< Ezekieli 23 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
Hina Gode da nama amane sia: i,
2 “Iwe mwana wa munthu, panali atsikana awiri ana a mayi mmodzi.
“Dunu egefe! Dalusi aduna esalu.
3 Iwo ankachita za chiwerewere ku Igupto. Za chiwerewerezo anayamba ali achichepere. Kumeneko anthu ankangowasisita pa chifuwa ndi kuwagwiragwira mawere awo aja.
Ela da a: finia Idibidi sogega esalu, dunu da elama dawa: digi dagoi, amola ela da hina: da: i bidi lasu uda hamosu.
4 Wamkulu dzina lake anali Ohola, ndipo mngʼono wakeyo anali Oholiba. Ine ndinawakwatira ndipo anabereka ana aamuna ndi ana aakazi. Ohola ndiye Samariya, ndipo Yerusalemu ndiye Oholiba.
Magobo ea dio da Ouhoula (ea fedege da Samelia soge) amola eya ea dio da Ouhouliba (ea fedege da Yelusaleme). Na da ele galu lale, mano lalelegei.
5 “Ohola anachita zachiwerewere ngakhale anali mkazi wanga; ndipo iye anakangamira abwenzi ake a ku Asiriya.
Ouhoula da Na: , be ea wadela: i lasu hou hame fisi. E da ema dawa: digisu Asilia dunu ilima gilisili golamusa: bagade hanai galu.
6 Amenewo anali asilikali ovala zibakuwa zamlangali, abwanamkubwa ndiponso atsogoleri a nkhondo. Onsewo anali anyamata osiririka ndipo ankakwera pa akavalo.
Ilia da dadi gagui ouligisu dunu, abula nina: hamoi haisewe amoga ga: i. Huluane da hosi da: iya fila heda: le ahoasu.
7 Ohola anachita zachiwerewere ndi onsewa, anthu otchuka a ku Asiriya. Iye anadziyipitsa ndi mafano a munthu aliyense amene anagona naye.
E da amo Asilia dadi gagui ouligisu dunu amola gilisili golale, amola ilima bagade hanaiba: le, e da Asilia ogogosu ‘gode’ ilima nodone sia: ne gadoiba: le, ea hou hi ledo hamoi.
8 Iye sanaleke za chiwerewere zimene anaziphunzira ku Igupto. Paja akanali mtsikana anyamata ankagona naye. Iwo ankamusisita mawere akanali anthete nachita naye zachiwerewere.
E da Idibidi ganodini, wadela: i lasu hou muni hemosu, amo mae yolele, hamonanu. E da a: finia ganini, dunu da ema gilisili golasu dawa: digi. Ilia da e da hina: da: i bidi lasu uda defele dawa: i.
9 “Nʼchifukwa chake Ine ndinamupereka kwa achikondi ake, Asiriya, amene iye ankawalakalaka.
E da ea Asilia dawa: digisu dunu ilima bagade hanaiba: le, Na da e ilima iagai.
10 Iwowa anamuvula, namulanda ana ake aamuna ndi aakazi ndipo anamupha ndi lupanga. Ndipo atalangidwa choncho, iye anasanduka chinthu chonyozeka pakati pa akazi.
Ilia da ea abula gigisa: le fasili, nabado yolesili, ea mano huluane fane legei. Amalu, ilia da eme gegesu gobihei bagade amoga fane legei. Uda huluane da ea bogobeba: le, ema doaga: i hou udigili sia: dasu.
11 “Mphwake Oholiba anaona zimenezi natengerako. Koma iye anachita zachiwerewere kuposa mkulu wake.
Ea eya Ouhouliba da amo hou ba: i dagoi. Be ea wadela: i hanai lasu hou da eaba Ouhoula amo ea hou bagade baligi.
12 Iyenso anakangamira Asiriya, abwanamkubwa, olamulira asilikali, ankhondo ovala zovala zonse za nkhondo ndi okwera pa akavalo. Onsewa anali anyamata osiririka.
