< Ezekieli 21 >
1 Yehova anandiyankhula nati:
Et la parole du Seigneur me vint, disant:
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane ku Yerusalemu ndipo ulalike mawu odzudzula malo ake opatulika. Unenere zodzudzula anthu a ku Yerusalemu.
À cause de cela, prophétise, fils de l'homme, tourne ton visage contre Jérusalem, et regarde ses lieux saints, et prophétise contre la terre d'Israël.
3 Uwawuze kuti, Ambuye Yehova akuti, ‘Taona, Ine ndidzalimbana nawe. Ndidzasolola lupanga langa mʼchimake ndi kuwononga anthu olungama ndi ochimwa omwe.
Et dis à la terre d'Israël: Ainsi parle le Seigneur: Voilà que je suis contre toi, et je tirerai le glaive du fourreau, et j'exterminerai parmi-toi l'injuste et le pécheur.
4 Motero ndidzapha aliyense kuchokera kummawa mpaka kumpoto.
Et parce que j'exterminerai en toi l'injuste et le pécheur, mon glaive sortira du fourreau, contre toute chair, de l'orient à l'aquilon.
5 Pamenepo anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndasolola lupanga langa mʼchimake; sindidzalilowetsanso mʼchimakemo.’
Et toute chair saura que moi, le Seigneur, j'aurai tiré le glaive du fourreau, et je ne le remettrai plus.
6 “Tsono iwe mwana wa munthu, buwula. Buwula pamaso pawo ndi mtima wosweka ndi wachisoni chachikulu.
Et toi, fils de l'homme, pousse des soupirs à te rompre les reins; et en tes douleurs gémis devant leurs yeux.
7 Ndipo akadzakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukubuwula?’ Iwe udzayankhe kuti, ‘Ndikubuwula chifukwa cha nkhani imene ndamva. Zikadzachitika zimenezi, mitima yonse idzangoti fumu, manja onse adzangolefuka, mpweya wawo udzawathera, ndipo mawondo onse adzangoti zii.’ Izi zikubwera! Ndipo zidzachitika ndithu, akutero Ambuye Yehova.”
Et s'ils te disent: Pourquoi gémis-tu? réponds: À cause d'une nouvelle, parce que l'ennemi vient; et tout cœur sera brisé, et toutes mains seront énervées; et toute chair, tout souffle seront défaillants, et tous genoux souillés d'humeurs; car voilà qu'il vient, dit le Seigneur.
8 Yehova anandiyankhulanso kuti,
Et la parole du Seigneur me vint, disant:
9 “Iwe mwana wa munthu, unenere ndipo unene kuti, Ambuye Yehova akuti, “Izi ndi zimene Yehova akunena: Lupanga, lupanga, lanoledwa ndipo lapukutidwa.
Fils de l'homme, prophétise, et dis: Ainsi parle le Seigneur: Dis: Glaive, glaive, aiguise-toi, et mets-toi en fureur,
10 Lanoledwa kuti likaphe, lapukutidwa kuti lingʼanime ngati mphenzi! “‘Kodi tingakondwere bwanji? Wanyoza ndodo, mwana wanga ndi chilichonse cha mtengo.
Pour égorger des victimes; aiguise-toi pour briller; prépare-toi pour tout affaiblir. Égorge, anéantis, abats tout arbre.
11 “‘Lupanga laperekedwa kuti lipukutidwe, ndi kuti linyamulidwe, lanoledwa ndi kupukutidwa, kuti liperekedwe mʼmanja mwa munthu amene amapha.
Et il l'a préparé pour le tenir en sa main. Le glaive est aiguisé, il est préparé pour être dans la main de celui qui transperce.
12 Fuwula ndi kulira, iwe mwana wa munthu, pakuti zimenezi zidzagwera anthu anga; zidzagweranso akalonga onse a Israeli. Adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi anthu anga. Chifukwa chake udzigugude pa chifuwa ndi chisoni.
Pousse des cris et des hurlements, fils de l'homme; car ce glaive est venu sur mon peuple, il est venu sur tous les princes d'Israël; ils seront comme des passagers; le jugement avec le glaive est venu sur mon peuple. C'est pourquoi bats des mains.
