< Ezekieli 20 >

1 Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu, chaka chachisanu ndi chiwiri, ena mwa akuluakulu a Israeli anabwera kudzapempha nzeru kwa Yehova, ndipo anakhala pansi pamaso panga.
Tamy andro faha-folo’ i volam-paha-lime’ i taom-paha-fitoy, le nivotra­k’ amako ty ila’ o androanavi’ Israeleo hañontane Iehovà, vaho niambesatse aoloko eo.
2 Tsono Yehova anandiyankhula nati:
Niheo amako amy zao ty tsara’ Iehovà nanao ty hoe:
3 “Iwe mwana wa munthu, ayankhule akuluakulu a Israeli ndi kuwawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Kodi mwabwera kudzapempha nzeru kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, Ine sindidzakulolani kupempha nzeru kwa Ine, akutero Ambuye Yehova.’
O ana’ ondatio, misaontsia amo androa­navi’ Israeleo ty hoe: Hoe ty nafè’ Iehovà Talè: Niheo mb’etoy hao nahareo hañontane ahy? Amy te Izaho veloñe, hoe t’Iehovà Talè, tsy hañontanea’ areo.
4 “Kodi uwaweruza? Iwe mwana wa munthu, kodi ugamula mlandu wawo? Uwadziwitse tsono zonyansa zimene anachita makolo awo, uwawuze kuti,
Te hizaka iareo hao irehe? Ho zakae’o hao, ry ana’ ondaty? Tohino ami’ty haloloan-droae’ iareo:
5 ‘Ambuye Yehova akuti: Pa tsiku limene ndinasankha Israeli, ndinalumbira kwa zidzukulu za nyumba ya Yakobo ndipo ndinadziwulula kwa iwo ku Igupto. Ndinalumbira ndi kuwawuza kuti: Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Le ano ty hoe: Inao ty nafè’ Iehovà Talè; Amy andro nijoboñeko Israeley, naho nañonjon-tsirañ’ ami’ty tirin’ anjomba’ Iakobe, naho nampahafohineko iareo iraho an-tane Mitsraime añe, ie nañonjonako sirañe, nanao ty hoe: Izaho Iehovà ro Andrianañahare’ areo;
6 Pa tsiku limenelo ndinalumbira kwa iwo kuti ndidzawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kupita nawo ku dziko limene ndinawapezera, dziko la mwana alirenji, dziko lokongola kwambiri kupambana mayiko ena.
amy andro nizonjoako sirañe am-panta t’ie hakareko an-tane Mitsraime ao pak’an-tane nihen­tseñeko ho a iareo, tane orikorihen-dronono naho tantele, ty loho fanjaka amy ze hene tane,
7 Ndipo ndinawawuza kuti, ‘Aliyense ataye zinthu zonse zonyansa zimene ankasangalala nazo, ndipo musadziyipitse ndi mafano a Igupto, Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
le hoe iraho am’ iereo, Fonga ahi­fiho añe ze hativañe mahasinda fihaino, vaho ko mileotse amo samposampo’ i Mitsraimeo; Izaho Iehovà Andrianañahare’ areo.
8 “‘Koma iwo anandiwukira ndipo sanafune kundimvera. Palibe amene anataya zonyansa zonse zimene ankasangalala nazo. Panalibenso amene anasiya mafano a ku Igupto. Tsono ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwaonetsa mkwiyo wanga mʼdziko la Igupto momwemo.
F’ie niola amako, toe nanjehatse, songa tsy nimete nañifike ty hativañe am-pihaino’e, naho tsy napo’ iareo o samposampo’ i Mitsraimeo; aa le hoe iraho, hakofòko am’ iereo ty fiforoforoako, vaho ho henefako ama’e ty habosehako añivo-tane Mitsraime ao.
9 Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene ankakhala pakati pawo. Paja ndinali nditaonetsa mphamvu zanga pamaso pa mitunduyo potulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto.
Ie amy zao, ty añarako ro nitoloñako, tsy ho tivaeñe añatrefa’ o kilakila’ ndaty añivo’ iareoo, ie aolo’ iareo eo ty nampahafohineko ahy, amy nampiakareñe iereo an-tane Mitsraimey.
