< Ezekieli 2 >
1 Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, imirira kuti ndiyankhule nawe.”
I rzekł do mnie: Synu człowieczy! stań na nogi twe, a będę mówił z tobą.
2 Pamene ankayankhula nane, Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa, ndipo ndinamva Iye akundiyankhula.
I wstąpił w mię duch, gdy przemówił do mnie, a postawił mię na nogi moje, i słyszałem mówiącego do mnie;
3 Iye anati, “Iwe mwana wa munthu, Ine ndikukutuma kwa Aisraeli, mtundu wa anthu owukira umene wandiwukira Ine; Iwo ndi makolo awo akhala akundiwukira Ine mpaka lero lino.
Który rzekł do mnie: Synu człowieczy! Ja cię posyłam do synów Izraelskich, do narodów odpornych, którzy mi się sprzeciwili; oni i ojcowie ich występowali przeciwko mnie aż prawie do dnia tego:
4 Ndikukutuma kwa anthu okanika ndiponso nkhutukumve. Ndikukutuma kuti akawawuze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena.
Do tych, mówię, synów niewstydliwej twarzy, i zatwardziałego serca Ja cię posyłam, i rzeczesz im: Tak mówi panujący Pan.
5 Kaya akamva kaya sakamvera, pakuti iwo ndi anthu opanduka, komabe adzadziwa kuti mneneri ali pakati pawo.
Niech oni słuchają albo nie, gdyż domem odpornym są, przecież niech wiedzą, że prorok był w pośrodku ich.
6 Tsono iwe mwana wa munthu, usachite nawo mantha kapena kuopa zimene azikanena. Usachite mantha, ngakhale minga ndi mkandankhuku zikuzinge ndipo ukukhala pakati pa zinkhanira. Usachite mantha ndi zimene akunena kapena kuopsedwa ndi nkhope zawo, popeza anthuwa ndi awupandu.
Ale ty, synu człowieczy! nie bój się ich, ani się lękaj słów ich, że odporni a jako ciernie są przeciwko tobie, a że między niedźwiadkami mieszkasz; słów ich nie bój się, ani się twarzy ich lękaj, przeto, że domem odpornym są.
7 Ukawawuze ndithu mawu anga, kaya akamva kaya sakamva. Paja anthuwa ndi awupandu.
Ale mów słowa moje do nich, niech oni słuchają albo nie, gdyż odpornymi są.
8 Koma iwe mwana wa munthu, mvetsera zimene ndikukuwuza. Usakhale wowukira ngati iwowo. Tsono yasama pakamwa pako kuti udye chimene ndikukupatsa.”
Lecz ty, synu człowieczy! słuchaj, co Ja mówię do ciebie: Nie bądź odporny, jako ten dom odporny; otwórz usta swe, a zjedz, coć dam.
9 Nditayangʼana ndinangoona dzanja litaloza ine, litagwira mpukutu wolembedwa.
I widziałem, a oto ręka była wyciągniona do mnie, a oto w niej zwinione księgi,
10 Anawufunyulura pamaso panga. Mpukutu wonse unali wolembedwa kuseri nʼkuseri. Ndipo mawu amene analembedwa mʼmenemo anali a madandawulo, maliro ndi matemberero.
Które rozwinął przedemną; a były popisane z przodku i z końca, a w nich były napisane narzekania, i wzdychania i bieda.