E amola da Asilia dadi gagui ouligisu dunu, abula nina: hamoi haisewe amoga ga: i amola hosi da: iya fila heda: le ahoasu, ilima gilisili golamusa: hanai bagade galu.
13 Ndinaona kuti iyenso anadziyipitsa; ndipo onse awiriwo anatsata njira imodzi.
Na ba: loba, e da udigili hi hanaiga adole lasu hou hamonanu. Amola, e da eaba ea hou defele wadela: le hamosu.
14 “Koma Oholiba uja anachita chigololo kopitirira mkulu wake. Iye anaona zithunzi za amuna pa khoma, zithunzi za Ababuloni zolembedwa ndi inki yofiira,
15 atamanga malamba mʼchiwuno mwawo ndi kuvala nduwira pa mitu yawo. Onse amaoneka ngati atsogoleri a magaleta a Ababuloni, mbadwa za ku Kaldeya.
E da wadela: i hou dewane hamonanu. E da Ba: bilone ouligisu ilia ifaga dobea damana dununa debei, amo da ulasuga unasi amola abulaga bulu idiniginisi amola abula habuga ilia dialumaga figisi, amo ba: beba: le, ilima hanai galu.
16 Oholiba atangowaona, anawalakalaka ndipo anatuma amithenga ku Kaldeya kukawayitana.
E da amo ba: beba: le, ili gilisili golamusa: bagade hanai galu. E da ilima sia: alofele iasu dunu asunasi.
17 Ndipo Ababuloni anabwera nʼkudzagona naye. Choncho mwa chilakolako chawo anamuyipitsa. Koma atamuyipitsa choncho, iye ananyansidwa nawo.
Ba: bilone dunu da ema gilisili golamusa: misi. Ilia da ema bagadewane gilisili golabeba: le, e da ea hanai gumini ilima hihi.
18 Iye atachita chiwerewere chake poyera ndi kuonetsa umaliseche wake, Ine ndinamuchokera monyansidwa monga mmene ndinachitira ndi mʼbale wake.
Amalalu, e da ea wadela: i lasu hou amola da: i nabadowane mae gogosiane dunu huluane odagiaba: le ahoasu. Na da eaba wadela: i houba: le higa: i amo defele, ea hou higasu.
19 Koma anachitabe zachiwerewere osalekeza. Ankakumbukira masiku a ubwana wake pamene ankachita za chiwerewere mʼdziko la Igupto.
E da wadela: i lasu hou baligili hamoi. E da a: finia Idibidi sogega degabo hamoi amo defele hamoi.
20 Kumeneko iye ankalakalaka zibwenzi zake, amene ziwalo zawo zinali ngati za abulu ndipo kutentha kwawo kunali ngati kwa akavalo.
E da ema dawa: digi dunu amo ilia sema bagade da dougi ea sema agoai, amoma bagade hanasu.
21 Motero, iwe Oholiba unafuna kuchitanso zadama monga unkachitira ku Igupto pamene unali mtsikana. Nthawi imene ija ankakusisita pa chifuwa ndi kugwiragwira mawere ako osagwa aja.
Ouhouliba! Di da dia musa: wadela: i adole lasu hou Idibidi sogega hamoi (amogai dunu da dia dodo lala bugisu, amola di da dia dunu hame dawa: digisu hou amo degabo fisi) amo bu hamomu bagade hanai galu.
22 “Tsono iwe Oholiba, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakudzutsira zibwenzi zako zimene unkanyansidwa nazo zija kuti zilimbane nawe. Ndidzaziyitana kuti zibwere kuchokera mbali zonse.
Defea! Ouhouliba! Na, Ouligisudafa Hina Gode, da dima amane sia: sa, ‘Di da dima dawa: digisu dunuma wali higasa. Be amo dunu Na da dima ougima: ne hamomu, amola di sisiga: ma: ne, ili oule misunu.
