< Ezekieli 22 >
1 Yehova anandiyankhula nati:
La parole de Yahvé me fut adressée, en ces termes:
2 “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza mzinda uwo wa anthu akupha anzawo? Tsono uwudzudzule chifukwa cha machitidwe ake onse onyansa
Toi, fils de l'homme, jugeras-tu? Vas-tu juger la ville sanglante? Alors fais-lui connaître toutes ses abominations.
3 ndipo unene kuti, ‘Ambuye akuti: Iwe mzinda umene wadzigwetsa wekha mʼtsoka pa kukhetsa magazi pakati pako ndi kudziyipitsa popanga mafano,
Tu diras: « Le Seigneur Yahvé dit: « Ville qui verse le sang en son sein, pour que son heure vienne, et qui se fait des idoles pour se souiller!
4 wapezekatu wolakwa chifukwa cha magazi amene wakhetsa, ndipo wadziyipitsa chifukwa cha mafano amene wapanga. Choncho wachepetsa masiku ako, ndipo zaka zako zafika kumapeto. Nʼchifukwa chake ndalola kuti anthu a mitundu ina akunyoze ndiponso kuti anthu a mayiko onse akuseke.
Tu t'es rendue coupable par le sang que tu as versé, et tu t'es souillée par les idoles que tu as faites! Tu as fait approcher tes jours, et tu es arrivée au terme de tes années. C'est pourquoi j'ai fait de toi un objet d'opprobre pour les nations, un objet de moquerie pour tous les pays.
5 Mayiko amene ali pafupi ndi mayiko omwe ali kutali adzakunyoza, iwe mzinda wa mbiri yoyipa, wodzaza ndi chiwawa.
Ceux qui sont près de toi et ceux qui sont loin de toi se moqueront de toi, infâme, plein de tumulte.
6 “‘Taona momwe aliyense wa atsogoleri a Israeli amagwiritsira mphamvu zake kupha anthu.
"« Voici, les princes d'Israël, chacun selon sa puissance, ont été chez toi pour verser le sang.
7 Mu mzindamo anthu amanyoza abambo ndi amayi awo. Iwo amapondereza alendo ndi kuzunza ana amasiye ndi akazi amasiye.
Ils ont méprisé chez toi le père et la mère. Au milieu de toi, ils ont opprimé l'étranger. Chez toi, on a fait tort à l'orphelin et à la veuve.
8 Wanyoza zinthu zanga zopatulika ndi kuyipitsa Masabata anga.
Vous avez méprisé mes sanctuaires, Vous avez profané mes sabbats.
9 Mwa iwe muli anthu onenera anzawo zabodza kuti aphedwe. Mwa iwe mulinso amene amadyera zansembe pa mapiri a chipembedzo. Enanso amachita zonyansa.
Il y a eu chez toi des calomniateurs pour répandre le sang. Ils ont mangé chez vous sur les montagnes. Ils se sont livrés à l'impudicité au milieu de toi.
10 Mwa iwe muli ena ogonana ndi akazi a abambo awo, muli enanso amene amavuta akazi pamene ali woyipitsidwa ndi msambo.
C'est chez toi qu'ils ont découvert la nudité de leurs pères, Et qu'ils ont humilié celle qui était dans l'ombre. Chez toi, on a humilié celle qui était impure dans son impureté.
11 Ena amachita chigololo ndi akazi a anzawo, ndipo ena, mopanda manyazi, amayipitsa mkazi wa mwana wawo. Palinso ena amene amayipitsa alongo awo, ana aakazi a abambo awo.
L'un a commis une abomination avec la femme de son prochain, et l'autre a souillé sa belle-fille. Un autre, parmi vous, a humilié sa sœur, la fille de son père.
12 Mwa iwe muli anthu amene amalandira ziphuphu kuti aphe anzawo; ena amachita katapira ndi kupeza phindu loposera muyeso; enanso amapeza phindu mwachinyengo poopseza anzawo. Ndipo mwandiyiwala Ine, akutero Ambuye Yehova.
Chez toi, on a accepté des pots-de-vin pour verser le sang. Tu as pris des intérêts et de l'argent, tu t'es enrichi par l'oppression de ton prochain, et tu m'as oublié, dit le Seigneur Yahvé.
13 “‘Koma Ine ndachita kuwomba mʼmanja kuti phuu nʼkudabwa chifukwa cha phindu lachinyengo limene mwapeza ndiponso chifukwa cha kuphana kumene kumachitika pakati panu.
"« Voici, j'ai frappé ma main sur le gain malhonnête que tu as fait, et sur le sang qui a été versé au milieu de toi.
14 Kodi mtima wako udzakhala wolimbabe kapena manja ako adzakhalabe amphamvu ndikadzatsiriza kukulanga iwe? Ine Yehova ndayankhula, ndipo ndidzazichitadi.
Ton cœur pourra-t-il résister, et tes mains seront-elles fortes, dans les jours où je traiterai avec toi? Moi, Yahvé, je l'ai dit, et je le ferai.
15 Ndidzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukumwazirani ku mayiko onse. Umu ndi mmene ndidzachotsere zoyipa zako.
Je vous disperserai parmi les nations, je vous disperserai dans les pays. Je purgerai de vous vos souillures.
16 Udzanyozedwa pamaso pa anthu a mitundu ina. Pambuyo pake udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
Vous serez profanés en vous-même, aux yeux des nations. Alors vous saurez que je suis Yahvé. »'"
17 Yehova anandiyankhula nati:
La parole de Yahvé me fut adressée, en ces termes:
18 “Iwe mwana wa munthu, Aisraeli asanduka chinthu cha chabechabe kwa Ine. Onse ali ngati mkuwa, chitini, chitsulo ndi mtovu zotsala mʼngʼanjo atayeretsa siliva.