13 “‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Ndikuwayesa anthu anga, ndipo ngati satembenuka mtima, ndiye kuti zimenezi sizidzalephera kuwagwera.’
Car il est condamné. Et qu'arrivera-t-il, si la famille entière est répudiée? Cela ne sera pas, dit le Seigneur Maître.
14 “Tsono mwana wa munthu, nenera ndipo uwombe mʼmanja. Lupanga likanthe kawiri ngakhale katatu. Limenelo ndilo lupanga lophera anthu. Inde ndilodi lupanga lophera anthu koopsa limene likuwazungulira.
Et toi, fils de l'homme, prophétise et bats des mains; prends deux glaives; et prends-en un troisième, le glaive, le grand glaive des tués. Mets-les hors d'eux-mêmes;
15 Ndawayikira pa zipata zawo zonse lupanga laphuliphuli kuti ataye mtima ndiponso kuti anthu ambiri agwe. Aa! Lapangidwa lupanga kuti lizingʼanima ngati mphenzi ndi kuti azilisolola kuphera anthu.
De peur que leur cœur ne se brise, et que les malades ne se multiplient auprès de toutes les portes; c'est par le glaive qu'ils doivent périr; il est tout prêt à les égorger; il est tout prêt à resplendir.
16 Iwe lupanga, ipha anthu kumanja, kenaka kumanzere, kulikonse kumene msonga yako yaloza.
Accours, glaive, aiguise-toi à droite, aiguise-toi à gauche, aiguise-toi sur toutes tes faces.
17 Inenso ndidzawomba mʼmanja mwanga, ndipo ndidzaziziritsa ukali wanga Ine Yehova ndayankhula.”
Et moi aussi, je battrai des mains, et j'assouvirai ma colère; c'est moi, le Seigneur, qui ai parlé.
18 Yehova anandiyankhulanso kuti,
Et la parole du Seigneur me vint, disant:
19 “Iwe mwana wa munthu, ulembe zizindikiro za misewu iwiri imene lupanga la mfumu ya ku Babuloni lingathe kudzeramo. Misewu yonse ikhale yochokera mʼdziko limodzi. Ika chikwangwani pa mphambano yopita mu mzinda.
Et toi, fils de l'homme, représente-toi deux voies par où entrera le glaive du roi de Babylone. Toutes les deux partiront d'une même contrée; et il y aura une main à l'extrémité du chemin de la ville; tu la traceras à l'extrémité du chemin,
20 Ulembe chizindikiro pa msewu umene lupanga lidzadzere popita ku Raba wa ku Amoni, ndiponso ku Yuda ndi ku Yerusalemu, mzinda wotetezedwa.
Par où le glaive entrera pour attaquer Rabbath, l'un des fils d'Ammon, puis la Judée, et au milieu Jérusalem.
21 Pakuti mfumu ya ku Babuloni yayima pa msewu, pa mphambano ya misewu iwiriyo. Ikuwombeza ndi mivi yake kuti idziwe njira yoyenera kudzeramo. Ikupempha nzeru kwa milungu yake ndipo ikuyangʼana chiwindi cha nyama yoperekedwa ku nsembe.
Car le roi de Babylone s'arrêtera sur le vieux chemin, à la tête des deux chemins; attendant que les devins prennent les augures, que l'eau bouillante rejette une baguette, que l'on consulte les idoles, et que l'on interroge à droite le foie des victimes.
22 Mʼdzanja lake lamanja muli muvi waula wolembedwa Yerusalemu. Kumeneko mfumuyo idzayika zida zogumulira, idzalamula kupha anthu ndiponso kufuwula mfuwu wa nkhondo. Mfumuyo idzapanga zida zogumulira makoma, kuwunda mitumbira ya nkhondo ndi kumanga nsanja za nkhondo.
Et la divination a été faite contre Jérusalem; et le roi y plantera des palissades, il ouvrira la bouche pour crier, et il poussera une voix formidable; il plantera des palissades devant les portes de la ville, il fera des levées de terre, et il établira des balistes.
