< Ezekieli 20 >

1 Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu, chaka chachisanu ndi chiwiri, ena mwa akuluakulu a Israeli anabwera kudzapempha nzeru kwa Yehova, ndipo anakhala pansi pamaso panga.
and to be in/on/with year [the] seventh in/on/with fifth in/on/with ten to/for month to come (in): come human from old: elder Israel to/for to seek [obj] LORD and to dwell to/for face: before my
2 Tsono Yehova anandiyankhula nati:
and to be word LORD to(wards) me to/for to say
3 “Iwe mwana wa munthu, ayankhule akuluakulu a Israeli ndi kuwawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Kodi mwabwera kudzapempha nzeru kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, Ine sindidzakulolani kupempha nzeru kwa Ine, akutero Ambuye Yehova.’
son: child man to speak: speak with old: elder Israel and to say to(wards) them thus to say Lord YHWH/God to/for to seek [obj] me you(m. p.) to come (in): come alive I if: surely no to seek to/for you utterance Lord YHWH/God
4 “Kodi uwaweruza? Iwe mwana wa munthu, kodi ugamula mlandu wawo? Uwadziwitse tsono zonyansa zimene anachita makolo awo, uwawuze kuti,
to judge [obj] them to judge son: child man [obj] abomination father their to know them
5 ‘Ambuye Yehova akuti: Pa tsiku limene ndinasankha Israeli, ndinalumbira kwa zidzukulu za nyumba ya Yakobo ndipo ndinadziwulula kwa iwo ku Igupto. Ndinalumbira ndi kuwawuza kuti: Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
and to say to(wards) them thus to say Lord YHWH/God in/on/with day to choose I in/on/with Israel and to lift: vow hand: vow my to/for seed: children house: household Jacob and to know to/for them in/on/with land: country/planet Egypt and to lift: vow hand: vow my to/for them to/for to say I LORD God your
6 Pa tsiku limenelo ndinalumbira kwa iwo kuti ndidzawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kupita nawo ku dziko limene ndinawapezera, dziko la mwana alirenji, dziko lokongola kwambiri kupambana mayiko ena.
in/on/with day [the] he/she/it to lift: vow hand: vow my to/for them to/for to come out: send them from land: country/planet Egypt to(wards) land: country/planet which to spy to/for them to flow: flowing milk and honey beauty he/she/it to/for all [the] land: country/planet
7 Ndipo ndinawawuza kuti, ‘Aliyense ataye zinthu zonse zonyansa zimene ankasangalala nazo, ndipo musadziyipitse ndi mafano a Igupto, Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
and to say to(wards) them man: anyone abomination eye his to throw and in/on/with idol Egypt not to defile I LORD God your
8 “‘Koma iwo anandiwukira ndipo sanafune kundimvera. Palibe amene anataya zonyansa zonse zimene ankasangalala nazo. Panalibenso amene anasiya mafano a ku Igupto. Tsono ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwaonetsa mkwiyo wanga mʼdziko la Igupto momwemo.
and to rebel in/on/with me and not be willing to/for to hear: hear to(wards) me man: anyone [obj] abomination eye their not to throw and [obj] idol Egypt not to leave: forsake and to say to/for to pour: pour rage my upon them to/for to end: expend face: anger my in/on/with them in/on/with midst land: country/planet Egypt
9 Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene ankakhala pakati pawo. Paja ndinali nditaonetsa mphamvu zanga pamaso pa mitunduyo potulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto.
and to make: do because name my to/for lest to profane/begin: profane to/for eye: seeing [the] nation which they(masc.) in/on/with midst their which to know to(wards) them to/for eye: seeing their to/for to come out: send them from land: country/planet Egypt
10 Choncho ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kubwera nawo mʼchipululu.
and to come out: send them from land: country/planet Egypt and to come (in): bring them to(wards) [the] wilderness
11 Ndinawapatsa malangizo anga ndi kuwadziwitsa malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo.
and to give: give to/for them [obj] statute my and [obj] justice: judgement my to know [obj] them which to make: do [obj] them [the] man and to live in/on/with them
12 Ndinawapatsanso Masabata ngati chizindikiro pakati pathu, kuti adziwe kuti Ine Yehova ndinawapatula.
and also [obj] Sabbath my to give: give to/for them to/for to be to/for sign: indicator between me and between them to/for to know for I LORD to consecrate: consecate them
13 “‘Komabe anthu a Israeli anandiwukira mʼchipululu. Iwo sanatsatire malangizo anga koma anakana malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo. Ndipo anayipitsa kotheratu Masabata anga. Choncho, ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawononga mʼchipululu.
