< Ezekieli 22 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
Un Tā Kunga vārds notika uz mani sacīdams:
2 “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza mzinda uwo wa anthu akupha anzawo? Tsono uwudzudzule chifukwa cha machitidwe ake onse onyansa
Tad nu, ak cilvēka bērns, vai gribi tiesāt, vai gribi tiesāt to asins pilsētu? Tad rādi viņai visas viņas negantības.
3 ndipo unene kuti, ‘Ambuye akuti: Iwe mzinda umene wadzigwetsa wekha mʼtsoka pa kukhetsa magazi pakati pako ndi kudziyipitsa popanga mafano,
Un saki: tā saka Tas Kungs Dievs: ak pilsēta, kas asinis izlej savā vidū, lai viņas laiks nāk, un kas sev taisa elkus un apgānās.
4 wapezekatu wolakwa chifukwa cha magazi amene wakhetsa, ndipo wadziyipitsa chifukwa cha mafano amene wapanga. Choncho wachepetsa masiku ako, ndipo zaka zako zafika kumapeto. Nʼchifukwa chake ndalola kuti anthu a mitundu ina akunyoze ndiponso kuti anthu a mayiko onse akuseke.
Caur tām asinīm, ko izlējusi, tu esi noziegusies, un ar saviem elkiem, ko taisījusi, tu esi sagānījusies, un tavām dienām esi likusi tuvu nākt, un esi nākusi savos gados. Tādēļ Es tevi esmu nodevis pagāniem par nievāšanu un visām zemēm par apsmieklu.
5 Mayiko amene ali pafupi ndi mayiko omwe ali kutali adzakunyoza, iwe mzinda wa mbiri yoyipa, wodzaza ndi chiwawa.
Kas tuvu un kas tālu no tevis, tie tevi apsmies, tevi, kam vārds sagānīts un kas nekārtības pilna.
6 “‘Taona momwe aliyense wa atsogoleri a Israeli amagwiritsira mphamvu zake kupha anthu.
Redzi, Israēla valdnieki ikviens cik spēdams izlej asinis tavā vidū.
7 Mu mzindamo anthu amanyoza abambo ndi amayi awo. Iwo amapondereza alendo ndi kuzunza ana amasiye ndi akazi amasiye.
Tēvu un māti tie pie tevis nicina, svešiniekam tie dara varas darbu tavā vidū, bāriņus un atraitnes tie apspiež pie tevis.
8 Wanyoza zinthu zanga zopatulika ndi kuyipitsa Masabata anga.
Manus svētumus tu nicini, un Manas svētās dienas tu sagāni.
9 Mwa iwe muli anthu onenera anzawo zabodza kuti aphedwe. Mwa iwe mulinso amene amadyera zansembe pa mapiri a chipembedzo. Enanso amachita zonyansa.
Mēlneši ir pie tevis, kas asinis izlej; tie ēd tavā vidū uz (elku)kalniem, dara bezkaunību tavā vidū.
10 Mwa iwe muli ena ogonana ndi akazi a abambo awo, muli enanso amene amavuta akazi pamene ali woyipitsidwa ndi msambo.
Tie atsedz pie tevis tēva kaunumu, un pieguļ pie tevis sārņiem nešķīstas sievas.
11 Ena amachita chigololo ndi akazi a anzawo, ndipo ena, mopanda manyazi, amayipitsa mkazi wa mwana wawo. Palinso ena amene amayipitsa alongo awo, ana aakazi a abambo awo.
Cits ar sava tuvāka sievu dara negantību, cits bezkaunīgi apgāna savu vedeklu, atkal cits atzīst savu māsu, sava tēva meitu, tavā vidū.
12 Mwa iwe muli anthu amene amalandira ziphuphu kuti aphe anzawo; ena amachita katapira ndi kupeza phindu loposera muyeso; enanso amapeza phindu mwachinyengo poopseza anzawo. Ndipo mwandiyiwala Ine, akutero Ambuye Yehova.
Tie ņem pie tevis dāvanas, izliet asinis; tu piedzen augļus un plēs pagaidus, un esi plēsīga pie sava tuvākā ar varasdarbu, bet Mani tu esi aizmirsusi, saka Tas Kungs Dievs.
13 “‘Koma Ine ndachita kuwomba mʼmanja kuti phuu nʼkudabwa chifukwa cha phindu lachinyengo limene mwapeza ndiponso chifukwa cha kuphana kumene kumachitika pakati panu.
Redzi, tad Es sasitu savas rokas par to mantu, ko tu plēsi, un par tām asinīm, kas tavā vidū izlietas.
14 Kodi mtima wako udzakhala wolimbabe kapena manja ako adzakhalabe amphamvu ndikadzatsiriza kukulanga iwe? Ine Yehova ndayankhula, ndipo ndidzazichitadi.
Vai tava sirds pastāvēs, vai tavas rokas būs stipras tanīs dienās, kad Es ar tevi tiesāšos? Es Tas Kungs to esmu runājis un to darīšu.
15 Ndidzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukumwazirani ku mayiko onse. Umu ndi mmene ndidzachotsere zoyipa zako.
Un Es tevi izkaisīšu starp tautām un tevi izklīdināšu pa valstīm un darīšu galu tavai nešķīstībai tavā vidū.
16 Udzanyozedwa pamaso pa anthu a mitundu ina. Pambuyo pake udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
Un tu būsi nesvēta caur sevi pašu priekš pagānu acīm un samanīsi, ka Es esmu Tas Kungs.
17 Yehova anandiyankhula nati:
Un Tā Kunga vārds notika uz mani sacīdams:
18 “Iwe mwana wa munthu, Aisraeli asanduka chinthu cha chabechabe kwa Ine. Onse ali ngati mkuwa, chitini, chitsulo ndi mtovu zotsala mʼngʼanjo atayeretsa siliva.