10 Choncho ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kubwera nawo mʼchipululu.
Aa le nakareko an-tane Mitsraime ao vaho nenteko mb’am-patrambey añe;
11 Ndinawapatsa malangizo anga ndi kuwadziwitsa malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo.
le nitolorako o fañèkoo vaho nitaroñako o fepèkoo, o mahaveloñe ondaty mañavelo ama’eoo.
12 Ndinawapatsanso Masabata ngati chizindikiro pakati pathu, kuti adziwe kuti Ine Yehova ndinawapatula.
Nitolorako o Sabatekoo ka ho viloñe añivo’ iareo naho Izaho, haharendreha’ iareo te Izaho Iehovà ro Mpampiavake iareo.
13 “‘Komabe anthu a Israeli anandiwukira mʼchipululu. Iwo sanatsatire malangizo anga koma anakana malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo. Ndipo anayipitsa kotheratu Masabata anga. Choncho, ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawononga mʼchipululu.
Fe niola amako an-dratraratra añe ty anjomba’Israele; tsy nañavelo amo fañèkoo, naho nimavoe’ iereo o fepèkoo, o maha-veloñe ondatio t’ie ambenañe, vaho loho nitivà’ iareo o Sabatekoo; aa le hoe iraho: Hakofòko am’ iereo ty haviñerako am-patram-bey añe le ho mongo­reko.
14 Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Igupto.
F’ie nitoloñeko avao tsy ho tivàñe añatrefa’ o kilakila’ ndatio ty añarako, ie am-pahaoniña’ iareo ty nañakarako iareo.
15 Ndinalumbiranso kwa iwo mʼchipululu muja, nditakweza dzanja, kuti sindidzawalowetsanso mʼdziko limene ndinawapatsa, dziko la mwana alirenji, lokoma kwambiri kuposa mayiko ena onse.
Aa le mbe nazonjoko am’ iereo am-patrañe ao ty tañako naho nifanta te tsy hampiziliheko amy tane orikorihen-dronono naho tantele natoloko iareoy—ty enge’ ze hene tane;
16 Paja anakana malamulo anga, sanatsatire malangizo anga ndipo anayipitsa masabata anga. Mitima yawo inakonda mafano.
amy te nitsam­bolitio’ iareo o fepèkoo naho tsy nañavelo amo fañèkoo, te mone tiniva’ iareo o Sabatekoo; ie nañori­ke samposampon-draha ty arofo’ iareo.
17 Komabe ndinawamvera chisoni ndipo sindinawawononge kapena kuwatheratu mʼchipululu.
Ie amy hoe zay, niferenaiña’ o masokoo le tsy nizamaneko, vaho tsy nimongoreko am-patrambey añe;
18 Tsono kwa ana awo mʼchipululu ndinati, ‘Musatsatire malangizo a makolo anu kapena kusunga malamulo awo kapena kudziyipitsa ndi mafano awo.
fa hoe iraho amo ana’eo an-dratraratra añe: Ko añaveloa’ areo o fañèn-droae’ areoo le ko ambena’ areo o fepè’eo vaho ko mandeo-batañe amo samposampo’ iareoo.
19 Ine ndine Yehova Mulungu wanu; tsatirani malangizo anga ndipo sungani malamulo anga.
Izaho Iehovà Andrianañahare’ areo. Mañaveloa amo fañèkoo, ambeno o fepèkoo vaho ano;
20 Masabata anga muziwasunga ngati opatulika kuti akhale chizindikiro pakati pa Ine ndi inu. Mukatero mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
hamasiño o Sabotse­koo; ie viloñe añivoko naho nahareo, hahafohina’ areo te Izaho Iehovà Andrianañahare’ areo.
21 “‘Koma ana awo anandiwukira. Iwo sanatsatire malangizo anga, sanamvere malamulo anga, ngakhale kuti amapereka moyo kwa munthu amene amawamvera. Ndiponso anayipitsa Masabata anga. Choncho ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawonongeratu mʼchipululu momwemo.