and to rebel in/on/with me house: household Israel in/on/with wilderness in/on/with statute my not to go: walk and [obj] justice: judgement my to reject which to make: do [obj] them [the] man and to live in/on/with them and [obj] Sabbath my to profane/begin: profane much and to say to/for to pour: pour rage my upon them in/on/with wilderness to/for to end: finish them
14 Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Igupto.
and to make: do because name my to/for lest to profane/begin: profane to/for eye: seeing [the] nation which to come out: send them to/for eye: seeing their
15 Ndinalumbiranso kwa iwo mʼchipululu muja, nditakweza dzanja, kuti sindidzawalowetsanso mʼdziko limene ndinawapatsa, dziko la mwana alirenji, lokoma kwambiri kuposa mayiko ena onse.
and also I to lift: vow hand: vow my to/for them in/on/with wilderness to/for lest to come (in): bring [obj] them to(wards) [the] land: country/planet which to give: give to flow: flowing milk and honey beauty he/she/it to/for all [the] land: country/planet
16 Paja anakana malamulo anga, sanatsatire malangizo anga ndipo anayipitsa masabata anga. Mitima yawo inakonda mafano.
because in/on/with justice: judgement my to reject and [obj] statute my not to go: walk in/on/with them and [obj] Sabbath my to profane/begin: profane for after idol their heart their to go: went
17 Komabe ndinawamvera chisoni ndipo sindinawawononge kapena kuwatheratu mʼchipululu.
and to pity eye my upon them from to ruin them and not to make [obj] them consumption in/on/with wilderness
18 Tsono kwa ana awo mʼchipululu ndinati, ‘Musatsatire malangizo a makolo anu kapena kusunga malamulo awo kapena kudziyipitsa ndi mafano awo.
and to say to(wards) son: child their in/on/with wilderness in/on/with statute: decree father your not to go: walk and [obj] justice: judgement their not to keep: obey and in/on/with idol their not to defile
19 Ine ndine Yehova Mulungu wanu; tsatirani malangizo anga ndipo sungani malamulo anga.
I LORD God your in/on/with statute my to go: walk and [obj] justice: judgement my to keep: careful and to make: do [obj] them
20 Masabata anga muziwasunga ngati opatulika kuti akhale chizindikiro pakati pa Ine ndi inu. Mukatero mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
and [obj] Sabbath my to consecrate: consecate and to be to/for sign: indicator between me and between you to/for to know for I LORD God your
21 “‘Koma ana awo anandiwukira. Iwo sanatsatire malangizo anga, sanamvere malamulo anga, ngakhale kuti amapereka moyo kwa munthu amene amawamvera. Ndiponso anayipitsa Masabata anga. Choncho ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawonongeratu mʼchipululu momwemo.
and to rebel in/on/with me [the] son: child in/on/with statute my not to go: walk and [obj] justice: judgement my not to keep: careful to/for to make: do [obj] them which to make: do [obj] them [the] man and to live in/on/with them [obj] Sabbath my to profane/begin: profane and to say to/for to pour: pour rage my upon them to/for to end: expend face: anger my in/on/with them in/on/with wilderness
22 Koma sindinatero chifukwa cha dzina langa kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Iguptomo.
and to return: turn back [obj] hand my and to make: do because name my to/for lest to profane/begin: profane to/for eye: seeing [the] nation which to come out: send [obj] them to/for eye: seeing their
23 Choncho ndinalumbira mʼchipululu, nditakweza dzanja langa, kuti ndidzawabalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwamwazira ku mayiko akutali,
also I to lift: vow [obj] hand: vow my to/for them in/on/with wilderness to/for to scatter [obj] them in/on/with nation and to/for to scatter [obj] them in/on/with land: country/planet
24 chifukwa sanamvere malamulo anga, anakana malangizo anga, nayipitsa masabata anga, ndi kupembedza mafano a makolo awo.
because justice: judgement my not to make: do and statute my to reject and [obj] Sabbath my to profane/begin: profane and after idol father their to be eye their
25 Ine ndinawapatsanso malangizo amene sanali abwino ndi malamulo amene sakanatha kupeza nawo moyo.
and also I to give: give to/for them statute: decree not pleasant and justice: judgement not to live in/on/with them
26 Ndinawalekerera kuti adziyipitse ndi mphatso zawo zomwe, makamaka popereka ana awo oyamba kubadwa ngati nsembe zopsereza. Ndinatero kuti ndiwadetse nkhawa ndi kuti adziwe kuti Ine ndine Yehova.’
