< Ezekieli 22 >
1 Yehova anandiyankhula nati:
Opět stalo se slovo Hospodinovo ke mně, řkoucí:
2 “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza mzinda uwo wa anthu akupha anzawo? Tsono uwudzudzule chifukwa cha machitidwe ake onse onyansa
Ty pak synu člověčí, zastával-li bys, zastával-liž bys toho města vražedlného? Raději mu oznam všecky ohavnosti jeho,
3 ndipo unene kuti, ‘Ambuye akuti: Iwe mzinda umene wadzigwetsa wekha mʼtsoka pa kukhetsa magazi pakati pako ndi kudziyipitsa popanga mafano,
A rci: Takto praví Panovník Hospodin: Přicházíť čas města toho, jenž prolévá krev u prostřed sebe, a dělá ukydané bohy proti sobě, aby se poškvrňovalo.
4 wapezekatu wolakwa chifukwa cha magazi amene wakhetsa, ndipo wadziyipitsa chifukwa cha mafano amene wapanga. Choncho wachepetsa masiku ako, ndipo zaka zako zafika kumapeto. Nʼchifukwa chake ndalola kuti anthu a mitundu ina akunyoze ndiponso kuti anthu a mayiko onse akuseke.
Ty krví svou, kterouž jsi prolilo, zavinivší, a ukydanými bohy svými, jichž jsi nadělalo, sebe poškvrnivší, to jsi způsobilo, že se přiblížili dnové tvoji, a přišlo jsi k letům svým. Protož vydám tě v pohanění národům, a ku posměchu všechněm zemím.
5 Mayiko amene ali pafupi ndi mayiko omwe ali kutali adzakunyoza, iwe mzinda wa mbiri yoyipa, wodzaza ndi chiwawa.
Blízké i daleké od tebe budou se tobě posmívati, ó zlopověstné a různic plné.
6 “‘Taona momwe aliyense wa atsogoleri a Israeli amagwiritsira mphamvu zake kupha anthu.
Aj, knížata Izraelská jeden každý vší silou na to se vydali, aby krev v tobě prolévali.
7 Mu mzindamo anthu amanyoza abambo ndi amayi awo. Iwo amapondereza alendo ndi kuzunza ana amasiye ndi akazi amasiye.
Otce i matku zlehčují v tobě, pohostinnému činí nátisk u prostřed tebe, sirotka a vdovu utiskují v tobě.
8 Wanyoza zinthu zanga zopatulika ndi kuyipitsa Masabata anga.
Svatými věcmi mými zhrdáš, a sobot mých poškvrňuješ.
9 Mwa iwe muli anthu onenera anzawo zabodza kuti aphedwe. Mwa iwe mulinso amene amadyera zansembe pa mapiri a chipembedzo. Enanso amachita zonyansa.
Utrhači jsou v tobě, aby prolévali krev, a na horách jídají v tobě; nešlechetnost páší u prostřed tebe.
10 Mwa iwe muli ena ogonana ndi akazi a abambo awo, muli enanso amene amavuta akazi pamene ali woyipitsidwa ndi msambo.
Nahotu otce syn odkrývá v tobě, a nečisté v oddělení ponižují v tobě.
11 Ena amachita chigololo ndi akazi a anzawo, ndipo ena, mopanda manyazi, amayipitsa mkazi wa mwana wawo. Palinso ena amene amayipitsa alongo awo, ana aakazi a abambo awo.
Jiný pak s ženou bližního svého páše ohavnost, a jiný s nevěstou svou poškvrňuje se nešlechetností, a jiný sestry své, dcery otce svého, ponižuje v tobě.
12 Mwa iwe muli anthu amene amalandira ziphuphu kuti aphe anzawo; ena amachita katapira ndi kupeza phindu loposera muyeso; enanso amapeza phindu mwachinyengo poopseza anzawo. Ndipo mwandiyiwala Ine, akutero Ambuye Yehova.
Dar berou v tobě, aby krev prolili; lichvu a úrok béřeš, a zisku hledáš s útiskem bližního svého, na mne se pak zapomínáš, dí Panovník Hospodin.
13 “‘Koma Ine ndachita kuwomba mʼmanja kuti phuu nʼkudabwa chifukwa cha phindu lachinyengo limene mwapeza ndiponso chifukwa cha kuphana kumene kumachitika pakati panu.
Protož aj, já tleskl jsem rukama svýma nad ziskem tvým, jehož dobýváš, i nad tou krví, kteráž byla u prostřed tebe.
14 Kodi mtima wako udzakhala wolimbabe kapena manja ako adzakhalabe amphamvu ndikadzatsiriza kukulanga iwe? Ine Yehova ndayankhula, ndipo ndidzazichitadi.
Zdali ostojí srdce tvé? Zdaž odolají ruce tvé dnům, v nichž já budu zacházeti s tebou? Já Hospodin mluvil jsem i učiním.
15 Ndidzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukumwazirani ku mayiko onse. Umu ndi mmene ndidzachotsere zoyipa zako.
Nebo rozptýlím tě mezi pohany, a rozženu tě po krajinách, a do konce vyprázdním nečistotu tvou z tebe.
16 Udzanyozedwa pamaso pa anthu a mitundu ina. Pambuyo pake udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
A zavrženo jsuc před očima pohanů, poznáš, že já jsem Hospodin.
