< Ezekieli 21 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
The word of ye Lord came to me againe, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane ku Yerusalemu ndipo ulalike mawu odzudzula malo ake opatulika. Unenere zodzudzula anthu a ku Yerusalemu.
Sonne of man, set thy face toward Ierusalem, and drop thy word toward the holy places, and prophecie against the land of Israel.
3 Uwawuze kuti, Ambuye Yehova akuti, ‘Taona, Ine ndidzalimbana nawe. Ndidzasolola lupanga langa mʼchimake ndi kuwononga anthu olungama ndi ochimwa omwe.
And say to the land of Israel, Thus saith the Lord, Beholde, I come against thee, and will drawe my sword out of his sheath, and cut off from thee both the righteous and the wicked.
4 Motero ndidzapha aliyense kuchokera kummawa mpaka kumpoto.
Seeing then that I will cut off from thee both the righteous and wicked, therefore shall my sworde goe out of his sheath against all flesh from the South to the North,
5 Pamenepo anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndasolola lupanga langa mʼchimake; sindidzalilowetsanso mʼchimakemo.’
That all flesh may knowe that I the Lord haue drawen my sworde out of his sheath, and it shall not returne any more.
6 “Tsono iwe mwana wa munthu, buwula. Buwula pamaso pawo ndi mtima wosweka ndi wachisoni chachikulu.
Mourne therefore, thou sonne of man, as in the paine of thy reines, and mourne bitterly before them.
7 Ndipo akadzakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukubuwula?’ Iwe udzayankhe kuti, ‘Ndikubuwula chifukwa cha nkhani imene ndamva. Zikadzachitika zimenezi, mitima yonse idzangoti fumu, manja onse adzangolefuka, mpweya wawo udzawathera, ndipo mawondo onse adzangoti zii.’ Izi zikubwera! Ndipo zidzachitika ndithu, akutero Ambuye Yehova.”
And if they say vnto thee, Wherefore mournest thou? then answere, Because of the bruite: for it commeth, and euery heart shall melt, and all handes shall be weake, and all mindes shall faint, and all knees shall fall away as water: beholde, it commeth, and shall be done, saith the Lord God.
8 Yehova anandiyankhulanso kuti,
Againe, the word of the Lord came vnto me, saying,
9 “Iwe mwana wa munthu, unenere ndipo unene kuti, Ambuye Yehova akuti, “Izi ndi zimene Yehova akunena: Lupanga, lupanga, lanoledwa ndipo lapukutidwa.
Sonne of man, prophecie, and say, Thus saith the Lord God, say, A sworde, a sworde both sharpe, and fourbished.
10 Lanoledwa kuti likaphe, lapukutidwa kuti lingʼanime ngati mphenzi! “‘Kodi tingakondwere bwanji? Wanyoza ndodo, mwana wanga ndi chilichonse cha mtengo.
It is sharpened to make a sore slaughter, and it is fourbished that it may glitter: how shall we reioyce? for it contemneth the rod of my sonne, as all other trees.
11 “‘Lupanga laperekedwa kuti lipukutidwe, ndi kuti linyamulidwe, lanoledwa ndi kupukutidwa, kuti liperekedwe mʼmanja mwa munthu amene amapha.
And he hath giuen it to be fourbished, that he may handle it: this sword is sharpe, and is fourbished, that he may giue it into ye hand of the slayer.
12 Fuwula ndi kulira, iwe mwana wa munthu, pakuti zimenezi zidzagwera anthu anga; zidzagweranso akalonga onse a Israeli. Adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi anthu anga. Chifukwa chake udzigugude pa chifuwa ndi chisoni.
Cry, and houle, sonne of man: for this shall come to my people, and it shall come vnto all the princes of Israel: the terrours of the sword shall be vpon my people: smite therefore vpon thy thigh.
13 “‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Ndikuwayesa anthu anga, ndipo ngati satembenuka mtima, ndiye kuti zimenezi sizidzalephera kuwagwera.’
For it is a triall, and what shall this be, if the sworde contemne euen the rodde? It shall be no more, saith the Lord God.
14 “Tsono mwana wa munthu, nenera ndipo uwombe mʼmanja. Lupanga likanthe kawiri ngakhale katatu. Limenelo ndilo lupanga lophera anthu. Inde ndilodi lupanga lophera anthu koopsa limene likuwazungulira.
Thou therefore, sonne of man, prophecie, and smite hand to hand, and let the sworde be doubled: let the sworde that hath killed, returne the third time: it is the sword of the great slaughter entring into their priuie chambers.
15 Ndawayikira pa zipata zawo zonse lupanga laphuliphuli kuti ataye mtima ndiponso kuti anthu ambiri agwe. Aa! Lapangidwa lupanga kuti lizingʼanima ngati mphenzi ndi kuti azilisolola kuphera anthu.
I haue brought the feare of the sword into all their gates to make their heart to faint, and to multiplie their ruines. Ah it is made bright, and it is dressed for the slaughter.
16 Iwe lupanga, ipha anthu kumanja, kenaka kumanzere, kulikonse kumene msonga yako yaloza.
Get thee alone: goe to the right hande, or get thy selfe to the left hande, whithersoeuer thy face turneth.
17 Inenso ndidzawomba mʼmanja mwanga, ndipo ndidzaziziritsa ukali wanga Ine Yehova ndayankhula.”
I wil also smite mine hands together, and wil cause my wrath to cease. I the Lord haue said it.
18 Yehova anandiyankhulanso kuti,
The worde of the Lord came vnto mee againe, saying,
19 “Iwe mwana wa munthu, ulembe zizindikiro za misewu iwiri imene lupanga la mfumu ya ku Babuloni lingathe kudzeramo. Misewu yonse ikhale yochokera mʼdziko limodzi. Ika chikwangwani pa mphambano yopita mu mzinda.