and to defile [obj] them in/on/with gift their in/on/with to pass all firstborn womb because be desolate: destroyed them because which to know which I LORD
27 “Tsono iwe mwana wa munthu, yankhula nawo Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti makolo anu anandinyozanso posaonetsa moyo wokhulupirika.
to/for so to speak: speak to(wards) house: household Israel son: child man and to say to(wards) them thus to say Lord YHWH/God still this to blaspheme [obj] me father your in/on/with be unfaithful they in/on/with me unfaithfulness
28 Nditawalowetsa mʼdziko limene ndinachita kulumbirira kuti ndidzawapatsa, iwo tsono ankapita kulikonse kumene anaona chitunda chachitali ndi mtengo wa masamba ambiri kukapereka kumeneko nsembe ndi zopereka zawo zimene zinkandikwiyitsa. Kumeneko ankapereka nsembe za fungo lokoma ndiponso nsembe za zakumwa.
and to come (in): bring them to(wards) [the] land: country/planet which to lift: vow [obj] hand: vow my to/for to give: give [obj] her to/for them and to see: see all hill to exalt and all tree leafy and to sacrifice there [obj] sacrifice their and to give: give there vexation offering their and to set: put there aroma soothing their and to pour there [obj] drink offering their
29 Tsono ndinawafunsa kuti: Kodi chitunda chimene mukupitako nʼchotani? Chitundachi chakhala chikutchedwa mpaka lero kuti ‘Chitunda cha Chipembedzo.’
and to say to(wards) them what? [the] high place which you(m. p.) [the] to come (in): come there and to call: call by name her Bamah till [the] day: today [the] this
30 “Tsono uwawuze Aisraeli kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi mudzadziyipitsa nokha monga anachitira makolo anu ndi kuchita chigololo ndi milungu yawo yonyansa?
to/for so to say to(wards) house: household Israel thus to say Lord YHWH/God in/on/with way: conduct father your you(m. p.) to defile and after abomination their you(m. p.) to fornicate
31 Pamene mubwera kudzapereka mphatso zanu ndi kudzapereka ana kuti akhale ngati nsembe zopsereza mumadziyipitsa ndi mafano anu mpaka lero. Kodi Aisraeli, ndingathe kukulolani bwanji kuti mulandire malangizo kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, sindidzalola kuti mupemphe nzeru kwa Ine.
and in/on/with to lift: bear gift your in/on/with to pass son: child your in/on/with fire you(m. p.) to defile to/for all idol your till [the] day: today and I to seek to/for you house: household Israel alive I utterance Lord YHWH/God if: surely no to seek to/for you
32 “‘Inu munanena kuti, ‘Tikufuna tikhale ngati anthu a mitundu ina, ngati anthu adziko lapansi, amene amapembedza mtengo ndi mwala.’ Koma zimene mukuganizazo sizidzachitika.
and [the] to ascend: rise upon spirit your to be not to be which you(m. p.) to say to be like/as nation like/as family [the] land: country/planet to/for to minister tree: wood and stone
33 Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ndi dzanja langa lamphamvu, nditasamula mkono wanga mokwiya kwambiri, Ine ndidzakhala wokulamulani.
alive I utterance Lord YHWH/God if: surely yes not in/on/with hand: power strong and in/on/with arm to stretch and in/on/with rage to pour: pour to reign upon you
34 Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndikukusonkhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munamwazikirako, ndi dzanja langa lamphamvu ndi lotambasuka ndili wokwiya kwambiri.
and to come out: send [obj] you from [the] people and to gather [obj] you from [the] land: country/planet which to scatter in/on/with them in/on/with hand: power strong and in/on/with arm to stretch and in/on/with rage to pour: pour
35 Ndidzakulowetsani mʼchipululu cha anthu a mitundu ina ndipo kumeneko, moonana maso ndi maso, ndidzakuzengani mlandu.
and to come (in): bring [obj] you to(wards) wilderness [the] people and to judge with you there face to(wards) face
36 Monga ndinawalangira makolo anu mʼchipululu cha dziko la Igupto, motero ndidzakulangani, akutero Ambuye Yehova.
like/as as which to judge with father your in/on/with wilderness land: country/planet Egypt so to judge with you utterance Lord YHWH/God
37 Ndidzakuwerengani ndi ndodo ya mʼbusa, kukulowetsani mʼchimango cha pangano langa.
and to pass [obj] you underneath: under [the] tribe: staff and to come (in): bring [obj] you in/on/with pledge [the] covenant
38 Ndidzakuchotserani anthu amene anandigalukira ndi kundiwukira. Ngakhale ndidzawatulutsa mʼdziko limene akukhalamo, koma sadzalowamo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
and to purify from you [the] to rebel and [the] to transgress in/on/with me from land: country/planet sojourning their to come out: send [obj] them and to(wards) land: soil Israel not to come (in): come and to know for I LORD
39 “‘Koma inu Aisraeli, zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Pitani katumikireni mafano anu onse, aliyense wa inu! Koma mʼtsogolo mwake mudzandimvera ndithu ndipo simudzayipitsa dzina langa lopatulika popereka mphatso zanu kwa mafano.
