< Ezekieli 21 >
1 Yehova anandiyankhula nati:
И дође ми реч Господња говорећи:
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane ku Yerusalemu ndipo ulalike mawu odzudzula malo ake opatulika. Unenere zodzudzula anthu a ku Yerusalemu.
Сине човечји, окрени лице своје према Јерусалиму, и покапљи према светим местима, и пророкуј против земље Израиљеве.
3 Uwawuze kuti, Ambuye Yehova akuti, ‘Taona, Ine ndidzalimbana nawe. Ndidzasolola lupanga langa mʼchimake ndi kuwononga anthu olungama ndi ochimwa omwe.
И реци земљи Израиљевој: Овако вели Господ: Ево ме на те; извући ћу мач свој из корица, и истребићу из тебе праведног и безбожног.
4 Motero ndidzapha aliyense kuchokera kummawa mpaka kumpoto.
Да истребим из тебе праведног и безбожног, зато ће изаћи мач мој из корица својих на свако тело од југа до севера.
5 Pamenepo anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndasolola lupanga langa mʼchimake; sindidzalilowetsanso mʼchimakemo.’
И познаће свако тело да сам ја Господ извукао мач свој из корица његових, неће се више вратити.
6 “Tsono iwe mwana wa munthu, buwula. Buwula pamaso pawo ndi mtima wosweka ndi wachisoni chachikulu.
А ти, сине човечји, уздиши као да су ти бедра поломљена, и горко уздиши пред њима.
7 Ndipo akadzakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukubuwula?’ Iwe udzayankhe kuti, ‘Ndikubuwula chifukwa cha nkhani imene ndamva. Zikadzachitika zimenezi, mitima yonse idzangoti fumu, manja onse adzangolefuka, mpweya wawo udzawathera, ndipo mawondo onse adzangoti zii.’ Izi zikubwera! Ndipo zidzachitika ndithu, akutero Ambuye Yehova.”
А кад ти кажу: Зашто уздишеш? Ти реци: За глас што иде, од ког ће се растопити свако срце и клонути све руке и сваког ће духа нестати, и свака ће колена постати као вода; ево, иде, и навршиће се, говори Господ Господ.
8 Yehova anandiyankhulanso kuti,
Потом дође ми реч Господња говорећи:
9 “Iwe mwana wa munthu, unenere ndipo unene kuti, Ambuye Yehova akuti, “Izi ndi zimene Yehova akunena: Lupanga, lupanga, lanoledwa ndipo lapukutidwa.
Сине човечји, пророкуј и реци: Овако вели Господ Господ: Реци: мач, мач је наоштрен, и углађен је.
10 Lanoledwa kuti likaphe, lapukutidwa kuti lingʼanime ngati mphenzi! “‘Kodi tingakondwere bwanji? Wanyoza ndodo, mwana wanga ndi chilichonse cha mtengo.
Наоштрен је да коље, углађен је да сева; хоћемо ли се радовати кад прут сина мог не хаје ни за како дрво?
11 “‘Lupanga laperekedwa kuti lipukutidwe, ndi kuti linyamulidwe, lanoledwa ndi kupukutidwa, kuti liperekedwe mʼmanja mwa munthu amene amapha.
Дао га је да се углади да се узме у руку; мач је наоштрен и углађен, да се да у руку убици.
12 Fuwula ndi kulira, iwe mwana wa munthu, pakuti zimenezi zidzagwera anthu anga; zidzagweranso akalonga onse a Israeli. Adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi anthu anga. Chifukwa chake udzigugude pa chifuwa ndi chisoni.
Вичи и ридај, сине човечји; јер он иде на народ мој, на све кнезове Израиљеве; под мач ће бити окренути с народом мојим, за то удри се по бедру.
13 “‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Ndikuwayesa anthu anga, ndipo ngati satembenuka mtima, ndiye kuti zimenezi sizidzalephera kuwagwera.’
Кад беше карање, шта би? Еда ли ни од прута који не хаје неће бити ништа? Говори Господ Господ.
14 “Tsono mwana wa munthu, nenera ndipo uwombe mʼmanja. Lupanga likanthe kawiri ngakhale katatu. Limenelo ndilo lupanga lophera anthu. Inde ndilodi lupanga lophera anthu koopsa limene likuwazungulira.
Ти дакле, сине човечји, пророкуј и пљескај рукама, јер ће мач доћи и другом и трећом, мач који убија, мач који велике убија, који продире у клети.
15 Ndawayikira pa zipata zawo zonse lupanga laphuliphuli kuti ataye mtima ndiponso kuti anthu ambiri agwe. Aa! Lapangidwa lupanga kuti lizingʼanima ngati mphenzi ndi kuti azilisolola kuphera anthu.
Да се растопе срца и умножи погибао, метнуо сам на сва врата њихова страх од мача; јаох! Приправљен је да сева, наоштрен да коље.
16 Iwe lupanga, ipha anthu kumanja, kenaka kumanzere, kulikonse kumene msonga yako yaloza.
Стегни се, удри надесно, налево, куда се год обрнеш.
17 Inenso ndidzawomba mʼmanja mwanga, ndipo ndidzaziziritsa ukali wanga Ine Yehova ndayankhula.”
Јер ћу и ја пљескати рукама, и намирићу гнев свој. Ја Господ рекох.
