< Ezekieli 22 >
1 Yehova anandiyankhula nati:
And the word of Jehovah came to me, saying:
2 “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza mzinda uwo wa anthu akupha anzawo? Tsono uwudzudzule chifukwa cha machitidwe ake onse onyansa
Punish, punish, son of man, the city of blood, and show her all her abominations, and say,
3 ndipo unene kuti, ‘Ambuye akuti: Iwe mzinda umene wadzigwetsa wekha mʼtsoka pa kukhetsa magazi pakati pako ndi kudziyipitsa popanga mafano,
Thus saith the Lord Jehovah: O city that sheddest blood in the midst of thee, that thy time may come, and makest idols to defile thyself!
4 wapezekatu wolakwa chifukwa cha magazi amene wakhetsa, ndipo wadziyipitsa chifukwa cha mafano amene wapanga. Choncho wachepetsa masiku ako, ndipo zaka zako zafika kumapeto. Nʼchifukwa chake ndalola kuti anthu a mitundu ina akunyoze ndiponso kuti anthu a mayiko onse akuseke.
Through the blood which thou sheddest thou bringest guilt upon thyself, and through the idols which thou makest thou pollutest thyself, and thou causest thy days to draw near, and comest to thy years. Therefore do I make thee a reproach to the nations, and a derision to all countries.
5 Mayiko amene ali pafupi ndi mayiko omwe ali kutali adzakunyoza, iwe mzinda wa mbiri yoyipa, wodzaza ndi chiwawa.
Those that are near, and those that are far from thee, shall mock thee as infamous, full of confusion.
6 “‘Taona momwe aliyense wa atsogoleri a Israeli amagwiritsira mphamvu zake kupha anthu.
Behold the princes of Israel are engaged every one according to his strength within thee to shed blood.
7 Mu mzindamo anthu amanyoza abambo ndi amayi awo. Iwo amapondereza alendo ndi kuzunza ana amasiye ndi akazi amasiye.
In thee they set light by father and mother; in thee are they guilty of oppression to the stranger; in thee do they oppress the fatherless and the widow.
8 Wanyoza zinthu zanga zopatulika ndi kuyipitsa Masabata anga.
Thou hast despised my holy things, and profaned my sabbaths.
9 Mwa iwe muli anthu onenera anzawo zabodza kuti aphedwe. Mwa iwe mulinso amene amadyera zansembe pa mapiri a chipembedzo. Enanso amachita zonyansa.
In thee are men who carry tales, that they may shed blood; in thee do they eat upon the mountains; in the midst of thee do they commit lewdness.
10 Mwa iwe muli ena ogonana ndi akazi a abambo awo, muli enanso amene amavuta akazi pamene ali woyipitsidwa ndi msambo.
In thee doth the son uncover the father's nakedness; in thee do they lie with a woman in her uncleanness.
11 Ena amachita chigololo ndi akazi a anzawo, ndipo ena, mopanda manyazi, amayipitsa mkazi wa mwana wawo. Palinso ena amene amayipitsa alongo awo, ana aakazi a abambo awo.
And one committeth abomination with his neighbor's wife; and another, with incestuous lewdness, defileth his daughter-in-law; and in thee another lieth with his sister, his father's daughter.
12 Mwa iwe muli anthu amene amalandira ziphuphu kuti aphe anzawo; ena amachita katapira ndi kupeza phindu loposera muyeso; enanso amapeza phindu mwachinyengo poopseza anzawo. Ndipo mwandiyiwala Ine, akutero Ambuye Yehova.
In thee do they take a reward to shed blood. Thou takest usury and increase, and thou hast enriched thyself from thy neighbor by extortion, and hast forgotten me, saith the Lord Jehovah.
13 “‘Koma Ine ndachita kuwomba mʼmanja kuti phuu nʼkudabwa chifukwa cha phindu lachinyengo limene mwapeza ndiponso chifukwa cha kuphana kumene kumachitika pakati panu.
Therefore, behold, I have smitten my hands together at thy dishonest gain which thou hast made, and at the blood which hath been shed in the midst of thee.
14 Kodi mtima wako udzakhala wolimbabe kapena manja ako adzakhalabe amphamvu ndikadzatsiriza kukulanga iwe? Ine Yehova ndayankhula, ndipo ndidzazichitadi.
Can thy heart endure, or can thy hands be strong, in the day when I shall deal with thee? I, Jehovah, have spoken it, and will do it.
15 Ndidzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukumwazirani ku mayiko onse. Umu ndi mmene ndidzachotsere zoyipa zako.
I will scatter thee among the nations, and disperse thee in the countries, and will consume thine impurity out of thee;
16 Udzanyozedwa pamaso pa anthu a mitundu ina. Pambuyo pake udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
and thou shalt through thyself be profaned before the eyes of the nations, and thou shalt know that I am Jehovah.