Cilvēka bērns! Israēla nams Man ir palicis par sārņiem, tie visi ir varš un alva un dzelzs un svins ceplī, tie ir palikuši par sudraba sārņiem.
19 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Pakuti nonse mwasanduka chinthu cha chabechabe, Ine ndidzakusonkhanitsani mu Yerusalemu.
Tādēļ tā saka Tas Kungs Dievs: Tāpēc ka jūs visi esat palikuši par sārņiem, tad redzi, Es jūs sapulcināšu Jeruzālemes vidū.
20 Monga momwe anthu amasonkhanitsira siliva, mkuwa, chitsulo, mtovu ndi chitini mʼngʼanjo ndi kusonkhetsa moto kuti azisungunule, motero Inenso ndidzakusonkhanitsani ndili wokwiya ndi waukali, ndipo ndidzakuyikani mʼkati mwa mzinda, ndikukusungunurani.
Tā kā sudrabu un varu un dzelzi un svinu un alvu kopā liek ceplī, un uguni uzpūš apakšā, lai kausē, tā Es jūs sapulcināšu Savā dusmībā un bardzībā, un jūs ielikšu un kausēšu.
21 Ndidzakusonkhanitsani mu mzindamo ndi kukoleza moto wa mkwiyo wanga, ndipo inu mudzasungunuka mu mzindamo.
Tiešām, Es jūs sapulcināšu un uzpūtīšu pret jums Savas dusmības uguni, ka jūs tur iekšā topat kausēti.
22 Monga siliva amasungunulidwa mʼngʼanjo, kotero inunso mudzasungunuka mʼkati mwa mzinda ndipo Inu mudzadziwa kuti Ine Yehova ndakukwiyirani.’”
Tā kā sudrabs ceplī top kausēts, tāpat jūs tur tapsiet kausēti, un jūs samanīsiet, ka Es, Tas Kungs, Savu bardzību esmu izlējis pār jums.
23 Yehova anandiyankhulanso nati,
Un Tā Kunga vārds notika uz mani sacīdams:
24 “Iwe mwana wa munthu, uza dziko la Israeli kuti, ‘Iwe ndiwe dziko losayeretsedwa, ndiponso losavumbidwa ndi mvula chifukwa cha mkwiyo wanga.’
Cilvēka bērns, saki uz to: tu esi zeme, kas nav šķīstīta, kur nelīst dusmības dienā.
25 Atsogoleri ake mu mzindamo ali ngati mkango wobangula pogwira nyama. Apha anthu, alanda chuma ndi zinthu za mtengowapatali, ndiponso asandutsa amayi ambiri kukhala amasiye.
Viņas pravieši cēluši dumpi viņas vidū; tā kā rūcošs lauva, kad tas laupījumu laupa, tā tie ēd dvēseles, tie plēš naudu un mantu, tie dara daudz atraitņu viņas vidū.
26 Ansembe ake amaphwanya lamulo langa ndi kuyipitsa zinthu zanga zopatulika. Sasiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba. Saphunzitsa anthu kusiyana kwa zinthu zoyenera pa chipembedzo ndi zinthu zosayenera. Sasamalira za kusunga masabata anga. Motero Ine ndimanyozedwa pakati pawo.
Viņas priesteri neganti pārkāpj manu bauslību un sagāna manus svētumus, tie neizšķir svētu un nesvētu un nemāca izšķirt, kas šķīsts un kas nešķīsts, tie apsedz savas acis priekš manām, svētām dienām, un es viņu starpā topu sagānīts.
27 Atsogoleri ake ali ngati mimbulu yokhadzula nyama; amakhetsa magazi ndi kupha anthu kuti apeze phindu loyipa.
Viņas virsnieki ir viņas vidū kā vilki, kas laupa laupījumu, izlej asinis, samaitā dvēseles, mantas kārības dēļ.
28 Aneneri ake amabisa zonsezi monga muja amachitira anthu popaka njereza. Amazimphimba ndi zabodza zimene aona mʼmasomphenya awo ndi zonama za mʼmawula awo. Iwo amati, ‘Ambuye Yehova akuti,’ pamene Ine Yehova sindinayankhule.
Un viņas pravieši tos apmet ar nelīpamiem kaļķiem un redz aplamas parādīšanas un sludina tiem melus un saka: tā saka Tas Kungs Dievs; un tomēr Tas Kungs nav runājis.
29 Anthu a mʼdzikomo amasautsa anzawo ndi kulanda anthu osowa. Amazunza anthu osauka ndi amphawi. Amavutitsa alendo posawachitira zinthu mwachilungamo.
Tie ļaudis tai zemē dara varas darbu un laupīt laupa, un nabagu un bēdīgu tie plēš un svešinieku tie nospaida bez tiesas.
30 “Ndinafunafuna munthu pakati pawo woti amange linga, woti ayimirire dziko pamaso panga kundipepesa kuti ndisaliwononge, koma sindinamupeze.
Tad Es meklēju kādu vīru no tiem, kas atkal sataisītu sētu un stātos plaisumā, manā priekšā aizstāvēt to zemi, ka Es to nemaitātu, bet Es neatradu neviena.
31 Nʼchifukwa chake ndawakwiyira kwambiri. Ndawawonongeratu ndi mkwiyo wanga woyaka ngati moto. Ndawalanga molingana ndi zimene anachita. Akutero Ambuye Yehova.”
Tāpēc Es pār tiem esmu izlējis Savu bardzību, ar Savas dusmības uguni Es tiem esmu galu darījis, viņu grēkus Es tiem esmu metis uz viņu galvu, saka Tas Kungs Dievs.

< Ezekieli 22 >