< Ezekieli 20 >

1 Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu, chaka chachisanu ndi chiwiri, ena mwa akuluakulu a Israeli anabwera kudzapempha nzeru kwa Yehova, ndipo anakhala pansi pamaso panga.
I stało się roku siódmego, miesiąca piątego, dziesiątego dnia tegoż miesiąca, przyszli niektórzy z starszych Izraelskich, aby się radzili Pana; i usiedli przedemną.
2 Tsono Yehova anandiyankhula nati:
Tedy się stało słowo Pańskie do mnie, mówąc:
3 “Iwe mwana wa munthu, ayankhule akuluakulu a Israeli ndi kuwawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Kodi mwabwera kudzapempha nzeru kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, Ine sindidzakulolani kupempha nzeru kwa Ine, akutero Ambuye Yehova.’
Synu człowieczy! mów do starszych Izraelsich, a powiedz im: Tak mówi panujący Pan: Izali wy przychodzicie, abyście się mnie radzili? Jako żyję Ja, że się wy mnie nie radzicie, mówi panujący Pan;
4 “Kodi uwaweruza? Iwe mwana wa munthu, kodi ugamula mlandu wawo? Uwadziwitse tsono zonyansa zimene anachita makolo awo, uwawuze kuti,
Izali się za nich zastawiać będziesz? Izali się za nich zastawiać będziesz, synu człowieczy? Oznajmij im raczej obrzydliwości ojców ich,
5 ‘Ambuye Yehova akuti: Pa tsiku limene ndinasankha Israeli, ndinalumbira kwa zidzukulu za nyumba ya Yakobo ndipo ndinadziwulula kwa iwo ku Igupto. Ndinalumbira ndi kuwawuza kuti: Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
A rzecz do nich: Tak mówi panujacy Pan: Tego dnia, któregom wybrał Izraela, podniosłem rękę moję nasieniu domu Jakóbowego, i dałem się im poznać w ziemi Egipskiej; podniosłem rękę moję dla nich, mówiąc: Jam Pan, Bóg wasz.
6 Pa tsiku limenelo ndinalumbira kwa iwo kuti ndidzawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kupita nawo ku dziko limene ndinawapezera, dziko la mwana alirenji, dziko lokongola kwambiri kupambana mayiko ena.
Onego dnia podniosłem rękę moję dla nich, że ich wywiodę z ziemi Egipskiej do ziemi, którąm im upatrzył, opływającej mlekiem i miodem, która jest ozdobą wszystkich ziem.
7 Ndipo ndinawawuza kuti, ‘Aliyense ataye zinthu zonse zonyansa zimene ankasangalala nazo, ndipo musadziyipitse ndi mafano a Igupto, Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
I rzekłem im: Każdy z was niech porzuci obrzydliwości oczów swoich, a nie kalajcie się plugawemi bałwanami egipskiemi; bom Ja Pan, Bóg wasz.
8 “‘Koma iwo anandiwukira ndipo sanafune kundimvera. Palibe amene anataya zonyansa zonse zimene ankasangalala nazo. Panalibenso amene anasiya mafano a ku Igupto. Tsono ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwaonetsa mkwiyo wanga mʼdziko la Igupto momwemo.
Ale mi byli odpornymi, i nie chcieli mię słuchać; żaden z nich obrzydliwości oczów swoich nie odrzucił, i plugawych bałwanów egipskich nie opóścił; prztożem rzekł: Wyleję gniew mój na nich, a wypęłnie popędliwość moję nad nimi w pośrodku ziemi egipskiej.
9 Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene ankakhala pakati pawo. Paja ndinali nditaonetsa mphamvu zanga pamaso pa mitunduyo potulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto.
A wszakżem uczynił dla imienia mego, aby nie było zelżone przed oczyma tych narodów, między którymi oni byli, przed których oczyma dałem się im poznać, że ich chcę wywieść z ziemi egipskiej.
10 Choncho ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kubwera nawo mʼchipululu.
A tak wywiodłem ich z ziemi egipskiej, i przyprowadziłem ich na puszczę;
11 Ndinawapatsa malangizo anga ndi kuwadziwitsa malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo.
I dałem im ustawy moje, i sądy moje podałem im do wiadomości; które jeźliby człowiek zachowywał, żyć w nich będzie.
12 Ndinawapatsanso Masabata ngati chizindikiro pakati pathu, kuti adziwe kuti Ine Yehova ndinawapatula.
Nadto i sabaty moje dałem im, aby były znakiem między mną i między nimi, aby wiedzieli, żem Ja jest Pan, który ich poświęcam.
13 “‘Komabe anthu a Israeli anandiwukira mʼchipululu. Iwo sanatsatire malangizo anga koma anakana malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo. Ndipo anayipitsa kotheratu Masabata anga. Choncho, ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawononga mʼchipululu.
