< Ezekieli 21 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
Opět stalo se slovo Hospodinovo ke mně, řkoucí:
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane ku Yerusalemu ndipo ulalike mawu odzudzula malo ake opatulika. Unenere zodzudzula anthu a ku Yerusalemu.
Synu člověčí, obrať tvář svou k Jeruzalému, a vypusť jako rosu proti místům svatým, a prorokuj proti zemi Izraelské.
3 Uwawuze kuti, Ambuye Yehova akuti, ‘Taona, Ine ndidzalimbana nawe. Ndidzasolola lupanga langa mʼchimake ndi kuwononga anthu olungama ndi ochimwa omwe.
A rci zemi Izraelské: Takto praví Hospodin: Aj, já jsem proti tobě, a vytáhnu meč svůj z pošvy jeho, a vypléním z tebe spravedlivého i bezbožného.
4 Motero ndidzapha aliyense kuchokera kummawa mpaka kumpoto.
Proto, abych vyplénil z tebe spravedlivého i bezbožného, proto vyjde meč můj z pošvy své proti všelikému tělu, od poledne až na půlnoci.
5 Pamenepo anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndasolola lupanga langa mʼchimake; sindidzalilowetsanso mʼchimakemo.’
I zvíť všeliké tělo, že jsem já Hospodin vytáhl meč svůj z pošvy jeho; nenavrátíť se zase více.
6 “Tsono iwe mwana wa munthu, buwula. Buwula pamaso pawo ndi mtima wosweka ndi wachisoni chachikulu.
Ty pak synu člověčí, vzdychej, jako bys zlámaná měl bedra, a to s hořekováním vzdychej před očima jejich.
7 Ndipo akadzakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukubuwula?’ Iwe udzayankhe kuti, ‘Ndikubuwula chifukwa cha nkhani imene ndamva. Zikadzachitika zimenezi, mitima yonse idzangoti fumu, manja onse adzangolefuka, mpweya wawo udzawathera, ndipo mawondo onse adzangoti zii.’ Izi zikubwera! Ndipo zidzachitika ndithu, akutero Ambuye Yehova.”
I stane se, žeť řeknou: Nad čím ty vzdycháš? Tedy řekneš: Nad pověstí, kteráž přichází, k níž rozplyne se každé srdce, a každé ruce klesnou, a všeliký duch skormoutí se, a každá kolena rozplynou se jako voda. Aj, přicházíť a děje se, praví Panovník Hospodin.
8 Yehova anandiyankhulanso kuti,
Opět stalo se slovo Hospodinovo ke mně, řkoucí:
9 “Iwe mwana wa munthu, unenere ndipo unene kuti, Ambuye Yehova akuti, “Izi ndi zimene Yehova akunena: Lupanga, lupanga, lanoledwa ndipo lapukutidwa.
Synu člověčí, prorokuj a rci: Takto praví Hospodin: Rci: Meč, meč nabroušen, také i vyčištěn jest.
10 Lanoledwa kuti likaphe, lapukutidwa kuti lingʼanime ngati mphenzi! “‘Kodi tingakondwere bwanji? Wanyoza ndodo, mwana wanga ndi chilichonse cha mtengo.
Aby zabíjel k zabití oddané, nabroušen jest; aby se blyštěl, vyčištěn jest. Radovati-liž se budeme, když prut syna mého pohrdá každým dřevem?
11 “‘Lupanga laperekedwa kuti lipukutidwe, ndi kuti linyamulidwe, lanoledwa ndi kupukutidwa, kuti liperekedwe mʼmanja mwa munthu amene amapha.
Dalť jej vyčistiti, aby v ruku vzat byl; jestiť nabroušený meč, jest i vyčištěný, aby dán byl do ruky mordujícího.
12 Fuwula ndi kulira, iwe mwana wa munthu, pakuti zimenezi zidzagwera anthu anga; zidzagweranso akalonga onse a Israeli. Adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi anthu anga. Chifukwa chake udzigugude pa chifuwa ndi chisoni.
Křič a kvěl, synu člověčí, proto že ten bude proti lidu mému, tentýž proti všechněm knížatům Izraelským; uvrženi budou na meč s lidem mým, protož bí se v bedra.
