< Ezekieli 21 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
Ilizwi likaThixo lafika kimi lisithi:
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane ku Yerusalemu ndipo ulalike mawu odzudzula malo ake opatulika. Unenere zodzudzula anthu a ku Yerusalemu.
“Ndodana yomuntu, khangelisa ubuso bakho eJerusalema utshumayele okubi ngendawo engcwele. Phrofetha okubi ngelizwe lako-Israyeli
3 Uwawuze kuti, Ambuye Yehova akuti, ‘Taona, Ine ndidzalimbana nawe. Ndidzasolola lupanga langa mʼchimake ndi kuwononga anthu olungama ndi ochimwa omwe.
uthi kulo: ‘Nanku okutshiwo nguThixo Wobukhosi: Ngixabane lani. Ngizahwatsha inkemba yami emxhakeni wayo ngisuse kuwe abalungileyo lababi.
4 Motero ndidzapha aliyense kuchokera kummawa mpaka kumpoto.
Ngoba ngizasusa abalungileyo lababi, inkemba yami izahwatshelwa ukumelana labo bonke abavela eningizimu kanye lasenyakatho.
5 Pamenepo anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndasolola lupanga langa mʼchimake; sindidzalilowetsanso mʼchimakemo.’
Lapho-ke abantu bonke bazakwazi ukuthi mina nginguThixo sengihwatshe inkemba yami emxhakeni wayo, kayiyikubuyela futhi.’
6 “Tsono iwe mwana wa munthu, buwula. Buwula pamaso pawo ndi mtima wosweka ndi wachisoni chachikulu.
Ngakho-ke bubula ndodana yomuntu! Bubula phambi kwabo ngenhliziyo edabukileyo kanye losizi olukhulu.
7 Ndipo akadzakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukubuwula?’ Iwe udzayankhe kuti, ‘Ndikubuwula chifukwa cha nkhani imene ndamva. Zikadzachitika zimenezi, mitima yonse idzangoti fumu, manja onse adzangolefuka, mpweya wawo udzawathera, ndipo mawondo onse adzangoti zii.’ Izi zikubwera! Ndipo zidzachitika ndithu, akutero Ambuye Yehova.”
Nxa bekubuza besithi, ‘Kungani na ububula?’ uzakuthi, ‘Ngenxa yezindaba ezifikayo. Zonke inhliziyo zizenyela lezandla zonke zibe buthakathaka, imimoya yonke izaphela amandla lamadolo wonke abe buthakathaka njengamanzi.’ Kuyeza! Ngempela kuzakwenzakala, kutsho uThixo Wobukhosi.”
8 Yehova anandiyankhulanso kuti,
Ilizwi likaThixo lafika kimi lisithi:
9 “Iwe mwana wa munthu, unenere ndipo unene kuti, Ambuye Yehova akuti, “Izi ndi zimene Yehova akunena: Lupanga, lupanga, lanoledwa ndipo lapukutidwa.
“Ndodana yomuntu, phrofetha uthi, ‘Nanku okutshiwo nguThixo: Umhedla, umhedla, ilolwe njalo yalolongwa,
10 Lanoledwa kuti likaphe, lapukutidwa kuti lingʼanime ngati mphenzi! “‘Kodi tingakondwere bwanji? Wanyoza ndodo, mwana wanga ndi chilichonse cha mtengo.
Ilolelwe ukubulala, ilolongelwe ukuphazima njengombane. Kambe sizathokoza na ngentonga yobukhosi yendodana yami uJuda? Inkemba iyazeyisa zonke izigodo ezinjalo.
11 “‘Lupanga laperekedwa kuti lipukutidwe, ndi kuti linyamulidwe, lanoledwa ndi kupukutidwa, kuti liperekedwe mʼmanja mwa munthu amene amapha.
Inkemba ibekelwe ukuba ilolongwe, ukuba iphathwe ngesandla; iyalolwa ilolongwe, yenziwe ilungele isandla sombulali.
12 Fuwula ndi kulira, iwe mwana wa munthu, pakuti zimenezi zidzagwera anthu anga; zidzagweranso akalonga onse a Israeli. Adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi anthu anga. Chifukwa chake udzigugude pa chifuwa ndi chisoni.
Hlaba umkhosi ulile, ndodana yomuntu, ngoba imelane labantu bami; imelane lamakhosana wonke ako-Israyeli. Aphoselwa kuyo inkemba ndawonye labantu bami. Ngakho-ke bamba isihlathi sakho.
