< Ezekieli 20 >

1 Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu, chaka chachisanu ndi chiwiri, ena mwa akuluakulu a Israeli anabwera kudzapempha nzeru kwa Yehova, ndipo anakhala pansi pamaso panga.
Kwasekusithi ngomnyaka wesikhombisa, ngenyanga yesihlanu, ngolwetshumi lwenyanga, abathile babadala bakoIsrayeli beza ukuzabuza iNkosi, bahlala phambi kwami.
2 Tsono Yehova anandiyankhula nati:
Ilizwi leNkosi laselifika kimi lisithi:
3 “Iwe mwana wa munthu, ayankhule akuluakulu a Israeli ndi kuwawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Kodi mwabwera kudzapempha nzeru kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, Ine sindidzakulolani kupempha nzeru kwa Ine, akutero Ambuye Yehova.’
Ndodana yomuntu, khuluma kubadala bakoIsrayeli, uthi kubo: Itsho njalo iNkosi uJehova: Lize ukuzangibuza yini? Kuphila kwami, isibili kangiyikubuzwa yini, itsho iNkosi uJehova.
4 “Kodi uwaweruza? Iwe mwana wa munthu, kodi ugamula mlandu wawo? Uwadziwitse tsono zonyansa zimene anachita makolo awo, uwawuze kuti,
Uzabahlulela yini, uzabahlulela yini, ndodana yomuntu? Bazise izinengiso zaboyise;
5 ‘Ambuye Yehova akuti: Pa tsiku limene ndinasankha Israeli, ndinalumbira kwa zidzukulu za nyumba ya Yakobo ndipo ndinadziwulula kwa iwo ku Igupto. Ndinalumbira ndi kuwawuza kuti: Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
uthi kubo: Itsho njalo iNkosi uJehova: Ngosuku engakhetha ngalo uIsrayeli, ngaphakamisa isandla sami kunzalo yendlu kaJakobe, ngazazisa kubo elizweni leGibhithe, lapho ngiphakamisa isandla sami kibo, ngisithi: NgiyiNkosi uNkulunkulu wenu.
6 Pa tsiku limenelo ndinalumbira kwa iwo kuti ndidzawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kupita nawo ku dziko limene ndinawapezera, dziko la mwana alirenji, dziko lokongola kwambiri kupambana mayiko ena.
Ngalolusuku ngaphakamisa isandla sami kubo, ukuthi ngibakhuphe elizweni leGibhithe ngibase elizweni engangibahlolele lona, eligeleza uchago loluju, eliludumo lwawo wonke amazwe.
7 Ndipo ndinawawuza kuti, ‘Aliyense ataye zinthu zonse zonyansa zimene ankasangalala nazo, ndipo musadziyipitse ndi mafano a Igupto, Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
Ngasengisithi kubo: Lahlani ngulowo lalowo izinengiso zamehlo akhe, lingazingcolisi ngezithombe zeGibhithe: NgiyiNkosi uNkulunkulu wenu.
8 “‘Koma iwo anandiwukira ndipo sanafune kundimvera. Palibe amene anataya zonyansa zonse zimene ankasangalala nazo. Panalibenso amene anasiya mafano a ku Igupto. Tsono ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwaonetsa mkwiyo wanga mʼdziko la Igupto momwemo.
Kodwa bangivukela, bengavumi ukulalela kimi, kabalahlanga ngulowo lalowo izinengiso zamehlo abo, kabatshiyanga izithombe zeGibhithe. Ngasengisithi ngizathululela ukuthukuthela kwami phezu kwabo, ukuze ngiphelelise ulaka lwami ngimelene labo phakathi kwelizwe leGibhithe.
9 Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene ankakhala pakati pawo. Paja ndinali nditaonetsa mphamvu zanga pamaso pa mitunduyo potulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto.
Kodwa ngakwenza ngenxa yebizo lami, ukuze lingangcoliswa emehlweni ezizwe, ababephakathi kwazo, engazazisa kubo phambi kwamehlo azo, ukubakhupha elizweni leGibhithe.