Ale mi się odpornym stał dom Izraelski na puszczy; w ustawach moich nie chodzili, i sądy moje odrzucili, które jeźliby człowiek czynił, żyć w nich będzie. Sabaty też moje bardzo zgwałcili; prztożem mówił, iż wleję popędliwość moję na nich na pus zczy, abym ich wygubił.
14 Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Igupto.
Leczem uczynił dla imienia mego, aby nie było zelżone przed oczyma tych narodów przed którychem ich oczyma wywiódł.
15 Ndinalumbiranso kwa iwo mʼchipululu muja, nditakweza dzanja, kuti sindidzawalowetsanso mʼdziko limene ndinawapatsa, dziko la mwana alirenji, lokoma kwambiri kuposa mayiko ena onse.
A wszakżem podniósł rękę moję dla nich na tej puszczy, że ich nie wprowadzę do ziemi, którąm im był dał, opływającej mlekiem i miodem, i która jest ozdobą wszystkich ziem;
16 Paja anakana malamulo anga, sanatsatire malangizo anga ndipo anayipitsa masabata anga. Mitima yawo inakonda mafano.
Ponieważ sądy moje odrzucili, a w ustawach moich nie chodzili, i sabaty moje pogwałcili, a że serce ich za plugawemi bałwanami chodzi.
17 Komabe ndinawamvera chisoni ndipo sindinawawononge kapena kuwatheratu mʼchipululu.
Ale im przecie przepuściło oko moje, tak, żem ich nie wytracił, i nie wygładził do szczętu na puszczy.
18 Tsono kwa ana awo mʼchipululu ndinati, ‘Musatsatire malangizo a makolo anu kapena kusunga malamulo awo kapena kudziyipitsa ndi mafano awo.
I mówiłem do synów ich na tej puszczy: W ustawach ojców waszych nie chodźcie, i sądów ich nie przestrzegajcie, ani się plugawemi bałwanami ich kalajcie.
19 Ine ndine Yehova Mulungu wanu; tsatirani malangizo anga ndipo sungani malamulo anga.
Jam Pan, Bóg wasz; w ustawach moich chodźcie, a sądów moich strzeżcie, i czyńcie ich;
20 Masabata anga muziwasunga ngati opatulika kuti akhale chizindikiro pakati pa Ine ndi inu. Mukatero mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
Sabaty też moje święćcie, i będą znakiem między mną i między wami, abyście wiedzieli żem Ja Pan, Bóg wasz.
21 “‘Koma ana awo anandiwukira. Iwo sanatsatire malangizo anga, sanamvere malamulo anga, ngakhale kuti amapereka moyo kwa munthu amene amawamvera. Ndiponso anayipitsa Masabata anga. Choncho ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawonongeratu mʼchipululu momwemo.
Lecz mi byli odpornymi ci synowie; w ustawach moich nie chodzili, i sądów moich nie przestrzegali, aby je czynili, (które jeźliby czynił człowiek pewnieby żył w nich) i sabaty moje pogwałcili. I rzekłem: Wyleję popędliwość moję na nich, abym wyko nał gniew swój na nich na tej puszczy.
22 Koma sindinatero chifukwa cha dzina langa kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Iguptomo.
Alem odwrócił rękę moję, a uczyniłem to dla imienia mego, aby nie było zelżone przed oczyma tych narodów, przed którychem ich oczyma wywiódł.
23 Choncho ndinalumbira mʼchipululu, nditakweza dzanja langa, kuti ndidzawabalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwamwazira ku mayiko akutali,
Alem ja podniósł rękę moję dla nich na puszczy, żem ich miał rozproszyć między pogan, i rozwiać ich po ziemiach,
24 chifukwa sanamvere malamulo anga, anakana malangizo anga, nayipitsa masabata anga, ndi kupembedza mafano a makolo awo.
Przeto, że sądów moich nie czynili, i ustawy moje odrzucili, i sabaty moje pogwałcili, a za plugawemi bałwanami ojców swoich oczy swe obrócili.
25 Ine ndinawapatsanso malangizo amene sanali abwino ndi malamulo amene sakanatha kupeza nawo moyo.
Dlategoż i Jam im dał ustawy nie dobre i sądy, w których żyć nie będą;
26 Ndinawalekerera kuti adziyipitse ndi mphatso zawo zomwe, makamaka popereka ana awo oyamba kubadwa ngati nsembe zopsereza. Ndinatero kuti ndiwadetse nkhawa ndi kuti adziwe kuti Ine ndine Yehova.’
I splugawiłem ich z darami ich, gdy przewodzili przez ogień wszelkie otwarzające żywot, abym ich spustoszył, a żeby się dowiedzieli żem ja Pan.