Also thou sonne of man, appoint thee two wayes, that the sworde of the King of Babel may come: both twaine shall come out of one lande, and chuse a place, and chuse it in the corner of the way of the citie.
20 Ulembe chizindikiro pa msewu umene lupanga lidzadzere popita ku Raba wa ku Amoni, ndiponso ku Yuda ndi ku Yerusalemu, mzinda wotetezedwa.
Appoint a way, that the sworde may come to Rabbath of the Ammonites, and to Iudah in Ierusalem the strong citie.
21 Pakuti mfumu ya ku Babuloni yayima pa msewu, pa mphambano ya misewu iwiriyo. Ikuwombeza ndi mivi yake kuti idziwe njira yoyenera kudzeramo. Ikupempha nzeru kwa milungu yake ndipo ikuyangʼana chiwindi cha nyama yoperekedwa ku nsembe.
And the King of Babel stoode at the parting of the way, at the head of the two wayes, consulting by diuination, and made his arrowes bright: hee consulted with idoles, and looked in the liuer.
22 Mʼdzanja lake lamanja muli muvi waula wolembedwa Yerusalemu. Kumeneko mfumuyo idzayika zida zogumulira, idzalamula kupha anthu ndiponso kufuwula mfuwu wa nkhondo. Mfumuyo idzapanga zida zogumulira makoma, kuwunda mitumbira ya nkhondo ndi kumanga nsanja za nkhondo.
At his right hand was the diuination for Ierusalem to appoint captaines, to open their mouth in the slaughter, and to lift vp their voyce with shouting, to laye engines of warre against the gates, to cast a mount, and to builde a fortresse.
23 Koma kwa anthu a ku Yerusalemu zidzaoneka ngati zowombeza zabodza chifukwa cha malumbiro amene anachita kwa mfumuyo. Koma mfumuyo idzawakumbutsa za zolakwa zawo kuti atengedwe ku ukapolo.
And it shalbe vnto them as a false diuination in their sight for the othes made vnto them: but hee will call to remembrance their iniquitie, to the intent they should be taken.
24 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Popeza mwandikumbutsa zolakwa, moti kundiwukira kwanu kwaonekera poyera ndi kuti mu zochita zanu zonse mukuonetsa machimo anu, nʼchifukwa chake mudzagwidwa ndi kutengedwa ukapolo.
Therefore thus sayeth the Lord God, Because ye haue made your iniquitie to bee remembred, in discouering your rebellion, that in al your workes your sinnes might appeare: because, I say, that ye are come to remembrance, ye shall be taken with the hand.
25 “‘Tsono iwe kalonga wonyozedwa ndi woyipa wa Israeli, amene tsiku lako lafika, amene nthawi yako yolangidwa yafika penipeni,
And thou prince of Israel polluted, and wicked, whose day is come, when iniquitie shall haue an ende,
26 Ambuye Yehova akuti: Vula nduwira, chotsa chipewa chaufumu. Zinthu sizidzakhala monga zinalili: anthu wamba adzakwezedwa ndipo okwezedwa adzatsitsidwa.
Thus saith the Lord God, I will take away the diademe, and take off the crowne: this shalbe no more the same: I wil exalt the humble, and will abase him that is hie.
27 Chipasupasu! Chipasupasu! Ine ndidzawupasula mzindawo! Ndipo sadzawumanganso mpaka atafika amene ali woyenera kuwulandira; Ine ndidzawupereka kwa iyeyo.’
I wil ouerturne, ouerturne, ouerturne it, and it shall be no more vntill he come, whose right it is, and I will giue it him.
28 “Ndipo iwe mwana wa munthu, nenera kuti, ponena za Aamoni ndi zonyoza zawo, Ambuye Yehova akuti, “‘Lupanga, lupanga, alisolola kuti liphe anthu, alipukuta kuti liwononge ndi kuti lingʼanime ngati mphenzi.
And thou, sonne of man, prophecie, and say, Thus saith the Lord God to the children of Ammon, and to their blasphemie: say thou, I say, The sword, the sword is drawen foorth, and fourbished to the slaughter, to consume, because of the glittering:
29 Zimene akuti akuona mʼmasomphenya zokhudza inu ndi zabodza. Mawula awo okhudza inu ndi abodzanso. Mudzakhala pamodzi ndi anthu oyipa amene tsiku lawo lafika, ndiye kuti nthawi ya kulangidwa kwawo komaliza.
Whiles they see vanitie vnto thee, and prophecied a lie vnto thee to bring thee vpon the neckes of the wicked that are slaine, whose day is come when their iniquitie shall haue an ende.
30 “‘Bwezerani lupanga mʼchimake. Ku malo kumene inu munabadwira, mʼdziko la makolo anu, ndidzakuweruzani.
Shall I cause it to returne into his sheath? I will iudge thee in the place where thou wast created, euen in the land of thine habitation.
31 Ndidzakhuthula ukali wanga pa inu, ndipo mkwiyo wanga udzakuyakirani. Ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu ankhanza; anthu odziwa bwino kuwononga zinthu.
And I wil powre out mine indignation vpon thee, and will blowe against thee in the fire of my wrath, and deliuer thee into the hand of beastly men, and skilfull to destroy.
32 Mudzakhala ngati nkhuni pa moto. Ena adzakhetsa magazi anu mʼdziko lanu lomwe. Simudzakumbukiridwanso pakuti Ine Yehova ndayankhula.’”
Thou shalt bee in the fire to be deuoured: thy blood shall be in the middes of the lande, and thou shalt be no more remembred: for I the Lord haue spoken it.

< Ezekieli 21 >