< Ezekieli 20 >

1 Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu, chaka chachisanu ndi chiwiri, ena mwa akuluakulu a Israeli anabwera kudzapempha nzeru kwa Yehova, ndipo anakhala pansi pamaso panga.
А в седмата година, в петия месец, на десетия ден от месеца, някои от Израилевите старейшини дойдоха да се допитат до Господа, и седнаха пред мене.
2 Tsono Yehova anandiyankhula nati:
И Господното слово дойде към мене и рече:
3 “Iwe mwana wa munthu, ayankhule akuluakulu a Israeli ndi kuwawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Kodi mwabwera kudzapempha nzeru kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, Ine sindidzakulolani kupempha nzeru kwa Ine, akutero Ambuye Yehova.’
Сине човешки, говори на Израилевите старейшини и кажи им: Така казва Господ Иеова: Да се допитате до Мене ли сте дошли? Заклевам се в живота Си, казва Господ Иеова, не приемам да се допитате до мене.
4 “Kodi uwaweruza? Iwe mwana wa munthu, kodi ugamula mlandu wawo? Uwadziwitse tsono zonyansa zimene anachita makolo awo, uwawuze kuti,
Ще се застъпиш ли за тях, сине човешки? ще се застъпиш ли за тях? Покажи им мерзостите на техните бащи, като им речеш:
5 ‘Ambuye Yehova akuti: Pa tsiku limene ndinasankha Israeli, ndinalumbira kwa zidzukulu za nyumba ya Yakobo ndipo ndinadziwulula kwa iwo ku Igupto. Ndinalumbira ndi kuwawuza kuti: Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Така казва Господ Иеова: В деня, когато избрах Израиля, и се заклех към рода на Якововия дом, и им се открих в Египетската земя, и им се заклех като рекох: Аз съм Господ вашият Бог,
6 Pa tsiku limenelo ndinalumbira kwa iwo kuti ndidzawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kupita nawo ku dziko limene ndinawapezera, dziko la mwana alirenji, dziko lokongola kwambiri kupambana mayiko ena.
в оня ден заклех им се, че ще ги изведа из Египетската земя и ще ги доведа в земя, която бях промислил за тях, земя дето тече мляко и мед, с която се хвалят всички страни.
7 Ndipo ndinawawuza kuti, ‘Aliyense ataye zinthu zonse zonyansa zimene ankasangalala nazo, ndipo musadziyipitse ndi mafano a Igupto, Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
И рекох им: Отхвърлете всеки мерзостите, които е поставил пред очите си, и не се осквернявайте с египетските идоли; Аз съм Господ вашият Бог.
8 “‘Koma iwo anandiwukira ndipo sanafune kundimvera. Palibe amene anataya zonyansa zonse zimene ankasangalala nazo. Panalibenso amene anasiya mafano a ku Igupto. Tsono ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwaonetsa mkwiyo wanga mʼdziko la Igupto momwemo.
Те обаче въстанаха против Мене и не искаха да Ме послушат; не отхвърлиха всеки мерзостите, които бе поставил пред очите си, нито оставиха египетските идоли. Тогава рекох да излея яростта Си върху тях, за да изчерпя гнева Си против тях всред Египетската земя.
9 Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene ankakhala pakati pawo. Paja ndinali nditaonetsa mphamvu zanga pamaso pa mitunduyo potulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto.
Но подействувах заради името Си, да се не оскверни то пред народите, между които бяха, и пред които им се открих като ги изведох из Египетската земя,
10 Choncho ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kubwera nawo mʼchipululu.
Затова като ги изведох из Египетската земя, заведох ги в пустинята.
11 Ndinawapatsa malangizo anga ndi kuwadziwitsa malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo.
И дадох им повеленията Си и започнах ги със съдбите Си, които като извършва човек ще живее чрез тях.
12 Ndinawapatsanso Masabata ngati chizindikiro pakati pathu, kuti adziwe kuti Ine Yehova ndinawapatula.
Дадох им и съботите Си да бъдат знак между Мене и тях, за да познаят, че Аз Господ ги освещавам.
13 “‘Komabe anthu a Israeli anandiwukira mʼchipululu. Iwo sanatsatire malangizo anga koma anakana malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo. Ndipo anayipitsa kotheratu Masabata anga. Choncho, ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawononga mʼchipululu.
