< Ezekieli 22 >
1 Yehova anandiyankhula nati:
La parole de Yahweh me fut adressée en ces termes:
2 “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza mzinda uwo wa anthu akupha anzawo? Tsono uwudzudzule chifukwa cha machitidwe ake onse onyansa
« Et toi, fils de l’homme, jugeras-tu, jugeras-tu la ville de sang? Fais-lui connaître toutes ses abominations,
3 ndipo unene kuti, ‘Ambuye akuti: Iwe mzinda umene wadzigwetsa wekha mʼtsoka pa kukhetsa magazi pakati pako ndi kudziyipitsa popanga mafano,
et dis: Ainsi parle le Seigneur Yahweh: Ville qui répand le sang au dedans d’elle, pour que son temps vienne, et qui se couvre d’idoles infâmes pour se souiller!
4 wapezekatu wolakwa chifukwa cha magazi amene wakhetsa, ndipo wadziyipitsa chifukwa cha mafano amene wapanga. Choncho wachepetsa masiku ako, ndipo zaka zako zafika kumapeto. Nʼchifukwa chake ndalola kuti anthu a mitundu ina akunyoze ndiponso kuti anthu a mayiko onse akuseke.
Par le sang que tu as répandu, tu t’es rendue criminelle; par les idoles infâmes que tu as faites, tu t’es souillée; et tu as ainsi avancé tes jours, et tu es parvenue au terme de tes années. C’est pourquoi je t’ai rendue un objet d’ opprobre pour les nations et une risée dans tous les pays.
5 Mayiko amene ali pafupi ndi mayiko omwe ali kutali adzakunyoza, iwe mzinda wa mbiri yoyipa, wodzaza ndi chiwawa.
Ceux qui sont près et ceux qui sont loin de toi se moqueront de toi, souillée de réputation, grande en désordre!
6 “‘Taona momwe aliyense wa atsogoleri a Israeli amagwiritsira mphamvu zake kupha anthu.
Voici que les princes d’Israël, chacun selon ses forces, sont occupés chez toi à répandre le sang.
7 Mu mzindamo anthu amanyoza abambo ndi amayi awo. Iwo amapondereza alendo ndi kuzunza ana amasiye ndi akazi amasiye.
Chez toi, on méprise père et mère; au milieu de toi, on maltraite l’étranger; chez toi, on opprime l’orphelin et la veuve.
8 Wanyoza zinthu zanga zopatulika ndi kuyipitsa Masabata anga.
Tu méprises mon sanctuaire et tu profanes mes sabbats.
9 Mwa iwe muli anthu onenera anzawo zabodza kuti aphedwe. Mwa iwe mulinso amene amadyera zansembe pa mapiri a chipembedzo. Enanso amachita zonyansa.
Il y a chez toi des gens qui calomnient pour répandre le sang; chez toi, on mange sur les montagnes; on commet des énormités au milieu de toi.
10 Mwa iwe muli ena ogonana ndi akazi a abambo awo, muli enanso amene amavuta akazi pamene ali woyipitsidwa ndi msambo.
Chez toi, on découvre la nudité de son père; chez toi, on fait violence à la femme pendant sa souillure.
11 Ena amachita chigololo ndi akazi a anzawo, ndipo ena, mopanda manyazi, amayipitsa mkazi wa mwana wawo. Palinso ena amene amayipitsa alongo awo, ana aakazi a abambo awo.
L’un commet l’abomination avec la femme de son prochain, un autre souille par l’impureté sa belle-fille chez toi, un autre fait violence à sa sœur, fille de son père.
12 Mwa iwe muli anthu amene amalandira ziphuphu kuti aphe anzawo; ena amachita katapira ndi kupeza phindu loposera muyeso; enanso amapeza phindu mwachinyengo poopseza anzawo. Ndipo mwandiyiwala Ine, akutero Ambuye Yehova.
Chez toi, ou reçoit des présents pour répandre le sang; tu prends l’usure et un intérêt; tu dépouilles par la violence ton prochain; et moi, tu m’oublies, — oracle du Seigneur Yahweh.
13 “‘Koma Ine ndachita kuwomba mʼmanja kuti phuu nʼkudabwa chifukwa cha phindu lachinyengo limene mwapeza ndiponso chifukwa cha kuphana kumene kumachitika pakati panu.
Mais voici que je frappe dans ma main à cause du gain déshonnête que tu as fait, et à cause du sang qui est au milieu de toi.
14 Kodi mtima wako udzakhala wolimbabe kapena manja ako adzakhalabe amphamvu ndikadzatsiriza kukulanga iwe? Ine Yehova ndayankhula, ndipo ndidzazichitadi.
Ton cœur tiendra-t-il bon, tes mains seront-elles fermes aux jours où j’agirai contre toi? Moi, Yahweh, j’ai dit et j’agirai.
15 Ndidzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukumwazirani ku mayiko onse. Umu ndi mmene ndidzachotsere zoyipa zako.
Je te disperserai parmi les nations, je te sèmerai dans les pays, et j’ôterai de toi toute ta souillure,
16 Udzanyozedwa pamaso pa anthu a mitundu ina. Pambuyo pake udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
et tu seras profanée chez toi aux yeux des nations; et tu sauras que je suis Yahweh. »
17 Yehova anandiyankhula nati:
La parole de Yahweh me fut adressée en ces termes:
18 “Iwe mwana wa munthu, Aisraeli asanduka chinthu cha chabechabe kwa Ine. Onse ali ngati mkuwa, chitini, chitsulo ndi mtovu zotsala mʼngʼanjo atayeretsa siliva.