10 Choncho ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kubwera nawo mʼchipululu.
Ngakho ngabakhupha elizweni leGibhithe, ngabangenisa enkangala.
11 Ndinawapatsa malangizo anga ndi kuwadziwitsa malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo.
Ngabanika izimiso zami, ngabazisa izahlulelo zami, okuthi nxa umuntu ezenza, uzaphila ngazo.
12 Ndinawapatsanso Masabata ngati chizindikiro pakati pathu, kuti adziwe kuti Ine Yehova ndinawapatula.
Ngabanika futhi amasabatha ami ukuze abe yisibonakaliso phakathi kwami labo, ukuze bazi ukuthi ngiyiNkosi ebangcwelisayo.
13 “‘Komabe anthu a Israeli anandiwukira mʼchipululu. Iwo sanatsatire malangizo anga koma anakana malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo. Ndipo anayipitsa kotheratu Masabata anga. Choncho, ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawononga mʼchipululu.
Kodwa indlu kaIsrayeli yangivukela enkangala; kabahambanga ngezimiso zami, badelela izahlulelo zami, okuthi nxa umuntu ezenza, uzaphila ngazo; lamasabatha ami bawangcolisa kakhulu. Ngasengisithi ngizathululela ukuthukuthela kwami phezu kwabo enkangala, ukuze ngibaqede.
14 Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Igupto.
Kodwa ngakwenza ngenxa yebizo lami, ukuze lingangcoliswa emehlweni ezizwe, engabakhupha emehlweni azo.
15 Ndinalumbiranso kwa iwo mʼchipululu muja, nditakweza dzanja, kuti sindidzawalowetsanso mʼdziko limene ndinawapatsa, dziko la mwana alirenji, lokoma kwambiri kuposa mayiko ena onse.
Futhi lami ngabaphakamisela isandla sami enkangala, ukuthi kangiyikubaletha elizweni engangilinike bona, eligeleza uchago loluju, eliludumo lwawo wonke amazwe;
16 Paja anakana malamulo anga, sanatsatire malangizo anga ndipo anayipitsa masabata anga. Mitima yawo inakonda mafano.
ngoba badelela izahlulelo zami, kabahambanga ngezimiso zami, kodwa bangcolisa amasabatha ami, ngoba inhliziyo yabo yalandela izithombe zabo.
17 Komabe ndinawamvera chisoni ndipo sindinawawononge kapena kuwatheratu mʼchipululu.
Lanxa kunjalo ilihlo lami labahawukela ukuze ngingababhubhisi, futhi kangibaqedanga enkangala.
18 Tsono kwa ana awo mʼchipululu ndinati, ‘Musatsatire malangizo a makolo anu kapena kusunga malamulo awo kapena kudziyipitsa ndi mafano awo.
Kodwa ngathi kubantwana babo enkangala: Lingahambi ngezimiso zaboyihlo, lingagcini izahlulelo zabo, lingazingcolisi ngezithombe zabo.
19 Ine ndine Yehova Mulungu wanu; tsatirani malangizo anga ndipo sungani malamulo anga.
NgiyiNkosi uNkulunkulu wenu; hambani ngezimiso zami, ligcine izahlulelo zami, lizenze.
20 Masabata anga muziwasunga ngati opatulika kuti akhale chizindikiro pakati pa Ine ndi inu. Mukatero mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
Lingcwelise amasabatha ami, abe yisibonakaliso phakathi kwami lani, ukuze lazi ukuthi ngiyiNkosi uNkulunkulu wenu.
21 “‘Koma ana awo anandiwukira. Iwo sanatsatire malangizo anga, sanamvere malamulo anga, ngakhale kuti amapereka moyo kwa munthu amene amawamvera. Ndiponso anayipitsa Masabata anga. Choncho ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawonongeratu mʼchipululu momwemo.
Kodwa abantwana bangivukela; kabahambanga ngezimiso zami, kabagcinanga izahlulelo zami ukuthi bazenze; okuthi nxa umuntu ezenza, uzaphila ngazo; bawangcolisa amasabatha ami; ngasengisithi ngizathululela intukuthelo yami phezu kwabo, ukuthi ngiphelelise ulaka lwami ngimelene labo enkangala.
