< Ezekieli 22 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
And there is a word of YHWH to me, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza mzinda uwo wa anthu akupha anzawo? Tsono uwudzudzule chifukwa cha machitidwe ake onse onyansa
“And you, son of man, do you judge? Do you judge the city of blood? Then you have caused it to know all its abominations,
3 ndipo unene kuti, ‘Ambuye akuti: Iwe mzinda umene wadzigwetsa wekha mʼtsoka pa kukhetsa magazi pakati pako ndi kudziyipitsa popanga mafano,
and you have said, Thus said Lord YHWH: The city is shedding blood in its midst, For the coming in of its time, And it has made idols on it for defilement.
4 wapezekatu wolakwa chifukwa cha magazi amene wakhetsa, ndipo wadziyipitsa chifukwa cha mafano amene wapanga. Choncho wachepetsa masiku ako, ndipo zaka zako zafika kumapeto. Nʼchifukwa chake ndalola kuti anthu a mitundu ina akunyoze ndiponso kuti anthu a mayiko onse akuseke.
You have been guilty by your blood that you have shed, And you have been defiled by your idols that you have made, And you cause your days to draw near, And have come to your years, Therefore I have given you [for] a reproach to nations, And a derision to all the lands.
5 Mayiko amene ali pafupi ndi mayiko omwe ali kutali adzakunyoza, iwe mzinda wa mbiri yoyipa, wodzaza ndi chiwawa.
The near and the far-off from you scoff at you, O defiled of name—abounding in trouble.
6 “‘Taona momwe aliyense wa atsogoleri a Israeli amagwiritsira mphamvu zake kupha anthu.
Behold, princes of Israel—each according to his arm Have been in you to shed blood.
7 Mu mzindamo anthu amanyoza abambo ndi amayi awo. Iwo amapondereza alendo ndi kuzunza ana amasiye ndi akazi amasiye.
They have made light of father and mother in you, They dealt oppressively to a sojourner in your midst, They oppressed fatherless and widow in you.
8 Wanyoza zinthu zanga zopatulika ndi kuyipitsa Masabata anga.
You have despised My holy things, And you have defiled My Sabbaths.
9 Mwa iwe muli anthu onenera anzawo zabodza kuti aphedwe. Mwa iwe mulinso amene amadyera zansembe pa mapiri a chipembedzo. Enanso amachita zonyansa.
Men of slander have been in you to shed blood, And they have eaten on the mountains in you, They have done wickedness in your midst.
10 Mwa iwe muli ena ogonana ndi akazi a abambo awo, muli enanso amene amavuta akazi pamene ali woyipitsidwa ndi msambo.
One has uncovered the nakedness of a father in you, They humbled the menstruous woman in you.
11 Ena amachita chigololo ndi akazi a anzawo, ndipo ena, mopanda manyazi, amayipitsa mkazi wa mwana wawo. Palinso ena amene amayipitsa alongo awo, ana aakazi a abambo awo.
And each has done abomination with the wife of his neighbor, And each has defiled his daughter-in-law through wickedness, And each has humbled his sister, his father’s daughter, in you.
12 Mwa iwe muli anthu amene amalandira ziphuphu kuti aphe anzawo; ena amachita katapira ndi kupeza phindu loposera muyeso; enanso amapeza phindu mwachinyengo poopseza anzawo. Ndipo mwandiyiwala Ine, akutero Ambuye Yehova.
They have taken a bribe to shed blood in you, You have taken usury and increase, And cut off your neighbor by oppression, And you have forgotten Me, A declaration of Lord YHWH!
13 “‘Koma Ine ndachita kuwomba mʼmanja kuti phuu nʼkudabwa chifukwa cha phindu lachinyengo limene mwapeza ndiponso chifukwa cha kuphana kumene kumachitika pakati panu.
And behold, I have struck My hand, Because of your dishonest gain that you have gained, And for your blood that has been in your midst.
14 Kodi mtima wako udzakhala wolimbabe kapena manja ako adzakhalabe amphamvu ndikadzatsiriza kukulanga iwe? Ine Yehova ndayankhula, ndipo ndidzazichitadi.
Does your heart stand—are your hands strong, For the days that I am dealing with you? I, YHWH, have spoken and have done [it].
15 Ndidzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukumwazirani ku mayiko onse. Umu ndi mmene ndidzachotsere zoyipa zako.
And I have scattered you among nations, And have spread you out among lands, And consumed your uncleanness out of you.
16 Udzanyozedwa pamaso pa anthu a mitundu ina. Pambuyo pake udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
And you have been defiled in yourself Before the eyes of nations, And you have known that I [am] YHWH.”
17 Yehova anandiyankhula nati:
And there is a word of YHWH to me, saying,
18 “Iwe mwana wa munthu, Aisraeli asanduka chinthu cha chabechabe kwa Ine. Onse ali ngati mkuwa, chitini, chitsulo ndi mtovu zotsala mʼngʼanjo atayeretsa siliva.