Но Израилевият дом въстана против Мене в пустинята; не ходиха в повеленията Ми, но отхвърлиха съдбите Ми, които като извършва човек ще живее чрез тях, и твърде много оскверниха съботите Ми. Тогава рекох да излея яростта Си върху тях в пустинята, за да ги изтребя.
14 Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Igupto.
Но подействувах заради името Си, да се не оскверни то пред народите, пред които бях ги извел.
15 Ndinalumbiranso kwa iwo mʼchipululu muja, nditakweza dzanja, kuti sindidzawalowetsanso mʼdziko limene ndinawapatsa, dziko la mwana alirenji, lokoma kwambiri kuposa mayiko ena onse.
При това, Аз им се заклех в пустинята, че не ще ги заведа в земята, която им бях дал, земя, гдето тече мляко и мед, с която се хвалят всичките страни,
16 Paja anakana malamulo anga, sanatsatire malangizo anga ndipo anayipitsa masabata anga. Mitima yawo inakonda mafano.
защото отхвърлиха съдбите Ми, не ходиха в повеленията Ми, и оскверниха съботите Ми; понеже сърцата им отиваха след идолите им.
17 Komabe ndinawamvera chisoni ndipo sindinawawononge kapena kuwatheratu mʼchipululu.
Обаче, окото Ми ги пощади, та не ги изтребих, нито ги довърших в пустинята.
18 Tsono kwa ana awo mʼchipululu ndinati, ‘Musatsatire malangizo a makolo anu kapena kusunga malamulo awo kapena kudziyipitsa ndi mafano awo.
И рекох на чадата им в пустинята: Не ходете по повеленията на бащите си, нито се осквернявайте с идолите им.
19 Ine ndine Yehova Mulungu wanu; tsatirani malangizo anga ndipo sungani malamulo anga.
Аз съм Господ вашият Бог; в Моите повеления ходете, и Моите съдби пазете и извършвайте ги;
20 Masabata anga muziwasunga ngati opatulika kuti akhale chizindikiro pakati pa Ine ndi inu. Mukatero mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
освещавайте още и съботите Ми, и нека бъдат знак между Мене и вас, за да познаете, че Аз Господ съм ваш Бог.
21 “‘Koma ana awo anandiwukira. Iwo sanatsatire malangizo anga, sanamvere malamulo anga, ngakhale kuti amapereka moyo kwa munthu amene amawamvera. Ndiponso anayipitsa Masabata anga. Choncho ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawonongeratu mʼchipululu momwemo.
Обаче, чадата въстанаха против Мене; не ходиха в повеленията ми, нито опазиха съдбите ми да ги вършат, които ако извършва човек, ще живее чрез тях, и оскверниха съботите Ми. Тогава рекох да излея яростта Си върху тях, за да изчерпя гнева Си против тях в пустинята.
22 Koma sindinatero chifukwa cha dzina langa kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Iguptomo.
Но оттеглих ръката Си, и подействувах заради името Си, да се не оскверни то пред народите, пред които ги бях извел.
23 Choncho ndinalumbira mʼchipululu, nditakweza dzanja langa, kuti ndidzawabalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwamwazira ku mayiko akutali,
При това, Аз им се заклех в пустинята, че ще ги разпръсна между народите, и ще ги разсея по разни страни,
24 chifukwa sanamvere malamulo anga, anakana malangizo anga, nayipitsa masabata anga, ndi kupembedza mafano a makolo awo.
защото не извършиха съдбите Ми, но отхвърлиха повеленията Ми, оскверниха съботите Ми, и очите им бяха към идолите на бащите им.
25 Ine ndinawapatsanso malangizo amene sanali abwino ndi malamulo amene sakanatha kupeza nawo moyo.
Затова, и Аз им дадох повеления, които не бяха добри, и съдби, чрез които не щяха да живеят,
26 Ndinawalekerera kuti adziyipitse ndi mphatso zawo zomwe, makamaka popereka ana awo oyamba kubadwa ngati nsembe zopsereza. Ndinatero kuti ndiwadetse nkhawa ndi kuti adziwe kuti Ine ndine Yehova.’
и оставих ги да се осквернят в приносите си, дето превеждаха през огън всяко първородно, за да ги запустя, та да познаят, че Аз съм Господ.