23 Koma kwa anthu a ku Yerusalemu zidzaoneka ngati zowombeza zabodza chifukwa cha malumbiro amene anachita kwa mfumuyo. Koma mfumuyo idzawakumbutsa za zolakwa zawo kuti atengedwe ku ukapolo.
Cependant à leurs yeux il ne sera pour eux qu'un devin prenant les augures; mais il se rappellera les iniquités de leur prince.
24 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Popeza mwandikumbutsa zolakwa, moti kundiwukira kwanu kwaonekera poyera ndi kuti mu zochita zanu zonse mukuonetsa machimo anu, nʼchifukwa chake mudzagwidwa ndi kutengedwa ukapolo.
C'est pourquoi voici ce que dit le Seigneur: Parce que vous lui avez donné occasion de se rappeler le souvenir de votre iniquité, en dévoilant votre impiété, en faisant voir vos péchés: à cause de toutes vos impiétés et de vos idoles, en punition des crimes que vous lui avez rappelés, vous périrez.
25 “‘Tsono iwe kalonga wonyozedwa ndi woyipa wa Israeli, amene tsiku lako lafika, amene nthawi yako yolangidwa yafika penipeni,
Et toi, profane, impie roi d'Israël, dont le jour est venu, le jour marqué comme terme à ton iniquité,
26 Ambuye Yehova akuti: Vula nduwira, chotsa chipewa chaufumu. Zinthu sizidzakhala monga zinalili: anthu wamba adzakwezedwa ndipo okwezedwa adzatsitsidwa.
Voici ce que dit le Seigneur: Tu lui as ôté la tiare, tu as mis à sa place ta couronne, et il n'y en aura plus de pareille; tu as abaissé ce qui était haut; tu as élevé ce qui était bas.
27 Chipasupasu! Chipasupasu! Ine ndidzawupasula mzindawo! Ndipo sadzawumanganso mpaka atafika amene ali woyenera kuwulandira; Ine ndidzawupereka kwa iyeyo.’
À cette couronne j'imputerai iniquité, iniquité, iniquité. Malheur à elle! telle elle restera, jusqu'à ce que vienne celui à qui elle est destinée, et je la lui livrerai.
28 “Ndipo iwe mwana wa munthu, nenera kuti, ponena za Aamoni ndi zonyoza zawo, Ambuye Yehova akuti, “‘Lupanga, lupanga, alisolola kuti liphe anthu, alipukuta kuti liwononge ndi kuti lingʼanime ngati mphenzi.
Et toi, fils de l'homme, prophétise et dis: Ainsi parle le Seigneur aux fils d'Ammon pour leur opprobre: Glaive, glaive, tiré pour le carnage, et tiré pour la destruction, lève-toi pour briller!
29 Zimene akuti akuona mʼmasomphenya zokhudza inu ndi zabodza. Mawula awo okhudza inu ndi abodzanso. Mudzakhala pamodzi ndi anthu oyipa amene tsiku lawo lafika, ndiye kuti nthawi ya kulangidwa kwawo komaliza.
Pendant ta vision vaine, ô Ammon, pendant ta fausse divination, glaive, anime-toi pour frapper au col les impies dont le jour est venu, le jour marqué comme terme à l'iniquité d'Ammon!
30 “‘Bwezerani lupanga mʼchimake. Ku malo kumene inu munabadwira, mʼdziko la makolo anu, ndidzakuweruzani.
Rentre dans le fourreau; mais tu ne trouveras pas le repos au lieu où tu es né; je te jugerai en ta propre terre.
31 Ndidzakhuthula ukali wanga pa inu, ndipo mkwiyo wanga udzakuyakirani. Ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu ankhanza; anthu odziwa bwino kuwononga zinthu.
Et je ferai tomber ma colère sur toi; je soufflerai contre toi dans le feu de ma colère, et je te livrerai aux mains d'hommes barbares, habiles à porter avec eux la destruction.
32 Mudzakhala ngati nkhuni pa moto. Ena adzakhetsa magazi anu mʼdziko lanu lomwe. Simudzakumbukiridwanso pakuti Ine Yehova ndayankhula.’”
Tu seras la pâture du feu; ton sang sera au milieu de ta terre, et il ne restera de toi aucun souvenir; car c'est moi, le Seigneur, qui ai parlé.