“Son of man, the house of Israel has been for dross to Me, All of them [are] bronze, and tin, and iron, and lead, In the midst of a furnace—silver has been dross,
19 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Pakuti nonse mwasanduka chinthu cha chabechabe, Ine ndidzakusonkhanitsani mu Yerusalemu.
Therefore, thus said Lord YHWH: Because you have all become dross, Therefore, behold, I am gathering you into the midst of Jerusalem,
20 Monga momwe anthu amasonkhanitsira siliva, mkuwa, chitsulo, mtovu ndi chitini mʼngʼanjo ndi kusonkhetsa moto kuti azisungunule, motero Inenso ndidzakusonkhanitsani ndili wokwiya ndi waukali, ndipo ndidzakuyikani mʼkati mwa mzinda, ndikukusungunurani.
A gathering of silver, and bronze, and iron, and lead, and tin, Into the midst of a furnace—to blow fire on it, to melt it, So I gather in My anger and in My fury, And I have let rest, and have melted you.
21 Ndidzakusonkhanitsani mu mzindamo ndi kukoleza moto wa mkwiyo wanga, ndipo inu mudzasungunuka mu mzindamo.
And I have heaped you up, And blown on you in the fire of My wrath, And you have been melted in its midst.
22 Monga siliva amasungunulidwa mʼngʼanjo, kotero inunso mudzasungunuka mʼkati mwa mzinda ndipo Inu mudzadziwa kuti Ine Yehova ndakukwiyirani.’”
As the melting of silver in the midst of a furnace, So you are melted in its midst, And you have known that I, YHWH, have poured out My fury on you.”
23 Yehova anandiyankhulanso nati,
And there is a word of YHWH to me, saying,
24 “Iwe mwana wa munthu, uza dziko la Israeli kuti, ‘Iwe ndiwe dziko losayeretsedwa, ndiponso losavumbidwa ndi mvula chifukwa cha mkwiyo wanga.’
“Son of man, say to it, You [are] a land, It [is] not cleansed nor rained on in a day of indignation.
25 Atsogoleri ake mu mzindamo ali ngati mkango wobangula pogwira nyama. Apha anthu, alanda chuma ndi zinthu za mtengowapatali, ndiponso asandutsa amayi ambiri kukhala amasiye.
A conspiracy of its prophets [is] in its midst, As a roaring lion tearing prey; They have devoured the soul, They have taken wealth and glory, Its widows have multiplied in its midst.
26 Ansembe ake amaphwanya lamulo langa ndi kuyipitsa zinthu zanga zopatulika. Sasiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba. Saphunzitsa anthu kusiyana kwa zinthu zoyenera pa chipembedzo ndi zinthu zosayenera. Sasamalira za kusunga masabata anga. Motero Ine ndimanyozedwa pakati pawo.
Its priests have wronged My law, And they defile My holy things, They have not made separation between holy and common, And they have not made known [the difference] between the unclean and the clean, And they have hidden their eyes from My Sabbaths, And I am pierced in their midst.
27 Atsogoleri ake ali ngati mimbulu yokhadzula nyama; amakhetsa magazi ndi kupha anthu kuti apeze phindu loyipa.
Its princes [are] as wolves in its midst, Tearing prey, to shed blood, to destroy souls, For the sake of gaining dishonest gain.
28 Aneneri ake amabisa zonsezi monga muja amachitira anthu popaka njereza. Amazimphimba ndi zabodza zimene aona mʼmasomphenya awo ndi zonama za mʼmawula awo. Iwo amati, ‘Ambuye Yehova akuti,’ pamene Ine Yehova sindinayankhule.
And its prophets have coated with chalk for them, Seeing a vain thing, and divining a lie for them, Saying, Thus said Lord YHWH, And YHWH has not spoken.
29 Anthu a mʼdzikomo amasautsa anzawo ndi kulanda anthu osowa. Amazunza anthu osauka ndi amphawi. Amavutitsa alendo posawachitira zinthu mwachilungamo.
The people of the land have used oppression, And have taken plunder away violently, And have oppressed humble and needy, And oppressed the sojourner without judgment.
30 “Ndinafunafuna munthu pakati pawo woti amange linga, woti ayimirire dziko pamaso panga kundipepesa kuti ndisaliwononge, koma sindinamupeze.
And I seek from them a man making a wall, And standing in the breach before Me, In behalf of the land—not to destroy it, And I have found none.
31 Nʼchifukwa chake ndawakwiyira kwambiri. Ndawawonongeratu ndi mkwiyo wanga woyaka ngati moto. Ndawalanga molingana ndi zimene anachita. Akutero Ambuye Yehova.”
And I pour out My indignation on them, I have consumed them by [the] fire of My wrath, I have put their way on their own head, A declaration of Lord YHWH!”

< Ezekieli 22 >