira asilikali, ankhondo ovala zovala zonse za nkhondo ndi okwera pa akavalo. Onsewa anali anyamata osiririka.
S Assyrskými frejů hleděla, s vývodami a knížaty blízkými, oděnými nádherně, s jezdci jezdícími na koních, a všemi mládenci krásnými.
13 Ndinaona kuti iyenso anadziyipitsa; ndipo onse awiriwo anatsata njira imodzi.
I viděl jsem, že se poškvrnila, a že cesta jednostejná jest obou dvou.
14 “Koma Oholiba uja anachita chigololo kopitirira mkulu wake. Iye anaona zithunzi za amuna pa khoma, zithunzi za Ababuloni zolembedwa ndi inki yofiira,
Ale tato ještě to přičinila k smilstvím svým, že viduc muže vyryté na stěně, obrazy Kaldejských vymalované barvou,
15 atamanga malamba mʼchiwuno mwawo ndi kuvala nduwira pa mitu yawo. Onse amaoneka ngati atsogoleri a magaleta a Ababuloni, mbadwa za ku Kaldeya.
Přepásané pasem po bedrách jejich, a klobouky barevné na hlavách jejich, a že jsou všickni na pohledění jako hejtmané, podobní synům Babylonským v Kaldejské zemi, jejichž ona vlast jest,
16 Oholiba atangowaona, anawalakalaka ndipo anatuma amithenga ku Kaldeya kukawayitana.
I zahořela k nim z pohledění očima svýma, a vyslala posly k nim do země Kaldejské.
17 Ndipo Ababuloni anabwera nʼkudzagona naye. Choncho mwa chilakolako chawo anamuyipitsa. Koma atamuyipitsa choncho, iye ananyansidwa nawo.
Tedy vešli k ní Babylonští na lůže nepoctivé, a poškvrnili ji smilstvím svým. A když se poškvrnila s nimi, odloučila se duše její od nich.
18 Iye atachita chiwerewere chake poyera ndi kuonetsa umaliseche wake, Ine ndinamuchokera monyansidwa monga mmene ndinachitira ndi mʼbale wake.
A odkryla smilství svá, odkryla též nahotu svou, i odloučila se duše má od ní, tak jako se odloučila duše má od sestry její.
19 Koma anachitabe zachiwerewere osalekeza. Ankakumbukira masiku a ubwana wake pamene ankachita za chiwerewere mʼdziko la Igupto.
Nebo rozmnožila smilství svá, rozpomínajíc se na dny mladosti své, v nichž smilnila v zemi Egyptské,
20 Kumeneko iye ankalakalaka zibwenzi zake, amene ziwalo zawo zinali ngati za abulu ndipo kutentha kwawo kunali ngati kwa akavalo.
A frejovala s kuběnáři jejich, jejichž tělo jest jako tělo oslů, a tok jejich jako tok koňský.
21 Motero, iwe Oholiba unafuna kuchitanso zadama monga unkachitira ku Igupto pamene unali mtsikana. Nthawi imene ija ankakusisita pa chifuwa ndi kugwiragwira mawere ako osagwa aja.
A tak jsi zase navrátila se k nešlechetnosti mladosti své, když mačkali Egyptští prsy tvé z příčiny prsů mladosti tvé.
22 “Tsono iwe Oholiba, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakudzutsira zibwenzi zako zimene unkanyansidwa nazo zija kuti zilimbane nawe. Ndidzaziyitana kuti zibwere kuchokera mbali zonse.
Protož ó Aholiba, takto praví Panovník Hospodin: Aj, já vzbudím frejíře tvé proti tobě, ty, od nichž se odloučila duše tvá, a přivedu je na tě odevšad,
23 Ndidzayitana anthu a ku Babuloni ndi Akaldeya onse, anthu a ku Pekodi, Sowa ndi Kowa pamodzi ndi Asiriya onse. Onsewa ndi amuna osiririka, abwanamkubwa, atsogoleri a ankhondo, oyenda pa magaleta, anthu a maudindo akuluakulu. Onsewa ndi okwera akavalo.
Babylonské a všecky Kaldejské, Pekodské, a Šohejské, i Kohejské, všecky syny Assyrské s nimi, mládence krásné, vývody a knížata všecka, hejtmany a slovoutné, všecky jezdící na koních.
24 Iwo adzabwera kudzalimbana nawe ndi zida za nkhondo, magaleta ndi ngolo, pamodzi ndi anthu ambiri. Adzakuzinga mbali zonse atavala zishango zankhondo ndi zipewa zankhondo. Ndidzakupereka kwa iwo kuti akulange ndipo adzakulanga monga momwe adzafunire.