27 “Tsono iwe mwana wa munthu, yankhula nawo Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti makolo anu anandinyozanso posaonetsa moyo wokhulupirika.
Prztoż mów do domu Izraelskigo, synu człowieczy! a powiedz im: Tak mówi panujący Pan: Jeszcze i w tem lżyli mię ojcowie wasi, dopuszczając się przeciwko mnie przestępstwa,
28 Nditawalowetsa mʼdziko limene ndinachita kulumbirira kuti ndidzawapatsa, iwo tsono ankapita kulikonse kumene anaona chitunda chachitali ndi mtengo wa masamba ambiri kukapereka kumeneko nsembe ndi zopereka zawo zimene zinkandikwiyitsa. Kumeneko ankapereka nsembe za fungo lokoma ndiponso nsembe za zakumwa.
Że gdym ich wwiódł do ziemi, o którąm był podniósł rękę moję, żem ją im dać miał, gdzie ujrzeli jaki pagórek wysoki, albo jakie drzewo gałęziste, zaraz tam ofiarowali ofiary swoje, i dawali tam draźniące dary swoje, tamże kładli i wdzięczną wonno ść swoję, tamże sprawowali mokre ofiary swoje.
29 Tsono ndinawafunsa kuti: Kodi chitunda chimene mukupitako nʼchotani? Chitundachi chakhala chikutchedwa mpaka lero kuti ‘Chitunda cha Chipembedzo.’
A chociażem mówił do nich: Cóż to za wyżyna, do której wy chadzacie? Przecie ją zowią wyżyną aż do dnia tego.
30 “Tsono uwawuze Aisraeli kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi mudzadziyipitsa nokha monga anachitira makolo anu ndi kuchita chigololo ndi milungu yawo yonyansa?
Przetoż rzecz domowi Izraelskiemu: Tak mówi panujący Pan: Izali się wy drogami ojców waszych kalać macie, a z obrzydliwościami ich nierząd płodzić?
31 Pamene mubwera kudzapereka mphatso zanu ndi kudzapereka ana kuti akhale ngati nsembe zopsereza mumadziyipitsa ndi mafano anu mpaka lero. Kodi Aisraeli, ndingathe kukulolani bwanji kuti mulandire malangizo kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, sindidzalola kuti mupemphe nzeru kwa Ine.
I macież się kalać przy wszystkich plugawych bałwanach waszych, przynosząc dary wasze i przewodząc synów waszych przez ogień aż do dnia tego, a przecie odemnie rady szukać, o domie Izraelski? Jako żyję Ja, mówi panujący Pan, że się wy mnie więcej radzić nie będziecie.
32 “‘Inu munanena kuti, ‘Tikufuna tikhale ngati anthu a mitundu ina, ngati anthu adziko lapansi, amene amapembedza mtengo ndi mwala.’ Koma zimene mukuganizazo sizidzachitika.
A to, co wstępuje na myśl waszę, nigdy się nie stanie. Wy mówicie: Będziemy jako inne narody, jako pokolenia innych ziem, drewnu i kamieniowi służące;
33 Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ndi dzanja langa lamphamvu, nditasamula mkono wanga mokwiya kwambiri, Ine ndidzakhala wokulamulani.
Jako żyję Ja, mówi panujący Pan, że ręką możną i ramieniem wyciągnionem, a w popędliwości wylanej będę królował nad wami;
34 Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndikukusonkhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munamwazikirako, ndi dzanja langa lamphamvu ndi lotambasuka ndili wokwiya kwambiri.
I wywiodę was z narodów, a zgromadzę was z ziem, do którycheście rozproszeni, ręką możną, i ramieniem wyciągnionem, i w popędliwości wylanej;
35 Ndidzakulowetsani mʼchipululu cha anthu a mitundu ina ndipo kumeneko, moonana maso ndi maso, ndidzakuzengani mlandu.
A prowadząc was po puszczy tych narodów, tam się z wami twarzą w twarz sądzić będę.
36 Monga ndinawalangira makolo anu mʼchipululu cha dziko la Igupto, motero ndidzakulangani, akutero Ambuye Yehova.
Jakom się sądził z ojcami waszymi na puszczy ziemi Egipskiej, tak się z wami sądzić będę, mówi panujący Pan;
37 Ndidzakuwerengani ndi ndodo ya mʼbusa, kukulowetsani mʼchimango cha pangano langa.
I popędzę was pod rózgą, abym was przywiódł do związku przymierza.
38 Ndidzakuchotserani anthu amene anandigalukira ndi kundiwukira. Ngakhale ndidzawatulutsa mʼdziko limene akukhalamo, koma sadzalowamo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Ale z was wybiorę odpornych i występujących przeciwko mnie; z ziemi pielgrzymstwa ich wywiodę ich, wszakże do ziemi Izraelskiej nie wnijdą; i poznacie, żem Ja Pan.