22 Koma sindinatero chifukwa cha dzina langa kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Iguptomo.
Kodwa ngabuyisa isandla sami, ngenza ngenxa yebizo lami, ukuze lingangcoliswa phambi kwamehlo ezizwe, engangibakhuphe phambi kwamehlo azo.
23 Choncho ndinalumbira mʼchipululu, nditakweza dzanja langa, kuti ndidzawabalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwamwazira ku mayiko akutali,
Mina ngabaphakamisela isandla sami futhi enkangala, ukuthi ngizabahlakaza phakathi kwezizwe, ngibasabalalisele emazweni;
24 chifukwa sanamvere malamulo anga, anakana malangizo anga, nayipitsa masabata anga, ndi kupembedza mafano a makolo awo.
ngoba bengazenzanga izahlulelo zami, kodwa badelela izimiso zami, bangcolisa amasabatha ami, lamehlo abo alandela izithombe zaboyise.
25 Ine ndinawapatsanso malangizo amene sanali abwino ndi malamulo amene sakanatha kupeza nawo moyo.
Ngakho mina ngabanika futhi izimiso ezazingalunganga, lezahlulelo ababengeke baphile ngazo.
26 Ndinawalekerera kuti adziyipitse ndi mphatso zawo zomwe, makamaka popereka ana awo oyamba kubadwa ngati nsembe zopsereza. Ndinatero kuti ndiwadetse nkhawa ndi kuti adziwe kuti Ine ndine Yehova.’
Ngasengibangcolisa kuzo izipho zabo, ekudabuliseni kwaboemlilweni konke okuvula isizalo, ukuze ngibachithe, ukuze bazi ukuthi ngiyiNkosi.
27 “Tsono iwe mwana wa munthu, yankhula nawo Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti makolo anu anandinyozanso posaonetsa moyo wokhulupirika.
Ngakho, ndodana yomuntu, khuluma kuyo indlu yakoIsrayeli, uthi kubo: Itsho njalo iNkosi uJehova: Lakulokhu oyihlo bangihlambazile, ngokuthi baphambeke isiphambeko bemelene lami.
28 Nditawalowetsa mʼdziko limene ndinachita kulumbirira kuti ndidzawapatsa, iwo tsono ankapita kulikonse kumene anaona chitunda chachitali ndi mtengo wa masamba ambiri kukapereka kumeneko nsembe ndi zopereka zawo zimene zinkandikwiyitsa. Kumeneko ankapereka nsembe za fungo lokoma ndiponso nsembe za zakumwa.
Lapho sengibalethe elizweni, engaphakamisela isandla sami ngalo ukuthi ngibanike lona, babona lonke uqaqa oluphakemeyo, lazo zonke izihlahla eziqatha, bahlaba khona imihlatshelo yabo, banikela khona isicunulo somnikelo wabo, bafaka khona iphunga labo elimnandi, bathulula khona iminikelo yabo yokunathwayo.
29 Tsono ndinawafunsa kuti: Kodi chitunda chimene mukupitako nʼchotani? Chitundachi chakhala chikutchedwa mpaka lero kuti ‘Chitunda cha Chipembedzo.’
Ngasengisithi kubo: Iyini indawo ephakemeyo eliya kuyo? Lebizo layo lithiwa yiNdawo ePhakemeyo kuze kube lamuhla.
30 “Tsono uwawuze Aisraeli kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi mudzadziyipitsa nokha monga anachitira makolo anu ndi kuchita chigololo ndi milungu yawo yonyansa?
Ngakho tshono kuyo indlu kaIsrayeli: Itsho njalo iNkosi uJehova: Lizazingcolisa ngendlela yaboyihlo yini, liphinge lilandela izinengiso zabo?