A přitáhnou na tě na vozích železných a přikrytých, i kárách, a to s zběří národů, s pavézami a štíty i lebkami, položí se proti tobě vůkol, i předložím jim právo, aby tě soudili soudy svými.
25 Ndidzaonetsa mkwiyo wanga pa iwe ndipo iwo adzakulanga iwe mwankhanza. Adzadula mphuno zanu ndi makutu anu, ndipo amene adzatsalira mwa iwe adzaphedwa ndi lupanga. Iwo adzakulanda ana ako aamuna ndi aakazi ndipo amene adzatsalira adzaphedwa ndi moto.
Vyleji zajisté horlení své na tebe, tak že naloží s tebou prchlivě, nos tvůj i uši tvé odejmou, a ostatek tebe mečem padne. Ti syny tvé i dcery tvé poberou, a ostatek tebe spáleno bude ohněm.
26 Adzakuvulaninso zovala zanu ndikukulandani zodzikongoletsera zanu zamtengowapatali.
A vyvlekou tě z roucha tvého, a rozberou šperky okrasy tvé.
27 Motero ndidzathetsa zonyansa zako ndi zachigololo zomwe unaziyamba ku Igupto. Choncho sudzalakalaka za ku Igupto kapena kuzikumbukiranso.
A tak přítrž učiním při tobě nešlechetnosti tvé, i smilství tvému z země Egyptské vzatému, a nepozdvihneš očí svých k nim, a na Egypt nezpomeneš více.
28 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikukupereka mʼmanja mwa amene amadana nawe, kwa iwo amene unawafulatira moyipidwa nawo.
Nebo takto praví Panovník Hospodin: Aj, já dám tebe v ruku těch, kterýchž nenávidíš, v ruku těch, od nichž se odloučila duše tvá,
29 Adzachita nawe mwachidani. Adzakulanda zonse zimene unagwirira ntchito. Adzakusiya wamaliseche ndiponso wausiwa. Kuyipa kwa makhalidwe ako achiwerewere kudzakhala pammbalambanda. Zonyansa zako ndi chiwerewere chako,
I budou nakládati s tebou podlé nenávisti, a poberou všecko úsilé tvé, a nechají tě nahé a obnažené. A tak bude zřejmá nahota smilství tvého a nešlechetnosti tvé, smilství, pravím, tvého.
30 zabweretsa izi pa iwe chifukwa unachita zonyansa ndi anthu a mitundu ndi kudziyipitsa ndi mafano awo.
Což vše učiní tobě proto, že jsi smilnila, následujíc pohanů, proto že jsi poškvrnila se ukydanými bohy jejich.
31 Unatsata zochita za mkulu wako; choncho Ine ndidzayika chikho cha chilango chake mʼdzanja lako.
Cestou sestry své chodila jsi, protož dám kalich její v ruku tvou.
32 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Udzamwera chikho cha mkulu wako, chikho chachikulu ndi chakuya; anthu adzakuseka ndi kukunyoza, pakuti chikhocho ndi chodzaza kwambiri.
Takto praví Panovník Hospodin: Kalich sestry své píti budeš hluboký a široký; budeť sporý, tak že smích a žert budou míti z tebe.
33 Udzaledzera ndipo mtima wako udzadzaza ndi chisoni. Chimenechi ndi chikho chachiwonongeko ndi chipasupasu, chikho cha mkulu wako Samariya.
Opilstvím a zámutkem naplněna budeš, kalichem pustiny a zpuštění, kalichem sestry své Samaří.
34 Udzamwa chikhocho mpaka kugugudiza. Tsono udzaphwanyaphwanya chikhocho ndipo udzangʼamba mawere ako ndi zigoba zake. Ine ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
I vypiješ jej a vyvážíš, a než jej polámeš, snáze prsy své roztrháš; neboť jsem já mluvil, praví Panovník Hospodin.
35 “Chifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza wandiyiwala Ine ndi kundifulatira, chomwecho uyenera kulangidwa chifukwa cha zonyansa zako ndi chiwerewere chako.”
Protož takto praví Panovník Hospodin: Z té příčiny, že jsi zapomenula na mne, a zavrhlas mne za hřbet svůj, i ty také vezmi za svou nešlechetnost, a za smilství svá.
36 Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza Ohola ndi Oholiba? Tsono uwayimbe mlandu chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
I řekl Hospodin ke mně: Synu člověčí, budeš-liž zastávati Ahole neb Aholiby? Nýbrž oznam jim ohavnosti jejich,
37 Iwo achita chigololo ndipo anapha anthu. Anachita chigololo popembedza mafano awo. Ngakhale ana amene anandiberekera Ine anawapereka kwa mafanowo ngati chakudya chawo.
