< Ezekieli 22 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
La parole de l'Éternel me fut adressée en ces mots:
2 “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza mzinda uwo wa anthu akupha anzawo? Tsono uwudzudzule chifukwa cha machitidwe ake onse onyansa
Et toi, fils de l'homme, juge; juge la ville sanguinaire, et fais-lui connaître toutes ses abominations.
3 ndipo unene kuti, ‘Ambuye akuti: Iwe mzinda umene wadzigwetsa wekha mʼtsoka pa kukhetsa magazi pakati pako ndi kudziyipitsa popanga mafano,
Dis: Ainsi a dit le Seigneur, l'Éternel: Ville qui répands le sang dans ton sein, afin que ton jour arrive, et qui te fais des idoles pour en être souillée!
4 wapezekatu wolakwa chifukwa cha magazi amene wakhetsa, ndipo wadziyipitsa chifukwa cha mafano amene wapanga. Choncho wachepetsa masiku ako, ndipo zaka zako zafika kumapeto. Nʼchifukwa chake ndalola kuti anthu a mitundu ina akunyoze ndiponso kuti anthu a mayiko onse akuseke.
Par le sang que tu as répandu, tu t'es rendue coupable, et par les idoles que tu as faites, tu t'es souillée. Tu as avancé tes jours, et tu es parvenue au terme de tes années; c'est pourquoi je vais faire de toi un objet d'opprobre pour les nations, et de moquerie pour tous les pays.
5 Mayiko amene ali pafupi ndi mayiko omwe ali kutali adzakunyoza, iwe mzinda wa mbiri yoyipa, wodzaza ndi chiwawa.
Ceux qui sont près et ceux qui sont loin se moqueront de toi, qui es souillée de réputation et remplie de troubles.
6 “‘Taona momwe aliyense wa atsogoleri a Israeli amagwiritsira mphamvu zake kupha anthu.
Voici, dans ton sein les princes d'Israël contribuent de tout leur pouvoir à répandre le sang.
7 Mu mzindamo anthu amanyoza abambo ndi amayi awo. Iwo amapondereza alendo ndi kuzunza ana amasiye ndi akazi amasiye.
Chez toi, l'on méprise père et mère; chez toi, on use de violence envers l'étranger; chez toi, on opprime l'orphelin et la veuve.
8 Wanyoza zinthu zanga zopatulika ndi kuyipitsa Masabata anga.
Tu méprises mes choses saintes, et tu profanes mes sabbats.
9 Mwa iwe muli anthu onenera anzawo zabodza kuti aphedwe. Mwa iwe mulinso amene amadyera zansembe pa mapiri a chipembedzo. Enanso amachita zonyansa.
Chez toi, se trouvent des calomniateurs pour répandre le sang; chez toi, on mange sur les montagnes; chez toi, l'on commet des atrocités.
10 Mwa iwe muli ena ogonana ndi akazi a abambo awo, muli enanso amene amavuta akazi pamene ali woyipitsidwa ndi msambo.
Chez toi, on découvre la nudité d'un père; chez toi, l'on humilie la femme à l'époque de sa souillure.
11 Ena amachita chigololo ndi akazi a anzawo, ndipo ena, mopanda manyazi, amayipitsa mkazi wa mwana wawo. Palinso ena amene amayipitsa alongo awo, ana aakazi a abambo awo.
Chez toi, l'un se livre à des abominations avec la femme de son prochain, l'autre souille sa belle-fille par l'inceste, et l'autre fait violence à sa sœur, la fille de son père.
12 Mwa iwe muli anthu amene amalandira ziphuphu kuti aphe anzawo; ena amachita katapira ndi kupeza phindu loposera muyeso; enanso amapeza phindu mwachinyengo poopseza anzawo. Ndipo mwandiyiwala Ine, akutero Ambuye Yehova.
Chez toi, l'on reçoit des présents pour répandre le sang; tu prends l'intérêt et l'usure, tu dépouilles ton prochain par la violence, et tu m'oublies, dit le Seigneur, l'Éternel.
13 “‘Koma Ine ndachita kuwomba mʼmanja kuti phuu nʼkudabwa chifukwa cha phindu lachinyengo limene mwapeza ndiponso chifukwa cha kuphana kumene kumachitika pakati panu.
Voici, je frappe des mains à cause des spoliations que tu as commises, et du sang qui a été répandu au milieu de toi.
14 Kodi mtima wako udzakhala wolimbabe kapena manja ako adzakhalabe amphamvu ndikadzatsiriza kukulanga iwe? Ine Yehova ndayankhula, ndipo ndidzazichitadi.
Ton cœur tiendra-t-il bon, tes mains resteront-elles fermes, dans les jours où j'agirai contre toi? Moi, l'Éternel, j'ai parlé, et je le ferai.
15 Ndidzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukumwazirani ku mayiko onse. Umu ndi mmene ndidzachotsere zoyipa zako.
Je te disperserai parmi les nations; je te disséminerai en divers pays, et je ferai disparaître la souillure du milieu de toi.
16 Udzanyozedwa pamaso pa anthu a mitundu ina. Pambuyo pake udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
Alors tu seras avilie par toi-même, aux yeux des nations, et tu sauras que je suis l'Éternel.
17 Yehova anandiyankhula nati:
La parole de l'Éternel me fut adressée en ces mots:
18 “Iwe mwana wa munthu, Aisraeli asanduka chinthu cha chabechabe kwa Ine. Onse ali ngati mkuwa, chitini, chitsulo ndi mtovu zotsala mʼngʼanjo atayeretsa siliva.