27 “Tsono iwe mwana wa munthu, yankhula nawo Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti makolo anu anandinyozanso posaonetsa moyo wokhulupirika.
Затова, сине човешки, говори на Израилевия дом, като им речеш: Така казва Господ Иеова: Още и в това Ме охулиха бащите ви, дето вършиха престъпления против Мене.
28 Nditawalowetsa mʼdziko limene ndinachita kulumbirira kuti ndidzawapatsa, iwo tsono ankapita kulikonse kumene anaona chitunda chachitali ndi mtengo wa masamba ambiri kukapereka kumeneko nsembe ndi zopereka zawo zimene zinkandikwiyitsa. Kumeneko ankapereka nsembe za fungo lokoma ndiponso nsembe za zakumwa.
Защото, като ги доведох в земята, която бях се заклел да им дам, тогава разгледаха всеки висок хълм и всяко сенчесто дърво, и там принасяха жертвите си, там представяха оскърбителните си приноси, там полагаха благоуханията си, и там изливаха възлиянията си.
29 Tsono ndinawafunsa kuti: Kodi chitunda chimene mukupitako nʼchotani? Chitundachi chakhala chikutchedwa mpaka lero kuti ‘Chitunda cha Chipembedzo.’
Тогава им рекох: Що е това високо място, на което отивате, та да се нарича Вама и до днес?
30 “Tsono uwawuze Aisraeli kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi mudzadziyipitsa nokha monga anachitira makolo anu ndi kuchita chigololo ndi milungu yawo yonyansa?
Затова, кажи на Израилевия дом - Така казва Господ Иеова: Като се осквернявате по примера на бащите си, и блудствувате с мерзостите им,
31 Pamene mubwera kudzapereka mphatso zanu ndi kudzapereka ana kuti akhale ngati nsembe zopsereza mumadziyipitsa ndi mafano anu mpaka lero. Kodi Aisraeli, ndingathe kukulolani bwanji kuti mulandire malangizo kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, sindidzalola kuti mupemphe nzeru kwa Ine.
и до днес се осквернявате с всичките си идоли, като принасяте даровете си и превеждате синовете си през огъня, то до Мене ли ще се допитате, доме Израилев? Заклевам се в живота Си, казва Господ Иеова, не приемам да се допитате до Мене.
32 “‘Inu munanena kuti, ‘Tikufuna tikhale ngati anthu a mitundu ina, ngati anthu adziko lapansi, amene amapembedza mtengo ndi mwala.’ Koma zimene mukuganizazo sizidzachitika.
И онова, което размишлявате, никак няма да се сбъдне, дето казвате: Ще станем като народите, като племената на другите страни; ще служим на дървета и на камъни.
33 Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ndi dzanja langa lamphamvu, nditasamula mkono wanga mokwiya kwambiri, Ine ndidzakhala wokulamulani.
Заклевам се в живота Си, казва Господ Иеова, непременно с мощна ръка, с издигната мишца, и с излеяна ярост ще царувам над вас.
34 Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndikukusonkhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munamwazikirako, ndi dzanja langa lamphamvu ndi lotambasuka ndili wokwiya kwambiri.
Като ви изведа измежду племената, и ви събера от страните, в които сте разпръснати с мощна ръка, с издигната мишца, и с излеяна ярост,
35 Ndidzakulowetsani mʼchipululu cha anthu a mitundu ina ndipo kumeneko, moonana maso ndi maso, ndidzakuzengani mlandu.
ще ви заведа в пустинята на заточение между племената, и там ще се съдя с вас лице с лице.
36 Monga ndinawalangira makolo anu mʼchipululu cha dziko la Igupto, motero ndidzakulangani, akutero Ambuye Yehova.
Както се съдих с бащите ви в пустинята на Египетската земя, така ще се съдя с вас, казва Господ Иеова.
37 Ndidzakuwerengani ndi ndodo ya mʼbusa, kukulowetsani mʼchimango cha pangano langa.
Ще ви прекарам под жезъла и ще ви заведа във връзките на завета.
38 Ndidzakuchotserani anthu amene anandigalukira ndi kundiwukira. Ngakhale ndidzawatulutsa mʼdziko limene akukhalamo, koma sadzalowamo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
И ще изчистя отсред вас бунтовниците и ония, които вършат престъпления против Мене; ще ги извадя из земята, гдето пришелствуват; но те няма да влязат в Израилевата земя; и ще познаете, че Аз съм Господ.
