< Ezekieli 21 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
Hina Gode da nama amane sia: i,
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane ku Yerusalemu ndipo ulalike mawu odzudzula malo ake opatulika. Unenere zodzudzula anthu a ku Yerusalemu.
“Dunu egefe! Di Yelusaleme fi ilima mimogoa fofada: ma! Sogebi amoga dunu ilia ogogosu ‘gode’ ilima nodone sia: ne gadosa, amoma mimogoa fofada: ma. Isala: ili sogega sisane amane sia: ma,
3 Uwawuze kuti, Ambuye Yehova akuti, ‘Taona, Ine ndidzalimbana nawe. Ndidzasolola lupanga langa mʼchimake ndi kuwononga anthu olungama ndi ochimwa omwe.
‘Na, Hina Gode, da dilima amane sia: sa, Na da dilima ha lai dunu esala. Na da Na gegesu gobihei duga: le gadole, dili huluane, noga: i amola wadela: i defele medole legemu.
4 Motero ndidzapha aliyense kuchokera kummawa mpaka kumpoto.
Na da dunu huluanedafa, ga (north) asili ga (south) esalebe, ilima Na gegesu gobiheiga gegemu.
5 Pamenepo anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndasolola lupanga langa mʼchimake; sindidzalilowetsanso mʼchimakemo.’
Dunu huluane da Na, Hina Gode, Na da Na gegesu gobihei amo duga: le gadole, bu hame salimu, amo ilia dawa: mu.
6 “Tsono iwe mwana wa munthu, buwula. Buwula pamaso pawo ndi mtima wosweka ndi wachisoni chachikulu.
Dunu egefe! Dia se baligili nababe dunu defele, gogonomoma. Gogolo nabi dunu defele, dunu huluane ba: ma: ne, gogonomoma.
7 Ndipo akadzakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukubuwula?’ Iwe udzayankhe kuti, ‘Ndikubuwula chifukwa cha nkhani imene ndamva. Zikadzachitika zimenezi, mitima yonse idzangoti fumu, manja onse adzangolefuka, mpweya wawo udzawathera, ndipo mawondo onse adzangoti zii.’ Izi zikubwera! Ndipo zidzachitika ndithu, akutero Ambuye Yehova.”
Ilia da dia gogonomosu bai dima adole ba: sea, ilima se iasu bagade da misunuba: le, di da gogonomosa sia: ma. Amo se nabasu da doaga: sea, ilia da bagade beda: mu, ilia lobo da gadaiamu, ilia da nimi hame ba: mu, amola ilia muguni da yagugumu. Eso da doaga: i dagoi,” Ouligisudafa Hina Gode da sia: i dagoi.
8 Yehova anandiyankhulanso kuti,
Hina Gode da nama amane sia: i,
9 “Iwe mwana wa munthu, unenere ndipo unene kuti, Ambuye Yehova akuti, “Izi ndi zimene Yehova akunena: Lupanga, lupanga, lanoledwa ndipo lapukutidwa.
“Dunu egefe! Ba: la: loma! Na, Hina Gode, Na sia: be amo dunuma adosisima, ‘Gegesu gobihei mei amola ela: mei diala.
10 Lanoledwa kuti likaphe, lapukutidwa kuti lingʼanime ngati mphenzi! “‘Kodi tingakondwere bwanji? Wanyoza ndodo, mwana wanga ndi chilichonse cha mtengo.
Gobihei da fane legemusa: debele mei. Amola ha: ha: na agoane ela: mene gala: ma: ne ela: mei. Na fi dunu da sisasu amola se iasu ea olelei, amo huluane hame nababeba: le, nodosu hamomu da hamedei.
11 “‘Lupanga laperekedwa kuti lipukutidwe, ndi kuti linyamulidwe, lanoledwa ndi kupukutidwa, kuti liperekedwe mʼmanja mwa munthu amene amapha.
Gobihei da giga: ne ela: mene gaguli lamusa: momagele legei dagoi diala. Amalu debele, giga: ne, medole legesu dunu ilia lobo da: iya ligisima: ne, momagei diala.
12 Fuwula ndi kulira, iwe mwana wa munthu, pakuti zimenezi zidzagwera anthu anga; zidzagweranso akalonga onse a Israeli. Adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi anthu anga. Chifukwa chake udzigugude pa chifuwa ndi chisoni.
Dunu egefe! Gogolole ha: gi dima! Amo gobihei da Na dunu amola Isala: ili ouligisu dunu huluane, ili medole legema: ne diala. Ili amola Na dunu huluane eno amola da gilisili medole legei dagoi ba: mu. Di da heawini se bagade nababeba: le, dia bida: gia lulufugima.
13 “‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Ndikuwayesa anthu anga, ndipo ngati satembenuka mtima, ndiye kuti zimenezi sizidzalephera kuwagwera.’
Na da Na dunuma adoba: sa. Amola ilia da sinidigimu higasea, amo sia: i liligi huluane da ilima doaga: mu.
