< Ezekieli 21 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
RAB bana şöyle seslendi:
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane ku Yerusalemu ndipo ulalike mawu odzudzula malo ake opatulika. Unenere zodzudzula anthu a ku Yerusalemu.
“Ey insanoğlu, yüzünü Yeruşalim'e çevir, kutsal yerlerine karşı konuş, İsrail ülkesine karşı peygamberlik et.
3 Uwawuze kuti, Ambuye Yehova akuti, ‘Taona, Ine ndidzalimbana nawe. Ndidzasolola lupanga langa mʼchimake ndi kuwononga anthu olungama ndi ochimwa omwe.
Ona de ki, ‘RAB şöyle diyor: Ben sana karşıyım! Kılıcımı kınından çıkaracak, içindeki doğru kişiyi de kötü kişiyi de kesip yok edeceğim.
4 Motero ndidzapha aliyense kuchokera kummawa mpaka kumpoto.
Doğru kişiyi de kötü kişiyi de kesip yok etmek için kılıcım kınından çıkacak ve güneyden kuzeye herkese karşı olacak.
5 Pamenepo anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndasolola lupanga langa mʼchimake; sindidzalilowetsanso mʼchimakemo.’
Böylece herkes kılıcını kınından çıkaranın ben RAB olduğumu anlayacak. Onu bir daha yerine koymayacağım.’
6 “Tsono iwe mwana wa munthu, buwula. Buwula pamaso pawo ndi mtima wosweka ndi wachisoni chachikulu.
“Sen, ey insanoğlu, inle! Onların gözü önünde ezik bir yürekle acı acı inle!
7 Ndipo akadzakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukubuwula?’ Iwe udzayankhe kuti, ‘Ndikubuwula chifukwa cha nkhani imene ndamva. Zikadzachitika zimenezi, mitima yonse idzangoti fumu, manja onse adzangolefuka, mpweya wawo udzawathera, ndipo mawondo onse adzangoti zii.’ Izi zikubwera! Ndipo zidzachitika ndithu, akutero Ambuye Yehova.”
Sana, ‘Neden böyle inliyorsun?’ diye sorduklarında, ‘Yakında duyulacak haberden ötürü’ diye yanıtlayacaksın. ‘Her yürek eriyecek, her el gevşeyecek, her ruh baygın düşecek, her dizin bağı çözülecek. Evet, haber duyulacak! Bu kesinlikle yerine gelecek.’ Egemen RAB böyle diyor.”
8 Yehova anandiyankhulanso kuti,
RAB bana şöyle seslendi:
9 “Iwe mwana wa munthu, unenere ndipo unene kuti, Ambuye Yehova akuti, “Izi ndi zimene Yehova akunena: Lupanga, lupanga, lanoledwa ndipo lapukutidwa.
“İnsanoğlu, peygamberlik et ve de ki, ‘Rab şöyle diyor: “‘Kılıç, kılıç, Bilendi, cilalandı.
10 Lanoledwa kuti likaphe, lapukutidwa kuti lingʼanime ngati mphenzi! “‘Kodi tingakondwere bwanji? Wanyoza ndodo, mwana wanga ndi chilichonse cha mtengo.
Öldürmek için bilendi, Şimşek gibi çaksın diye cilalandı. Nasıl sevinebiliriz? Kılıç oğlumun asasını sıradan bir sopa gibi küçümsedi.
11 “‘Lupanga laperekedwa kuti lipukutidwe, ndi kuti linyamulidwe, lanoledwa ndi kupukutidwa, kuti liperekedwe mʼmanja mwa munthu amene amapha.
Kılıç kullanılmak için Cilalanmaya verildi; Öldürenin eline verilsin diye bilenip cilalandı.
12 Fuwula ndi kulira, iwe mwana wa munthu, pakuti zimenezi zidzagwera anthu anga; zidzagweranso akalonga onse a Israeli. Adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi anthu anga. Chifukwa chake udzigugude pa chifuwa ndi chisoni.
İnsanoğlu, bağır, haykır! Çünkü bu kılıç halkıma karşı; Bütün İsrail önderlerine karşı. Onlar halkımla birlikte kılıca teslim edildiler. Bunun için bağrını döv.