39 “‘Koma inu Aisraeli, zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Pitani katumikireni mafano anu onse, aliyense wa inu! Koma mʼtsogolo mwake mudzandimvera ndithu ndipo simudzayipitsa dzina langa lopatulika popereka mphatso zanu kwa mafano.
Wy tedy, o domie Izraelski! tak mówi panujący Pan: Idźcież, służcie każdy plugawym bałwanom swoim i na potem, ponieważ mnie nie słuchacie; a imienia mego świętego nie kalajcie więcej darami waszemi, i plugawemi bałwanami waszemi.
40 Pakuti pa phiri langa lopatulika, phiri lalitali la ku Israeli, akutero Ambuye Yehova, Aisraeli onse adzanditumikira, ndipo kumeneko Ine ndidzawalandira. Kumeneko ndidzayembekeza zopereka zanu ndi mphatso zanu zopambana, pamodzi ndi nsembe zanu zonse zopatulika.
Bo na świętej górze mojej, na wysokiej górze Izraeskiej, mówi panujący Pan, tam mi służyć będzie wszystek dom Izraeski, ile ich będzie w onej ziemi; tam ich łaskawie przyjmę, i tam się pytać będę o ofiarach waszych podnoszonych, i o pierwiastkach darów waszych ze wszystkiemi świętemi rzeczami waszemi.
41 Ndidzakulandirani ngati nsembe ya fungo lokoma ndikadzakutulutsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukusokhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munabalalitsidwirako. Motero ndidzadzionetsa pakati panu kuti ndine woyera ndipo mitundu ya anthu idzaona.
Z wdzięczną wonnością łaskawie was przyjmę, gdy was wywiodę z narodów, a zgromadzę was z onych ziem, do którycheście rozproszeni byli, a tak poświęcony będę w was przed oczyma onych narodów.
42 Tsono mudzadziwa kuti ndine Yehova ndikadzabwera nanu ku dziko la Israeli, dziko limene ndinalumbira kuti ndidzapereka kwa makolo anu.
A poznacie, żem Ja Pan, gdy was wprowadzę do ziemi Izraelskiej, do ziemi onej, o którąm podniósł rękę moję, że ją dam ojcom waszym;
43 Kumeneko mudzakumbukira makhalidwe anu ndi machitidwe anu onse amene munadziyipitsa nawo, ndipo mudzanyansidwa nokha chifukwa cha zoyipa zimene munachita.
A wspomnicie tam na drogi wasze, i na wszystkie sprawy wasze, któremiście się splugawili, a obmierzniecie sami sobie przed obliczem waszem dla wszystkich złości waszych, któreście czynili.
44 Inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzakuchitirani zabwino chifukwa cha dzina langa koma osati molingana ndi njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu okhota, inu Aisraeli, akutero Ambuye Yehova.’”
Tam się dowiecie, żem Ja Pan, gdy wam to uczynię dla imienia mego, nie według dróg waszych złych, ani według spraw waszych skażonych, o domie Izraelski! mówi panujący Pan.
45 Yehova anandiyankhula nati:
I stało się słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
46 “Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane kummwera; ndipo lalika mawu odzudzula anthu akummwera ndipo unenere zodzudzula dziko la nkhalango ya kummwera.
Synu człowieczy! obróć twarz twoję ku stronie południowej, a krop jako rosą na południe, i prorokuj przeciwko losowi pola południowego,
47 Iwuze nkhalango yakummwera kuti, ‘Imvani mawu a Yehova! Ambuye Yehova akuti: Ndikuyatsa moto ndipo motowo udzapsereza mitengo yako yonse yayiwisi ndi yowuma yomwe. Malawi ake sadzazimitsika ndipo aliyense kuchokera kummwera mpaka kumpoto adzapsa nawo.
A rzecz lasowi południowemu: Słuchaj słowa Pańskiego: Tak mówi panujący Pan: Oto Ja rozniecę w tobie ogień, który pożre w tobie wszelkie drzewo zielone, i wszelkie drzewo suche; nie będzie ugaszony płomień pałający, i zgoreją w nim wszystkie twar ze od południa aż do północy.
48 Aliyense adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndayatsa motowo, ndipo sudzazimitsidwa.’”
I ujrzy wszelkie ciało, żem go Ja Pan zapalił; nie będzie ugaszony.
49 Ndipo ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova! Anthu akungondinena kuti, ‘Kodi suja amangonena nthano chabe ameneyu!’”
I rzekłem: Ach panujący Panie! Oni mówią o mnie: Ten tylko w przypowieściach mówi.

< Ezekieli 20 >