23 Ndidzayitana anthu a ku Babuloni ndi Akaldeya onse, anthu a ku Pekodi, Sowa ndi Kowa pamodzi ndi Asiriya onse. Onsewa ndi amuna osiririka, abwanamkubwa, atsogoleri a ankhondo, oyenda pa magaleta, anthu a maudindo akuluakulu. Onsewa ndi okwera akavalo.
Na da Ba: bilone dunu, Ga: ledia: ne dunu, Bigode dunu, Sioua dunu, Goua dunu, amola Asilia dunu huluane oule misunu. Na da ayeligi ouligisu dunu amola dadi gagui ouligisu dunu amola dadi gagui ouligisu bagade amo da hosi da: iya fila heda: le ahoa, amo huluane gagadole, oule misunu.
24 Iwo adzabwera kudzalimbana nawe ndi zida za nkhondo, magaleta ndi ngolo, pamodzi ndi anthu ambiri. Adzakuzinga mbali zonse atavala zishango zankhondo ndi zipewa zankhondo. Ndidzakupereka kwa iwo kuti akulange ndipo adzakulanga monga momwe adzafunire.
Ilia da dadi gagui gilisisu bagade, amola ‘sa: liode’ bagohame amola hosiga hiougi liligi gaguli ahoasu amo oule misini, ga (north) la: di amoga dima doagala: mu. Ilia da gaga: su liligi amola gaga: su habuga gaga: iwane, dima sisiga: mu. Na da di ilima iagamu, amola ilia da ilia malei defele dima fofada: mu.
25 Ndidzaonetsa mkwiyo wanga pa iwe ndipo iwo adzakulanga iwe mwankhanza. Adzadula mphuno zanu ndi makutu anu, ndipo amene adzatsalira mwa iwe adzaphedwa ndi lupanga. Iwo adzakulanda ana ako aamuna ndi aakazi ndipo amene adzatsalira adzaphedwa ndi moto.
Ilia dima ougiwane se ima: ne, Na da logo doasimu. Bai Na amola da dima ougiba: le. Ilia da dia mi amola ge hedofalesilalu, dia mano huluane fane legemu. Dafawane! Ilia da mano huluane lale, esalumuna: laluma gobesimu.
26 Adzakuvulaninso zovala zanu ndikukulandani zodzikongoletsera zanu zamtengowapatali.
Ilia da dia abula gisa: le fasili, dia nina: hamoi liligi lamu.
27 Motero ndidzathetsa zonyansa zako ndi zachigololo zomwe unaziyamba ku Igupto. Choncho sudzalakalaka za ku Igupto kapena kuzikumbukiranso.
Di Idibidi esalua amonini wadela: i lasu hou amola gegebole sia: ne bagade hamosu. Be amo logo Na da hedofamu. Di da ogogosu ‘gode’ ili bu hame ba: mu, amola Idibidi ea hou bu hame dawa: mu.”
28 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikukupereka mʼmanja mwa amene amadana nawe, kwa iwo amene unawafulatira moyipidwa nawo.
Ouligisudafa Hina Gode da amane sia: sa, “Na da di, dunu fi amo di da bagadewane higasa, ilima iagamu.
29 Adzachita nawe mwachidani. Adzakulanda zonse zimene unagwirira ntchito. Adzakusiya wamaliseche ndiponso wausiwa. Kuyipa kwa makhalidwe ako achiwerewere kudzakhala pammbalambanda. Zonyansa zako ndi chiwerewere chako,
Ilia da di bagadewane higabeba: le, dia liligi di da hawa: hamone lai, amo huluane lamu. Ilia dia abula gisa: le fasili, hina: da: i bidi lasu uda defele, da: i nabado agoane yolesimu.
30 zabweretsa izi pa iwe chifukwa unachita zonyansa ndi anthu a mitundu ndi kudziyipitsa ndi mafano awo.
Di da wadela: i lasu hanaiba: le, amola da: i bidi lasu hou dawa: beba: le, amo logo di fawane fodoi.