« Fils d'homme, la maison d'Israël est devenue pour moi une scorie. Ils sont tous comme le bronze, l'étain, le fer et le plomb au milieu de la fournaise. Ils sont les scories de l'argent.
19 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Pakuti nonse mwasanduka chinthu cha chabechabe, Ine ndidzakusonkhanitsani mu Yerusalemu.
C'est pourquoi le Seigneur Yahvé dit: « Parce que vous êtes tous devenus des déchets, voici que je vais vous rassembler au milieu de Jérusalem.
20 Monga momwe anthu amasonkhanitsira siliva, mkuwa, chitsulo, mtovu ndi chitini mʼngʼanjo ndi kusonkhetsa moto kuti azisungunule, motero Inenso ndidzakusonkhanitsani ndili wokwiya ndi waukali, ndipo ndidzakuyikani mʼkati mwa mzinda, ndikukusungunurani.
Comme on rassemble l'argent, le bronze, le fer, le plomb et l'étain au milieu de la fournaise, pour y souffler le feu et les faire fondre, ainsi je vous rassemblerai dans ma colère et dans ma fureur, je vous déposerai là et je vous ferai fondre.
21 Ndidzakusonkhanitsani mu mzindamo ndi kukoleza moto wa mkwiyo wanga, ndipo inu mudzasungunuka mu mzindamo.
Oui, je vous rassemblerai, et je soufflerai sur vous avec le feu de ma colère, et vous serez fondus au milieu d'elle.
22 Monga siliva amasungunulidwa mʼngʼanjo, kotero inunso mudzasungunuka mʼkati mwa mzinda ndipo Inu mudzadziwa kuti Ine Yehova ndakukwiyirani.’”
Comme l'argent se fond au milieu de la fournaise, ainsi vous serez fondus au milieu de celle-ci; et vous saurez que moi, Yahvé, j'ai déversé sur vous ma colère.'"
23 Yehova anandiyankhulanso nati,
La parole de Yahvé me fut adressée, en ces termes:
24 “Iwe mwana wa munthu, uza dziko la Israeli kuti, ‘Iwe ndiwe dziko losayeretsedwa, ndiponso losavumbidwa ndi mvula chifukwa cha mkwiyo wanga.’
« Fils d'homme, dis-lui: « Tu es un pays qui n'est pas purifié et sur lequel il ne pleut pas au jour de la colère ».
25 Atsogoleri ake mu mzindamo ali ngati mkango wobangula pogwira nyama. Apha anthu, alanda chuma ndi zinthu za mtengowapatali, ndiponso asandutsa amayi ambiri kukhala amasiye.
Il y a en elle une conspiration de ses prophètes, comme un lion rugissant qui dévore une proie. Ils dévorent les âmes. Ils s'emparent des trésors et des objets précieux. Ils y ont fait beaucoup de veuves.
26 Ansembe ake amaphwanya lamulo langa ndi kuyipitsa zinthu zanga zopatulika. Sasiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba. Saphunzitsa anthu kusiyana kwa zinthu zoyenera pa chipembedzo ndi zinthu zosayenera. Sasamalira za kusunga masabata anga. Motero Ine ndimanyozedwa pakati pawo.
Ses prêtres ont violé ma loi et profané mes choses saintes. Ils n'ont pas fait la différence entre ce qui est saint et ce qui est commun, ils n'ont pas fait discerner ce qui est impur et ce qui est pur, et ils ont caché leurs yeux de mes sabbats. C'est ainsi que je suis profané au milieu d'eux.
27 Atsogoleri ake ali ngati mimbulu yokhadzula nyama; amakhetsa magazi ndi kupha anthu kuti apeze phindu loyipa.
Ses princes sont au dedans comme des loups qui dévorent leur proie, pour répandre le sang et détruire les âmes, afin d'en tirer un gain malhonnête.
28 Aneneri ake amabisa zonsezi monga muja amachitira anthu popaka njereza. Amazimphimba ndi zabodza zimene aona mʼmasomphenya awo ndi zonama za mʼmawula awo. Iwo amati, ‘Ambuye Yehova akuti,’ pamene Ine Yehova sindinayankhule.
Ses prophètes les ont enduits de chaux, ils ont eu de fausses visions, ils leur ont fait des prédictions mensongères, ils ont dit: « Le Seigneur Yahvé dit », alors que Yahvé n'a pas parlé.
29 Anthu a mʼdzikomo amasautsa anzawo ndi kulanda anthu osowa. Amazunza anthu osauka ndi amphawi. Amavutitsa alendo posawachitira zinthu mwachilungamo.
Les habitants du pays ont usé de l'oppression et exercé le brigandage. Oui, ils ont troublé le pauvre et l'indigent, et ils ont opprimé l'étranger à tort.
30 “Ndinafunafuna munthu pakati pawo woti amange linga, woti ayimirire dziko pamaso panga kundipepesa kuti ndisaliwononge, koma sindinamupeze.
« J'ai cherché parmi eux un homme qui bâtirait la muraille et se tiendrait dans la brèche devant moi pour le pays, afin que je ne le détruise pas; mais je n'ai trouvé personne.
31 Nʼchifukwa chake ndawakwiyira kwambiri. Ndawawonongeratu ndi mkwiyo wanga woyaka ngati moto. Ndawalanga molingana ndi zimene anachita. Akutero Ambuye Yehova.”
C'est pourquoij'ai répandu sur eux ma fureur. Je les ai consumés par le feu de ma colère. Je fais retomber sur leur tête leur propre voie, dit le Seigneur Yahvé.