18 Yehova anandiyankhulanso kuti,
Још ми дође реч Господња говорећи:
19 “Iwe mwana wa munthu, ulembe zizindikiro za misewu iwiri imene lupanga la mfumu ya ku Babuloni lingathe kudzeramo. Misewu yonse ikhale yochokera mʼdziko limodzi. Ika chikwangwani pa mphambano yopita mu mzinda.
А ти, сине човечји, начини два пута, куда ће доћи мач цара вавилонског; из једне земље нека излазе оба; и избери страну, где се почиње пут градски, избери.
20 Ulembe chizindikiro pa msewu umene lupanga lidzadzere popita ku Raba wa ku Amoni, ndiponso ku Yuda ndi ku Yerusalemu, mzinda wotetezedwa.
Начини пут којим ће доћи мач на Раву синова Амонових, и у Јудеју на тврди Јерусалим.
21 Pakuti mfumu ya ku Babuloni yayima pa msewu, pa mphambano ya misewu iwiriyo. Ikuwombeza ndi mivi yake kuti idziwe njira yoyenera kudzeramo. Ikupempha nzeru kwa milungu yake ndipo ikuyangʼana chiwindi cha nyama yoperekedwa ku nsembe.
Јер ће цар вавилонски стати на распутици, где почињу два пута, те ће врачати, гладиће стреле, питаће ликове, гледаће у јетру.
22 Mʼdzanja lake lamanja muli muvi waula wolembedwa Yerusalemu. Kumeneko mfumuyo idzayika zida zogumulira, idzalamula kupha anthu ndiponso kufuwula mfuwu wa nkhondo. Mfumuyo idzapanga zida zogumulira makoma, kuwunda mitumbira ya nkhondo ndi kumanga nsanja za nkhondo.
Надесно ће му врачање показати Јерусалим да намести убојне справе, да отвори уста на клање, да подигне глас подвикујући, да намести убојне справе према вратима, да начини опкопе, да погради куле.
23 Koma kwa anthu a ku Yerusalemu zidzaoneka ngati zowombeza zabodza chifukwa cha malumbiro amene anachita kwa mfumuyo. Koma mfumuyo idzawakumbutsa za zolakwa zawo kuti atengedwe ku ukapolo.
И учиниће се врачање залудно заклетима, а то ће напоменути безакоње да се ухвате.
24 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Popeza mwandikumbutsa zolakwa, moti kundiwukira kwanu kwaonekera poyera ndi kuti mu zochita zanu zonse mukuonetsa machimo anu, nʼchifukwa chake mudzagwidwa ndi kutengedwa ukapolo.
Зато овако вели Господ Господ: Што напомињете своје безакоње, те се открива невера ваша и греси се ваши виде у свим делима вашим, за то што дођосте на памет, бићете похватани руком.
25 “‘Tsono iwe kalonga wonyozedwa ndi woyipa wa Israeli, amene tsiku lako lafika, amene nthawi yako yolangidwa yafika penipeni,
А ти, нечисти безбожниче, кнеже Израиљев, коме дође дан кад би на крају безакоње,
26 Ambuye Yehova akuti: Vula nduwira, chotsa chipewa chaufumu. Zinthu sizidzakhala monga zinalili: anthu wamba adzakwezedwa ndipo okwezedwa adzatsitsidwa.
Овако вели Господ Господ: Скини ту капу и сврзи тај венац, неће га бити; ниског ћу узвисити а високог ћу понизити.
27 Chipasupasu! Chipasupasu! Ine ndidzawupasula mzindawo! Ndipo sadzawumanganso mpaka atafika amene ali woyenera kuwulandira; Ine ndidzawupereka kwa iyeyo.’
Уништићу, уништићу, уништићу га, и неће га бити, докле не дође онај коме припада, и њему ћу га дати.
28 “Ndipo iwe mwana wa munthu, nenera kuti, ponena za Aamoni ndi zonyoza zawo, Ambuye Yehova akuti, “‘Lupanga, lupanga, alisolola kuti liphe anthu, alipukuta kuti liwononge ndi kuti lingʼanime ngati mphenzi.
А ти, сине човечји, пророкуј и реци: Овако вели Господ Господ за синове Амонове и за њихову срамоту; реци дакле: мач, мач је извучен, углађен да коље, да затире, да сева,
29 Zimene akuti akuona mʼmasomphenya zokhudza inu ndi zabodza. Mawula awo okhudza inu ndi abodzanso. Mudzakhala pamodzi ndi anthu oyipa amene tsiku lawo lafika, ndiye kuti nthawi ya kulangidwa kwawo komaliza.
Докле ти виђају таштину, докле ти гатају лаж, да те метну на вратове побијеним безбожницима, којима дође дан кад би крај безакоњу.
30 “‘Bwezerani lupanga mʼchimake. Ku malo kumene inu munabadwira, mʼdziko la makolo anu, ndidzakuweruzani.
Остави мач у корице, на месту где си се родио, у земљи где си постао, судићу ти;
31 Ndidzakhuthula ukali wanga pa inu, ndipo mkwiyo wanga udzakuyakirani. Ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu ankhanza; anthu odziwa bwino kuwononga zinthu.
И излићу на те гнев свој, огњем гнева свог дунућу на те и предаћу те у руке жестоким људима, вештим у затирању.
32 Mudzakhala ngati nkhuni pa moto. Ena adzakhetsa magazi anu mʼdziko lanu lomwe. Simudzakumbukiridwanso pakuti Ine Yehova ndayankhula.’”
Огњу ћеш бити храна, крв ће ти бити посред земље, нећеш се спомињати, јер ја Господ рекох.