14 “Tsono mwana wa munthu, nenera ndipo uwombe mʼmanja. Lupanga likanthe kawiri ngakhale katatu. Limenelo ndilo lupanga lophera anthu. Inde ndilodi lupanga lophera anthu koopsa limene likuwazungulira.
Dunu egefe! Na gasa bagade sia: Yelusaleme fi ilima adosima! Dia lobo fama! Amasea, gegesu gobihei sedade da eno fane, eno fane, fananumu. Amo gegesu gobihei da medole legema: ne, amola dunu beda: gia: ma: ne hamosu dawa:
15 Ndawayikira pa zipata zawo zonse lupanga laphuliphuli kuti ataye mtima ndiponso kuti anthu ambiri agwe. Aa! Lapangidwa lupanga kuti lizingʼanima ngati mphenzi ndi kuti azilisolola kuphera anthu.
Amo gegesu gobihei ea hamobeba: le, Na fi dunu da beda: igia: sa amola dafasa. Na da gobihei amo da ha: ha: na agoane gagala: sa, amola medole legemusa: momagei dagoi, amoga ilia moilai amoma magagisa.
16 Iwe lupanga, ipha anthu kumanja, kenaka kumanzere, kulikonse kumene msonga yako yaloza.
Gobihei mei! Di da dia lobodafadili, amola fofadidili ele galu damuma! Di da habodili delegisia, amo defele damuma.
17 Inenso ndidzawomba mʼmanja mwanga, ndipo ndidzaziziritsa ukali wanga Ine Yehova ndayankhula.”
Na da Na lobo famu, amasea Na ougi da gumi ba: mu. Na, Hina Gode da sia: i dagoi.”
18 Yehova anandiyankhulanso kuti,
Hina Gode da nama amane sia: i,
19 “Iwe mwana wa munthu, ulembe zizindikiro za misewu iwiri imene lupanga la mfumu ya ku Babuloni lingathe kudzeramo. Misewu yonse ikhale yochokera mʼdziko limodzi. Ika chikwangwani pa mphambano yopita mu mzinda.
“Dunu egefe! Ba: bilone hina bagade dunu da ea gobihei gaguli misa: ne, logo aduna ilegema. Ela da soge afadafa amoga hemomu. Logo da sagulufai galea, amogai dawa: digisu ifa bugima.
20 Ulembe chizindikiro pa msewu umene lupanga lidzadzere popita ku Raba wa ku Amoni, ndiponso ku Yuda ndi ku Yerusalemu, mzinda wotetezedwa.
Logo afae da Ba: bilone hina bagade dunu amoma A: mounaide moilai bai bagade La: ba amoga ahoasu logo olelemu, amola eno da Yuda fi ilia moilai bai bagade Yelusaleme gasa bagade gagili sali, amoga ahoasu olelemu.
21 Pakuti mfumu ya ku Babuloni yayima pa msewu, pa mphambano ya misewu iwiriyo. Ikuwombeza ndi mivi yake kuti idziwe njira yoyenera kudzeramo. Ikupempha nzeru kwa milungu yake ndipo ikuyangʼana chiwindi cha nyama yoperekedwa ku nsembe.
Ba: bilone hina bagade dunu da logo sagulufaia, dawa: digima: ne ifala dafulili lela. E da ea logo masunu dawa: ma: ne, ea dadi fofoga: sa. E da ea ogogosu loboga hamoi ‘gode’ ilima adole ba: sa. E da gobele salasu ohe ea habe abedesa.
22 Mʼdzanja lake lamanja muli muvi waula wolembedwa Yerusalemu. Kumeneko mfumuyo idzayika zida zogumulira, idzalamula kupha anthu ndiponso kufuwula mfuwu wa nkhondo. Mfumuyo idzapanga zida zogumulira makoma, kuwunda mitumbira ya nkhondo ndi kumanga nsanja za nkhondo.
Waha! Ea lobodafa da sou amoga ‘Yelusaleme’ dedei, amo gagui dialebe ba: sa. Amo da ema agoane olelesa. E da Yelusaleme amoga asili, ifa damui dou sosu amoga logo ga: su muguluma: ne, amola gegemusa: gini bulalisu, amola osobo gasa: gala: su, amola gegesu adobo dogosu, hamoma: ne olelesa.
23 Koma kwa anthu a ku Yerusalemu zidzaoneka ngati zowombeza zabodza chifukwa cha malumbiro amene anachita kwa mfumuyo. Koma mfumuyo idzawakumbutsa za zolakwa zawo kuti atengedwe ku ukapolo.
Yelusaleme fi dunu da musa: Ba: bilone hina bagade ema gousa: su ilegeiba: le, e da Yelusaleme amoma doagala: mu sia: , amo ilia da ogogosuyale dawa: mu. Be amo ba: la: lusu da ilia wadela: i hou hamoi ili dawa: digima: ne, amola ilia huluane da enoga doagala: le fedei dagoi ba: mu, amo olelema: ne misi.