« Fils de l’homme, la maison d’Israël s’ est changée pour moi en scories; eux tous sont de l’airain, de l’étain, du fer et du plomb au milieu du fourneau; ils sont devenus les scories de l’argent.
19 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Pakuti nonse mwasanduka chinthu cha chabechabe, Ine ndidzakusonkhanitsani mu Yerusalemu.
C’est pourquoi ainsi parle le Seigneur Yahweh: Parce que vous êtes tous devenus des scories, à cause de cela, voici que je vais vous rassembler au milieu de Jérusalem.
20 Monga momwe anthu amasonkhanitsira siliva, mkuwa, chitsulo, mtovu ndi chitini mʼngʼanjo ndi kusonkhetsa moto kuti azisungunule, motero Inenso ndidzakusonkhanitsani ndili wokwiya ndi waukali, ndipo ndidzakuyikani mʼkati mwa mzinda, ndikukusungunurani.
Comme ou met ensemble l’argent, l’airain, le fer, le plomb et l’étain au milieu d’un fourneau et qu’on souffle le feu sur le fourneau pour les fondre, ainsi je vous rassemblerai dans ma colère et mon courroux; je vous mettrai là et je vous fondrai.
21 Ndidzakusonkhanitsani mu mzindamo ndi kukoleza moto wa mkwiyo wanga, ndipo inu mudzasungunuka mu mzindamo.
Je vous rassemblerai et je soufflerai sur vous, avec le feu de ma fureur, et vous serez fondus au milieu de Jérusalem.
22 Monga siliva amasungunulidwa mʼngʼanjo, kotero inunso mudzasungunuka mʼkati mwa mzinda ndipo Inu mudzadziwa kuti Ine Yehova ndakukwiyirani.’”
Comme on fond l’argent au milieu d’un fourneau, ainsi vous serez fondus au milieu d’elle; et vous saurez que moi, Yahweh, j’ai répandu mon courroux sur vous. »
23 Yehova anandiyankhulanso nati,
La parole de Yahweh me fut adressée en ces termes:
24 “Iwe mwana wa munthu, uza dziko la Israeli kuti, ‘Iwe ndiwe dziko losayeretsedwa, ndiponso losavumbidwa ndi mvula chifukwa cha mkwiyo wanga.’
« Fils de l’homme, dis-lui: Tu es une terre qui n’a pas été purifiée, qui n’a pas été lavée par la pluie, en un jour de colère.
25 Atsogoleri ake mu mzindamo ali ngati mkango wobangula pogwira nyama. Apha anthu, alanda chuma ndi zinthu za mtengowapatali, ndiponso asandutsa amayi ambiri kukhala amasiye.
Il y a au milieu d’elle une conspiration de ses prophètes. Comme un lion rugissant qui déchire sa proie, ils dévorent les âmes, ils s’emparent des biens et des trésors, ils multiplient ses veuves au milieu d’elle.
26 Ansembe ake amaphwanya lamulo langa ndi kuyipitsa zinthu zanga zopatulika. Sasiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba. Saphunzitsa anthu kusiyana kwa zinthu zoyenera pa chipembedzo ndi zinthu zosayenera. Sasamalira za kusunga masabata anga. Motero Ine ndimanyozedwa pakati pawo.
Ses prêtres ont violé ma loi et profané mon sanctuaire; ils ne distinguent pas entre le saint et le profane; ils n’enseignent pas la différence entre celui qui est souillé et celui qui est pur; ils ferment leurs yeux sur mes sabbats, et je suis profané au milieu d’eux.
27 Atsogoleri ake ali ngati mimbulu yokhadzula nyama; amakhetsa magazi ndi kupha anthu kuti apeze phindu loyipa.
Ses chefs sont au milieu d’elle comme des loups qui déchirent leur proie, répandant le sang, perdant des âmes pour faire des gains.
28 Aneneri ake amabisa zonsezi monga muja amachitira anthu popaka njereza. Amazimphimba ndi zabodza zimene aona mʼmasomphenya awo ndi zonama za mʼmawula awo. Iwo amati, ‘Ambuye Yehova akuti,’ pamene Ine Yehova sindinayankhule.
Et ses prophètes leur plâtrent tous ces crimes; ils ont des visions vaines et des oracles menteurs; ils disent: « Ainsi parle le Seigneur Yahweh »; et Yahweh n’a point parlé.
29 Anthu a mʼdzikomo amasautsa anzawo ndi kulanda anthu osowa. Amazunza anthu osauka ndi amphawi. Amavutitsa alendo posawachitira zinthu mwachilungamo.
Le peuple du pays commet des violences et s’adonne à la rapine; ils foulent le malheureux et l’indigent, et font violence à l’étranger sans motif.
30 “Ndinafunafuna munthu pakati pawo woti amange linga, woti ayimirire dziko pamaso panga kundipepesa kuti ndisaliwononge, koma sindinamupeze.
J’ai cherché parmi eux un homme qui fit une clôture et qui se tint à la brèche devant moi pour le pays, afin que je ne détruise pas; et je ne l’ai pas trouvé.
31 Nʼchifukwa chake ndawakwiyira kwambiri. Ndawawonongeratu ndi mkwiyo wanga woyaka ngati moto. Ndawalanga molingana ndi zimene anachita. Akutero Ambuye Yehova.”
Et j’ai répandu sur eux mon courroux, et je les ai consumés par le feu de ma fureur, et j’ai fait retomber leurs œuvres sur leur tête, — oracle du Seigneur Yahweh. »