Ndra te izay, niola amako o ana’eo: tsy nañavelo amo fañèkoo, tsy nañambeñe o fepèkoo hanoeñe, o mahaveloñe ondaty t’ie anoeñe, vaho nileora’ iareo o Sabotsekoo; le hoe iraho: ho nadoako am’ iereo am-patrambey ao ty fiforoforoako hampanintsiñe ty habosehako.
22 Koma sindinatero chifukwa cha dzina langa kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Iguptomo.
Fe sinintoko ty tañako naho nañalañalañe ty amy añarakoy tsy mone ho tivàñe añatrefa’ o kilakila’ ndatio, ie am-pahaoniña’e eo ty nañakarako iareo,
23 Choncho ndinalumbira mʼchipululu, nditakweza dzanja langa, kuti ndidzawabalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwamwazira ku mayiko akutali,
Toe nizonjoñako sira ka am-patrambey añe nifanta t’ie haparatsiako amo kilakila’ ndatio vaho haboeleko añivo’ o fifeheañeo;
24 chifukwa sanamvere malamulo anga, anakana malangizo anga, nayipitsa masabata anga, ndi kupembedza mafano a makolo awo.
amy te tsy nanoe’ iereo o fepèkoo, naho tsinambolitio’ iereo o fañèkoo, naho tiniva’ iareo o Sabatekoo, vaho norihem-pihaino’ iareo o samposampon-droae’eo.
25 Ine ndinawapatsanso malangizo amene sanali abwino ndi malamulo amene sakanatha kupeza nawo moyo.
Ie amy zay, tinoloko fañè tsy ho lefe, naho fepè tsy mahaveloñe,
26 Ndinawalekerera kuti adziyipitse ndi mphatso zawo zomwe, makamaka popereka ana awo oyamba kubadwa ngati nsembe zopsereza. Ndinatero kuti ndiwadetse nkhawa ndi kuti adziwe kuti Ine ndine Yehova.’
le nileorako amo banabana’ iareoo, ie nampirangà’ iareo añ’afo ao ze manoka-koviñe, hampangoakoahako iareo, vaho hahafohiñe te Izaho Iehovà.
27 “Tsono iwe mwana wa munthu, yankhula nawo Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti makolo anu anandinyozanso posaonetsa moyo wokhulupirika.
Ie amy zay, ry ana’ondaty, misaontsia amy anjomba’ Israeley le ano ty hoe: Inao ty nafè’ Iehovà Talè: Inao ka ty niterateràn-droae’ areo ahy ie niola amako hoe zao,
28 Nditawalowetsa mʼdziko limene ndinachita kulumbirira kuti ndidzawapatsa, iwo tsono ankapita kulikonse kumene anaona chitunda chachitali ndi mtengo wa masamba ambiri kukapereka kumeneko nsembe ndi zopereka zawo zimene zinkandikwiyitsa. Kumeneko ankapereka nsembe za fungo lokoma ndiponso nsembe za zakumwa.
ie nasese­ko an-tane nañonjonako sirañe hanolorako iareo, naho niisa’ iareo ze hene haboañe naho hatae mandrevake naho nañenga soroñe ey, naho nibanabana enga hanigiha’ iareo ahy, nañemboke ty mandrifondrifoñe, vaho nañiliñ’ engan-drano.
29 Tsono ndinawafunsa kuti: Kodi chitunda chimene mukupitako nʼchotani? Chitundachi chakhala chikutchedwa mpaka lero kuti ‘Chitunda cha Chipembedzo.’
Aa le nanoeko ty hoe, Inoñe ze o haboañe omba’ areo zao? Vaho natao Bamà ty añara’ i aoy ampara henaneo.
30 “Tsono uwawuze Aisraeli kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi mudzadziyipitsa nokha monga anachitira makolo anu ndi kuchita chigololo ndi milungu yawo yonyansa?
Aa le ano ty hoe i Anjom­ba’ Israeley, Inao ty nafè’ Iehovà Talè: Hera nileore’ ty satan-droae’ areo? Ke manao hakarapiloañe manahake ty hativa’ iareo?