17 Yehova anandiyankhula nati:
Potom stalo se slovo Hospodinovo ke mně, řkoucí:
18 “Iwe mwana wa munthu, Aisraeli asanduka chinthu cha chabechabe kwa Ine. Onse ali ngati mkuwa, chitini, chitsulo ndi mtovu zotsala mʼngʼanjo atayeretsa siliva.
Synu člověčí, obrátili se mi dům Izraelský v trůsku, všickni napořád jsou měď, cín, železo a olovo u prostřed peci, trůsky stříbra jsou.
19 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Pakuti nonse mwasanduka chinthu cha chabechabe, Ine ndidzakusonkhanitsani mu Yerusalemu.
Pročež takto praví Panovník Hospodin: Proto že jste vy všickni obrátili se v trůsky, protož aj, já shromáždím vás do Jeruzaléma.
20 Monga momwe anthu amasonkhanitsira siliva, mkuwa, chitsulo, mtovu ndi chitini mʼngʼanjo ndi kusonkhetsa moto kuti azisungunule, motero Inenso ndidzakusonkhanitsani ndili wokwiya ndi waukali, ndipo ndidzakuyikani mʼkati mwa mzinda, ndikukusungunurani.
Jakž se shromažďuje stříbro a měď, železo, olovo i cín do prostřed peci, k rozdmýchání ohně vůkol něho a k rozpouštění: tak shromáždím v hněvě a v prchlivosti své, a slože, rozpouštěti vás budu.
21 Ndidzakusonkhanitsani mu mzindamo ndi kukoleza moto wa mkwiyo wanga, ndipo inu mudzasungunuka mu mzindamo.
Sberu vás, pravím, a rozdmýchám okolo vás oheň prchlivosti své, i rozpustíte se u prostřed města.
22 Monga siliva amasungunulidwa mʼngʼanjo, kotero inunso mudzasungunuka mʼkati mwa mzinda ndipo Inu mudzadziwa kuti Ine Yehova ndakukwiyirani.’”
Jakž se stříbro rozpouští v peci, tak se rozpustíte u prostřed něho, i zvíte, že já Hospodin vylil jsem prchlivost svou na vás.
23 Yehova anandiyankhulanso nati,
Ještě stalo se slovo Hospodinovo ke mně, řkoucí:
24 “Iwe mwana wa munthu, uza dziko la Israeli kuti, ‘Iwe ndiwe dziko losayeretsedwa, ndiponso losavumbidwa ndi mvula chifukwa cha mkwiyo wanga.’
Synu člověčí, rci: Ty země jsi nečistá, nebudeš deštěm svlažena v den rozhněvání.
25 Atsogoleri ake mu mzindamo ali ngati mkango wobangula pogwira nyama. Apha anthu, alanda chuma ndi zinthu za mtengowapatali, ndiponso asandutsa amayi ambiri kukhala amasiye.
Spiknutí proroků jejích u prostřed ní, jsou podobni lvu řvoucímu, uchvacujícímu loupež, duše žerou, bohatství a věci drahé berou, a činí mnoho vdov u prostřed ní.
26 Ansembe ake amaphwanya lamulo langa ndi kuyipitsa zinthu zanga zopatulika. Sasiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba. Saphunzitsa anthu kusiyana kwa zinthu zoyenera pa chipembedzo ndi zinthu zosayenera. Sasamalira za kusunga masabata anga. Motero Ine ndimanyozedwa pakati pawo.
Kněží její natahují zákona mého, a svaté věci mé poškvrňují, mezi svatým a poškvrněným rozdílu nečiní, a mezi nečistým a čistým nerozeznávají. Nadto od sobot mých skrývají oči své, tak že zlehčován bývám mezi nimi.
27 Atsogoleri ake ali ngati mimbulu yokhadzula nyama; amakhetsa magazi ndi kupha anthu kuti apeze phindu loyipa.
Knížata její u prostřed ní jsou jako vlci uchvacující loupež, vylévajíce krev, hubíce duše, aby sháněli mrzký zisk.
28 Aneneri ake amabisa zonsezi monga muja amachitira anthu popaka njereza. Amazimphimba ndi zabodza zimene aona mʼmasomphenya awo ndi zonama za mʼmawula awo. Iwo amati, ‘Ambuye Yehova akuti,’ pamene Ine Yehova sindinayankhule.
Proroci pak jejich obmítají jim vápnem ničemným, předpovídají marné věci, a hádají jim lež, říkajíce: Takto praví Panovník Hospodin, ješto Hospodin nemluvil.
29 Anthu a mʼdzikomo amasautsa anzawo ndi kulanda anthu osowa. Amazunza anthu osauka ndi amphawi. Amavutitsa alendo posawachitira zinthu mwachilungamo.
Lid této země činí nátisk, a cizí věci mocí béře, chudému a nuznému ubližují, a pohostinného utiskují nespravedlivě.
30 “Ndinafunafuna munthu pakati pawo woti amange linga, woti ayimirire dziko pamaso panga kundipepesa kuti ndisaliwononge, koma sindinamupeze.
Hledaje pak někoho z nich, kterýž by udělal hradbu, a postavil se v mezeře před tváří mou za tuto zemi, abych jí nezkazil, žádného nenacházím.
31 Nʼchifukwa chake ndawakwiyira kwambiri. Ndawawonongeratu ndi mkwiyo wanga woyaka ngati moto. Ndawalanga molingana ndi zimene anachita. Akutero Ambuye Yehova.”
Protož vyleji na ně rozhněvání své, ohněm prchlivosti své konec jim učiním, cestu jejich jim na hlavu obrátím, praví Panovník Hospodin.