Fils de l'homme, la maison d'Israël est devenue pour moi comme des scories; ils sont tous de l'airain, de l'étain, du fer et du plomb dans un creuset; ce sont des scories d'argent.
19 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Pakuti nonse mwasanduka chinthu cha chabechabe, Ine ndidzakusonkhanitsani mu Yerusalemu.
C'est pourquoi, ainsi a dit le Seigneur, l'Éternel: Parce que vous êtes tous devenus semblables à des scories, voici je vous rassemblerai au milieu de Jérusalem.
20 Monga momwe anthu amasonkhanitsira siliva, mkuwa, chitsulo, mtovu ndi chitini mʼngʼanjo ndi kusonkhetsa moto kuti azisungunule, motero Inenso ndidzakusonkhanitsani ndili wokwiya ndi waukali, ndipo ndidzakuyikani mʼkati mwa mzinda, ndikukusungunurani.
Comme on réunit dans le creuset l'argent, l'airain, le fer, le plomb et l'étain, et qu'on y souffle le feu afin de les fondre, ainsi je vous rassemblerai dans ma colère et dans ma fureur, et je vous mettrai au creuset pour vous fondre.
21 Ndidzakusonkhanitsani mu mzindamo ndi kukoleza moto wa mkwiyo wanga, ndipo inu mudzasungunuka mu mzindamo.
Je vous amasserai, je soufflerai contre vous le feu de ma fureur, et vous serez fondus au milieu de Jérusalem.
22 Monga siliva amasungunulidwa mʼngʼanjo, kotero inunso mudzasungunuka mʼkati mwa mzinda ndipo Inu mudzadziwa kuti Ine Yehova ndakukwiyirani.’”
Comme fond l'argent dans un creuset, ainsi vous serez fondus au milieu d'elle, et vous saurez que moi, l'Éternel, j'ai répandu sur vous ma fureur.
23 Yehova anandiyankhulanso nati,
La parole de l'Éternel me fut encore adressée en ces mots:
24 “Iwe mwana wa munthu, uza dziko la Israeli kuti, ‘Iwe ndiwe dziko losayeretsedwa, ndiponso losavumbidwa ndi mvula chifukwa cha mkwiyo wanga.’
Fils de l'homme, dis à Jérusalem: Tu es une terre qui n'a point été purifiée, et qui n'est point arrosée de pluie au jour de la colère.
25 Atsogoleri ake mu mzindamo ali ngati mkango wobangula pogwira nyama. Apha anthu, alanda chuma ndi zinthu za mtengowapatali, ndiponso asandutsa amayi ambiri kukhala amasiye.
Ses prophètes forment des complots en son sein; pareils au lion rugissant qui déchire sa proie, ils dévorent les âmes, ils s'emparent des richesses et des choses précieuses et multiplient les veuves au milieu d'elle.
26 Ansembe ake amaphwanya lamulo langa ndi kuyipitsa zinthu zanga zopatulika. Sasiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba. Saphunzitsa anthu kusiyana kwa zinthu zoyenera pa chipembedzo ndi zinthu zosayenera. Sasamalira za kusunga masabata anga. Motero Ine ndimanyozedwa pakati pawo.
Ses sacrificateurs violent ma loi et profanent mes choses saintes; ils ne distinguent pas entre ce qui est saint et ce qui est profane; ils ne font pas connaître la différence entre ce qui est souillé et ce qui est pur; ils ferment les yeux sur mes sabbats, et je suis profané au milieu d'eux.
27 Atsogoleri ake ali ngati mimbulu yokhadzula nyama; amakhetsa magazi ndi kupha anthu kuti apeze phindu loyipa.
Ses chefs dans son sein sont pareils à des loups qui dévorent leur proie en répandant le sang, en perdant les âmes pour commettre des rapines.
28 Aneneri ake amabisa zonsezi monga muja amachitira anthu popaka njereza. Amazimphimba ndi zabodza zimene aona mʼmasomphenya awo ndi zonama za mʼmawula awo. Iwo amati, ‘Ambuye Yehova akuti,’ pamene Ine Yehova sindinayankhule.
Ses prophètes les enduisent de mortier; ils ont des visions trompeuses, et prononcent des oracles menteurs en disant: “Ainsi a dit le Seigneur, l'Éternel”, quand l'Éternel n'a point parlé.
29 Anthu a mʼdzikomo amasautsa anzawo ndi kulanda anthu osowa. Amazunza anthu osauka ndi amphawi. Amavutitsa alendo posawachitira zinthu mwachilungamo.
Le peuple du pays use de violence; ils commettent des rapines, et font tort à l'affligé et au pauvre, et contrairement à toute justice ils oppriment l'étranger.
30 “Ndinafunafuna munthu pakati pawo woti amange linga, woti ayimirire dziko pamaso panga kundipepesa kuti ndisaliwononge, koma sindinamupeze.
Je cherche au milieu d'eux quelqu'un qui relève la muraille, qui se tienne sur la brèche devant ma face en faveur du pays, afin que je ne le détruise pas; mais je ne trouve personne.
31 Nʼchifukwa chake ndawakwiyira kwambiri. Ndawawonongeratu ndi mkwiyo wanga woyaka ngati moto. Ndawalanga molingana ndi zimene anachita. Akutero Ambuye Yehova.”
C'est pourquoi je répandrai sur eux ma fureur, et je les consumerai par le feu de ma colère; je ferai retomber leur conduite sur leurs têtes, dit le Seigneur, l'Éternel.

< Ezekieli 22 >