17 Yehova anandiyankhula nati:
And the word of Jehovah came to me, saying:
18 “Iwe mwana wa munthu, Aisraeli asanduka chinthu cha chabechabe kwa Ine. Onse ali ngati mkuwa, chitini, chitsulo ndi mtovu zotsala mʼngʼanjo atayeretsa siliva.
Son of man, the house of Israel is become dross to me; all of them are brass, and tin, and iron, and lead, in the midst of the furnace; they are the dross of silver.
19 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Pakuti nonse mwasanduka chinthu cha chabechabe, Ine ndidzakusonkhanitsani mu Yerusalemu.
Therefore thus saith the Lord Jehovah: Because ye are all of you become dross, therefore, behold, I will gather you into the midst of Jerusalem.
20 Monga momwe anthu amasonkhanitsira siliva, mkuwa, chitsulo, mtovu ndi chitini mʼngʼanjo ndi kusonkhetsa moto kuti azisungunule, motero Inenso ndidzakusonkhanitsani ndili wokwiya ndi waukali, ndipo ndidzakuyikani mʼkati mwa mzinda, ndikukusungunurani.
As men gather silver, and brass, and iron, and lead, and tin, into the midst of the furnace, to blow the fire upon it, to melt it, so will I gather you in my anger and in my fury, and I will place you there and melt you.
21 Ndidzakusonkhanitsani mu mzindamo ndi kukoleza moto wa mkwiyo wanga, ndipo inu mudzasungunuka mu mzindamo.
Yea, I will gather you, and blow upon you with the fire of my wrath, and ye shall be melted in the midst thereof.
22 Monga siliva amasungunulidwa mʼngʼanjo, kotero inunso mudzasungunuka mʼkati mwa mzinda ndipo Inu mudzadziwa kuti Ine Yehova ndakukwiyirani.’”
As silver is melted in the midst of the furnace, so shall ye be melted in the midst thereof; and ye shall know that I, Jehovah, have poured out my fury upon you.
23 Yehova anandiyankhulanso nati,
And the word of Jehovah came to me, saying:
24 “Iwe mwana wa munthu, uza dziko la Israeli kuti, ‘Iwe ndiwe dziko losayeretsedwa, ndiponso losavumbidwa ndi mvula chifukwa cha mkwiyo wanga.’
Son of man, say to her, Thou art a land that is not cleansed, nor rained upon in the day of indignation.
25 Atsogoleri ake mu mzindamo ali ngati mkango wobangula pogwira nyama. Apha anthu, alanda chuma ndi zinthu za mtengowapatali, ndiponso asandutsa amayi ambiri kukhala amasiye.
There is a conspiracy of her prophets in the midst of her; like a roaring lion tearing the prey, they devour the lives of men; they take possession of treasures, and precious things, and make many widows in the midst of her.
26 Ansembe ake amaphwanya lamulo langa ndi kuyipitsa zinthu zanga zopatulika. Sasiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba. Saphunzitsa anthu kusiyana kwa zinthu zoyenera pa chipembedzo ndi zinthu zosayenera. Sasamalira za kusunga masabata anga. Motero Ine ndimanyozedwa pakati pawo.
Her priests violate my law, and profane my holy things. They make no distinction between the holy and profane, and show not the difference between the clean and the unclean; and they hide their eyes from my sabbaths, and I am profaned among them.
27 Atsogoleri ake ali ngati mimbulu yokhadzula nyama; amakhetsa magazi ndi kupha anthu kuti apeze phindu loyipa.
Her princes in the midst of her are like wolves tearing the prey. They shed blood, they destroy life, that they may get gain.
28 Aneneri ake amabisa zonsezi monga muja amachitira anthu popaka njereza. Amazimphimba ndi zabodza zimene aona mʼmasomphenya awo ndi zonama za mʼmawula awo. Iwo amati, ‘Ambuye Yehova akuti,’ pamene Ine Yehova sindinayankhule.
Her prophets daub for them with untempered mortar, seeing falsehood, and divining to them, saying, “Thus saith the Lord Jehovah,” when Jehovah hath not spoken.
29 Anthu a mʼdzikomo amasautsa anzawo ndi kulanda anthu osowa. Amazunza anthu osauka ndi amphawi. Amavutitsa alendo posawachitira zinthu mwachilungamo.
The people of the land are guilty of oppression, and practise robbery, and distress the poor and needy; yea, they oppress the stranger, and have no justice.
30 “Ndinafunafuna munthu pakati pawo woti amange linga, woti ayimirire dziko pamaso panga kundipepesa kuti ndisaliwononge, koma sindinamupeze.
I have sought for a man among them that should make a wall, and stand in the gap before me for the land, that I might not destroy it; but I found none.
31 Nʼchifukwa chake ndawakwiyira kwambiri. Ndawawonongeratu ndi mkwiyo wanga woyaka ngati moto. Ndawalanga molingana ndi zimene anachita. Akutero Ambuye Yehova.”
Therefore will I pour out my indignation upon them; I will consume them with the fire of my wrath; I will bring their way upon their heads, saith the Lord Jehovah.