31 Pamene mubwera kudzapereka mphatso zanu ndi kudzapereka ana kuti akhale ngati nsembe zopsereza mumadziyipitsa ndi mafano anu mpaka lero. Kodi Aisraeli, ndingathe kukulolani bwanji kuti mulandire malangizo kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, sindidzalola kuti mupemphe nzeru kwa Ine.
Ngoba lapho linikela izipho zenu, lapho lisenza amadodana enu adabule emlilweni, liyazingcolisa ngezithombe zenu zonke kuze kube lamuhla. Mina-ke ngizabuzwa yini na, wena ndlu kaIsrayeli? Kuphila kwami, itsho iNkosi uJehova, isibili kangiyikubuzwa yini.
32 “‘Inu munanena kuti, ‘Tikufuna tikhale ngati anthu a mitundu ina, ngati anthu adziko lapansi, amene amapembedza mtengo ndi mwala.’ Koma zimene mukuganizazo sizidzachitika.
Lalokho okuvela engqondweni yenu kakuyikuba khona ngitsho, elikutshoyo ukuthi: Sizakuba njengabezizwe, njengensapho zamazwe, ukuthi sikhonze isigodo lelitshe.
33 Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ndi dzanja langa lamphamvu, nditasamula mkono wanga mokwiya kwambiri, Ine ndidzakhala wokulamulani.
Kuphila kwami, itsho iNkosi uJehova, isibili ngizabusa phezu kwenu ngesandla esilamandla langengalo eyeluliweyo langolaka oluthululiweyo!
34 Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndikukusonkhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munamwazikirako, ndi dzanja langa lamphamvu ndi lotambasuka ndili wokwiya kwambiri.
Ngoba ngizalikhupha ebantwini, ngiliqoqe emazweni elihlakazekele kuwo, ngesandla esilamandla langengalo eyeluliweyo langolaka oluthululiweyo.
35 Ndidzakulowetsani mʼchipululu cha anthu a mitundu ina ndipo kumeneko, moonana maso ndi maso, ndidzakuzengani mlandu.
Njalo ngizaliletha enkangala yabantu, ngizaphikisana lani lapho ubuso ngobuso.
36 Monga ndinawalangira makolo anu mʼchipululu cha dziko la Igupto, motero ndidzakulangani, akutero Ambuye Yehova.
Njengalokhu ngaphikisana laboyihlo enkangala yelizwe leGibhithe, ngokunjalo ngizaphikisana lani, itsho iNkosi uJehova.
37 Ndidzakuwerengani ndi ndodo ya mʼbusa, kukulowetsani mʼchimango cha pangano langa.
Njalo ngizalidlulisa ngaphansi kwentonga, ngilingenise kusibopho sesivumelwano.
38 Ndidzakuchotserani anthu amene anandigalukira ndi kundiwukira. Ngakhale ndidzawatulutsa mʼdziko limene akukhalamo, koma sadzalowamo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Ngihlanze ngikhuphe phakathi kwenu abavukeli lalabo abaphambeka bemelene lami, ngibakhuphe elizweni lokuhlala kwabo njengabezizwe, kodwa kabayikungena emhlabathini wakoIsrayeli. Khona lizakwazi ukuthi ngiyiNkosi.
39 “‘Koma inu Aisraeli, zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Pitani katumikireni mafano anu onse, aliyense wa inu! Koma mʼtsogolo mwake mudzandimvera ndithu ndipo simudzayipitsa dzina langa lopatulika popereka mphatso zanu kwa mafano.
Lina-ke, ndlu kaIsrayeli, itsho njalo iNkosi uJehova, hambani likhonze, ngulowo lalowo izithombe zakhe, langemva kwalokho, uba lingangilaleli; kodwa lingangcolisi futhi ibizo lami elingcwele ngezipho zenu langezithombe zenu.
40 Pakuti pa phiri langa lopatulika, phiri lalitali la ku Israeli, akutero Ambuye Yehova, Aisraeli onse adzanditumikira, ndipo kumeneko Ine ndidzawalandira. Kumeneko ndidzayembekeza zopereka zanu ndi mphatso zanu zopambana, pamodzi ndi nsembe zanu zonse zopatulika.