Že cizoložily, a krev jest na rukou jejich, a s ukydanými bohy svými cizoložily. Také i syny své, kteréž mně zplodily, vodily jim, aby sežráni byli.
38 Anachitanso izi: Iwo anayipitsa malo anga opatulika ndi kudetsa masabata anga.
Ještě i toto činily mi, že zanečišťovaly svatyni mou v tentýž den, a sobot mých poškvrňovaly.
39 Atapereka ana awo kwa mafano, tsiku lomwelo anakalowanso mʼNyumba yanga yopatulika ndi kuyipitsamo. Izi ndi zimene anachita mʼNyumba mwanga.
Nebo obětovavše syny své ukydaným bohům svým, vcházely do svatyně mé v tentýž den, aby ji poškvrnily. Aj hle, takť jsou činívaly u prostřed mého domu.
40 “Iwo anatuma amithenga kukayitana amuna a ku mayiko akutali. Anthuwo atabwera, abale awiri aja anasambasamba, kudzola utoto wodzikometsera kumaso, kenaka ndi kuvala zovala zamakaka.
Nadto, že vysílaly k mužům, jenž by přišli zdaleka, kteříž, jakž posel vyslán k nim, aj, hned přicházívali. Jimž jsi se umývala, a tvář svou líčila, a okrašlovalas se okrasou.
41 Anakhala pa bedi lokongola ndipo patsogolo pawo panali tebulo pamene munayikapo lubani ndi mafuta. Zonse zowapatsa Ine.
A usazovalas se na loži slavném, před nímž stůl připravený byl, na něž jsi i kadidlo mé i masti mé vynakládala.
42 “Mfuwu wa chigulu cha anthu unamveka. Anthu oledzera ochokera ku chipululu anabwera pamodzi ndi anthu wamba ndipo anaveka akaziwo zibangiri kumanja ndi zipewa zaufumu zokongola ku mutu.
Když pak hlas toho množství poutichl, tedy i k mužům z obecného lidu vysílaly, jenž bývali přivozováni ožralí z pouště. I dávali náramky na ruce jejich, i koruny ozdobné na hlavy jejich.
43 Ndipo ine ndinati za mkazi wotheratu ndi chigololoyo, ‘Tsono asiyeni kuti achite naye monga wachiwerewere, pakuti ichi ndi chimene iye ali basi.’
A ačkoli jsem se domlouval na cizoložství té lotryně, a že oni jednak s jednou, jednak s druhou smilství provodí,
44 Tsono anapita kwa iwo monga mmene anthu amapitira kwa mkazi wadama. Momwemo anapita kwa Ohola ndi kwa Oholiba kukachita nawo zadama.
A že každý z nich vchází k ní, tak jako někdo vchází k ženě nevěstce: však vždy vcházeli k Ahole a Aholibě, ženám přenešlechetným.
45 Koma anthu olungama adzawazenga anthuwa mlandu wa chigololo ndi wa kupha anthu. Ndi iwodi anthu achigololo ndiponso mʼmanja mwawo muli magazi.
Protož muži spravedliví, tiť je souditi budou soudem cizoložných a soudem těch, jenž vylévaly krev, proto že cizoložily, a krev jest na rukou jejich.
46 “Ambuye Yehova akuti: Itanitsani chigulu cha anthu kuti chidzawalange ndi kulanda chuma chawo.
Nebo takto praví Panovník Hospodin: Přivedu na ně vojsko, a dám je v posmýkání i v loupež.
47 Anthuwo adzawaponye miyala akazi awiriwo ndi kuwatema ndi malupanga awo. Ana awo aamuna ndi aakazi adzawaphe ndi kutentha nyumba zawo.
I uhází je to shromáždění kamením, a poseká je meči svými; syny jejich i dcery jejich pomordují, a domy jejich ohněm popálí.
48 “Motero Ine ndidzathetsa zachigololo mʼdzikomo, ndipo akazi onse adzatengapo phunziro kuti asadzachite zachigololo monga za iwowo.
A tak přítrž učiním nešlechetnosti v zemi této, i budou se tím káti všecky ženy, a nedopustí se nešlechetnosti podobné vaší.
49 Ndidzawalanga chifukwa cha ntchito zawo za dama ndipo adzazunzika chifukwa cha tchimo lawo lopembedza mafano. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.”
Nebo vzložena bude na vás nešlechetnost vaše, a ponesete hříchy ukydaných bohů svých. I zvíte, že já jsem Panovník Hospodin.

< Ezekieli 23 >