24 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Popeza mwandikumbutsa zolakwa, moti kundiwukira kwanu kwaonekera poyera ndi kuti mu zochita zanu zonse mukuonetsa machimo anu, nʼchifukwa chake mudzagwidwa ndi kutengedwa ukapolo.
Na, Ouligisudafa Hina Gode, da amane sia: sa, ‘Dilia wadela: i hou musa: wamolegei dialu, wali dunu huluane ba: ma: ne odagia ba: sa. Dilia hamobe huluane da dilia wadela: i hou olelesa. Dilia dafawanedafa wadela: idafa hamoiba: le, Na da dilima fofada: ne, se iasu imunu gala. Na da dilia ha lai dunuma dili iagamu.
25 “‘Tsono iwe kalonga wonyozedwa ndi woyipa wa Israeli, amene tsiku lako lafika, amene nthawi yako yolangidwa yafika penipeni,
Di, wadela: idafa, hadigi hame, Isala: ili hina bagade dunu! Na da dima bogoma: ne se bidi imunu.
26 Ambuye Yehova akuti: Vula nduwira, chotsa chipewa chaufumu. Zinthu sizidzakhala monga zinalili: anthu wamba adzakwezedwa ndipo okwezedwa adzatsitsidwa.
Na, Ouligisudafa Hina Gode, da sia: i dagoi. Dia gouliga hamoi habuga, amola abulaga hamoi habuga, gisa: le fasima. Waha hou da afadenene, musa: agoane bu hame ba: mu. Na da hame gagui dunu, ilia soge gasawane ouligima: ne, gaguia gadomu. Na da wali gasa fi ouligisu dunu amo fadegale fasili, ilia da gudu sa: i dagoi ba: mu.
27 Chipasupasu! Chipasupasu! Ine ndidzawupasula mzindawo! Ndipo sadzawumanganso mpaka atafika amene ali woyenera kuwulandira; Ine ndidzawupereka kwa iyeyo.’
Gugunufinisisu! Dafawane! Yelusaleme da wadela: lesi dagoi ba: mu! Na da amo wadela: lesimu. Be dunu amo Na da e Yelusaleme fi ilima se ima: ne ilegei, amo da doaga: sea fawane amo hou ba: mu. Amasea, Na da Yelusaleme ema iagamu.
28 “Ndipo iwe mwana wa munthu, nenera kuti, ponena za Aamoni ndi zonyoza zawo, Ambuye Yehova akuti, “‘Lupanga, lupanga, alisolola kuti liphe anthu, alipukuta kuti liwononge ndi kuti lingʼanime ngati mphenzi.
“Dunu egefe! Ba: la: loma! Di, A:mounaide dunu (amo da Na fi Isala: ili dunuma gadesa) ilima Na gasa bagade sia: adosima. Amane sia: ma, ‘Gegesu gobihei bagade da dili wadela: lesimusa: momagei diala. E da medole legemusa: , amola ha: ha: na agoane nene gagala: musa: , ela: mei diala.
29 Zimene akuti akuona mʼmasomphenya zokhudza inu ndi zabodza. Mawula awo okhudza inu ndi abodzanso. Mudzakhala pamodzi ndi anthu oyipa amene tsiku lawo lafika, ndiye kuti nthawi ya kulangidwa kwawo komaliza.
Esala ba: su dilia ba: lala, amo da ogogosa. Amola dia ba: la: lusu da ogogosa. Dilia da wadela: idafa, amola dilia wadela: mu eso da mana. Fedege agoane, gegesu gobihei bagade da dilia galogoa hedofamu.
30 “‘Bwezerani lupanga mʼchimake. Ku malo kumene inu munabadwira, mʼdziko la makolo anu, ndidzakuweruzani.
Bu mae gegema: ne, dilia gegesu gobihei hina: salasuga sanasima. Na da dilia hahamoi soge amola dilia lalelegei soge amoga dilima fofada: mu.
31 Ndidzakhuthula ukali wanga pa inu, ndipo mkwiyo wanga udzakuyakirani. Ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu ankhanza; anthu odziwa bwino kuwononga zinthu.
Na da lalu agoane, Na ougi se bidi imunu, amola dilia da amo se nabimu. Amola Na da dili sa: digini fasu dawa: dunu, amo dili wadela: lesima: ne iagamu.
32 Mudzakhala ngati nkhuni pa moto. Ena adzakhetsa magazi anu mʼdziko lanu lomwe. Simudzakumbukiridwanso pakuti Ine Yehova ndayankhula.’”
Dilia da laluga gugunufinisi dagoi ba: mu. Dilia sogedafa amo ganodini, eno dunu da dili medole legemu. Amola, dunu enoga dili bu hame dawa: lumu. Bai Na, Hina Gode da sia: i dagoi.’”

< Ezekieli 21 >