Ngoba entabeni yami engcwele, entabeni yengqonga yakoIsrayeli, itsho iNkosi uJehova, lapho izangikhonza indlu yonke yakoIsrayeli, bonke elizweni; khona ngizabemukela, lakhona ngibize iminikelo yenu, lezithelo zokuqala zeminikelo yenu, lazo zonke izinto zenu ezingcwele.
41 Ndidzakulandirani ngati nsembe ya fungo lokoma ndikadzakutulutsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukusokhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munabalalitsidwirako. Motero ndidzadzionetsa pakati panu kuti ndine woyera ndipo mitundu ya anthu idzaona.
Ngizalemukela ngephunga elimnandi nxa ngilikhupha ebantwini, ngiliqoqe emazweni ebelihlakazelwe kuwo; njalo ngizangcweliswa phakathi kwenu phambi kwamehlo ezizwe.
42 Tsono mudzadziwa kuti ndine Yehova ndikadzabwera nanu ku dziko la Israeli, dziko limene ndinalumbira kuti ndidzapereka kwa makolo anu.
Lizakwazi-ke ukuthi ngiyiNkosi, lapho sengilingenise emhlabathini wakoIsrayeli, elizweni engaliphakamisela isandla sami ukulinika oyihlo.
43 Kumeneko mudzakumbukira makhalidwe anu ndi machitidwe anu onse amene munadziyipitsa nawo, ndipo mudzanyansidwa nokha chifukwa cha zoyipa zimene munachita.
Lapho-ke lizakhumbula izindlela zenu lezenzo zenu zonke, elazingcolisa ngazo; njalo lizazenyanya phambi kobuso benu ngenxa yazo zonke izinto ezimbi elizenzileyo.
44 Inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzakuchitirani zabwino chifukwa cha dzina langa koma osati molingana ndi njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu okhota, inu Aisraeli, akutero Ambuye Yehova.’”
Beselisazi ukuthi ngiyiNkosi, nxa ngenze kini ngenxa yebizo lami, hatshi njengokwezindlela zenu ezimbi, kumbe njengokwezenzo zenu zenkohlakalo, lina ndlu kaIsrayeli, itsho iNkosi uJehova.
45 Yehova anandiyankhula nati:
Ilizwi leNkosi lafika kimi futhi lisithi:
46 “Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane kummwera; ndipo lalika mawu odzudzula anthu akummwera ndipo unenere zodzudzula dziko la nkhalango ya kummwera.
Ndodana yomuntu, misa ubuso bakho ngasendleleni yeningizimu, utshumayele ngaseningizimu, uprofethe umelene legusu lensimu yeningizimu;
47 Iwuze nkhalango yakummwera kuti, ‘Imvani mawu a Yehova! Ambuye Yehova akuti: Ndikuyatsa moto ndipo motowo udzapsereza mitengo yako yonse yayiwisi ndi yowuma yomwe. Malawi ake sadzazimitsika ndipo aliyense kuchokera kummwera mpaka kumpoto adzapsa nawo.
uthi kilo igusu leningizimu: Zwana ilizwi leNkosi: Itsho njalo iNkosi uJehova: Khangela, ngizaphemba umlilo phakathi kwakho, njalo uzaqeda phakathi kwakho sonke isihlahla esiluhlaza laso sonke isihlahla esomileyo; ilangabi elivuthayo kaliyikucitshwa, kodwa kuzatshiswa ngalo bonke ubuso kusukela eningizimu kuze kufike enyakatho.
48 Aliyense adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndayatsa motowo, ndipo sudzazimitsidwa.’”
Futhi yonke inyama izabona ukuthi mina Nkosi ngiwuphembile, kawuyikucitshwa.
49 Ndipo ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova! Anthu akungondinena kuti, ‘Kodi suja amangonena nthano chabe ameneyu!’”
Ngasengisithi: Hawu, Nkosi Jehova! Bathi ngami: Kakhulumi imifanekiso yini?

< Ezekieli 20 >