and you(m. p.) house: household Israel thus to say Lord YHWH/God man: anyone idol his to go: went to serve and after if nothing you to hear: hear to(wards) me and [obj] name holiness my not to profane/begin: profane still in/on/with gift your and in/on/with idol your
40 Pakuti pa phiri langa lopatulika, phiri lalitali la ku Israeli, akutero Ambuye Yehova, Aisraeli onse adzanditumikira, ndipo kumeneko Ine ndidzawalandira. Kumeneko ndidzayembekeza zopereka zanu ndi mphatso zanu zopambana, pamodzi ndi nsembe zanu zonse zopatulika.
for in/on/with mountain: mount holiness my in/on/with mountain: mount height Israel utterance Lord YHWH/God there to serve: minister me all house: household Israel all his in/on/with land: country/planet there to accept them and there to seek [obj] contribution your and [obj] first: best tribute your in/on/with all holiness your
41 Ndidzakulandirani ngati nsembe ya fungo lokoma ndikadzakutulutsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukusokhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munabalalitsidwirako. Motero ndidzadzionetsa pakati panu kuti ndine woyera ndipo mitundu ya anthu idzaona.
in/on/with aroma soothing to accept [obj] you in/on/with to come out: send I [obj] you from [the] people and to gather [obj] you from [the] land: country/planet which to scatter in/on/with them and to consecrate: holiness in/on/with you to/for eye: seeing [the] nation
42 Tsono mudzadziwa kuti ndine Yehova ndikadzabwera nanu ku dziko la Israeli, dziko limene ndinalumbira kuti ndidzapereka kwa makolo anu.
and to know for I LORD in/on/with to come (in): bring I [obj] you to(wards) land: soil Israel to(wards) [the] land: country/planet which to lift: vow [obj] hand: vow my to/for to give: give [obj] her to/for father your
43 Kumeneko mudzakumbukira makhalidwe anu ndi machitidwe anu onse amene munadziyipitsa nawo, ndipo mudzanyansidwa nokha chifukwa cha zoyipa zimene munachita.
and to remember there [obj] way: conduct your and [obj] all wantonness your which to defile in/on/with them and to loath in/on/with face of your in/on/with all bad: evil your which to make
44 Inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzakuchitirani zabwino chifukwa cha dzina langa koma osati molingana ndi njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu okhota, inu Aisraeli, akutero Ambuye Yehova.’”
and to know for I LORD in/on/with to make: do I with you because name my not like/as way: conduct your [the] bad: evil and like/as wantonness your [the] to ruin house: household Israel utterance Lord YHWH/God
45 Yehova anandiyankhula nati:
and to be word LORD to(wards) me to/for to say
46 “Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane kummwera; ndipo lalika mawu odzudzula anthu akummwera ndipo unenere zodzudzula dziko la nkhalango ya kummwera.
son: child man to set: make face your way: direction south [to] and to drip/prophesy to(wards) south and to prophesy to(wards) wood [the] land: country Negeb
47 Iwuze nkhalango yakummwera kuti, ‘Imvani mawu a Yehova! Ambuye Yehova akuti: Ndikuyatsa moto ndipo motowo udzapsereza mitengo yako yonse yayiwisi ndi yowuma yomwe. Malawi ake sadzazimitsika ndipo aliyense kuchokera kummwera mpaka kumpoto adzapsa nawo.
and to say to/for wood [the] Negeb to hear: hear word LORD thus to say Lord YHWH/God look! I to kindle in/on/with you fire and to eat in/on/with you all tree fresh and all tree dry not to quench flame flame and to burn in/on/with her all face from Negeb north [to]
48 Aliyense adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndayatsa motowo, ndipo sudzazimitsidwa.’”
and to see: see all flesh for I LORD to burn: burn her not to quench
49 Ndipo ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova! Anthu akungondinena kuti, ‘Kodi suja amangonena nthano chabe ameneyu!’”
and to say alas! Lord YHWH/God they(masc.) to say to/for me not to use a proverb proverb he/she/it

< Ezekieli 20 >