13 “‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Ndikuwayesa anthu anga, ndipo ngati satembenuka mtima, ndiye kuti zimenezi sizidzalephera kuwagwera.’
Ukuhlolwa kuyeza impela. Njalo kuzakuba njani nxa intonga kaJuda yobukhosi, edelelwa yinkemba, ingasaqhubeki? kutsho uThixo Wobukhosi.’
14 “Tsono mwana wa munthu, nenera ndipo uwombe mʼmanja. Lupanga likanthe kawiri ngakhale katatu. Limenelo ndilo lupanga lophera anthu. Inde ndilodi lupanga lophera anthu koopsa limene likuwazungulira.
Ngakho-ke, ndodana yomuntu, phrofetha uqakeze izandla zakho. Inkemba kayigadle kabili, lanxa kungaba kathathu. Yinkemba yokubulala, inkemba yokubulala kakhulu, ebahanqayo ivela macele wonke.
15 Ndawayikira pa zipata zawo zonse lupanga laphuliphuli kuti ataye mtima ndiponso kuti anthu ambiri agwe. Aa! Lapangidwa lupanga kuti lizingʼanima ngati mphenzi ndi kuti azilisolola kuphera anthu.
Ukuze inhliziyo zibe buthakathaka labawileyo babebanengi, sengibeke inkemba yokubulala kuwo wonke amasango abo. Bheka! Yenzelwe ukuphazima njengombane, iphathelwe ukubulala.
16 Iwe lupanga, ipha anthu kumanja, kenaka kumanzere, kulikonse kumene msonga yako yaloza.
Wena nkemba, geca kwesokudla, uphinde kwesenxele, loba kungaphi ubukhali bakho obuphendukela khona.
17 Inenso ndidzawomba mʼmanja mwanga, ndipo ndidzaziziritsa ukali wanga Ine Yehova ndayankhula.”
Lami futhi ngizaqakeza izandla zami, njalo ulaka lwami luzadeda. Mina Thixo sengikhulumile.”
18 Yehova anandiyankhulanso kuti,
Ilizwi likaThixo lafika kimi lisithi:
19 “Iwe mwana wa munthu, ulembe zizindikiro za misewu iwiri imene lupanga la mfumu ya ku Babuloni lingathe kudzeramo. Misewu yonse ikhale yochokera mʼdziko limodzi. Ika chikwangwani pa mphambano yopita mu mzinda.
“Ndodana yomuntu, canda imigwaqo emibili yenkemba yenkosi yaseBhabhiloni ukuba ihambe kuyo, yomibili iqalise elizweni linye. Yenza insika yesiqondiso lapho okuphambuka khona umgwaqo oya edolobheni.
20 Ulembe chizindikiro pa msewu umene lupanga lidzadzere popita ku Raba wa ku Amoni, ndiponso ku Yuda ndi ku Yerusalemu, mzinda wotetezedwa.
Canda omunye umgwaqo wenkemba ukuba izemelana leRabha yama-Amoni, lomunye ukumelana loJuda kanye leJerusalema elivikelweyo.
21 Pakuti mfumu ya ku Babuloni yayima pa msewu, pa mphambano ya misewu iwiriyo. Ikuwombeza ndi mivi yake kuti idziwe njira yoyenera kudzeramo. Ikupempha nzeru kwa milungu yake ndipo ikuyangʼana chiwindi cha nyama yoperekedwa ku nsembe.
Ngoba inkosi yaseBhabhiloni izakuma lapho imigwaqo eyehlukana khona, lapho okuhlangana khona imigwaqo emibili, ukuba ifune ibika: Izaphosa inkatho ngemitshoko, izabuza izithombe zayo, izahlola isibindi.
22 Mʼdzanja lake lamanja muli muvi waula wolembedwa Yerusalemu. Kumeneko mfumuyo idzayika zida zogumulira, idzalamula kupha anthu ndiponso kufuwula mfuwu wa nkhondo. Mfumuyo idzapanga zida zogumulira makoma, kuwunda mitumbira ya nkhondo ndi kumanga nsanja za nkhondo.
Esandleni sayo sokudla kuzakuza inkatho yeJerusalema, lapho ezamisa khona imigqala yokudiliza, lokunika umlayo wokubulala, lokuhlaba umkhosi wempi, lokumisa imigqala yokudiliza amasango, lokwakha amadundulu kanye lokumisa izindawo zokuvimbezela.