31 Pamene mubwera kudzapereka mphatso zanu ndi kudzapereka ana kuti akhale ngati nsembe zopsereza mumadziyipitsa ndi mafano anu mpaka lero. Kodi Aisraeli, ndingathe kukulolani bwanji kuti mulandire malangizo kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, sindidzalola kuti mupemphe nzeru kwa Ine.
Ie mañenga, naho ampirangà’ areo añ’afo o ana-dahi’ areoo, naho mandeo-batañe amo samposampo’ areoo pake henane; aa vaho hañontanea’ areo hao iraho ry anjomba’ Israele? Amy te Izaho veloñe, hoe t’Iehovà Talè, tsy hañontanea’ areo.
32 “‘Inu munanena kuti, ‘Tikufuna tikhale ngati anthu a mitundu ina, ngati anthu adziko lapansi, amene amapembedza mtengo ndi mwala.’ Koma zimene mukuganizazo sizidzachitika.
Le lia’e tsy hipaoke o fitsa­korea’ areoo ie atao’ areo ty hoe: Hitsikombe o kilakila’ndatio tika, o fifokoam-pifeheañe mitoroñe vato naho hataeo.
33 Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ndi dzanja langa lamphamvu, nditasamula mkono wanga mokwiya kwambiri, Ine ndidzakhala wokulamulani.
Kanao velon-dRaho hoe t’Iehovà Talè, toe an-taña maozatse naho an-tsira natora-kitsy naho am-pifombo nadoañe, le tsy mahay tsy ho feheko nahareo;
34 Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndikukusonkhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munamwazikirako, ndi dzanja langa lamphamvu ndi lotambasuka ndili wokwiya kwambiri.
le haka­reko am’ ondatio naho hatontoko boak’ amo fifeheañe nampipara­tsiahañe anahareo, an-taña maozatse naho an-tsira natora­kitsy vaho am-pifombo nadoañe.
35 Ndidzakulowetsani mʼchipululu cha anthu a mitundu ina ndipo kumeneko, moonana maso ndi maso, ndidzakuzengani mlandu.
Le haseseko mb’am-patrambei’ ondatio mb’eo, vaho ao ty hizakàko tarehe miatre-daharañe,
36 Monga ndinawalangira makolo anu mʼchipululu cha dziko la Igupto, motero ndidzakulangani, akutero Ambuye Yehova.
manahake ty nizakako o roae’ areo am-patram-bei’ i Mitsraimeo, izay ty hañodiako anahareo, hoe t’Iehovà Talè.
37 Ndidzakuwerengani ndi ndodo ya mʼbusa, kukulowetsani mʼchimango cha pangano langa.
Le hampiarieko ambane kobaiñe; naho hase­seko mb’ami’ty fifehea’ i fañinay ao;
38 Ndidzakuchotserani anthu amene anandigalukira ndi kundiwukira. Ngakhale ndidzawatulutsa mʼdziko limene akukhalamo, koma sadzalowamo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
naho ho tranaheko ama’ areo ao o mpiolao naho o nikitrok’ ahio; hakareko amy tane nitaveaña’ iareo fa tsy himoake an-tane’ Israele ao, vaho ho fohi’ areo te Izaho Iehovà.
39 “‘Koma inu Aisraeli, zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Pitani katumikireni mafano anu onse, aliyense wa inu! Koma mʼtsogolo mwake mudzandimvera ndithu ndipo simudzayipitsa dzina langa lopatulika popereka mphatso zanu kwa mafano.
Aa inahareo ry anjomba’ Israele, hoe ty nafè’ Iehovà Talè: Akia songa mitoroñe o sampo­sampo’eo, ndra t’ie nainai’e, naho tsy te hañaoñe ahy, fe ko tiva’ areo amo enga’ areo naho samposampo’ areoo ty añarako masiñe.
40 Pakuti pa phiri langa lopatulika, phiri lalitali la ku Israeli, akutero Ambuye Yehova, Aisraeli onse adzanditumikira, ndipo kumeneko Ine ndidzawalandira. Kumeneko ndidzayembekeza zopereka zanu ndi mphatso zanu zopambana, pamodzi ndi nsembe zanu zonse zopatulika.