39 “‘Koma inu Aisraeli, zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Pitani katumikireni mafano anu onse, aliyense wa inu! Koma mʼtsogolo mwake mudzandimvera ndithu ndipo simudzayipitsa dzina langa lopatulika popereka mphatso zanu kwa mafano.
А вие, доме Израилев, така казва Господ Иеова: Ако не искате да слушате Мене, идете, служете и за напред всеки на идолите си; но не осквернявайте вече светото Ми име с даровете си и с идолите си.
40 Pakuti pa phiri langa lopatulika, phiri lalitali la ku Israeli, akutero Ambuye Yehova, Aisraeli onse adzanditumikira, ndipo kumeneko Ine ndidzawalandira. Kumeneko ndidzayembekeza zopereka zanu ndi mphatso zanu zopambana, pamodzi ndi nsembe zanu zonse zopatulika.
Защото на Моя свят хълм, на Израилевия висок хълм, казва Господ Иеова, там целият Израилев дом, всичките в страната, ще Ми служат; там ще ги приема, и там ще поискам приносите ви и първаците на даровете ви, както и всичките ви свети неща.
41 Ndidzakulandirani ngati nsembe ya fungo lokoma ndikadzakutulutsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukusokhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munabalalitsidwirako. Motero ndidzadzionetsa pakati panu kuti ndine woyera ndipo mitundu ya anthu idzaona.
Ще ви приема като благоухание, когато ви изведа изсред племената и ви събера от страните, в които бяхте пръснати; и ще се осветя във вас пред народите.
42 Tsono mudzadziwa kuti ndine Yehova ndikadzabwera nanu ku dziko la Israeli, dziko limene ndinalumbira kuti ndidzapereka kwa makolo anu.
И ще познаете, че Аз съм Господ, когато ви доведа в Израилевата земя, в страната, която се заклех да дам на бащите ви.
43 Kumeneko mudzakumbukira makhalidwe anu ndi machitidwe anu onse amene munadziyipitsa nawo, ndipo mudzanyansidwa nokha chifukwa cha zoyipa zimene munachita.
Там ще си спомните за постъпките си, и за всичките си дела, в които се осквернихте; и ще се погнусите сами от себе си поради всичките злини, които сторихте.
44 Inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzakuchitirani zabwino chifukwa cha dzina langa koma osati molingana ndi njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu okhota, inu Aisraeli, akutero Ambuye Yehova.’”
И ще познаете, че Аз съм Господ, когато така постъпя с вас заради името Си, а не според злите ви постъпки нито според развратните ви дела, доме Израилев, казва Господ Иеова.
45 Yehova anandiyankhula nati:
И Господното слово дойде към мене и рече:
46 “Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane kummwera; ndipo lalika mawu odzudzula anthu akummwera ndipo unenere zodzudzula dziko la nkhalango ya kummwera.
Сине човешки, насочи лицето си към юг и направи да капне словото ти към юг и пророкувай против леса на южното поле.
47 Iwuze nkhalango yakummwera kuti, ‘Imvani mawu a Yehova! Ambuye Yehova akuti: Ndikuyatsa moto ndipo motowo udzapsereza mitengo yako yonse yayiwisi ndi yowuma yomwe. Malawi ake sadzazimitsika ndipo aliyense kuchokera kummwera mpaka kumpoto adzapsa nawo.
Кажи на южния лес: Слушай Господното слово. Така казва Господ Иеова: Ето, Аз ще запаля огън в тебе, който ще изяде всяка зелено дърво в тебе, и всяко сухо дърво; пламтящият пламък не ще угасне, а от него ще изгори цялата повърхност от юг до север.
48 Aliyense adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndayatsa motowo, ndipo sudzazimitsidwa.’”
Всяка твар ще види, че Аз Господ го запалих; няма да угасне.
49 Ndipo ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova! Anthu akungondinena kuti, ‘Kodi suja amangonena nthano chabe ameneyu!’”
Тогава рекох: Горко, Господи Иеова! Те казват за мене: Този не говори ли притчи?

< Ezekieli 20 >