23 Koma kwa anthu a ku Yerusalemu zidzaoneka ngati zowombeza zabodza chifukwa cha malumbiro amene anachita kwa mfumuyo. Koma mfumuyo idzawakumbutsa za zolakwa zawo kuti atengedwe ku ukapolo.
Kuzakhanya angathi libika amanga kulabo asebefungele ukuthobeka kuyo, kodwa yona izabakhumbuza icala labo ibathumbe.
24 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Popeza mwandikumbutsa zolakwa, moti kundiwukira kwanu kwaonekera poyera ndi kuti mu zochita zanu zonse mukuonetsa machimo anu, nʼchifukwa chake mudzagwidwa ndi kutengedwa ukapolo.
Ngakho nanku okutshiwo nguThixo Wobukhosi: ‘Njengoba lina bantu lingikhumbuze icala lenu ngokuhlamuka kwenu okusobala, libonakalisa izono zenu kukho konke elikwenzayo njengoba lenze lokhu, lizathunjwa.
25 “‘Tsono iwe kalonga wonyozedwa ndi woyipa wa Israeli, amene tsiku lako lafika, amene nthawi yako yolangidwa yafika penipeni,
Wena nkosana yako-Israyeli exhwalileyo njalo embi, usuku lwakho selufikile, lesikhathi sokujeziswa kwakho sesifike emaphethelweni,
26 Ambuye Yehova akuti: Vula nduwira, chotsa chipewa chaufumu. Zinthu sizidzakhala monga zinalili: anthu wamba adzakwezedwa ndipo okwezedwa adzatsitsidwa.
nanku okutshiwo nguThixo Wobukhosi: Khupha iqhiye, yethula umqhele. Akuyikuba njengoba kwakunjalo: Abaphansi bazaphakanyiswa kuthi abaphakemeyo behliselwe phansi.
27 Chipasupasu! Chipasupasu! Ine ndidzawupasula mzindawo! Ndipo sadzawumanganso mpaka atafika amene ali woyenera kuwulandira; Ine ndidzawupereka kwa iyeyo.’
Unxiwa! Unxiwa! Ngizawenza ube lunxiwa! Kawuyikubuyiselwa kuze kufike lowo ongowakhe ngokuqondileyo, onguye engizamnika wona.’
28 “Ndipo iwe mwana wa munthu, nenera kuti, ponena za Aamoni ndi zonyoza zawo, Ambuye Yehova akuti, “‘Lupanga, lupanga, alisolola kuti liphe anthu, alipukuta kuti liwononge ndi kuti lingʼanime ngati mphenzi.
Njalo wena, ndodana yomuntu, phrofetha uthi, ‘Nanku okutshiwo nguThixo Wobukhosi ngama-Amoni kanye lezithuko zawo: Inkemba, inkemba, ihwatshelwe ukubulala, ilolongelwe ukuqothula lokuphazima njengombane!
29 Zimene akuti akuona mʼmasomphenya zokhudza inu ndi zabodza. Mawula awo okhudza inu ndi abodzanso. Mudzakhala pamodzi ndi anthu oyipa amene tsiku lawo lafika, ndiye kuti nthawi ya kulangidwa kwawo komaliza.
Langaphezu kwemibono yamanga ngawe, lokuhlahlula okungamanga ngawe, izabekwa entanyeni zababi okumele babulawe, abasuku lwabo selufikile, abasikhathi sokujeziswa kwabo sesifike emaphethelweni aso.
30 “‘Bwezerani lupanga mʼchimake. Ku malo kumene inu munabadwira, mʼdziko la makolo anu, ndidzakuweruzani.
Buyisela inkemba emxhakeni wayo. Endaweni owadalelwa kuyo, elizweni labokhokho bakho, ngizakwahlulela khona.
31 Ndidzakhuthula ukali wanga pa inu, ndipo mkwiyo wanga udzakuyakirani. Ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu ankhanza; anthu odziwa bwino kuwononga zinthu.
Ngizathululela ulaka lwami phezu kwakho ngiphefumlele lentukuthelo yami etshisayo kuwe; ngizakunikela ebantwini abalesihluku, abantu abakwaziyo ukuqothula.
32 Mudzakhala ngati nkhuni pa moto. Ena adzakhetsa magazi anu mʼdziko lanu lomwe. Simudzakumbukiridwanso pakuti Ine Yehova ndayankhula.’”
Uzakuba zinkuni zomlilo, igazi lakho lizachithelwa elizweni lakini, kawuyikukhunjulwa futhi; ngoba mina Thixo sengikhulumile.’”

< Ezekieli 21 >