13 “‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Ndikuwayesa anthu anga, ndipo ngati satembenuka mtima, ndiye kuti zimenezi sizidzalephera kuwagwera.’
Když jsem je trestával, co bylo? Nemám-liž metly hubící již přičiniti? dí Hospodin zástupů.
14 “Tsono mwana wa munthu, nenera ndipo uwombe mʼmanja. Lupanga likanthe kawiri ngakhale katatu. Limenelo ndilo lupanga lophera anthu. Inde ndilodi lupanga lophera anthu koopsa limene likuwazungulira.
Ty tedy synu člověčí, prorokuj a tleskej rukama; nebo po druhé i po třetí přijde meč, meč mordujících, ten meč mordujících bez lítosti, pronikajících i do pokojů jejich.
15 Ndawayikira pa zipata zawo zonse lupanga laphuliphuli kuti ataye mtima ndiponso kuti anthu ambiri agwe. Aa! Lapangidwa lupanga kuti lizingʼanima ngati mphenzi ndi kuti azilisolola kuphera anthu.
Tak aby se rozplynulo srdce, a rozmnoženi byli úrazové, v každé bráně jejich postavím ostří meče. Ach, vyčištěnť jest, aby se blyštěl, zaostřen, aby zabíjel.
16 Iwe lupanga, ipha anthu kumanja, kenaka kumanzere, kulikonse kumene msonga yako yaloza.
Shlukni se a pusť se na pravo i na levo, kamžkoli a načkoli se tobě nahodí.
17 Inenso ndidzawomba mʼmanja mwanga, ndipo ndidzaziziritsa ukali wanga Ine Yehova ndayankhula.”
I jáť také tleskati budu rukama svýma, a doložím prchlivost svou. Já Hospodin mluvil jsem.
18 Yehova anandiyankhulanso kuti,
V tom stalo se slovo Hospodinovo ke mně, řkoucí:
19 “Iwe mwana wa munthu, ulembe zizindikiro za misewu iwiri imene lupanga la mfumu ya ku Babuloni lingathe kudzeramo. Misewu yonse ikhale yochokera mʼdziko limodzi. Ika chikwangwani pa mphambano yopita mu mzinda.
Ty pak synu člověčí, předlož sobě dvě cesty, kudy by jíti měl meč krále Babylonského. Z země jedné ať vycházejí obě dvě, a na rozcestí vybeř tu k městu, tu vybeř.
20 Ulembe chizindikiro pa msewu umene lupanga lidzadzere popita ku Raba wa ku Amoni, ndiponso ku Yuda ndi ku Yerusalemu, mzinda wotetezedwa.
Ukaž cestu, kudy by jíti měl meč, k Rabbat-li synů Ammon, čili k Judstvu, na Jeruzalémské pevnosti,
21 Pakuti mfumu ya ku Babuloni yayima pa msewu, pa mphambano ya misewu iwiriyo. Ikuwombeza ndi mivi yake kuti idziwe njira yoyenera kudzeramo. Ikupempha nzeru kwa milungu yake ndipo ikuyangʼana chiwindi cha nyama yoperekedwa ku nsembe.
Proto že stane král Babylonský na rozcestí, na počátku dvou cest, obíraje se s hádáním, vyčistí střely, doptávati se bude modl, hleděti bude do jater.
22 Mʼdzanja lake lamanja muli muvi waula wolembedwa Yerusalemu. Kumeneko mfumuyo idzayika zida zogumulira, idzalamula kupha anthu ndiponso kufuwula mfuwu wa nkhondo. Mfumuyo idzapanga zida zogumulira makoma, kuwunda mitumbira ya nkhondo ndi kumanga nsanja za nkhondo.
Po pravé ruce jeho hádání ukáže Jeruzalém, aby sšikoval hejtmany, kteříž by ponoukali k mordování, a pozdvihovali hlasu s prokřikováním, aby přistavili berany válečné proti branám, aby vysypán byl násyp, a vzdělání byli šancové.