13 “‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Ndikuwayesa anthu anga, ndipo ngati satembenuka mtima, ndiye kuti zimenezi sizidzalephera kuwagwera.’
“‘Deneme kuşkusuz gelecek. Kılıcın küçümsediği asa varlığını sürdüremezse ne olur? Böyle diyor Egemen RAB.’
14 “Tsono mwana wa munthu, nenera ndipo uwombe mʼmanja. Lupanga likanthe kawiri ngakhale katatu. Limenelo ndilo lupanga lophera anthu. Inde ndilodi lupanga lophera anthu koopsa limene likuwazungulira.
“Sen, ey insanoğlu, peygamberlik et, el çırp. Bırak kılıç iki, üç kez vursun. Bu öldüren bir kılıçtır, Çok sayıda insan kıran, İnsanı her yandan saran kılıçtır.
15 Ndawayikira pa zipata zawo zonse lupanga laphuliphuli kuti ataye mtima ndiponso kuti anthu ambiri agwe. Aa! Lapangidwa lupanga kuti lizingʼanima ngati mphenzi ndi kuti azilisolola kuphera anthu.
Yürekleri erisin, Tökezleyip düşenler çok olsun diye Bütün kapılarında öldürmek için Görevlendirdim kılıcı. Ah, kılıç şimşek gibi parladı, Öldürmek için bilendi.
16 Iwe lupanga, ipha anthu kumanja, kenaka kumanzere, kulikonse kumene msonga yako yaloza.
Ey kılıç, sağa, sonra sola savrul, Ağzın nereye dönerse, oraya savrul!
17 Inenso ndidzawomba mʼmanja mwanga, ndipo ndidzaziziritsa ukali wanga Ine Yehova ndayankhula.”
Ben de elimi çırpacağım Ve öfkem dinecek. Bunu ben RAB söylüyorum.”
18 Yehova anandiyankhulanso kuti,
RAB bana şöyle seslendi:
19 “Iwe mwana wa munthu, ulembe zizindikiro za misewu iwiri imene lupanga la mfumu ya ku Babuloni lingathe kudzeramo. Misewu yonse ikhale yochokera mʼdziko limodzi. Ika chikwangwani pa mphambano yopita mu mzinda.
“İnsanoğlu, Babil Kralı'nın kılıcı gelsin diye iki yol belirle; ikisi de aynı ülkeden başlamalı. Kent yolunun başladığı yere bir işaret koy.
20 Ulembe chizindikiro pa msewu umene lupanga lidzadzere popita ku Raba wa ku Amoni, ndiponso ku Yuda ndi ku Yerusalemu, mzinda wotetezedwa.
Ammonlular'ın Rabba Kenti'ne ya da Yahuda'ya ve surlarla çevrili Yeruşalim'e ilerlesin diye kılıç için yol belirle.
21 Pakuti mfumu ya ku Babuloni yayima pa msewu, pa mphambano ya misewu iwiriyo. Ikuwombeza ndi mivi yake kuti idziwe njira yoyenera kudzeramo. Ikupempha nzeru kwa milungu yake ndipo ikuyangʼana chiwindi cha nyama yoperekedwa ku nsembe.
Çünkü Babil Kralı iki yolun ayrıldığı, yolların çatallaştığı yerde fala bakmak için duracak. Okları silkeleyecek, aile putlarına danışacak, kurban edilen bir hayvanın ciğerine bakacak.
22 Mʼdzanja lake lamanja muli muvi waula wolembedwa Yerusalemu. Kumeneko mfumuyo idzayika zida zogumulira, idzalamula kupha anthu ndiponso kufuwula mfuwu wa nkhondo. Mfumuyo idzapanga zida zogumulira makoma, kuwunda mitumbira ya nkhondo ndi kumanga nsanja za nkhondo.
Kütük yerleştirmek, öldür buyruğunu vermek, savaş naraları atmak, kapılara kütük yerleştirmek, toprak rampalar oluşturmak, kuşatma duvarları yapmak için sağ elinde Yeruşalim'i gösteren ok olacak.
23 Koma kwa anthu a ku Yerusalemu zidzaoneka ngati zowombeza zabodza chifukwa cha malumbiro amene anachita kwa mfumuyo. Koma mfumuyo idzawakumbutsa za zolakwa zawo kuti atengedwe ku ukapolo.