31 Unatsata zochita za mkulu wako; choncho Ine ndidzayika chikho cha chilango chake mʼdzanja lako.
Di da diaba ea hou amoma fa: no bobogei. Amaiba: le, Na da ema se bidi iasu defele, dima imunu.”
32 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Udzamwera chikho cha mkulu wako, chikho chachikulu ndi chakuya; anthu adzakuseka ndi kukunyoza, pakuti chikhocho ndi chodzaza kwambiri.
Ouligisudafa Hina Gode da amane sia: sa, “Di da diaba ea faigelei amoga waini hano manu. Amo faigelei da bagade amola osodogone gala. Dunu huluane da dima higale oufesega: mu. Bai faigelei da nabai dagoi.
33 Udzaledzera ndipo mtima wako udzadzaza ndi chisoni. Chimenechi ndi chikho chachiwonongeko ndi chipasupasu, chikho cha mkulu wako Samariya.
Amo faigelei (diaba Samelia ea faigelei) da wadela: lesisu amola beda: igia: su amoga nabai gala. Amo nasea, di da bagadewane da: i dione feloale masunu.
34 Udzamwa chikhocho mpaka kugugudiza. Tsono udzaphwanyaphwanya chikhocho ndipo udzangʼamba mawere ako ndi zigoba zake. Ine ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
Di da amo waini hano nanu, faigelei da ebelele hafoga: i dagoi ba: mu. Faigelei da goudane, di da sosoa: i amoga dia bida: igi fofa: gimu. Na, Ouligisudafa Hina Gode da sia: i dagoi.”
35 “Chifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza wandiyiwala Ine ndi kundifulatira, chomwecho uyenera kulangidwa chifukwa cha zonyansa zako ndi chiwerewere chako.”
Wali, Ouligisudafa Hina Gode da amane sia: sa, “Di Nama gogolele amola baligi fa: iba: le, di da dia wadela: i lasu hanai hou amola dia da: i hodo bidi lasu hou amo hamobeba: le, se bagade hahanini nabimu.”
36 Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza Ohola ndi Oholiba? Tsono uwayimbe mlandu chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
Hina Gode da nama amane sia: i, “Dunu egefe! Di da Ouhoula amola Ouhouliba amolama fofada: musa: momagebela: ? Ela da baligili wadela: le hamobeba: le, elama diwaneya udidima!
37 Iwo achita chigololo ndipo anapha anthu. Anachita chigololo popembedza mafano awo. Ngakhale ana amene anandiberekera Ine anawapereka kwa mafanowo ngati chakudya chawo.
Ela da fedege agoane, ogogosu ‘gode’ ilima nodone sia: ne gadobeba: le, inia dunu adole lasu hou hamosu. Amola, mano ela da Nama lalelegei, amo medole lelegesu. Ela da Na manolali amo ogogosu “gode” liligima gobele salasu.
38 Anachitanso izi: Iwo anayipitsa malo anga opatulika ndi kudetsa masabata anga.
Be amo fawane hame. Ela da Na Debolo Diasu ledo hamoi amola Sa: bade eso malei Na hamoi, amo wadela: lesi.
39 Atapereka ana awo kwa mafano, tsiku lomwelo anakalowanso mʼNyumba yanga yopatulika ndi kuyipitsamo. Izi ndi zimene anachita mʼNyumba mwanga.
Eso amogalawane ela da Na mano fuga: le, ogogosu loboga hamoi ‘gode’ ilima gobele sali, ela Na Debolo amoga misini ledo hamoi dagoi.
40 “Iwo anatuma amithenga kukayitana amuna a ku mayiko akutali. Anthuwo atabwera, abale awiri aja anasambasamba, kudzola utoto wodzikometsera kumaso, kenaka ndi kuvala zovala zamakaka.