23 Koma kwa anthu a ku Yerusalemu zidzaoneka ngati zowombeza zabodza chifukwa cha malumbiro amene anachita kwa mfumuyo. Koma mfumuyo idzawakumbutsa za zolakwa zawo kuti atengedwe ku ukapolo.
I budou to míti za hádání marné před očima svýma ti, jenž se zavázali přísahami; a toť přivede na pamět nepravost, kterouž by popadeni byli.
24 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Popeza mwandikumbutsa zolakwa, moti kundiwukira kwanu kwaonekera poyera ndi kuti mu zochita zanu zonse mukuonetsa machimo anu, nʼchifukwa chake mudzagwidwa ndi kutengedwa ukapolo.
Protož takto praví Panovník Hospodin: Proto že ku paměti přivodíte nepravost svou, a odkrývá se nevěra vaše, tak že jsou patrní hříchové vaši ve všech činech vašich, proto že na pamět přicházíte, rukou tou popadeni budete.
25 “‘Tsono iwe kalonga wonyozedwa ndi woyipa wa Israeli, amene tsiku lako lafika, amene nthawi yako yolangidwa yafika penipeni,
Ty pak nečistý bezbožníče, kníže Izraelské, jehož den přichází, a čas skonání nepravosti,
26 Ambuye Yehova akuti: Vula nduwira, chotsa chipewa chaufumu. Zinthu sizidzakhala monga zinalili: anthu wamba adzakwezedwa ndipo okwezedwa adzatsitsidwa.
Takto praví Panovník Hospodin: Sejmi tu čepici, a svrz tu korunu, kteráž nikdy již taková nebude; toho, kterýž na snížení přišel, povyš, a vyvýšeného poniž.
27 Chipasupasu! Chipasupasu! Ine ndidzawupasula mzindawo! Ndipo sadzawumanganso mpaka atafika amene ali woyenera kuwulandira; Ine ndidzawupereka kwa iyeyo.’
Zmotanou, zmotanou, zmotanou učiním ji, (čehož prvé nebývalo), až přijde ten, jenž má právo, kteréž jsem jemu dal.
28 “Ndipo iwe mwana wa munthu, nenera kuti, ponena za Aamoni ndi zonyoza zawo, Ambuye Yehova akuti, “‘Lupanga, lupanga, alisolola kuti liphe anthu, alipukuta kuti liwononge ndi kuti lingʼanime ngati mphenzi.
Ty pak synu člověčí, prorokuj a rci: Takto praví Panovník Hospodin o synech Ammon, i o pohanění jejich, rci, pravím: Meč, meč dobyt jest, k zabíjení vyčištěn jest, aby hubil všecko, a aby se blyštěl.
29 Zimene akuti akuona mʼmasomphenya zokhudza inu ndi zabodza. Mawula awo okhudza inu ndi abodzanso. Mudzakhala pamodzi ndi anthu oyipa amene tsiku lawo lafika, ndiye kuti nthawi ya kulangidwa kwawo komaliza.
A ačkoli předpovídají tobě marné věci, a hádají tobě lež, aby tě přiložili k hrdlům zbitých bezbožníků, jejichž den přichází a čas skonání nepravosti:
30 “‘Bwezerani lupanga mʼchimake. Ku malo kumene inu munabadwira, mʼdziko la makolo anu, ndidzakuweruzani.
Schovej meč do pošvy jeho. Na místě, na kterémž jsi zplozena, v zemi přebývání tvého, budu tě souditi.
31 Ndidzakhuthula ukali wanga pa inu, ndipo mkwiyo wanga udzakuyakirani. Ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu ankhanza; anthu odziwa bwino kuwononga zinthu.
A vyleji na tě rozhněvání své, ohněm prchlivosti své na tě dmýchati budu, a dám tě v ruku lidí vzteklých, řemeslníků všecko kazících.
32 Mudzakhala ngati nkhuni pa moto. Ena adzakhetsa magazi anu mʼdziko lanu lomwe. Simudzakumbukiridwanso pakuti Ine Yehova ndayankhula.’”
Budeš ohni k sežrání, krev tvá bude u prostřed země, nebudeš připomínána; neboť jsem já Hospodin mluvil.

< Ezekieli 21 >