Onunla ant içerek antlaşma yapanlar fala yanlış bakıldığını sanacak. Ama kral suçlarını anımsatıp onları tutsak alacak.
24 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Popeza mwandikumbutsa zolakwa, moti kundiwukira kwanu kwaonekera poyera ndi kuti mu zochita zanu zonse mukuonetsa machimo anu, nʼchifukwa chake mudzagwidwa ndi kutengedwa ukapolo.
“Bundan ötürü Egemen RAB şöyle diyor: ‘Madem suçlarınızı, isyanlarınızı anımsattırdınız, bütün uygulamalarınızda günahlarınızı açığa çıkardınız, madem bütün bunları yaptınız, siz de tutsak alınıp götürüleceksiniz.
25 “‘Tsono iwe kalonga wonyozedwa ndi woyipa wa Israeli, amene tsiku lako lafika, amene nthawi yako yolangidwa yafika penipeni,
“‘Sen, ey saygısız, kötü İsrail önderi, günün yaklaştı, sonunda yargı günün geldi.
26 Ambuye Yehova akuti: Vula nduwira, chotsa chipewa chaufumu. Zinthu sizidzakhala monga zinalili: anthu wamba adzakwezedwa ndipo okwezedwa adzatsitsidwa.
Egemen RAB şöyle diyor: Sarığı çıkar, tacı kaldır. Artık eskisi gibi olmayacak. Alçakgönüllü yükseltilecek, gururlu alçaltılacak.
27 Chipasupasu! Chipasupasu! Ine ndidzawupasula mzindawo! Ndipo sadzawumanganso mpaka atafika amene ali woyenera kuwulandira; Ine ndidzawupereka kwa iyeyo.’
Yıkım! Yıkım! Kenti yerle bir edeceğim! Hak sahibi gelinceye dek onarılmayacak. Kenti ona vereceğim.’
28 “Ndipo iwe mwana wa munthu, nenera kuti, ponena za Aamoni ndi zonyoza zawo, Ambuye Yehova akuti, “‘Lupanga, lupanga, alisolola kuti liphe anthu, alipukuta kuti liwononge ndi kuti lingʼanime ngati mphenzi.
“Sen, ey insanoğlu, peygamberlik et ve de ki, ‘Aşağılayıcı sözler söyleyen Ammonlular için Egemen RAB şöyle diyor: “‘Kılıç, kılıç, Öldürmek için kınından çekilmiş, Yok etmek için, Şimşek gibi parlamak için cilalanmış!
29 Zimene akuti akuona mʼmasomphenya zokhudza inu ndi zabodza. Mawula awo okhudza inu ndi abodzanso. Mudzakhala pamodzi ndi anthu oyipa amene tsiku lawo lafika, ndiye kuti nthawi ya kulangidwa kwawo komaliza.
Size ilişkin görümler aldatıcıdır, Açılan fal yalandır. Öldürülecek kötülerin enseleri üzerine Yerleştirileceksin, ey kılıç! Onların günü yaklaştı, Sonunda yargı günleri geldi.
30 “‘Bwezerani lupanga mʼchimake. Ku malo kumene inu munabadwira, mʼdziko la makolo anu, ndidzakuweruzani.
Kılıç kınına koyulsun! Yaratıldığınız yerde, Atalarınızın ülkesinde Yargılayacağım sizi.
31 Ndidzakhuthula ukali wanga pa inu, ndipo mkwiyo wanga udzakuyakirani. Ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu ankhanza; anthu odziwa bwino kuwononga zinthu.
Öfkemi üzerinize dökeceğim, Kızgınlığımı üzerinize üfleyeceğim; Acımasız adamların, Yakıp yok etmekte usta kişilerin eline Teslim edeceğim sizi.
32 Mudzakhala ngati nkhuni pa moto. Ena adzakhetsa magazi anu mʼdziko lanu lomwe. Simudzakumbukiridwanso pakuti Ine Yehova ndayankhula.’”
Ateşe yakıt olacaksınız, Kanınız ülkenizin ortasında dökülecek, Bir daha anılmayacaksınız. Çünkü bunu ben RAB söylüyorum.’”

< Ezekieli 21 >