Fa amy vohin-kamasiñako an-kaboa’ Israele eoy, hoe ty nafè’ Iehovà Talè, eo ty hitoroña’ ze hene anjomba’ Israele ahy amy taney, ie iaby amy taney ao; le ao ty hiantofako iereo, le ao ty hipaiako ty enga’ areo, ty loha-voa banabanae’ areo, miharo amo harao’ areo miavakeo.
41 Ndidzakulandirani ngati nsembe ya fungo lokoma ndikadzakutulutsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukusokhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munabalalitsidwirako. Motero ndidzadzionetsa pakati panu kuti ndine woyera ndipo mitundu ya anthu idzaona.
Ho noko ty amo raha marifondrifoñeo nahareo, ie fa nakareko am’ ondatio, naho fa natontoko amo fifeheañe nampiparatsiahañeo; vaho havahe’ areo iraho am-pihaino’ o kilakila’ ndatio.
42 Tsono mudzadziwa kuti ndine Yehova ndikadzabwera nanu ku dziko la Israeli, dziko limene ndinalumbira kuti ndidzapereka kwa makolo anu.
Le ho fohi’ areo te izaho Iehovà ie hase­se­ko mb’an-tane’ Israele mb’amy fifeheañe nañonjonako sirañe hanolo­rako aze aman-droae’ areo añey.
43 Kumeneko mudzakumbukira makhalidwe anu ndi machitidwe anu onse amene munadziyipitsa nawo, ndipo mudzanyansidwa nokha chifukwa cha zoyipa zimene munachita.
Eo ty hahatiahia’ areo o sata’ areoo naho o fitoloña’ areo iabio, o nandeotse anahareoo; toe hampangorý anahareo ty sandri’ areo ampahaisaha’ areo ty amo haloloañe nanoe’ areoo.
44 Inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzakuchitirani zabwino chifukwa cha dzina langa koma osati molingana ndi njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu okhota, inu Aisraeli, akutero Ambuye Yehova.’”
Le ho fohi’ areo te Izaho Iehovà, ty nañalañalañe ho anahareo ty amy añarakoy, fa tsy ty amo halò-tsere’ areoo naho tsy ty amo fitoloña’ areo maleotseo, ry anjomba’ Israele, hoe t’Iehovà Talè.
45 Yehova anandiyankhula nati:
Niheo amako ty tsara’ Iehovà nanao ty hoe:
46 “Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane kummwera; ndipo lalika mawu odzudzula anthu akummwera ndipo unenere zodzudzula dziko la nkhalango ya kummwera.
O ana’ ondatio, ampiatrefo miañatimo ty lahara’o le mitaroña mañatimo vaho mitokia amy alay naho amy tane atimoy;
47 Iwuze nkhalango yakummwera kuti, ‘Imvani mawu a Yehova! Ambuye Yehova akuti: Ndikuyatsa moto ndipo motowo udzapsereza mitengo yako yonse yayiwisi ndi yowuma yomwe. Malawi ake sadzazimitsika ndipo aliyense kuchokera kummwera mpaka kumpoto adzapsa nawo.
le ty hoe ty hataro’o amy ala atimoy, Janjiño ty tsara’ Iehovà. Inao ty nafè’ Iehovà Talè: Ingo te hamiañe afo ama’o iraho, hamorototo ze hatae antsetra ama’o ao naho ze hatae maike; tsy hakipeke i lel’afo mibelabelay le ho mae iaby ze tarehe atimo pak’ avaratse añe.
48 Aliyense adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndayatsa motowo, ndipo sudzazimitsidwa.’”
Le ho oni’ ze hene nofotse te Izaho Iehovà ro namiañe aze; ie le lia’e tsy ho vonoeñe.
49 Ndipo ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova! Anthu akungondinena kuti, ‘Kodi suja amangonena nthano chabe ameneyu!’”
Aa le hoe ty asako, Ry Iehovà Talè! Ty hoe ty asa’ iareo ty amako: Tsy mpandrazan-drehake hao re?

< Ezekieli 20 >