Eso enoenoi ela da dunu badilia esala, amo elama misa: ne sia: musa: , sia: na ahoasu dunu asunasi. Amalalu, amo dunu da elama misi. Ela da hano ulasili, siba: le ulasu uli, nina: hamoma: ne, su gaga: su.
41 Anakhala pa bedi lokongola ndipo patsogolo pawo panali tebulo pamene munayikapo lubani ndi mafuta. Zonse zowapatsa Ine.
Ela da fila heda: su fafai ida: iwane amoga fisu, amola ilia liligi legesu fafai amo da: iya, liligi ida: iwane gala, mogili da gabusiga: manoma amola olife susuligi (amo Na da elagili i) amo dialebe ba: su.
42 “Mfuwu wa chigulu cha anthu unamveka. Anthu oledzera ochokera ku chipululu anabwera pamodzi ndi anthu wamba ndipo anaveka akaziwo zibangiri kumanja ndi zipewa zaufumu zokongola ku mutu.
Dunu gilisisu amo ilia hahawane gugulubi da nabasu. Ilia da dunu eno hafoga: i sogega esalu, amo elama oule misi. Ilia da ela loboga nabu ga: si amola ela dialumaga habuga ida: iwane figisi.
43 Ndipo ine ndinati za mkazi wotheratu ndi chigololoyo, ‘Tsono asiyeni kuti achite naye monga wachiwerewere, pakuti ichi ndi chimene iye ali basi.’
Amola Na da Nisu amane sia: i, ‘Asilia dunu da uda amo da wadela: i lasu bagade hamobeba: le, gasa hame ba: sa, amoma wadela: i lasu hou hamonanebe.
44 Tsono anapita kwa iwo monga mmene anthu amapitira kwa mkazi wadama. Momwemo anapita kwa Ohola ndi kwa Oholiba kukachita nawo zadama.
Ilia da wadela: i da: i bidi lasu uda amoma enoenoia buhagisu. Ilia da Ouhoula amola Ouhouliba (wadela: i hina: da: i bidi lasu uda) elama buhagisu.
45 Koma anthu olungama adzawazenga anthuwa mlandu wa chigololo ndi wa kupha anthu. Ndi iwodi anthu achigololo ndiponso mʼmanja mwawo muli magazi.
Moloi hamosu dunu da elama disili sia: mu. Bai ela da inia dunu adole lasu amola medole legesu hou hamosu.”
46 “Ambuye Yehova akuti: Itanitsani chigulu cha anthu kuti chidzawalange ndi kulanda chuma chawo.
Ouligisudafa Hina Gode da amane sia: sa, “Ela beda: ma: ne amola ela liligi gegena lama: ne, dunu wa: i elama oule misa.
47 Anthuwo adzawaponye miyala akazi awiriwo ndi kuwatema ndi malupanga awo. Ana awo aamuna ndi aakazi adzawaphe ndi kutentha nyumba zawo.
Dunu wa: i da ela igiga medoma: mu amola gegesu gobihei sedadega ela doagala: ma: mu amola ela mano medole legema: mu amola ela diasu ulagisima: mu.
48 “Motero Ine ndidzathetsa zachigololo mʼdzikomo, ndipo akazi onse adzatengapo phunziro kuti asadzachite zachigololo monga za iwowo.
Isala: ili fi soge huluane amo ganodini, Na da wadela: i lasu hou hedofamu. Amasea, uda huluane da ela inia dunu adole lasu hou defele mae hamoma: ne, sisasu agoane ba: mu.
49 Ndidzawalanga chifukwa cha ntchito zawo za dama ndipo adzazunzika chifukwa cha tchimo lawo lopembedza mafano. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.”
Amola dalusi aduna, alia: ! Alia da wadela: i lasu hou hamobeba: le, amola ogogosu loboga hamoi ‘gode’ ilima nodone sia: ne gadobeba: le, Na da alima se bidi imunu. Amasea, alia da Na da Ouligisu Hina Godedafa dawa: mu.”

< Ezekieli 23 >